< Numeri 36 >

1 Atsogoleri a mabanja a fuko la Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wa Manase omwe anali ochokera ku fuko la ana a Yosefe anabwera ndi kuyankhula ndi Mose, atsogoleri ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli.
The heads of the fathers’ households of the family of the children of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh [Causing to forget], of the families of the sons of Joseph [May he add], came near, and spoke before Moses [Drawn out], and before the princes, the heads of the fathers’ households of the children of Israel [God prevails].
2 Iwo anati, “Pamene Yehova analamula mbuye wanga kuti apereke dziko ngati cholowa kwa Aisraeli mwa maere, anakulamulani inu kupereka cholowa cha mʼbale wathu Zelofehadi kwa ana ake aakazi.
They said, “Adonai enjoined my lord to give the land for inheritance by lot to the children of Israel [God prevails]. My lord was enjoined by Adonai to give the inheritance of Zelophehad our brother to his daughters.
3 Tsopano ngati akwatiwa ndi aamuna ochokera ku mafuko ena a mitundu ya Aisraeli, cholowa chawo chidzatengedwa kuchoka pa cholowa cha makolo athu ndipo adzachiwonjezera ku fuko limene akwatiwakolo. Ndipo gawo lina la cholowacho, lopatsidwa kwa ife lidzatengedwa.
If they are married to any of the sons of the other tribes of the children of Israel [God prevails], then will their inheritance be taken away from the inheritance of our fathers, and will be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong. So will it be taken away from the lot of our inheritance.
4 Pamene chaka cha chikondwerero cha zaka makumi asanu, cha Aisraeli chafika, cholowa chawo chidzawonjezeredwa ku fuko limene iwo akwatiwako. Ndipo katundu wawo adzachotsedwa pa cholowa cha fuko la makolo athu.”
When the Jubilee of the children of Israel [God prevails] shall be, then will their inheritance be added to the inheritance of the tribe to which they shall belong. So their inheritance will be taken away from the inheritance of the tribe of our fathers.”
5 Tsono mwa lamulo la Yehova, Mose anapereka lamulo ili kwa Aisraeli: “Zimene ana a Yosefe akunena ndi zoona.
Moses [Drawn out] enjoined the children of Israel [God prevails] according to Adonai’s word, saying, “The tribe of the sons of Joseph [May he add] speaks right.
6 Izi ndi zimene Yehova akulamula kwa ana aakazi a Zelofehadi: Atha kukwatiwa ndi aliyense amene angakondweretsedwe naye koma zingakhale bwino atakwatiwa mʼfuko la abambo awo
This is the thing which Adonai does enjoin concerning the daughters of Zelophehad, saying, ‘Let them be married to whom they think best; only they shall marry into the family of the tribe of their father.
7 kuti cholowa cha Israeli chisapite ku fuko lina, pakuti Mwisraeli aliyense ayenera kusunga cholowa cha fuko la makolo ake.
So shall no inheritance of the children of Israel [God prevails] move from tribe to tribe; for the children of Israel [God prevails] shall all keep the inheritance of the tribe of his fathers.
8 Mwana wamkazi aliyense amene adzalandira cholowa cha dziko la fuko lililonse la Israeli ayenera kukwatiwa ndi munthu wa fuko la abambo ake.
Every daughter who possesses an inheritance in any tribe of the children of Israel [God prevails] shall be wife to one of the family of the tribe of her father, that the children of Israel [God prevails] may each possess the inheritance of his fathers.
9 Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”
So shall no inheritance move from one tribe to another tribe; for the tribes of the children of Israel [God prevails] shall each keep his own inheritance.’”
10 Choncho ana aakazi a Zelofehadi anachita monga Yehova analamulira Mose.
The daughters of Zelophehad did as Adonai enjoined Moses [Drawn out]:
11 Ana aakazi a Zelofehadi amene ndi Mahila, Tiriza, Hogila, Milika ndi Nowa, anakwatiwa ndi asuweni awo a ku mbali ya abambo awo.
for Mahlah, Tirzah, Hoglah, Milcah, and Noah [Rest], the daughters of Zelophehad, were married to their dod ·father’s· brothers’ sons.
12 Anakwatiwa mʼmafuko a zidzukulu za Manase mwana wa Yosefe, ndipo cholowa chawo chinakhalabe mʼfuko la abambo awo.
They were married into the families of the sons of Manasseh [Causing to forget] the son of Joseph [May he add]. Their inheritance remained in the tribe of the family of their father.
13 Awa ndi malamulo ndi malangizo amene Yehova anapereka kwa Aisraeli kupyolera mwa Mose ku chigwa cha Mowabu mʼmbali mwa Yorodani, ku Yeriko.
These are the mitzvot ·instructions· and the judgments which Adonai enjoined by the hand of Moses [Drawn out] to the children of Israel [God prevails] in the plains of Moab [From father] by the Jordan [Descender] across from Jericho [Fragrant, Moon].

< Numeri 36 >