< Danieli 5 >
1 Tsiku lina mfumu Belisazara anakonza phwando lalikulu la akalonga ake 1,000 ndipo anamwa vinyo pamodzi ndi iwo.
Цар Валтасар учини велику гозбу хиљади кнезова својих, и пијаше вино пред хиљадом њих.
2 Pamene Belisazara ankamwa vinyo, analamula kuti ziwiya zagolide ndi zasiliva zimene Nebukadinezara abambo ake anakatenga mʼNyumba ya Mulungu ku Yerusalemu zikatengedwe kuti mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi amweremo.
Напив се вина Валтасар заповеди да се донесу судови златни и сребрни, које беше однео Навуходоносор отац му из цркве јерусалимске, да из њих пију цар и кнезови му и жене његове и иноче његове.
3 Choncho anabweretsa ziwiya zagolide zimene anazitenga mʼNyumba ya Mulungu; ndipo mfumu ndi akalonga ake, akazi ake ndi azikazi ake anamweramo.
И донесоше златне судове које беху однели из цркве дома Господњег у Јерусалиму, и пијаху из њих цар и кнезови његови, жене његове и иноче његове.
4 Akumwa vinyo, anatamanda milungu yagolide ndi siliva, yamkuwa, chitsulo, yamtengo ndi mwala.
Пијаху вино, и хваљаху богове златне и сребрне и бронзане и дрвене и камене.
5 Mwadzidzidzi zala za dzanja la munthu zinaonekera ndi kulemba pa khoma, pafupi ndi choyikapo nyale mʼnyumba yaufumu. Mfumu inapenyetsetsa dzanjalo pamene limalemba.
У тај час изиђоше прсти руке човечије и писаху према свећњаку по окреченом зиду од царског двора, и цар виде руку која писаше.
6 Nkhope yake inasandulika ndipo inachita mantha, nkhongono zii, mawondo gwedegwede.
Тада се промени лице цару, и мисли га његове узнемирише и појас се око њега распаса и колена му удараху једно о друго.
7 Mfumu inafuwula kuyitana owombeza, alawuli ndi amawula kuti abwere. Ndipo anawawuza anthu anzeru a ku Babuloni kuti, “Aliyense amene awerenge malembawa ndi kundiwuza tanthauzo lake adzavekedwa chovala cha pepo ndi mkanda wa golide udzavekedwa mʼkhosi mwake, ndipo adzakhala wolamulira wachitatu mu ufumuwu.”
Повика цар гласно, те доведоше звездаре, Халдеје и гатаре; и проговори цар и рече мудрацима вавилонским: Ко прочита ово писмо и каже ми шта значи, онај ће се обући у скерлет, и носиће златну верижицу о врату, и биће трећи господар у царству.
8 Pamenepo anzeru onse a mfumu anabwera, koma sanakwanitse kuwerenga malembawo kapena kumutanthauzira mfumu.
Тада приступише сви мудраци цареви; али не могоше прочитати писма нити казати цару шта значи.
9 Choncho mfumu Belisazara anachita mantha koposa ndipo nkhope yake inapitirira kusinthika. Akalonga ake anathedwa nzeru.
Тада се цар Валтасар врло узнемири, и лице му се сасвим измени; и кнезови се његови препадоше.
10 Mfumukazi, pakumva mawu a mfumu ndi akalonga ake, analowa mʼchipinda cha phwando ndipo anati, “Mfumu mukhale ndi moyo wautali! Musavutike! Nkhope yanu isasinthike!
Дође царица ради тога што се догоди цару и кнезовима његовим у кућу где беше гозба, и проговори царица и рече: Царе, да си жив довека! Да те не узнемирују мисли твоје, и да ти се лице не мења.
11 Pali munthu wina mu ufumu wanu uno amene mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera. Pa nthawi ya ulamuliro wa abambo anu iye anapezeka kuti ali ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zonga za milungu. Mfumu Nebukadinezara, abambo anu, Ine ndikukuwuzani anamusankha iye kukhala mkulu wa amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula.
Има човек у твом царству, у коме је дух светих богова; и у време оца твог нађе се у њега видело и разум и мудрост, каква је у богова, и цар Навуходоносор, отац твој, царе, постави га главарем врачарима, звездарима, Халдејима и гатарима;
12 Munthu ameneyu dzina lake ndi Danieli, koma mfumu inamutcha Belitesezara ndipo ali ndi nzeru zapadera, ndi wodziwa ndi kuzindikira zinthu, ndiponso luso lakutanthauzira maloto, kufotokozera miyambi ndi kuthetsa mavuto osautsa. Muyitaneni Danieli, ndipo adzakuwuzani chomwe mawuwa akutanthauza.”
Јер велик дух и знање и разум за казивање снова и погађање загонетки и размршивање замршених ствари нађе се у Данила, коме цар наде име Валтасар; нека сада дозову Данила, и он ће казати шта значи.
13 Choncho anabwera naye Danieli pamaso pa mfumu ndipo inati kwa iye, “Kodi ndiwe Danieli, mmodzi mwa akapolo omwe abambo anga mfumu anabwera nawo kuchoka ku Yuda?
Тада Данило би доведен пред цара. Цар проговори Данилу и рече: Јеси ли ти Данило између робља Јудина, које доведе из јудејске цар отац мој?
14 Ndamva kuti mzimu wa milungu uli mwa iwe ndi kuti uli ndi chidziwitso, luntha ndi nzeru zapadera.
Чух за тебе да је дух светих богова у теби, и видело и разум и мудрост велика да се нађе у тебе.
15 Anzeru ndi owombeza anabwera pamaso panga kuti awerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake koma sanakwanitse kundifotokozera.
А сада су доведени преда ме мудраци, звездари, да прочитају писмо и кажу ми шта значи; али не могу да кажу шта то значи.
