< Deuteronomo 15 >

1 Kumapeto kwa zaka zisanu ndi ziwiri zilizonse, muzikhululukirana ngongole.
“In the seventh year, you shall perform a remission,
2 Zimenezi muzichita motere: wobwereketsa aliyense adzakhululukira ngongole imene anabwereketsa kwa Mwisraeli mnzake. Iye asadzafunenso kuti Mwisraeli mnzakeyo kapena mʼbale wake amubwezere chifukwa nthawi ya Ambuye yokhululukirana ngongole yalengezedwa.
which shall be celebrated according to this order. Anyone to whom anything is owed, by his friend or neighbor or brother, will not be able to request its return, because it is the year of remission of the Lord.
3 Mukhoza kulonjerera ngongole kwa mlendo, koma mukhululukire ngongole ina iliyonse imene mʼbale wanu ali nayo.
From the sojourner and the new arrival, you may require its return. From your fellow countryman and neighbor, you will not have the power to request its return.
4 Komabe pasadzakhale wosauka pakati panu chifukwa Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani kwambiri mʼdziko limene adzakupatsani kuti likhale lanu ngati cholowa chanu.
And there shall not be anyone indigent or begging among you, so that the Lord your God may bless you in the land which he will deliver to you as a possession.
5 Adzakudalitsani pokhapokha ngati mudzamveradi Yehova Mulungu wanu posunga ndi kutsatira malamulo onse amene ndikukupatsani lero.
But only if you heed the voice of the Lord your God, and keep to all that he has ordered, that which I am entrusting to you this day, will he bless you, just as he has promised.
6 Pakuti Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani monga analonjeza, ndipo inu mudzabwereketsa chuma kwa mitundu yambiri ya anthu koma inu simudzabwereka kwa aliyense. Mudzalamulira mitundu yambiri ya anthu koma inuyo palibe amene adzakulamulireni.
You shall lend money to many nations, and you yourselves shall borrow in return from no one. You shall rule over very many nations, and no one shall rule over you.
7 Ngati pali mʼbale wanu wina wosauka mu mzinda wanu wina uliwonse mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, musawumitse mitima yanu kapena kuchita kaligwiritsa kwa mʼbale wanu wosaukayo.
If one of your brothers, who dwells within the gates of your city, in the land which the Lord your God will give to you, falls into poverty, you shall not harden your heart, nor tighten your hand.
8 Koma mukhale ofewa manja ndipo mumukongoze mʼbale wanu momasuka pa chilichonse chimene akufuna.
Instead, you shall open your hand to the poor, and you shall lend to him whatever you perceive him to need.
9 Musayesere ndi pangʼono pomwe kusunga maganizo oyipa awa mu mtima mwanu: “Chaka chachisanu ndi chiwiri, chaka chokhululukirana ngongole, chayandikira,” kuti musaonetse mtima woyipa kwa mʼbale wanu wosauka nʼkusamupatsa chilichonse. Iye angadzakunenereni inu mlandu kwa Ambuye, ndipo mudzapezeka wochimwa.
Take care, lest perhaps an impious thought might creep within you, and you might say in your heart: ‘The seventh year of remission approaches.’ And so you might turn your eyes away from your poor brother, unwilling to lend to him what he has asked. If so, then he may cry out against you to the Lord, and it will be a sin for you.
10 Mumupatse iye mowolowamanja ndipo muchite zimenezi mosasungira kanthu kumtima. Tsono chifukwa cha zimenezi, Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa ntchito zanu zonse ndi pa chilichonse chimene mukhudza.
Instead, you shall give to him. Neither shall you do anything craftily while assisting him in his needs, so that the Lord your God may bless you, at all times and in all things to which you will put your hand.
11 Anthu osauka sadzatha mʼdziko lanu. Chomwecho ndikukulamulani kuti mukhale ofewa manja kwa abale anu ndi kwa osauka, osowa mʼdziko mwanu.
