< Eksodo 5 >
1 Zitachitika izi, Mose ndi Aaroni anapita kwa Farao ndipo anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Aloleni anthu anga apite, kuti akachite chikondwerero cha Ine mʼchipululu.’”
And after they went Moses and Aaron and they said to Pharaoh thus he says Yahweh [the] God of Israel let go people my so they may celebrate a festival to me in the wilderness.
2 Koma Farao anati, “Yehova ndani kuti ine ndimumvere ndi kulola Aisraeli kuti apite? Ine Yehova sindikumudziwa ndipo sindilola kuti Aisraeli apite.”
And he said Pharaoh who? [is] Yahweh that I will listen to voice his by letting go Israel not I know Yahweh and also Israel not I will let go.
3 Ndipo iwo anati, “Mulungu wa Ahebri anakumana nafe. Chonde tiloleni tipite ulendo wa masiku atatu ku chipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu, ngati sititero iye adzatipweteka ndi miliri kapena lupanga.”
And they said [the] God of the Hebrews he has met with us let us go please a journey of three days in the wilderness and let us sacrifice to Yahweh God our lest he should fall on us with pestilence or with the sword.
4 Koma mfumu ya Igupto inati, “Mose ndi Aaroni, chifukwa chiyani mukuchititsa anthuwa kuti asagwire ntchito zawo? Bwererani ku ntchito zanu!”
And he said to them [the] king of Egypt why? O Moses and Aaron are you causing to refrain the people from work its go to forced labor your.
5 Ndiponso Farao anati, “Taonani, anthuwa mʼdziko muno alipo ochuluka, ndipo inu mukuwaletsa kugwira ntchito.”
And he said Pharaoh here! [is] many now [the] people of the land and you have caused to cease them from forced labor their.
6 Pa tsiku lomwelo Farao analamulira akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu kuti
And he commanded Pharaoh on the day that the taskmasters over the people and foremen its saying.
7 “Inu musawapatsenso udzu wopangira njerwa monga mumachitira kale, iwo azipita ndi kukatenga udzu wawo.
Not you will repeat! to give straw to the people to make bricks the bricks as yesterday three days ago they let them go and they may gather for themselves straw.
8 Koma musawachepetsere chiwerengero cha njerwa chomwe munawalamulira kale kuti aziwumba. Iwowa ndi aulesi. Nʼchifukwa chake akulira kuti, ‘Tiloleni tipite tikapereke nsembe kwa Mulungu wathu.’
And [the] measurement of the bricks which they [were] making yesterday three days ago you will place on them not you will diminish from it for [are] idle they there-fore they [are] crying out saying let us go let us sacrifice to God our.
9 Muwakhawulitse ndi ntchito anthu amenewa kuti azitanganidwa, asakhale ndi mpata omvera zabodza.”
Let it be heavy the labor on the men so they may work in it and may not them pay attention to words of falsehood.
10 Choncho akapitawo a thangata ndi anzawo a Chiisraeli amene ankayangʼanira anthu anapita kwa anthu aja nati, “‘Farao akuti sadzakupatsaninso udzu.
And they went out [the] taskmasters of the people and foremen its and they said to the people saying thus he says Pharaoh not I [am] giving to you straw.
11 Mʼmalo mwake mupite mukadzimwetere udzu kulikonse kumene mungawupeze. Komabe ntchito yanu sichepetsedwa.’”
You go acquire for yourselves straw from where you will find [it] for not [is] diminished from labor your anything.
12 Kotero anthuwo anamwazikana mʼdziko lonse la Igupto kukamweta udzu.
And it scattered the people in all [the] land of Egypt to gather stubble for the straw.
13 Akapitawo a thangata aja anawafulumiza anthu aja nati, “Malizani kugwira ntchito yanu ya tsiku ndi tsiku monga mmene zinalili pamene munkapatsidwa udzu.”
And the taskmasters [were] pressing [them] saying complete work your a matter of a day in day its just as when was the straw.
14 Akapitawo a thangata a Farao ankawamenya oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja nawapanikiza kuti, “Chifukwa chiyani lero simunawumbe chiwerengero chovomerezeka cha njerwa monga chakale chija?”
And they were struck [the] foremen of [the] people of Israel whom they had appointed over them [the] taskmasters of Pharaoh saying why? not have you completed prescribed portion your by making bricks as yesterday three days ago neither yesterday nor this day.
15 Pamenepo oyangʼanira anzawo a Chiisraeli aja anapita kukadandaula kwa Farao kuti, “Chifukwa chiyani mwachitira antchito anu zotere?
And they went [the] foremen of [the] people of Israel and they cried out to Pharaoh saying why? are you doing thus to servants your.
16 Antchito anu sakupatsidwa udzu, komabe akutiwuza kuti, ‘Umbani njerwa!’ Antchito anu akumenyedwa, koma cholakwa sichili ndi anthu anu.”
Straw not [is being] given to servants your and bricks [people are] saying to us make and there! servants your [are] being struck and you have sinned people your.
17 Farao anati, “Ulesi, inu ndinu alesi! Nʼchifukwa chake mukumanena kuti, ‘Mutilole tipite kukapereka nsembe kwa Yehova.’
And he said [are] idle you idle there-fore you [are] saying let us go let us sacrifice to Yahweh.
18 Pitani tsopano kuntchito. Simudzapatsidwanso udzu komabe muyenera kuwumba muyeso wanu wovomerezeka wa njerwa.”
And now go work and straw not it will be given to you and [the] measurement of bricks you will give.
19 Oyangʼanira anzawo a Chiisraeli anazindikira kuti ali pa mavuto pamene anawuzidwa kuti, “Musachepetse chiwerengero cha njerwa chimene muyenera kuwumba tsiku lililonse.”
And they saw [the] foremen of [the] people of Israel themselves in trouble saying not you will diminish from bricks your a matter of a day in day its.
20 Atachoka pamaso pa Farao, anakumana ndi Mose ndi Aaroni akuwadikira,
And they met Moses and Aaron standing to meet them when came out they from with Pharaoh.
21 ndipo iwo anati, “Yehova akupenyeni ndi kukuweruzani popeza mwachititsa Farao ndi nduna zake kuti anyansidwe nafe ndipo mwayika lupanga mʼmanja mwawo kuti atiphe.”
And they said to them may he look Yahweh on you and may he judge that you have made stink odor our in [the] eyes of Pharaoh and in [the] eyes of servants his to put a sword in hand their to kill us.
22 Mose anabwerera kwa Yehova ndipo anati, “Chonde Ambuye, chifukwa chiyani mukuzunza anthu anu? Kodi munanditumira zimenezi?
And he returned Moses to Yahweh and he said O Lord why? have you done harm to the people this why? this did you send me.
23 Chipitireni changa kwa Farao kukamuyankhula mʼdzina lanu, iye wakhala akuzunza anthuwa, ndipo inu simunawapulumutse konse anthu anu.”
And from then I went to Pharaoh to speak in name your he has done harm to the people this and certainly not you have delivered people your.