< Amosi 4 >

1 Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
Hear the word this O cows of Bashan who [are] on [the] mountain of Samaria who oppress poor [people] who crush needy [people] who say to masters their bring! so we may drink.
2 Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
He has sworn [the] Lord Yahweh by holiness his for here! days [are] coming on you and someone will take away you with barbs and posterity your with hooks of fishing.
3 Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
And breaches you will go out each before herself and you will throw Harmon towards [the] utterance of Yahweh.
4 “Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
Come Beth-el and transgress Gilgal increase to transgress and bring to the morning sacrifices your to three days tithes your.
5 Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
And make smoke from a thing leavened a thank-offering and proclaim freewill offerings make [them] heard for thus you love O people of Israel [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
6 “Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
And also I I gave to you cleanness of teeth in all cities your and lack of bread in all places your and not you returned to me [the] utterance of Yahweh.
7 “Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
And also I I withheld from you the rain in yet three months [were] to the harvest and I sent rain on a city one and on a city one not I sent rain a portion of ground one it was rained on and a portion of ground which not it sent rain on it it dried up.
8 Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
And they staggered two three cities to a city one to drink water and not they were satisfied and not you returned to me [the] utterance of Yahweh.
9 “Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I struck you with blight and with mildew to make many gardens your and vineyards your and fig trees your and olive trees your it ate the locust and not you returned to me [the] utterance of Yahweh.
10 “Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I sent among you pestilence in [the] manner of Egypt I killed by the sword young men your with [the] capture of horses your and I caused to go up [the] stench of camp your in nose your and not you returned to me [the] utterance of Yahweh.
11 “Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
I overthrew among you like [the] overthrow of God Sodom and Gomorrah and you were like a piece of firewood plucked out (from [the] burning *L(abh)*) and not you returned to me [the] utterance of Yahweh.
12 “Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
Therefore thus I will do to you O Israel consequence for this I will do to you be prepared to meet God your O Israel.
13 Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.
For here! [one who] formed mountains and [one who] created wind and [one who] tells to humankind what? [is] thought his [one who] makes dawn darkness and [one who] treads on [the] high places of [the] earth [is] Yahweh God of hosts name his.

< Amosi 4 >