The poor will not be absent from the land of your habitation. For this reason, I instruct you to open your hand to your indigent and poor brother, who lives among you in the land.
12 Ngati mʼbale wanu wamwamuna kapena wamkazi adzigulitsa yekha kwa inu, nakugwirirani ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, muzimumasula mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri.
When your brother, a Hebrew man or a Hebrew woman, has been sold to you, and has served you for six years, in the seventh year you shall set him free.
13 Ndipo pamene mumumasula, musangomulola apite chimanjamanja.
And when you grant his freedom, you shall by no means permit him to go away empty.
14 Mumupatse mowolowamanja zochokera pa ziweto zanu, kopunthira tirigu ndi kopsinyira vinyo. Inu mumupatse iye monga Yehova Mulungu wanu wakudalitsirani.
Instead, you shall give to him, for his journey, from your flocks and threshing floor and winepress, with which the Lord your God has blessed you.
15 Kumbukirani kuti munali akapolo mʼdziko la Igupto ndipo Yehova Mulungu wanu anakupulumutsani. Nʼchifukwa chake ndikukupatsani lamulo ili lero lino.
Remember that you yourself also served in the land of Egypt, and the Lord your God set you free. And therefore, I now command this of you.
16 Koma ngati kapoloyo akuwuzani kuti, “Ine sindikufuna kumasulidwa,” chifukwa choti wakukondani inuyo pamodzi ndi banja lanu ndiponso kuti kwamukomera iyeyo kuti azikhalabe nanu,
But if he will say, ‘I am not willing to depart,’ because he loves you and your household, and because he feels that it would be good for him to stay with you,
17 pamenepo muzitenga chobowolera chachitsulo ndi kubowola khutu lake pa chitseko, ndipo mukatero adzakhala kapolo wanu moyo wake wonse. Mdzakazi wanu muzimuchitanso chimodzimodzi.
then you shall take an awl and pierce his ear, at the door of your house. And he shall serve you even forever. You shall also act similarly toward your woman servant.
18 Musaone ngati chopweteka kumasula wantchito wanu, chifukwa ntchito imene wayigwira pa zaka zisanu ndi chimodzi zimenezi ndi yopindula kawiri pa ntchito imene akanagwira waganyu chabe. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani pa chilichonse chimene mukuchita.
You should not avert your eyes from them when you set them free, because he has served you for six years, in a manner deserving of the pay of a hired hand. So may the Lord your God bless you in all the works that you do.
19 Mumupatulire Yehova Mulungu wanu choyamba kubadwa chachimuna chilichonse pa ngʼombe ndi nkhosa zanu. Musamazigwiritse ntchito ngʼombe zoyamba kubadwa kapena kumeta nkhosa zoyamba kubadwa.
Of the firstborn, those born from your herds and sheep, you shall sanctify to the Lord your God whatever is of the male sex. You shall not put the firstborn of the oxen to work, nor shall you shear the firstborn of the sheep.
20 Inuyo ndi banja lanu, chaka chilichonse muzizidya zimenezi pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene Iye adzasankhe.
In the sight of the Lord your God, you shall eat these, each year, in the place which the Lord will choose, you and your household.
21 Ngati chiweto chili ndi chilema monga kulumala kapena chosaona, kapena ngati chili ndi cholakwika chachikulu chilichonse, musachipereke nsembe kwa Yehova Mulungu wanu.
But if it has a blemish, or is lame, or is blind, or if it is in any part deformed or debilitated, it shall not be immolated to the Lord your God.
22 Muzichidya mʼmizinda yanuyanu. Onse odetsedwa monga mwa mwambo ndi oyeretsedwa omwe akhoza kuchidya monga akudya gwape kapena mbawala.
Instead, you shall eat it within the gates of your city. The clean as well as the unclean alike shall feed on these, such as the roe deer and the stag.
23 Koma musadye magazi ake. Muwathire pansi ngati madzi.
This alone shall you observe: that you do not eat their blood, but pour it upon the ground like water.”

< Deuteronomo 15 >