< Deuteronomo 29 >
1 Awa ndiwo mawu a mʼpangano limene Yehova analamula Mose kuti achite ndi Aisraeli ku Mowabu, powonjezera pa pangano limene anapangana nawo ku Horebu.
Telles sont les paroles de l'alliance que Yahvé ordonna à Moïse de conclure avec les enfants d'Israël au pays de Moab, en complément de l'alliance qu'il avait conclue avec eux à Horeb.
2 Mose anayitanitsa Aisraeli onse nati kwa iwo: Inu munaona zonse zimene Yehova anachita kwa Farao, nduna zake ndi dziko lake lonse ku Igupto.
Moïse appela tout Israël, et leur dit: Vos yeux ont vu tout ce que Yahvé a fait au pays d'Égypte à Pharaon, à tous ses serviteurs et à tout son pays,
3 Ndi maso anu munaona mayesero onse aja, zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zazikulu zija.
les grandes épreuves que vos yeux ont vues, les signes et ces grands prodiges.
4 Koma mpaka lero Yehova sanakupatseni mtima wozindikira kapena maso openya kapena makutu akumva.
Mais Yahvé ne vous a pas donné, jusqu'à ce jour, un cœur pour connaître, des yeux pour voir et des oreilles pour entendre.
5 Mʼzaka makumi anayi zimene ndinakutsogolerani mʼchipululu, zovala zanu ndiponso nsapato za ku mapazi anu sizinangʼambike.
Je vous ai conduits pendant quarante ans dans le désert. Vos vêtements n'ont pas vieilli sur vous, et vos sandales n'ont pas vieilli à vos pieds.
6 Inu simunadye buledi ndi kumwa vinyo kapena chakumwa chilichonse choledzeretsa. Ndinachita izi kuti mudziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
Vous n'avez pas mangé de pain, et vous n'avez pas bu de vin ni de boisson forte, afin que vous sachiez que je suis Yahvé votre Dieu.
7 Pamene munafika malo ano, Sihoni mfumu ya ku Hesiboni ndi Ogi mfumu ya ku Basani anabwera kudzamenyana nafe koma tinawagonjetsa iwo.
Lorsque vous êtes arrivés dans ce lieu, Sihon, roi de Hesbon, et Og, roi de Basan, sont sortis contre nous pour nous combattre, et nous les avons battus.
8 Tinatenga dziko lawo ndi kulipereka ngati cholowa cha fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase.
Nous avons pris leur pays et l'avons donné en héritage aux Rubénites, aux Gadites et à la demi-tribu des Manassites.
9 Tsatirani mosamalitsa mawu a mʼpangano ili kuti zinthu zizikuyenderani bwino pa zochitika zanu zonse.
Gardez donc les paroles de cette alliance et mettez-les en pratique, afin de prospérer dans tout ce que vous ferez.
10 Lero lino nonse mukuyima pamaso pa Yehova Mulungu wanu, atsogoleri a mafuko anu, akuluakulu ndi nduna zanu, ndi amuna ena onse a mu Israeli,
Vous vous tenez tous aujourd'hui devant l'Éternel, votre Dieu: vos chefs, vos tribus, vos anciens et vos officiers, tous les hommes d'Israël,
11 pamodzi ndi ana ndi akazi anu, kudzanso alendo amene akukhala pakati panu omwe amakuwazirani nkhuni ndi kukutungirani madzi.
vos petits enfants, vos femmes, et les étrangers qui sont au milieu de vos camps, depuis celui qui coupe votre bois jusqu'à celui qui tire votre eau,
12 Mukuyimirira pano kuti mulowe mʼpangano ndi Yehova Mulungu wanu, pangano limene Yehova akuchita ndi inu lero ndi kulisindikiza ndi malumbiro,
afin que vous entriez dans l'alliance de l'Éternel, votre Dieu, et dans le serment qu'il vous fait aujourd'hui,
13 kukukhazikitsani lero lino ngati anthu ake, ndi kuti Iye akhale Mulungu wanu monga anakulonjezani inu ndiponso monga analumbira kwa makolo anu Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
afin qu'il vous établisse aujourd'hui comme son peuple et qu'il soit votre Dieu, comme il vous l'a dit et comme il l'a juré à vos pères, Abraham, Isaac et Jacob.
14 Ndikupanga pangano ili ndi malumbiro ake osati kwa inu nokha,
Ce n'est pas seulement avec vous que je fais cette alliance et ce serment,
15 amene muli pano pamaso pa Yehova Mulungu wathu, koma ndi iwonso amene sali pano lero.
mais avec ceux qui se tiennent aujourd'hui avec nous devant Yahvé notre Dieu, et aussi avec ceux qui ne sont pas aujourd'hui avec nous
16 Inu nomwe mukudziwa mmene tinkakhalira ku Igupto ndi mmene tinadutsira mayiko pa ulendo wobwera kuno.
(car vous savez comment nous avons vécu dans le pays d'Égypte, et comment nous sommes passés au milieu des nations par lesquelles vous avez passé;
17 Ife tinaona pakati pawo mafanizo ndi mafano awo onyansa, amtengo ndi amiyala, asiliva ndi agolide.
et vous avez vu leurs abominations et leurs idoles de bois, de pierre, d'argent et d'or, qui étaient parmi elles);
18 Onetsetsani kuti pasapezeke mwamuna kapena mkazi, banja kapena fuko pakati panu lero amene mtima wawo udzapandukira Yehova Mulungu wanu ndi kupita kukapembedza milungu ya mitundu iyo. Onetsetsani kuti pasapezeke muzu pakati panu wotulutsa mankhwala akupha otere.
