< Deuteronomo 28 >

1 Ngati mumvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsatira mosamalitsa malamulo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, Yehova Mulungu wanu adzakukwezani pamwamba pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.
It shall happen, if you shall sh'ma ·hear obey· sh'ma ·hear obey· Adonai your God’s voice, to observe to do all his mitzvot ·instructions· which I enjoin you today, that Adonai your God will set you high above all the nations of the earth.
2 Madalitso awa adzabwera kwa inu ndi kuyenda nanu ngati mumvera Yehova Mulungu wanu:
All these blessings will come upon you, and overtake you, if you sh'ma ·hear obey· Adonai your God’s voice.
3 Mudzadalitsika mʼmizinda yanu ndi kudalitsika mʼdzikolo.
You shall be blessed in the city, and you shall be blessed in the field.
4 Yehova adzadalitsa ana anu, zokolola za mʼdziko lanu, ngʼombe zanu pamodzi ndi ziweto zanu zonse.
You shall be blessed in the fruit of your body, the fruit of your ground, the fruit of your animals, the increase of your livestock, and the young of your flock.
5 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzadalitsika.
Your basket and your kneading trough shall be blessed.
6 Mudzadalitsika pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
You shall be blessed when you come in, and you shall be blessed when you go out.
7 Yehova adzaonetsetsa kuti adani anu amene adzakuwukirani agonjetsedwe pamaso panu. Iwo adzabwera kwa inu kuchokera mbali imodzi koma adzakuthawani ku mbali zisanu ndi ziwiri.
Adonai will cause your enemies who rise up against you to be struck before you. They will come out against you one way, and will flee before you seven ways.
8 Yehova adzatumiza madalitso pa nkhokwe zanu ndi pa chilichonse chimene muchikhudza. Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani mʼdziko limene akukupatsani.
Adonai will enjoin the blessing on you in your barns, and in all that you put your hand to. He will bless you in the land which Adonai your God gives you.
9 Yehova Mulungu wanu adzachititsa kuti mukhale anthu ake opatulika, monga momwe analonjezera pa malumbiro ake, ngati musunga malamulo ake ndi kuyenda mʼnjira zake.
Adonai will establish you for a holy people to himself, as he has sworn to you, if you shall keep the mitzvot ·instructions· of Adonai your God, and walk in his ways.
10 Pamenepo anthu onse a dziko lapansi adzaona kuti mumadziwika ndi dzina la Yehova ndipo adzakuopani.
All the peoples of the earth shall see that you are called by Adonai’s name, and they will be afraid of you.
11 Yehova adzakupambanitsani kwambiri ndipo adzakupatsani ana ambiri, ziweto zambiri, ndi zokolola zochuluka, mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzakupatsani.
Adonai will grant you abundant prosperity, in the fruit of your body, in the fruit of your livestock, and in the fruit of your ground, in the land which Adonai swore to your fathers to give you.
12 Yehova adzatsekula kumwamba kumene amasungirako chuma chake, kutumiza mvula mʼdziko lanu pa nthawi yake ndi kudalitsa ntchito yonse ya manja anu. Mudzakongoza mitundu yambiri koma inu simudzakongola kwa aliyense.
Adonai will open to you his good treasure in the sky, to give the rain of your land in its season, and to bless all the work of your hand. You will lend to many nations, and you will not borrow.
13 Yehova adzakuthandizani kukhala mutu osati mchira. Mukakhala ndi chidwi ndi malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero lino ndi kuwatsata mosamalitsa, inu mudzakhala apamwamba nthawi zonse osati apansi.
Adonai will make you the head, and not the tail. You will be above only, and you will not be beneath; if you sh'ma ·hear obey· the mitzvot ·instructions· of Adonai your God, which I enjoin you today, to observe and to do,
14 Musapatukire ku dzanja lamanja kapena lamanzere pa lamulo lina lililonse limene ndikukupatsani lero lino ndi kumatsatira kapena kuyitumikira milungu ina.
and shall not turn aside from any of the words which I enjoin you today, to the right hand, or to the left, to go after other deities to abad ·serve· them.
