< Eksodo 3 >

1 Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu.
Kwathi uMosi eselusa izimvu zikayisezala uJethro, umphristi waseMidiyani, waseqhuba izimvu zaya kude ohlangothini lwenkangala wasefika eHorebhi, intaba kaNkulunkulu.
2 Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka.
Lapho-ke ingilosi kaThixo yabonakala kuye iphakathi kwamalangabi omlilo esixukwini. UMosi wabona ukuthi loba isixuku sasibhebha kasizange sitshe.
3 Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”
Ngakho uMosi wacabanga esithi, “Ngizasondela ngiyebona isimanga lesi ukuba kungani isixuku singatshi silothe.”
4 Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!” Ndipo anayankha, “Wawa.”
Kwathi uThixo ebona ukuthi usesondele ukuba ayekhangela, uNkulunkulu wasememeza ngelizwi elaliphuma kulesosixuku wathi, “Mosi! Mosi!” UMosi wathi, “Ngilapha.”
5 Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.”
UNkulunkulu wathi, “Ungasondeli. Khupha amanyathela akho, ngoba indawo omi kuyo ingumhlabathi ongcwele.”
6 Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.
Wasesithi njalo, “NginguNkulunkulu kayihlo, uNkulunkulu ka-Abhrahama, uNkulunkulu ka-Isaka loNkulunkulu kaJakhobe.” Ngalokhu, uMosi wafihla ubuso bakhe ngoba wayesesaba ukukhangela uNkulunkulu.
7 Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo.
UThixo wasesithi, “Impela ngilubonile usizi lwabantu bami eGibhithe. Ngibazwile bekhala ngenxa yezinduna zezigqili ezibancindezelayo, njalo ngiyakhathazeka ngokuhlupheka kwabo.
8 Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
Ngakho ngehlile ukuzabakhulula ezandleni zamaGibhithe ngibakhuphe kulelolizwe ngibase elizweni elilendawo enengi, ilizwe eligeleza uchago loluju, endaweni yamaKhenani, amaHithi, ama-Amori, amaPherizi, amaHivi lamaJebusi.
9 Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira.
Ukukhala kwabako-Israyeli sekufikile kimi, njalo sengibonile lendlela amaGibhithe ababahlukuluza ngayo.
10 Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”
Ngakho suka uhambe. Ngikuthuma kuFaro ukuthi uyekhupha abantu bami abako-Israyeli elizweni laseGibhithe.”
11 Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”
Kodwa uMosi wathi kuNkulunkulu, “Kambe ngingubani ukuba ngiye kuFaro ukuyakhupha abako-Israyeli elizweni laseGibhithe na?”
12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”
UNkulunkulu wasesithi, “Ngizakuba lawe. Lesi sizakuba yisibonakaliso sokuthi yimi engikuthumileyo: Nxa usubakhuphile abantu eGibhithe, lizakhonza uNkulunkulu kuyonale intaba.”
13 Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”
UMosi wathi kuNkulunkulu, “Aluba ngifika kwabako-Israyeli ngithi kubo, ‘UNkulunkulu waboyihlo ungithumile kini,’ besebengibuza bathi, ‘Ungubani ibizo lakhe?’ Ngizakuthini kubo?”
14 Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’”
UNkulunkulu wathi kuMosi, “Nginguye Onguye. Lokhu yikho ozakutsho kwabako-Israyeli ukuthi, ‘Unguye ungithumile kini.’”
15 Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.
UNkulunkulu wabuye wathi kuMosi, “Tshono kwabako-Israyeli uthi, ‘uThixo, uNkulunkulu waboyihlo, uNkulunkulu ka-Abhrahama, uNkulunkulu ka-Isaka, loNkulunkulu kaJakhobe ungithumile kini.’ Leli libizo lami laphakade, ibizo engizakhunjulwa ngalo kusukela kusizukulwane kusiya kwesinye isizukulwane.
16 “Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani.
Hamba uyebuthanisa abadala bako-Israyeli uthi kubo, ‘uThixo, uNkulunkulu waboyihlo, uNkulunkulu ka-Abhrahama, ka-Isaka loJakhobe, ubonakele kimi wathi: Bengilikhangele njalo ngikubonile okwenziwe kini eGibhithe.
17 Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’
Futhi ngithembisile ukulikhupha osizini lwenu elikulo eGibhithe ngilise elizweni lamaKhenani, amaHithi, ama-Amori, amaPherizi, amaHivi lamaJebusi, ilizwe eligeleza uchago loluju.’
18 “Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’
Abadala bako-Israyeli bazakulalela. Kuzakuthi wena kanye labadala liye enkosini yaseGibhithe lithi kuyo, ‘uThixo, uNkulunkulu wamaHebheru uhlangane lathi. Sivumele sithathe uhambo lwezinsuku ezintathu siye enkangala ukuyanikela imihlatshelo kuThixo uNkulunkulu wethu.’
19 Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza.
Kodwa ngiyakwazi ukuthi inkosi yaseGibhithe ayiyikulivumela ukuthi lihambe ngaphandle kokuba incindezelwe yisandla esilamandla.
20 Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.
Ngakho ngizakwelula isandla sami ngiwatshaye amaGibhithe ngazozonke izimanga engizazenza phakathi kwawo. Ngemva kwalokho, izalivumela lihambe.
21 “Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu.
Njalo ngizakwenza amaGibhithe abe lomusa kulababantu, ukuze kuthi mhla lisuka lingahambi lingaphethe lutho.
22 Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”
Wonke owesifazane kacele kumakhelwane wakhe lakuye wonke owesifazane ohlala endlini yakhe izinto eziligugu ezenziwe ngesiliva legolide kanye lezigqoko ezizagqokwa ngamadodana lamadodakazi enu. Ngaleyondlela lizawemuka impahla amaGibhithe.”

< Eksodo 3 >