< Danieli 4 >
1 Mfumu Nebukadinezara anatumiza mawu awa kwa anthu a mitundu yonse, ndi chiyankhulo chilichonse, amene amakhala pa dziko lonse lapansi: Mtendere uchuluke pakati panu!
Цар Навуходоносор свим народима, племенима и језицима што су по свој земљи, мир да вам се умножи.
2 Chandikomera kukuwuzani zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene Mulungu Wammwambamwamba wandichitira.
Свиде ми се да објавим знаке и чудеса што ми учини Бог Вишњи.
3 Zizindikiro zake ndi zazikulu,
Знаци Његови како су велики! И чудеса Његова како су силна! Царство је Његово царство вечно, и власт Његова од колена до колена.
4 Ine Nebukadinezara, ndinali kwathu mʼnyumba yanga yaufumu, mwa mtendere ndipo ndinali wokhutitsidwa.
Ја Навуходоносор бејах миран у кући својој и цветах у двору свом.
5 Ndili chigonere pa bedi langa, ndinalota maloto amene anandichititsa mantha. Zinthu ndi masomphenya zimene ndinaziona zinandiopsa.
Усних сан, који ме уплаши, и мисли на постељи мојој и утваре главе моје узнемирише ме.
6 Choncho ndinalamula kuti anthu onse a nzeru a ku Babuloni abwere pa maso panga kunditanthauzira malotowo.
И заповедих да се доведу преда ме сви мудраци вавилонски да ми кажу шта значи сан.
7 Pamene amatsenga, owombeza, alawuli ndi amawula anabwera, ndinawafotokozera maloto, koma sanathe kunditanthauzira.
Тада дођоше врачари, звездари, Халдеји и гатари, и приповедих им сан, али ми не могоше казати шта значи.
8 Potsiriza, anabwera Danieli uja amatchedwa Belitesezara, potsata dzina la mulungu wanga, ndipo mzimu wa milungu yoyera uli mwa iye. Iyeyu ndinamufotokozera malotowo.
Најпосле дође преда ме Данило, који се зове Валтасар по имену бога мог, и у коме је дух светих богова, и приповедих му сан.
9 Ndinati, “Belitesezara, mkulu wa amatsenga, ndikudziwa kuti mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe, ndipo palibe chinsinsi chomwe sungachidziwe. Awa ndi maloto anga; unditanthauzire.
Валтасаре, поглаваре врачима, знам да је дух светих богова у теби и никаква тајна није ти тешка; кажи сан мој што сам снио и шта значи.
10 Awa ndi masomphenya amene ine ndinaona pamene ndinali kugona pa bedi: Ndinaona, mtengo wautali kwambiri utayima pakati pa dziko lapansi.
А утвара главе моје на постељи мојој беше: Видех, гле, дрво усред земље, и висина му велика.
11 Mtengowo unakula ndi kulimba ndipo msonga yake inafika mpaka mlengalenga; umaonekera pa dziko lonse lapansi.
Дрво беше велико и јако, и висина му досезаше до неба, и виђаше се до краја све земље.
12 Masamba ake anali okongola, zipatso zinali zochuluka, ndipo mu mtengomo munali chakudya chokwanira anthu onse. Zirombo zakuthengo zimapeza mthunzi mʼmunsi mwake, ndipo mbalame zamlengalenga zimakhala pa nthambi zake: Cholengedwa chilichonse chinkadya za mu mtengowu.
Лишће му беше лепо и род обилат, и на њему беше хране свему, зверје пољско одмараше се у хладу његовом, и на гранама његовим становаху птице небеске, и од њега се храњаше свако тело.
13 “Ndikanali chigonere ndinaona mʼmasomphenya mngelo atayima pamaso panga, woyera, atatsika kuchokera kumwamba.
Видех у утварама главе своје на постељи својој, и гле, Стражар и Светац сиђе с неба.
14 Anayankhula mofuwula kuti, ‘Gwetsa mtengo ndi kusadza nthambi zake; yoyola masamba ake kuti nyama zakuthengo zithawe pa mthunzi pake ndi mbalame zithawe pa nthambi zake.
Повика јако и рече овако: Посеците дрво, и окрешите му гране, покидајте му лишће и разметните му род; нека побегну звери испод њега и птице с грана његових.
15 Koma musiye tsinde ndi mizu yake mʼnthaka. Tsindelo mulimange maunyolo a chitsulo ndi mkuwa, zikhalebe mʼnthaka, nʼkudya udzu mʼmunda. “‘Mumulole iye anyowe ndi mame akumwamba, ndipo iye akhale ndi nyama pakati pa zomera za mʼnthaka.
Али пањ са жилама оставите му у земљи, у оковима гвозденим и бронзаним у трави пољској, нека га кваси роса небеска и део да му је са зверјем од траве земаљске.