15 Koma ngati simumvera Yehova Mulungu wanu ndi kusatsata mosamalitsa malamulo ake ndi malangizo ake onse amene ndikukupatsani lero lino, matemberero awa adzabwera pa inu ndikukugonjetsani:
But it shall come to pass, if you will not sh'ma ·hear obey· Adonai your God’s voice, to observe to do all his mitzvot ·instructions· and his statutes which I enjoin you today, that all these curses will come on you, and overtake you.
16 Mudzatembereredwa mu mzinda ndi kutembereredwa mʼmudzi.
You will be cursed in the city, and you will be cursed in the field.
17 Dengu lanu ndi chiwaya chanu cha buledi zidzatembereredwa.
Your basket and your kneading trough will be cursed.
18 Zipatso za mʼmimba mwanu zidzatembereredwa, ndiponso zomera za mʼdziko lanu, ana angʼombe zanu ndi ana ankhosa zanu zidzatembereredwa.
The fruit of your body, the fruit of your ground, the increase of your livestock, and the young of your flock will be cursed.
19 Mudzatembereredwa pa kulowa kwanu ndi pa kutuluka kwanu.
You will be cursed when you come in, and you will be cursed when you go out.
20 Yehova adzakutumizirani matemberero, chisokonezo ndi minyozo pa chilichonse chimene mudzachichita mpaka mudzawonongedwa ndi kukhala bwinja mofulumira chifukwa cha zoyipa zimene mwazichita pa kumutaya Yehova.
Adonai will send on you cursing, confusion, and rebuke, in all that you put your hand to do, until you are destroyed, and until you perish quickly; because of the evil of your doings, by which you have forsaken me.
21 Yehova adzakugwetserani mliri wa matenda mpaka atakuwonongani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
Adonai will make the pestilence cling to you, until he has consumed you from off the land, where you go in to possess it.
22 Yehova adzakukanthani ndi nthenda yowondetsa, ya malungo ndi ya zotupatupa, ndi kutentha kwakukulu ndi chilala, ndi chinsikwi ndi chiwawu zimene zidzakusautsani mpaka mutawonongeka.
Adonai will strike you with consumption, with fever, with inflammation, with fiery heat, with the sword, with blight, and with tzara'at mildew. They will pursue you until you perish.
23 Mitambo ya pamutu panu idzawuma ngati mkuwa ndipo sidzagwetsa mvula mpaka nthaka yanu idzawuma gwaa ngati chitsulo.
Your sky that is over your head will be bronze, and the earth that is under you will be iron.
24 Mʼmalo mwa mvula Yehova adzakupatsani fumbi ndi dothi ndipo lidzakugwerani kuchokera kumwamba mpaka mutawonongeka.
Adonai will make the rain of your land powder and dust. It will come down on you from the sky, until you are destroyed.
25 Yehova adzalola kuti adani anu akugonjetseni. Mudzadzera njira imodzi pokalimbana ndi adani anu koma pothawa mudzabalalika mbali zisanu ndi ziwiri. Mudzakhala chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Adonai will cause you to be struck before your enemies. You will go out one way against them, and will flee seven ways before them. You will be tossed back and forth among all the kingdoms of the earth.
26 Mitembo yanu idzadyedwa ndi mbalame zamumlengalenga ndi nyama zakutchire, ndipo palibe amene adzaziyingitse.
Your dead body will be food to all birds of the sky, and to the animals of the earth; and there will be no one to frighten them away.
27 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa za ku Igupto ndi zotupatupa, zipere, ndi mphere zimene simudzachiritsika nazo.
Adonai will strike you with the boils of Egypt [Abode of slavery], with the tumors, with the scurvy, and with the itch, of which you cannot be healed.
28 Yehova adzakusautsani inu ndi misala, khungu ndi chisokonekero cha maganizo.
Adonai will strike you with madness, with blindness, and with astonishment of heart.
29 Masanasana mudzayenda ngati muli mu mdima, kumafufuzira njira ngati wosaona. Mudzakhala olephera pa chilichonse mungachite. Tsiku ndi tsiku mudzaponderezedwa ndi kuberedwa wopanda wokupulumutsani.
You will grope at noonday, as the blind gropes in darkness, and you shall not prosper in your ways. You will only be oppressed and robbed always, and there will be no one to save you.
30 Mudzachita chinkhoswe ndi mkazi, koma wina adzakulandani ndi kumukwatira. Mudzamanga nyumba koma simudzagonamo. Mudzalima munda wamphesa koma simudzadyako zipatso zake.
