< Eksodo 36 >

1 Choncho Bezaleli, Oholiabu pamodzi ndi anthu aluso onse amene Yehova anawapatsa luso ndi nzeru zodziwira kupanga zofunika zonse zomangira malo opatulika, adzapanga zonse iwowo, monga momwe Yehova analamulira.”
Potem so Becalél in Oholiáb in vsak človek modrega srca, v katerega je Gospod položil modrost in razumevanje, da ve, kako delati vse vrste dela za službo svetišča, izvršili glede na vse, kakor je zapovedal Gospod.
2 Ndipo Mose anayitana Bezaleli ndi Oholiabu ndiponso munthu aliyense waluso amene Yehova anamupatsa luso ndiponso amene anali ndi mtima wofuna kugwira ntchito.
Mojzes je poklical Becaléla in Oholiába in vsakega človeka modrega srca, v katerega srce je Gospod položil modrost, torej vsakega, ki ga je razvnelo srce, da pride k delu, da ga opravi
3 Iwo analandira kuchokera kwa Mose zopereka zonse Aisraeli anabweretsa kuti agwirire ntchito yomanga malo wopatulika. Ndipo anthu anapitirira kupereka zopereka zaufulu mmawa uliwonse.
in od Mojzesa so prejeli vso daritev, ki so jo Izraelovi otroci prinesli za delo službe svetišča, da to istočasno opravijo. In k njemu so še vsako jutro prinašali prostovoljne daritve.
4 Kotero amisiri onse amene amagwira ntchito yonse ya malo wopatulika anasiya ntchitoyo
Prišli so vsi modri možje, ki so opravljali delo pri svetišču, vsak človek od svojega dela, ki so ga opravljali
5 ndipo anati kwa Mose, “Anthu akubweretsa kuposa zimene zikufunika kugwirira ntchito imene Yehova analamulira kuti ichitike.”
in spregovorili Mojzesu, rekoč: »Ljudstvo prinaša veliko več kakor dovolj za delo služenja, ki ga je Gospod zapovedal narediti.«
6 Choncho Mose analamulira ndipo analengeza mu msasa onse, “Mwamuna kapena mayi aliyense asaperekenso chopereka chilichonse cha ku malo wopatulika.” Choncho anthu analetsedwa kubweretsa zambiri,
Mojzes je dal zapoved in naredili so, da je bila razglašena po taboru, rekoč: »Naj niti moški niti ženska ne opravlja več nobenega dela za darovanje svetišču.« Tako je bilo ljudstvo zadržano od prinašanja.
7 chifukwa zimene anali nazo zinali zoposera zimene zimafunika kugwirira ntchito yonse.
Kajti stvari, ki so jih imeli, je bilo zadosti za izvršitev vsega dela in še preveč.
8 Anthu onse aluso pakati pa anthu ogwira ntchitoyo anapanga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso anapeta pa nsaluzo Akerubi.
Vsak človek modrega srca med njimi, ki opravlja delo šotorskega svetišča, je naredil deset zaves iz sukane tančice, modre, vijolične in škrlatne. S kerubi spretne izdelave jih je naredil.
9 Nsalu zonse zinali zofanana. Mulitali mwake zinali mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
Dolžina ene zavese je bila osemindvajset komolcev in širina ene zavese štiri komolce. Zavese so bile vse ene velikosti.
10 Iwo analumikiza nsalu zisanu, kuti ikhale nsalu imodzi ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
Spojil je pet zaves eno k drugi in drugih pet zaves je spojil eno k drugi.
11 Kenaka anapanga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
Naredil je zanke iz modre na robu prve zavese od zarobitve v spoju. Podobno je naredil na zadnji strani druge zavese na spoju druge.
12 Iwo anasokerera zokolowekamo makumi asanu pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Anapanga kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
Petdeset zank je naredil na eni zavesi in petdeset zank je naredil na robu zavese, ki je bila na spoju druge. Zanke so eno zaveso držale k drugi.
13 Kenaka anapanga ngowe zagolide 50 zolumikizira nsalu ziwirizo kotero kuti zinapanga chihema chimodzi.
Naredil je petdeset zaponk iz zlata in zavese spojil z zaponkami skupaj eno k drugi. Tako je postalo eno šotorsko svetišče.
14 Iwo anapanga nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zinalipo khumi ndi imodzi.
Naredil je zavese iz kozje dlake za šotor nad šotorskim svetiščem. Naredil je enajst zaves.
15 Nsalu zonse khumi ndi imodzi zinali zofanana. Mulitali mwake munali mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake munali mamita awiri.
Dolžina ene zavese je bila trideset komolcev in štiri komolce je bila širina ene zavese. Enajst zaves je bilo ene velikosti.
16 Iwo analumikiza nsalu zisanu kukhala nsalu imodzi ndipo nsalu zinazo zisanu ndi imodzi, analumikizanso kukhala nsalu imodzinso.