16 Maganizo ake a umunthu asinthidwe ndipo apatsidwe maganizo a nyama ya kuthengo, mpaka zaka zisanu ndi ziwiri zitadutsa.
Срце човечје нека му се промени, и срце животињско нека му се да, и седам времена нека прође преко њега.
17 “‘Angelo oyera ndiwo akutsimikiza chilangochi. Tsono anthu adziwe kuti Mulungu Wammwambamwamba ali ndi mphamvu yolamulira maufumu onse, ndipo amawapereka kwa aliyense akumufuna, ngakhale munthu wamba kuti alamulire.’
То су одредили стражари и изрекли свети да би познали живи да Вишњи влада царством људским, и даје га коме хоће, и поставља над њим најнижег између људи.
18 “Amenewa ndi maloto amene ine, mfumu Nebukadinezara, ndinalota. Tsopano Belitesezara, undifotokozere tanthauzo lake, popeza palibe mwa anthu anzeru a mu ufumu wanga amene angathe kunditanthauzira. Koma iwe ukhoza, chifukwa mzimu wa milungu yoyera uli mwa iwe.”
Тај сан сних ја, цар Навуходоносор; а ти, Валтасаре, кажи шта значи, јер ниједан мудрац у царству мом не може да ми каже шта значи; а ти можеш, јер је у теби дух светих богова.
19 Pamenepo Danieli, amene amatchedwa Belitesezara, anavutika mu mtima kwambiri kwa kanthawi, ndipo anasautsidwa mʼmaganizo ake. Choncho mfumu inati, “Belitesezara usalole malotowa kapena tanthauzo lake likuopse.” Belitesezara anayankha kuti, “Mbuye wanga, ndikanakonda malotowa akanakhudza adani anu okha, ndi tanthauzo lake kwa iwo okusautsani!
Тада Данило, који се зваше Валтасар, оста у чуду за један сат, и мисли га узнемираваху. А цар проговори и рече: Валтасаре, сан и значење му да те не узнемирује. А Валтасар одговори и рече: Господару мој, сан да буде твојим ненавидницима, и значење његово непријатељима твојим.
20 Mtengo munawuona uja, umene unkakulirakulira kwambiri ndi kulimba, ndi msonga yake inafika mlengalenga, ndi kuonekera ku dziko lonse lapansi,
Дрво што си видео, велико и јако, коме висина досезаше до неба и које се виђаше по свој земљи,
21 mtengo umene masamba ake anali okongola ndiponso unali ndi zipatso zochuluka zokwanira kudya anthu onse a dziko lapansi. Mtengowu unkapereka mthunzi ku zirombo zonse zakuthengo, ndipo mbalame zamlengalenga zinayika zisa pa nthambi zake.
Коме лишће беше лепо и род обилан, и на коме беше хране свему, под којим становаше зверје пољско и на гранама му сеђаху птице небеске,
22 Inu mfumu, ndinu mtengo umenewo! Inu mwakhala wamkulu ndi wamphamvu; ukulu wanu wakula mpaka wakhudza mlengalenga, ndipo ufumu wanu wafika mpaka ku malo akutali a dziko lapansi.
То си ти, царе, који си велик и силан, и величина је твоја висока и досеже до неба и власт твоја до крајева земаљских.
23 “Inu mfumu munaona mthenga woyera, akuchokera kumwamba ndipo anati, ‘Gwetsani mtengo ndipo muwuwononge, koma musiye tsinde ndi mizu yake. Tsindelo mulimange ndi unyolo wa chitsulo ndi mkuwa ndipo mulisiye pakati pa udzu wa mʼmunda. Mulole kuti linyowe ndi mame akumwamba. Likhale ngati nyama zakuthengo, mpaka zaka zidutse zisanu ndi ziwiri.’
А што цар виде Стражара и Свеца где силажаше с неба и говораше: Посеците дрво и потрите га, али му пањ са жилама оставите у земљи у оковима гвозденим и бронзаним у трави пољској, да га кваси роса небеска, и са зверјем пољским нека му је део докле седам времена прође преко њега,
24 “Tanthauzo lake ndi ili mfumu, izi ndi zimene Mulungu Wammwambamwamba watsimikiza kuti zikugwereni mbuye wanga mfumu:
Ово значи, царе, и ово је наредба Вишњег која ће се извршити на мом господару цару:
25 Inu mudzachotsedwa pakati pa anthu ndipo mudzakhala ndi nyama zakuthengo; mudzadya udzu monga ngʼombe ndi kunyowa ndi mame akumwamba. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka mudzavomereze kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa ma ufumu a anthu, ndipo amawapereka kwa aliyense amene Iye wafuna.