You will betroth a wife, and another man shall lie with her. You will build a house, and you won’t dwell in it. You will plant a vineyard, and not use its fruit.
31 Ngʼombe yanu yamtheno idzaphedwa inu muli pomwepo koma simudzadyako. Bulu wanu adzalandidwa kwa inu mwamakani osabwera nayenso. Nkhosa zanu zidzapatsidwa kwa adani anu, ndipo palibe amene adzazipulumutsa.
Your ox will be slain before your eyes, and you will not eat any of it. Your donkey will be violently taken away from before your face, and will not be restored to you. Your sheep will be given to your enemies, and you will have no one to save you.
32 Ana anu aamuna ndi aakazi adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina ndipo inu mudzafika potopa ndi kulefuka nʼkudikirira tsiku ndi tsiku kuti mwina anawo abwerako.
Your sons and your daughters will be given to another people. Your eyes will look, and fail with longing for them all day long. There will be no power in your hand.
33 Anthu amene simukuwadziwa adzakudyerani zokolola zanu, ndipo mudzakhala mukuponderezedwa mwankhanza masiku onse.
A nation which you don’t know eat the fruit of your ground and all of your work. You will only be oppressed and crushed always;
34 Zimene muzidzaziona zidzakusokonezani mitu.
so that the sights that you see with your eyes will drive you mad.
35 Yehova adzakusautsani ndi zithupsa zaululu ndi zosachiritsika za mʼmawondo ndi mʼmiyendo ndipo zidzafalikira kuchoka kuphazi mpaka kumutu.
Adonai will strike you in the knees and in the legs with a sore boil, of which you cannot be healed, from the sole of your foot to the crown of your head.
36 Yehova adzakuthamangitsirani, inu ndi mafumu anu amene muwayika, ku dziko losadziwika kwa inu ndi kwa makolo anu. Kumeneko mudzakapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi miyala.
Adonai will bring you, and your king whom you will set over yourselves, to a nation that you have not known, you nor your fathers. There you will abad ·serve· other deities of wood and stone.
37 Inu mudzakhala chinthu chochititsa mantha kuchisunga ndiponso chinthu chotukwanidwa ndi chonyozeka kwa anthu a mitundu yonse kumene Yehova adzakuthamangitsirani.
You will become an astonishment, a proverb, and a byword among all the peoples where Adonai will lead you away.
38 Mudzadzala mbewu zambiri ku munda koma mudzakolola pangʼono, chifukwa dzombe lidzaziwononga.
You will carry much seed out into the field, and will gather little in; for the locust will consume it.
39 Mudzadzala mpesa ndi kulimirira koma vinyo wake simudzamumwa kapena kukolola mphesazo, chifukwa mphutsi zidzadya mphesazo.
You will plant vineyards and dress them, but you will neither drink of the wine, nor harvest, because worms will eat them.
40 Mudzakhala ndi mitengo ya olivi mʼdziko lanu lonse koma simudzagwiritsa ntchito mafuta ake, chifukwa zipatso zake zidzayoyoka.
You will have olive trees throughout all your borders, but you won’t anoint yourself with the oil; for your olives will drop off.
41 Mudzabereka ana aamuna ndi aakazi koma sadzakhala anu, chifukwa adzapita ku ukapolo.
You will father sons and daughters, but they will not be yours; for they will go into captivity.
42 Magulumagulu a dzombe adzawononga mitengo yanu ndi mbewu za mʼdziko lanu.
Locusts will consume all of your trees and the fruit of your ground.
43 Mlendo wokhala pakati panu adzatukuka kuposa inu, koma inuyo mudzaloweralowera pansi.
The foreigner who is among you will mount up above you higher and higher, and you will come down lower and lower.
44 Iye adzakubwereketsani, koma inu simudzatha kubwereketsa. Iye adzakhala mutu ndipo inu mudzakhala mchira.
He will lend to you, and you won’t lend to him. He will be the head, and you will be the tail.
45 Matemberero onsewa adzabwera pa inu. Adzakulondolani ndi kukugonjetsani mpaka mutawonongeka, chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo ndi malangizo amene anakupatsani.
All these curses will come on you, and will pursue you, and overtake you, until you are destroyed; because you didn’t sh'ma ·hear obey· Adonai your God’s voice, to keep his mitzvot ·instructions· and his statutes which he enjoined you.
