< Deuteronomo 28 >
1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
Si tu écoutes attentivement la voix de l'Éternel, ton Dieu, et si tu observes et mets en pratique tous ses commandements que je te prescris aujourd'hui, l'Éternel, ton Dieu, te placera au-dessus de toutes les nations de la terre.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
Toutes ces bénédictions viendront sur toi et t'envahiront, si tu écoutes la voix de l'Éternel, ton Dieu.
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
Tu seras béni dans la ville, et tu seras béni dans les champs.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
Tu seras béni par le fruit de ton corps, par le fruit de ton sol, par le fruit de tes animaux, par le produit de ton bétail et par les jeunes de ton troupeau.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Ta corbeille et ton pétrin seront bénis.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Tu seras béni quand tu entreras et tu seras béni quand tu sortiras.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
L'Éternel fera frapper devant toi tes ennemis qui s'élèvent contre toi. Ils sortiront contre toi par un chemin, et ils fuiront devant toi par sept chemins.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
L'Éternel ordonnera que tu sois béni dans tes greniers et dans tout ce que tu entreprendras. Il te bénira dans le pays que Yahvé, ton Dieu, te donne.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
L'Éternel t'établira comme un peuple saint pour lui, comme il te l'a juré, si tu gardes les commandements de l'Éternel, ton Dieu, et si tu marches dans ses voies.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
Tous les peuples de la terre verront que tu es appelé par le nom de l'Éternel, et ils auront peur de toi.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Yahvé t'accordera une abondante prospérité dans le fruit de ton corps, dans le fruit de ton bétail et dans le fruit de ton sol, dans le pays que Yahvé a juré à tes pères de te donner.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
Yahvé t'ouvrira son bon trésor dans le ciel, pour donner à ton pays la pluie en sa saison, et pour bénir tout le travail de ta main. Tu prêteras à beaucoup de nations, et tu n'emprunteras pas.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
Yahvé fera de toi la tête, et non la queue. Tu seras seulement en haut et tu ne seras pas en bas, si tu écoutes les commandements de l'Éternel, ton Dieu, que je te prescris aujourd'hui, si tu les observes et les mets en pratique,
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
et si tu ne te détournes d'aucune des paroles que je te prescris aujourd'hui, à droite ou à gauche, pour aller après d'autres dieux et les servir.
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
Mais si tu n'écoutes pas la voix de Yahvé ton Dieu, si tu n'observes pas et ne mets pas en pratique tous ses commandements et ses lois que je te prescris aujourd'hui, toutes ces malédictions viendront sur toi et t'atteindront.
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
Tu seras maudit dans la ville, et tu seras maudit dans les champs.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Ton panier et ton pétrin seront maudits.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
Le fruit de ton corps, le fruit de ton sol, le produit de ton élevage et les jeunes de ton troupeau seront maudits.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
Tu seras maudit quand tu entreras, et tu seras maudit quand tu sortiras.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
L'Éternel enverra sur toi la malédiction, la confusion et le châtiment dans tout ce que tu entreprendras, jusqu'à ce que tu sois détruit et que tu périsses rapidement, à cause de la méchanceté de tes actions, par lesquelles tu m'as abandonné.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
L'Éternel fera en sorte que la peste s'attache à vous, jusqu'à ce qu'elle vous consume du pays dont vous entrez en possession.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
L'Éternel vous frappera par la consomption, par la fièvre, par l'inflammation, par la chaleur ardente, par l'épée, par le fléau et par la moisissure. Ils te poursuivront jusqu'à ce que tu périsses.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Le ciel qui est au-dessus de ta tête sera d'airain, et la terre qui est sous toi sera de fer.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
L'Éternel rendra la pluie de ton pays poudreuse et poussiéreuse. Elle tombera sur toi du haut du ciel, jusqu'à ce que tu sois détruit.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