Spojil je pet zaves posebej in šest zaves posebej.
17 Kenaka anasokerera zokolowekamo makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija ndiponso anapanga zokolowekamo zina makumi asanu mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
Naredil je petdeset zank na zadnjem robu zavese na spoju in petdeset zank je naredil na robu zavese, ki spaja drugo.
18 Iwo anapanga ngowe 50 zamkuwa zolowetsa mu zokolowekazo ndipo anaphatikiza nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
Naredil je petdeset zaponk iz brona, da šotor spoji skupaj, da bo ta lahko eno.
19 Ndipo anapanga chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake anapanganso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
Naredil je pokrivalo za šotor iz rdeče barvanih ovnovih kož in nad tem pokrivalo iz jazbečevih kož.
20 Iwo anapanga maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
Naredil je deske za šotorsko svetišče iz akacijevega lesa, stoječe pokonci.
21 Feremu iliyonse inali yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake munali masentimita 69.
Dolžina deske je bila deset komolcev in širina deske en komolec in pol.
22 Thabwa lililonse linali ndi zolumikizira ziwiri. Iwo anapanga maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
Ena deska je imela dva zatiča, enako oddaljena eden od drugega. Tako je naredil za vse deske šotorskega svetišča.
23 Anapanga maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho,
Naredil je deske za šotorsko svetišče; dvajset desk za južno stran, proti jugu.
24 ndiponso anapanga matsinde 40 asiliva ndipo anawayika pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse anayika matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
Pod dvajsetimi deskami je naredil štirideset podstavkov iz srebra; dva podstavka pod eno desko za njena dva zatiča in dva podstavka pod drugo desko za njena dva zatiča.
25 Iwo anapanganso maferemu makumi awiri a mbali yakumpoto ya chihemacho,
Za drugo stran šotorskega svetišča, ki je proti severnemu vogalu, je naredil dvajset desk
26 ndiponso matsinde makumi anayi asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
in njihovih štirideset podstavkov iz srebra; dva podstavka pod eno desko in dva podstavka pod drugo desko.
27 Anapanganso maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo,
Za strani šotorskega svetišča proti zahodu je naredil šest desk.
28 ndiponso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
Dve deski je naredil za vogala šotorskega svetišča na dveh straneh.
29 Pa ngodya ziwirizi panali maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba atalumikizidwa pa ngowe imodzi. Maferemu onse anali ofanana.
Spojeni sta bili spodaj in skupaj spojeni pri njegovi glavi v en obroč. Tako je storil obema izmed njiju na obeh vogalih.
30 Choncho panali maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri anali pansi pa feremu iliyonse.
Bilo je osem desk in njihovih podstavkov je bilo šestnajst podstavkov iz srebra, pod vsako desko dva podstavka.
31 Iwo anapanganso mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha. Mitanda isanu inali ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
Naredil je zapahe iz akacijevega lesa; pet za deske ene strani šotorskega svetišča
32 mitanda isanu inanso inali ya maferemu a mbali inayo ndipo mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
in pet zapahov za deske druge strani šotorskega svetišča in pet zapahov za deske šotorskega svetišča proti zahodu.
33 Anapanga mtanda wapakati omwe umachokera pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
Naredil je srednji zapah, da je segal skozi deske od enega konca k drugemu.
34 Iwo anakuta maferemuwo ndi golide ndiponso anapanga mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso anayikuta ndi golide.
Deske je prevlekel z zlatom in njihove obroče naredil iz zlata, da bodo postavljeni za zapahe in zapahe je prevlekel z zlatom.
35 Anapanga nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo inali yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso anapetapo zithunzi za Akerubi.
Naredil je zagrinjalo iz modre, vijolične, škrlatne in sukane tančice. S kerubi spretne izdelave jih je naredil.
36 Iwo anapanga nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide. Anapanganso ngowe zagolide za nsanamirazo ndi matsinde asiliva anayi.
K temu je naredil štiri stebre iz akacijevega lesa in jih prevlekel z zlatom. Njihovi kavlji so bili iz zlata in zanje je ulil štiri podstavke iz srebra.
37 Anapanga nsalu ya pa chipata cholowera mu chihema, yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira yomwe inali yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
Naredil je tanko preprogo za vrata šotorskega svetišča iz modre, vijolične, škrlatne in sukane tančice, iz vezenine;
38 Anapanga nsanamira zisanu ndi ngowe zake. Anakuta pamwamba pa nsanamirazo ndi zomangira zake ndi golide, ndipo anapanganso matsinde asanu amkuwa.
in njenih pet stebrov z njihovimi kavlji. Njihove kapitele in njihove okrasne trakove je prevlekel z zlatom, toda njihovih pet podstavkov je bilo iz brona.

< Eksodo 36 >