46 Matemberero amenewa adzakhala chizindikiro ndi chozizwitsa kwa inu ndi zidzukulu zanu mpaka kalekale.
They will be for a sign and for a wonder to you and to your offspring forever.
47 Pakuti inu simunatumikire Yehova Mulungu wanu pa nthawi imene zinthu zinkakuyenderani bwino,
Because you didn’t abad ·serve· Adonai your God with joyfulness, and with gladness of heart, by reason of the abundance of all things;
48 chomwecho pa nthawi ya njala ndi ludzu, ya maliseche ndi umphawi woopsa, mudzatumikira adani amene Yehova adzakutumizirani. Iye adzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwanu kufikira atakuwonongani.
therefore you will abad ·serve· your enemies whom Adonai sends against you, in hunger, in thirst, in nakedness, and in lack of all things. He will put an iron yoke on your neck, until he has destroyed you.
49 Yehova adzakutumizirani mtundu wa anthu kuchokera kutali kumapeto kwa dziko lapansi nudzachita ngati mphungu yowulukira pansi, mtundu wa anthu umene chiyankhulo chawo simudzachimva,
Adonai will bring a nation against you from far, from the end of the earth, as the eagle flies; a nation whose language you will not sh'ma ·hear understand obey·;
50 mtundu wooneka wochititsa mantha, wopanda ulemu kwa okalamba kapena chisoni kwa ana.
a nation of fierce facial expressions, that does not respect the elderly, nor show favor to the young,
51 Iwo adzagwira ana a ziweto zanu, natenga zokolola za mʼdziko lanu kufikira mutawonongeka. Iwo sadzakusiyirani tirigu, vinyo watsopano kapena mafuta a olivi, kapena mwana wangʼombe aliyense kapena mwana wankhosa mpaka mutasanduka bwinja.
and they will eat the fruit of your livestock, and the fruit of your ground, until you are destroyed. They also won’t leave you grain, new wine, or oil, the increase of your livestock, or the young of your flock, until they have caused you to perish.
52 Iwo adzathira nkhondo mizinda yonse mʼdziko lanu lonse mpaka malinga anu ataliatali omwe mumadalira aja atagwa. Adzathira nkhondo mizinda yonse ya mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.
They will besiege you in all your gates, until your high and fortified walls come down, in which you trusted, throughout all your land. They will besiege you in all your gates throughout all your land, which Adonai your God has given you.
53 Chifukwa cha zosautsa zimene mdani wanu adzabweretsa pa nthawi yokuthirani nkhondo, inu mudzadya ana anu, mnofu wa ana anu aamuna ndi aakazi amene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
You will eat the fruit of your own body, the flesh of your sons and of your daughters, whom Adonai your God has given you, in the siege and in the distress with which your enemies will distress you.
54 Ngakhale munthu woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu sadzakhala ndi chifundo pa mʼbale wake weniweni kapena mkazi wake amene iye amamukonda kapena ana ake otsalawo,
The man who is tender among you, and very delicate, his eye will be evil toward his brother, toward the wife whom he loves, and toward the remnant of his children whom he has remaining;
55 ndipo sadzagawirako aliyense wa iwo mnofu wa ana ake amene akudyawo. Kadzakhala kali komweko basi kamene kamutsalira chifukwa cha msautso umene mdani wanu adzagwetsa pa nthawi yothira nkhondo mizinda yanu yonse.
so that he will not give to any of them of the flesh of his children whom he will eat, because he has nothing left to him, in the siege and in the distress with which your enemy will distress you in all your gates.
56 Mayi woleza mtima ndi wachifundo kwambiri pakati panu, uja woti sangayerekeze kuponda pansi, adzabisira mwamuna wake amene amamukonda ndi ana ake omwe aamuna ndi aakazi
The tender and delicate woman among you, who would not venture to set the sole of her foot on the ground for delicateness and tenderness, her eye will be evil toward the husband that she loves, toward her son, toward her daughter,
57 zotsalira za uchembere zochoka mʼmimba mwake ndi ana amene wabereka. Pakuti adzafuna kuti adye zimenezi yekha mobisa pa nthawi yothiridwa nkhondo chifukwa cha masautso amene mdani wanu adzagwetsa pa inu mʼmizinda yanu.
toward her young one who comes out from between her feet, and toward her children whom she bears; for she will eat them secretly for lack of all things, in the siege and in the distress with which your enemy will distress you in your gates.