L'Éternel te fera frapper devant tes ennemis. Tu sortiras d'un côté contre eux, et tu fuiras de sept côtés devant eux. Tu seras ballotté de droite à gauche parmi tous les royaumes de la terre.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Vos cadavres serviront de nourriture à tous les oiseaux du ciel et aux animaux de la terre, et il n'y aura personne pour les effrayer.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
L'Éternel vous frappera de l'ulcère d'Égypte, de la tumeur, du scorbut et de la démangeaison, dont vous ne pourrez pas guérir.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
Yahvé te frappera de folie, d'aveuglement et de stupeur.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
Tu tâtonneras en plein midi, comme l'aveugle tâtonne dans les ténèbres, et tu ne prospéreras pas dans tes voies. Tu seras toujours opprimé et dépouillé, et il n'y aura personne pour te sauver.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
Tu fianceras une femme, et un autre homme couchera avec elle. Tu construiras une maison, et tu ne l'habiteras pas. Tu planteras une vigne, et tu n'en utiliseras pas le fruit.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Ton bœuf sera égorgé sous tes yeux, et tu n'en mangeras pas. Ton âne sera violemment enlevé sous tes yeux, et on ne te le rendra pas. Tes brebis seront données à tes ennemis, et tu n'auras personne pour te sauver.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Tes fils et tes filles seront donnés à un autre peuple. Tes yeux les regarderont et se languiront d'eux tout le jour. Il n'y aura pas de force dans ta main.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
Une nation que tu ne connais pas mangera le fruit de ton sol et de tout ton travail. Tu ne seras qu'opprimé et écrasé en permanence,
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
si bien que les spectacles que tu verras de tes yeux te rendront fou.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
Yahvé te frappera aux genoux et aux jambes d'un ulcère dont tu ne pourras pas guérir, depuis la plante de ton pied jusqu'au sommet de ta tête.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
L'Éternel vous conduira, vous et le roi que vous établirez sur vous, dans une nation que vous n'avez pas connue, ni vous ni vos pères. Là, vous servirez d'autres dieux de bois et de pierre.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
Vous deviendrez un objet d'étonnement, un proverbe et une rengaine parmi tous les peuples où Yahvé vous conduira.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
Tu porteras beaucoup de semences dans les champs, et tu en recueilleras peu, car les sauterelles les dévoreront.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
Tu planteras des vignes et tu les cultiveras, mais tu ne boiras pas le vin et tu ne feras pas la récolte, car les vers les mangeront.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
Tu auras des oliviers dans tout ton territoire, mais tu ne t'oindras pas d'huile, car tes olives tomberont.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
Tu engendreras des fils et des filles, mais ils ne seront pas à toi, car ils iront en captivité.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Les sauterelles dévoreront tous tes arbres et le fruit de ton sol.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
L'étranger qui est au milieu de toi montera au-dessus de toi de plus en plus haut, et tu descendras de plus en plus bas.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
Il te prêtera, et tu ne lui prêteras pas. Il sera la tête, et vous serez la queue.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
Toutes ces malédictions viendront sur toi, te poursuivront et t'atteindront, jusqu'à ce que tu sois détruit, parce que tu n'as pas écouté la voix de l'Éternel, ton Dieu, pour garder ses commandements et ses lois qu'il t'a prescrits.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
Ils seront un signe et un prodige pour toi et pour ta descendance à jamais.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Parce que tu n'as pas servi Yahvé ton Dieu dans la joie et l'allégresse du cœur, à cause de l'abondance de toutes choses,
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
tu serviras tes ennemis que Yahvé envoie contre toi, dans la faim, dans la soif, dans la nudité et dans le manque de toutes choses. Il mettra sur ton cou un joug de fer, jusqu'à ce qu'il t'ait détruit.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
Yahvé fera venir contre toi une nation lointaine, de l'extrémité de la terre, au vol de l'aigle, une nation dont tu ne comprendras pas la langue,
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
une nation au visage farouche, qui ne respecte pas les vieillards et ne fait pas grâce aux jeunes.
