< Yoweli 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
[the] word of Yahweh which it came to Joel [the] son of Pethuel.
2 Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Hear this O elders and give ear O all [the] inhabitants of the land ¿ has it happened this in days your and or? in [the] days of ancestors your.
3 Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
On it to children your recount and children your to children their and children their to a generation another.
4 Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
[the] remainder of The locust[s] it has eaten the locust[s] and [the] remainder of the locust[s] it has eaten the locust[s] and [the] remainder of the locust[s] it has eaten the locust[s].
5 Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Awake O drunkards and weep and wail O all drinkers of wine on sweet wine for it has been cut off from mouth your.
6 Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
For a nation it has come up on land my mighty and there not [is] number teeth its [are the] teeth of a lion and [the] fangs of a lioness [belong] to it.
7 Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
It has made vine[s] my into a waste and fig tree[s] my into a stump completely it has stripped bare it and it has thrown [it] away they have become white branches its.
8 Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Wail like a virgin girded of sackcloth on [the] husband of youth her.
9 Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
It has been cut off grain offering and drink offering from [the] house of Yahweh they are in mourning the priests [the] servants of Yahweh.
10 Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
It is devastated [the] field[s] it is dried up [the] ground for it is devastated [the] grain it has dried up [the] new wine it has dried out [the] fresh oil.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
Be ashamed O farmers wail O vinedressers on [the] wheat and on [the] barley for it has perished [the] harvest of [the] field.
12 Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
The vine it has dried up and the fig tree it has dried out [the] pomegranate tree also [the] palm tree and [the] apple tree all [the] trees of the field they have dried up for it has been ashamed joy from [the] children of humankind.
13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
Gird yourselves and lament O priests wail O servants of [the] altar come spend [the] night in sackcloth O servants of God my for it has been withheld from [the] house of God your grain offering and drink offering.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
Consecrate a fast call an assembly gather [the] elders all [the] inhabitants of the land [the] house of Yahweh God your and cry out to Yahweh.
15 Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
Alas! for the day for [is] near [the] day of Yahweh and like devastation from [the] Almighty it will come.
16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
¿ Not before eyes our food has it been cut off from [the] house of God our joy and rejoicing.
17 Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
They have shriveled [the] seeds under shovels their they are desolate [the] storehouses they have been torn down [the] granaries for it has dried up [the] grain.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
How! it has groaned [the] livestock they have wandered in confusion [the] herds of cattle for not pasture [belongs] to them also [the] flocks of sheep they have suffered.
19 Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
To you O Yahweh I call for fire it has consumed [the] pastures of [the] wilderness and a flame it has set ablaze all [the] trees of the field.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.
Also [the] animals of [the] field it pants to you for they have dried up [the] channels of water and fire it has consumed [the] pastures of the wilderness.

< Yoweli 1 >