58 Ngati simutsata mosamalitsa mawu onse a malamulo awa amene alembedwa mʼbuku lino, komanso ngati simuopa dzina la ulemerero ndi loopsa, dzina la Yehova Mulungu wanu,
If you will not observe to do all the words of this Torah ·Teaching· that are written in this book, that you may fear this glorious and fearful name, Yahweh Eloheinu ·He sustains breathing Your God·;
59 Yehova adzatumiza pa inu ndi zidzukulu zanu miliri yoopsa, zosautsa zowawa ndi zokhalitsa, ndi matenda aakulu ndi ovuta kuchiritsika.
then Adonai will make your plagues fearful, and the plagues of your offspring, even great plagues, and of long duration, and severe sicknesses, and of long duration.
60 Adzakubweretserani matenda onse a ku Igupto aja mumawaopawa ndipo adzakukanirirani.
He will bring on you again all the diseases of Egypt [Abode of slavery], which you were afraid of; and they will cling to you.
61 Yehova adzakubweretseraninso mtundu uliwonse wa matenda ndi zosautsa zimene sizinalembedwe mʼbuku la malamulo lino, mpaka mutawonongeka.
Also every sickness and every plague, which is not written in the book of this Torah ·Teaching·, Adonai will bring them on you, until you are destroyed.
62 Inu aja munali ochuluka ngati nyenyezi zakumwamba mudzatsala ochepa chabe chifukwa simunamvere Yehova Mulungu wanu.
You will be left few in number, even though you were as the stars of the sky for multitude; because you didn’t sh'ma ·hear obey· Adonai your God’s voice.
63 Monga kunamukomera Yehova kukulemeretsani ndi kukuchulukitsani, momwemonso kudzamukondweretsa kukunthani ndi kukuwonongani. Inu mudzazulidwa kukuchotsani mʼdziko limene mukulowa kukalitengali.
It will happen that as Adonai rejoiced over you to do you good, and to multiply you, so Adonai will rejoice over you to cause you to perish, and to destroy you. You will be plucked from off of the land where you go in to possess it.
64 Kenaka Yehova adzakubalalitsani pakati pa anthu a mitundu yonse, kuchokera ku mapeto a dziko kufika ku mapeto ena. Kumeneko mudzapembedza milungu ina, milungu ya mitengo ndi ya miyala, imene inu eni kapena makolo anu sanayidziwepo.
Adonai will scatter you among all peoples, from one end of the earth to the other end of the earth. There you will abad ·serve· other deities, which you have not known, you nor your fathers, even wood and stone.
65 Pakati pa mitundu ya anthu imeneyi simudzapeza mpata, popanda malo woti nʼkuyikapo phazi. Kumeneko Yehova adzakupatsani moyo wa nkhawa, maso otopa ndi chiyembekezo, ndi mtima wosakhazikika.
Among these nations you will find no ease, and there will be no rest for the sole of your foot; but Adonai will give you there a trembling heart, failing of eyes, and pining of soul.
66 Inu mudzakhala osakhazikika mopitirira, odzazidwa ndi mantha usiku ndi usana womwe, osowa chitsimikizo cha pa moyo wanu.
Your life will hang in doubt before you. You will be afraid night and day, and will have no assurance of your life.
67 Mmawa muzidzati, “Chikhala anali madzulo!” ndipo madzulo mudzati, “Chikhala unali mmawa!” Mudzanena zimenezi chifukwa cha mantha amene adzakhale mu mtima mwanu ndi chifukwa cha zomwe muzidzaziona.
In the morning you will say, “I wish it were evening!” and at evening you will say, “I wish it were morning!” for the fear of your heart which you will fear, and for the sights which your eyes will see.
68 Yehova adzakubwezani ku Igupto pa sitima zapamadzi paulendo umene Ine ndinati musawuyendenso. Kumeneko mudzadzitsatsa nokha kwa adani anu monga akapolo aamuna ndi aakazi, koma palibe amene adzakuguleni.
Adonai will bring you into Egypt [Abode of slavery] again with ships, by the way of which I told to you that you would never see it again. There you will sell yourselves to your enemies for male and female slaves, and nobody will buy you.

< Deuteronomo 28 >