< Eksodo 20 >

1 Ndipo Mulungu anayankhula mawu onse awa nati:
UNkulunkulu wakhuluma amazwi wonke la wathi:
2 “Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo.
“NginguThixo uNkulunkulu wakho owakukhupha eGibhithe, elizweni lobugqili.
3 “Usakhale ndi milungu ina koma Ine ndekha.”
Ungabi labanye onkulunkulu ngaphandle kwami.
4 “Usadzipangire chofanizira chinthu chilichonse chakumwamba kapena cha pa dziko lapansi kapena cha mʼmadzi a pansi pa dziko.
Ungazenzeli isithombe ngesimo saloba yini esezulwini phezulu loba phansi emhlabeni kumbe ngaphansi kwamanzi.
5 Usazigwadire kapena kuzipembedza, pakuti Ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wansanje, wolanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo mpaka mʼbado wachitatu ndi wachinayi wa iwo amene amadana nane.
Ungazikhothameli loba ukuzikhonza; ngoba mina Thixo uNkulunkulu wakho nginguNkulunkulu olobukhwele, ojezisa abantwana ngenxa yezono zabazali babo kuze kube yisizukulwane sesithathu lesesine salabo abangizondayo,
6 Koma ndimaonetsa chikondi chosasinthika ku mibado miyandamiyanda ya anthu amene amandikonda, ndi kusunga malamulo anga.
kodwa ngitshengisela uthando kuzizukulwane eziyinkulungwane zalabo abangithandayo njalo begcina imilayo yami.
7 “Usagwiritse ntchito molakwika dzina la Yehova Mulungu wako, pakuti Yehova adzamutenga kukhala wochimwa aliyense amene akugwiritsa ntchito dzina lakelo molakwika.
Ungadlali ngebizo likaThixo uNkulunkulu wakho ngoba uThixo kayikumyekela olecala lokudlala ngebizo lakhe.
8 “Uzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika.
Khumbula usuku lweSabatha ngokulwenza lubengcwele.
9 Uzigwira ntchito zako zonse masiku asanu ndi limodzi.
Okwensuku eziyisithupha uzasebenza wenze yonke imisebenzi yakho,
10 Koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata, tsiku loperekedwa kwa Yehova Mulungu wako. Tsiku limeneli musagwire ntchito iliyonse, inuyo kapena mwana wanu wamwamuna kapena mwana wanu wamkazi, wantchito wanu wamwamuna kapena mdzakazi wanu, ziweto zanu kapena mlendo amene akukhala mʼmudzi mwanu.
kodwa usuku lwesikhombisa luyiSabatha kuThixo uNkulunkulu wakho. Ngalo awuyikwenza loba yiwuphi umsebenzi, wena, loba indodana yakho, loba indodakazi yakho, loba inceku kumbe incekukazi yakho, loba izifuyo zakho loba isihambi esikwethekeleleyo emzini wakho.
11 Pakuti Yehova anapanga kumwamba ndi dziko lapansi, nyanja ndi zonse zimene zili mʼmenemo mʼmasiku asanu ndi limodzi. Iye anapuma pa tsiku lachisanu ndi chiwiri. Kotero Yehova anadalitsa tsiku la Sabata kuti likhale loyera.
Ngoba ngensuku eziyisithupha uThixo wenza amazulu lomhlaba, ulwandle lakho konke okukukho, kodwa waphumula ngosuku lwesikhombisa. Ngakho-ke walubusisa usuku lweSabatha walwenza lwaba ngcwele.
12 “Lemekeza abambo ako ndi amayi ako kuti ukhale ndi moyo wautali mʼdziko limene Yehova Mulungu wako akukupatsa.
Hlonipha uyihlo lonyoko ukuze impilo yakho ibende elizweni akunika lona uThixo uNkulunkulu wakho.
13 “Usaphe.
Ungabulali.
14 “Usachite chigololo.
Ungafebi.
15 “Usabe.
Ungantshontshi.
16 “Usapereke umboni womunamizira mnzako.
Ungafakazi amanga ngomakhelwane wakho.
17 “Usasirire nyumba ya mnzako. Usasirire mkazi wa mnzako kapena wantchito wake wamwamuna kapena mdzakazi wake, ngʼombe yake kapena bulu wake, kapena chilichonse cha mnzako.”
Ungahawukeli indlu kamakhelwane wakho. Ungahawukeli umfazi kamakhelwane wakho, loba inceku kumbe incekukazi yakhe, inkabi yakhe loba ubabhemi wakhe loba yini ekamakhelwane wakho.”
18 Pamene anthu ankamva mabingu ndi kuona ziphaliwali ndi kumvanso lipenga ndi kuona utsi umene umafuka mʼphiri, ananjenjemera ndi mantha. Ndipo iwo anayima patali.
Kwathi abantu besizwa umdumo bebona lombane, besizwa icilongo njalo bebona intaba ithunqa intuthu, bathuthumela ngokwesaba. Bema khatshana,
19 Ndipo anati kwa Mose, “Iwe utiyankhule ndipo tidzamvera. Koma usalole kuti Mulungu atiyankhule, tingafe.”
bathi kuMosi, “Khuluma kithi wena sizakulalela. Kodwa uNkulunkulu kangakhulumi kithi yena ngokwakhe ngoba singafa.”
20 Koma Mose anati kwa anthuwo, “Musachite mantha. Mulungu wabwera kudzakuyesani kuti mukhale ndi mtima woopa Mulungu kuti musamuchimwire.”
UMosi wathi, “Lingesabi, uNkulunkulu uzelihlola ukuze limesabe lokuze lingoni.”
21 Anthu aja anayima patali koma Mose anayandikira mtambo wakuda kumene kunali Mulungu.
Abantu basala belokhu bemi bucwadlanyana, uMosi wangena phakathi komnyama waya lapho okwakuloNkulunkulu khona.
22 Ndipo Yehova anati kwa Mose, “Awuze izi Aisraeli: ‘Inu mwaona nokha kuti Ine ndakuyankhulani kuchokera kumwamba.
UThixo wathi kuMosi, “Tshela abantu bako-Israyeli uthi, ‘Lizibonele lina ngokwenu ukuthi ngikhulume lani ngisezulwini.
23 Choncho musadzipangire milungu yasiliva kapena yagolide kuti muziyipembedza pamodzi ndi Ine.’”
Lingenzi onkulunkulu ukuba babekhona kanye lami; lingazenzeli onkulunkulu besiliva kumbe onkulunkulu begolide.
24 Mundimangire guwa ladothi ndipo muziperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe zanu. Pamalo paliponse pamene Ine ndidzakonza kuti muzinditamandirapo, ndidzabwera ndi kukudalitsani.
Ngakhelani i-alithari ngomhlabathi lenzele kulo umhlatshelo womnikelo wokutshiswa, leminikelo yobudlelwano, izimvu lembuzi kanye lenkomo zenu. Loba kungaphi lapho engizakwenza ibizo lami lihlonitshwe khona, ngizakuza kini ngilibusise.
25 Ngati mudzandimangira guwa lansembe lamiyala, musagwiritse ntchito miyala yosema, pakuti mudzalidetsa mukadzagwiritsa ntchito zida.
Nxa lingakhela i-alithari ngamatshe, lingaze lawabaza lawomatshe ngoba lizalingcolisa nxa lingasebenzisa okokubaza kulo.
26 Musamakwere pa makwerero popita pa guwa langa lansembe kuti mungaonetse maliseche anu.
Lingaze laya e-alithareni lami ngezikhwelo funa ubunqunu benu bembulwe khona lapho.’”

< Eksodo 20 >