Бићеш прогнан између људи, и са зверима ћеш пољским живети, и храниће те травом као говеда, и роса ће те небеска квасити, и седам ће времена проћи преко тебе докле познаш да Вишњи влада царством људским и даје га коме хоће.
26 Lamulo losiya tsinde la mtengo ndi mizu yake litanthauza kuti ufumu wanu udzabwezeredwa kwa inu mukadzavomereza kuti Mulungu ndiye amalamulira.
А што се рече да се остави пањ са жилама од дрвета, царство ће ти остати, кад познаш да небеса владају.
27 Nʼchifukwa chake mfumu, chikukomereni kulandira malangizo anga: Lekani machimo ndipo muzichita zabwino, lekani mphulupulu zanu ndipo muzikomera mtima anthu opsinjika. Nʼkutheka kuti mtendere wanu udzapitirira.”
Зато, царе, да ти је угодан мој савет, опрости се греха својих правдом, и безакоња својих милошћу према невољнима, е да би ти се продужио мир.
28 Zonsezi zinamuchitikira mfumu Nebukadinezara.
Све ово дође на цара Навуходоносора.
29 Itapita miyezi khumi ndi iwiri, pamene mfumu inkayenda pa denga la nyumba ya ufumu ya ku Babuloni,
После дванаест месеци ходаше по царском двору у Вавилону.
30 iye anati, “Kodi Babuloni si mzinda wamphamvu ndi wokongola umene ndinamanga ndi mphamvu zanga ngati nyumba yanga yaufumu, kuonetsera ulemerero wa ufumu wanga?”
И проговори цар и рече: Није ли то Вавилон велики што га ја сазидах јаком силом својом да је столица царска, и слава величанству мом?
31 Akuyankhulabe izi mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Imvani izi, mfumu Nebukadinezara: Ufumu wako wachotsedwa.
Те речи још беху у устима цару, а глас дође с неба: Теби се говори, царе Навуходоносоре: Царство се узе од тебе.
32 Udzachotsedwa pakati pa anthu ndipo udzakhala ndi zirombo zakuthengo; udzadya udzu monga ngʼombe. Zaka zisanu ndi ziwiri zidzadutsa mpaka iwe utavomereza kuti Wammwambamwamba ndiye mwini ulamuliro pa maufumu a anthu ndipo amawupereka kwa aliyense amene iye afuna.”
И бићеш прогнан између људи, и живећеш са зверјем пољским, храниће те травом као говеда, и седам ће времена проћи преко тебе докле познаш да Вишњи влада царством људским и даје га коме хоће.
33 Nthawi yomweyo zonse zimene zinanenedwa zokhudza Nebukadinezara zinakwaniritsidwa. Iye anachotsedwa pakati pa anthu ndipo ankadya udzu ngati ngʼombe. Thupi lake linanyowa ndi mame akumwamba mpaka tsitsi lake linakula ngati nthenga za chiwombankhanga ndi zikhadabo ngati zikhadabo za mbalame.
У тај час испуни се та реч на Навуходоносору; и би прогнан између људи и једе траву као говеда, и роса небеска кваси му тело да му нарастоше длаке као пера у орла и нокти као у птица.
34 Pomaliza pa zaka zimenezo ine, Nebukadinezara ndinakweza maso anga kumwamba, ndipo nzeru zanga zinabwereramo. Kenaka ndinatamanda Wammwambamwamba; ndinamupatsa ulemu ndi kumulemekeza Iye amene akhala nthawi zonse.
Али после тог времена ја Навуходоносор подигох очи своје к небу, и ум мој врати ми се, и благослових Вишњег, и хвалих и славих Оног који живи довека, чија је власт власт вечна и чије је царство од колена до колена.
35 Anthu onse a dziko lapansi
И сви становници земаљски ништа нису према Њему, и ради шта хоће с војском небеском и са становницима земаљским, и нема никога да би Му руку зауставио и рекао Му: Шта радиш?
36 Pa nthawi yomweyo nzeru zanga zinabwereramo. Ndinalandiranso ulemu wanga ndi ufumu wanga. Nduna ndi akalonga anga anandilandiranso. Ndipo anandibwezera ufumu wanga ndi kukhalanso wamphamvu kuposa kale.
У то време ум мој врати ми се, и на слави царства мог врати ми се величанство моје и светлост моја; и дворани моји и кнезови моји потражише ме, и утврдих се у царству свом, и дода ми се више величанства.
37 Tsopano ine Nebukadinezara, ndikutamanda, kukweza ndi kulemekeza Mfumu yakumwamba chifukwa zonse zimene amachita ndi zoyenera ndipo njira zake zonse ndi zachilungamo. Ndipo onse amene amayenda modzikuza adzawatsitsa.
Сада ја Навуходоносор хвалим, узвишујем и славим цара небеског, чија су сва дела истина и чији су путеви праведни и који може оборити оне који ходе поносито.