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
Ils mangeront le fruit de ton bétail et le fruit de ton sol, jusqu'à ce que tu sois détruit. Ils ne te laisseront pas non plus le blé, le vin nouveau, l'huile, les produits de ton bétail et les jeunes de ton troupeau, jusqu'à ce qu'ils t'aient fait périr.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
Ils t'assiégeront dans toutes tes portes, jusqu'à ce que tes hautes et fortes murailles dans lesquelles tu te réfugiais s'écroulent dans tout ton pays. Ils t'assiégeront dans toutes tes portes, dans tout le pays que Yahvé, ton Dieu, t'a donné.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
Tu mangeras le fruit de ton propre corps, la chair de tes fils et de tes filles, que l'Éternel, ton Dieu, t'a donnés, dans le siège et dans la détresse où te plongeront tes ennemis.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
L'homme tendre et délicat parmi vous, son œil sera mauvais envers son frère, envers la femme qu'il aime, et envers le reste de ses enfants qui lui reste,
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
de sorte qu'il ne donnera à aucun d'eux de la chair de ses enfants qu'il mangera, parce qu'il ne lui reste rien, dans le siège et dans la détresse par lesquels votre ennemi vous accablera dans toutes vos portes.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
La femme d'entre vous, tendre et délicate, qui ne se risquerait pas à poser la plante de son pied sur le sol par délicatesse et tendresse, son œil sera mauvais envers le mari qu'elle aime, envers son fils, envers sa fille,
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
envers son petit qui sort d'entre ses pieds, et envers les enfants qu'elle porte, car elle les mangera en cachette, faute de tout, dans le siège et dans la détresse par lesquels votre ennemi vous affligera dans vos portes.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
Si tu n'observes pas et ne mets pas en pratique toutes les paroles de cette loi qui sont écrites dans ce livre, afin de craindre ce nom glorieux et redoutable, YAHVÉ ton Dieu,
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
alors Yahvé rendra redoutables tes fléaux et les fléaux de ta progéniture, même de grands fléaux, et de longue durée, et de graves maladies, et de longue durée.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
Il fera revenir sur toi toutes les maladies d'Égypte dont tu avais peur, et elles s'attacheront à toi.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
De même, toutes les maladies et tous les fléaux qui ne sont pas écrits dans le livre de cette loi, Yahvé les fera venir sur vous jusqu'à ce que vous soyez détruits.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
Vous resterez en petit nombre, alors que vous étiez comme les étoiles du ciel pour la multitude, parce que vous n'avez pas écouté la voix de Yahvé votre Dieu.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Il arrivera que, comme Yahvé s'est réjoui à votre sujet de vous faire du bien et de vous multiplier, ainsi Yahvé se réjouira à votre sujet de vous faire périr et de vous détruire. Vous serez arrachés du pays dont vous allez prendre possession.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
Yahvé vous dispersera parmi tous les peuples, d'un bout à l'autre de la terre. Là, vous servirez d'autres dieux que vous n'avez pas connus, ni vous ni vos pères, du bois et de la pierre.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
Chez ces nations, tu ne trouveras pas de repos, et la plante de ton pied ne reposera pas, mais l'Éternel te donnera un cœur tremblant, des yeux défaillants et une âme languissante.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Ta vie sera en suspens devant toi. Tu auras peur nuit et jour, et tu n'auras aucune assurance pour ta vie.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
Le matin, tu diras: « Je voudrais que ce soit le soir », et le soir, tu diras: « Je voudrais que ce soit le matin », à cause de la peur de ton cœur que tu craindras, et à cause des regards que tes yeux verront.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
Yahvé vous ramènera en Égypte avec des navires, par le chemin duquel je vous ai dit que vous ne la reverriez jamais. Là, vous vous offrirez à vos ennemis comme esclaves mâles et femelles, et personne ne vous achètera.