de peur qu'il n'y ait parmi vous un homme, une femme, une famille ou une tribu dont le cœur se détourne aujourd'hui de l'Éternel, notre Dieu, pour aller servir les dieux de ces nations, de peur qu'il n'y ait parmi vous une racine qui produise un poison amer,
19 Munthu wotere akamva mawu a lumbiro ili, asadzidalitse yekha mʼmaganizo mwake namati, “Ine ndidzapulumuka ngakhale nditapitiriza kuyenda njira yanga.” Zoterezi zidzadzetsa masautso pa nthaka ya chinyontho ndi yowuma yomwe.
et qu'en entendant les paroles de cette malédiction, il ne se bénisse dans son cœur, en disant: « J'aurai la paix, quoique je marche dans l'obstination de mon cœur », pour détruire l'humide par le sec.
20 Yehova sadzamukhululukira. Mkwiyo ndi nsanje ya Yehova zidzamuyakira munthuyo. Matemberero onse wolembedwa mʼbukuli adzamugwera iye ndipo Yehova adzafafaniza dzina lake pa dziko lapansi.
L'Éternel ne lui pardonnera pas, mais alors la colère et la jalousie de l'Éternel fumeront contre cet homme, et toute la malédiction écrite dans ce livre tombera sur lui, et l'Éternel effacera son nom de dessous le ciel.
21 Yehova adzasankha pakati pa Aisraeli anthu oyenera masautso monga mwa matemberero onse a mʼpangano olembedwa Mʼbuku la Malamulo.
Yahvé le mettra à part pour le mal, parmi toutes les tribus d'Israël, selon toutes les malédictions de l'alliance écrites dans ce livre de la loi.
22 Ana anu a mibado yakutsogolo ndi alendo amene adzachokera kutali adzaona matsoka amene adzakugwerani mʼdziko muno ndiponso matenda amene Yehova adzabweretsa pa dzikoli.
La génération à venir - tes enfants qui se lèveront après toi, et l'étranger qui viendra d'un pays lointain - dira, quand elle verra les plaies de ce pays, et les maladies dont Yahvé l'a rendu malade,
23 Dziko lonse lidzasanduka nthaka ya mchere ndi ya sulufule. Simudzadzalamo kanthu, simudzakhala chomera chilichonse, ndi mbewu yomera mʼmenemo. Dziko lanu lidzakhala lowonongeka ngati Sodomu ndi Gomora, Adima ndi Zeboimu, mizinda imene Yehova anayiwononga ndi mkwiyo wake waukulu.
que toute sa terre n'est que soufre, sel et brûlure, qu'elle ne se sème pas, ne produit pas, et qu'il n'y pousse pas d'herbe, comme Sodome, Gomorrhe, Adma et Tseboïm, que Yahvé a détruites dans sa colère et dans sa fureur.
24 Mitundu yonse ya anthu idzafunsa kuti, “Kodi chifukwa chiyani Yehova anachita zotere mʼdziko lake? Kodi chifukwa chiyani anaonetsa mkwiyo woopsa wotere?”
Toutes les nations diront: « Pourquoi Yahvé a-t-il fait cela à ce pays? Que signifie l'ardeur de cette grande colère? »
25 Ndipo yankho la mafunso amenewa lidzakhala lakuti, “Chifukwa chakuti anthu awa aphwanya pangano la Yehova Mulungu wa makolo awo, pangano limene Iye anapangana nawo pamene anawatulutsa ku Igupto.
Alors on dira: « Parce qu'ils ont abandonné l'alliance de Yahvé, le Dieu de leurs pères, qu'il avait conclue avec eux en les faisant sortir du pays d'Égypte,
26 Iwo anachoka ndi kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, milungu imene sanayidziwe, milungu imene sanawapatse.
ils sont allés servir d'autres dieux et se prosterner devant eux, des dieux qu'ils ne connaissaient pas et qu'il ne leur avait pas donnés.
27 Choncho Yehova anakwiyira dziko lino, kotero anabweretsa matemberero onse amene analembedwa mʼbuku lino.
Aussi la colère de Yahvé s'enflamma-t-elle contre ce pays, pour faire venir sur lui toutes les malédictions qui sont écrites dans ce livre.
28 Ndi mkwiyo komanso ukali wake woopsa Yehova anawazula mʼdziko lawo ndi kuwaponyera mʼdziko lina, monga mmene zilili lero lino.”
Yahvé les a déracinés de leur pays avec colère, avec fureur et avec une grande indignation, et il les a poussés dans un autre pays, comme c'est le cas aujourd'hui. »
29 Zinsinsi ndi za Yehova Mulungu wathu koma zinthu zimene zaululidwa ndi zathu ndi ana athu kwamuyaya, kuti titsatire mawu onse a mʼmalamulowa.
Les choses secrètes appartiennent à Yahvé notre Dieu; mais les choses révélées nous appartiennent, à nous et à nos enfants, pour toujours, afin que nous mettions en pratique toutes les paroles de cette loi.