16 Tsopano ndamva kuti iwe ukhoza kupereka matanthauzo ndi kuthetsa mavuto. Ngati ungawerenge zolembedwazi ndi kundiwuza tanthauzo lake, udzavekedwa chovala cha pepo ndi kuyikidwa mkanda wa golide mʼkhosi mwako, ndipo udzakhala wolamulira wachitatu mu ufumu uno.”
А за тебе ја чух да можеш протумачити и замршене ствари размрсити. Ако, дакле, можеш прочитати ово писмо и казати ми шта значи, обући ћеш се у скерлет, и златну верижицу носићеш о врату, и бићеш трећи господар у царству.
17 Pamenepo Danieli anayankha mfumu kuti, “Inu musunge mphatso zanuzo kwa inu nokha ndipo mupereke mphothoyo kwa wina aliyense. Komabe ine ndi kuwerengerani malembawa mfumu; ndikukuwuzani tanthauzo lake.
Тада одговори Данило и рече пред царем: Дарови твоји нека теби, и подај другом поклоне своје; а писмо ћу ја прочитати цару и казати шта значи.
18 “Inu mfumu, Mulungu Wammwambamwamba anapatsa abambo anu Nebukadinezara mphamvu ndi ukulu ndi ulemerero ndi ufumu.
Царе, Бог Вишњи даде царство величину и славу и част Навуходоносору, оцу твом.
19 Chifukwa cha udindo waukulu umene anapatsidwanso, anthu onse ndi mitundu ndi anthu aziyankhulo zosiyanasiyana ankanjenjemera ndikumuopa iye. Amene mfumu inafuna anawaphadi; amene inafuna kuwasunga, inawasunga; amene inafuna kuwakweza, inawakweza; ndipo amene inafuna kuwatsitsa, inawatsitsa.
И од величине коју му даде сви народи, племена и језици дрхтаху пред њим и бојаху га се; убијаше кога хоћаше, и остављаше у животу кога хоћаше, узвишаваше кога хоћаше, и понижаваше кога хоћаше.
20 Koma pamene inayamba kudzitama ndi kuwumitsa mtima wake ndi kuyamba kunyada, inachotsedwa pa mpando wake waufumu ndi kulandidwa ulemerero wake.
Али када му се подиже срце и дух му се посили у охолости, би сметнут с царског престола свог, и узеше му славу.
21 Iyo inachotsedwa pakati pa anthu ndi kupatsidwa mtima ngati wa nyama; inakhala pamodzi ndi abulu akutchire ndi kudya udzu ngati ngʼombe; ndipo thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba, mpaka pamene anavomereza kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye wolamulira maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
И би прогнан између људи и срце му поста као у звери, и стан му беше с дивљим магарцима, хранише га травом као говеда, и роса небеска кваси му тело, докле позна да Бог Вишњи влада царством људским, и кога хоће поставља над њим.
22 “Koma inu mwana wake, Belisazara, simunadzichepetse, ngakhale kuti mumadziwa zonsezi.
А ти, Валтасаре, сине његов, ниси понизио срца свог премда си знао све ово.
23 Mʼmalo mwake, mwadzikweza nokha kutsutsana ndi Ambuye wakumwamba. Inu mwatenga ziwiya za mʼNyumba mwake, ndipo inu ndi akalonga anu, akazi anu ndi azikazi anu mwamwera vinyo mu zimenezi. Inu munatamanda milungu yasiliva ndi golide, yamkuwa, chitsulo, mtengo ndi mwala, imene singaone kapena kumva kapena kuzindikira. Koma simunamupatse ulemu Mulungu amene asunga mʼmanja mwake moyo wanu ndi njira zanu zonse.
Него си се подигао на Господа небеског, и судове дома Његовог донесоше преда те, и писте из њих вино ти и кнезови твоји, жене твоје и иноче твоје, и ти хвали богове сребрне и златне, бронзане, гвоздене, дрвене и камене, који не виде нити чују, нити разумеју, а не слави Бога, у чијој је руци душа твоја и сви путеви твоји.
24 Choncho Iye watumiza dzanja limene lalemba mawu amenewa.
Зато од Њега би послана рука и ово писмо би написано.
25 “Mawu amene analembedwa ndi awa: MENE, MENE, TEKELI, PARASINI.
А ово је писмо написано: МЕНЕ, МЕНЕ, ТЕКЕЛ, УФАРСИН.
26 “Zimene mawuwa akutanthauza ndi izi:
А ово значе те речи: МЕНЕ, бројао је Бог твоје царство и до краја избројао.
27 Tekeli: Inu mwayesedwa pa sikelo ndipo mwapezeka kuti mukuperewera.
ТЕКЕЛ, измерен си на мерила, и нашао си се лак.
28 Parasini: Ufumu wanu wagawidwa ndi kupatsidwa kwa Amedi ndi Aperezi.”
ФЕРЕС, раздељено је царство твоје, и дано Мидијанима и Персијанима.
29 Mwa lamulo la Belisazara, Danieli anavekedwa chovala cha pepo, mkanda wagolide unayikidwa mʼkhosi mwake, ndipo analengeza kuti anali wachitatu mu ulamuliro mu ufumuwo.
Тада заповеди Валтасар, те обукоше Данила у скерлет, и метнуше му златну верижицу око врата, и прогласише за њ да је трећи господар у царству.
30 Usiku womwewo Belisazara, mfumu ya anthu a ku Babuloni, inaphedwa,
Исту ноћ би убијен Валтасар, цар халдејски.
31 ndipo Dariyo Mmedi analanda ufumuwo ali ndi zaka 62.
А Дарије Мидијанин преузе царство, и беше му око шездесет и две године.