< Machitidwe a Atumwi 4 >

1 Pamene Petro ndi Yohane amayankhula ndi anthu, kunabwera ansembe, mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu ndiponso Asaduki.
Kwathi besakhuluma ebantwini, abapristi lenduna yethempeli labaSadusi babafikela,
2 Iwo anakhumudwa kwambiri chifukwa atumwiwo amaphunzitsa anthu ndi kumalalikira za kuuka kwa akufa mwa Yesu.
benengekile ngoba babefundisa abantu, njalo betshumayela ukuvuka kwabafileyo ngoJesu.
3 Iwo anagwira Petro ndi Yohane, popeza kunali kutada, anawayika mʼndende mpaka mmawa mwake.
Babadumela ngezandla, babafaka esitokisini kwaze kwaba kusisa; ngoba kwasekuhlwile.
4 Koma anthu ambiri amene anamva uthenga anakhulupirira, ndipo chiwerengero cha anthu chinakwana 5,000.
Kodwa abanengi abalizwayo ilizwi bakholwa; lenani lamadoda lalingaba zinkulungwane ezinhlanu.
5 Mmawa mwake olamulira, akulu ndi aphunzitsi a malamulo anasonkhana mu Yerusalemu.
Kwasekusithi kusisa kwabuthana ababusi labadala lababhali babo eJerusalema,
6 Panali Anasi, Mkulu wa ansembe, Kayafa, Yohane ndi Alekisandro ndi ana a banja la mkulu wa ansembe.
loAnasi umpristi omkhulu, loKayafasi, loJohane, loAleksandro, labo bonke abendlu yompristi omkhulu.
7 Iwo anayimiritsa Petro ndi Yohane patsogolo pawo nayamba kuwafunsa kuti, “Kodi munachita zimenezi ndi mphamvu yanji kapena mʼdzina la yani?”
Sebebamise phakathi, babuza: Lokhu lina likwenze ngawaphi amandla kumbe ngaliphi ibizo?
8 Petro wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anawawuza kuti, “Inu olamulira ndi akulu!
Khona uPetro egcwaliswe nguMoya oNgcwele wathi kubo: Babusi babantu labadala bakoIsrayeli,
9 Ngati ife tikufunsidwa lero chifukwa cha ntchito yabwino imene yachitika pa munthu wolumala miyendo ndi mmene iye anachiritsidwira,
nxa thina sibuzwa lamuhla ngomsebenzi omuhle emuntwini obuthakathaka emzimbeni, ukuthi yena usiliswe ngani;
10 tsono dziwani izi inu ndi aliyense mu Israeli: munthuyu akuyima pamaso panu, wochiritsidwa kwathunthu, ndi chifukwa cha dzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti amene munamupachika koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa.
kakwaziwe yini lonke laso sonke isizwe sakoIsrayeli, ukuthi ngebizo likaJesu Kristu umNazaretha, lina elambethelayo, uNkulunkulu owamvusayo kwabafileyo, ngaye lo umi lapha phambi kwenu esesilile.
11 Iye ndi “‘Mwala umene amisiri omanga nyumba anawukana, umenewo wasanduka mwala wa pa ngodya!’
Yena lo uyilitshe elaliwa yini abakhi, eseliyinhloko yengonsi.
12 Chipulumutso sichipezeka mwa wina aliyense; pakuti palibe dzina lina pansi pa thambo limene lapatsidwa kwa anthu limene tiyenera kupulumutsidwa nalo.”
Njalo kalukho usindiso komunye; ngoba kalikho lelinye ibizo ngaphansi kwezulu elinikiweyo phakathi kwabantu, esimele sisindiswe ngalo.
13 Ataona kulimba mtima kwa Petro ndi Yohane ndi kuzindikira kuti anali osaphunzira, anthu wamba, anadabwa kwambiri ndipo anazindikira kuti anthuwa anakhala pamodzi ndi Yesu.
Kwathi bebona isibindi sikaPetro loJohane, njalo besazi ukuthi babengabantu abangafundanga njalo bengabantu nje, bamangala, njalo babazi ukuthi babeloJesu,
14 Koma popeza iwo amamuona munthu amene anachiritsidwa atayima pamodzi ndi iwo, palibe chimene akananena.
kodwa bebona umuntu osilisiweyo emi labo, babengelakuphika lutho.
15 Chifukwa chake anawalamula kuti atuluke mʼbwalo la milandu ndipo akulu abwalowo anayamba kukambirana.
Kodwa sebebalayile ukuthi baphume phandle emphakathini, bacebisana bodwa,
16 Iwo anafunsana kuti, “Kodi anthuwa tichite nawo chiyani? Pakuti aliyense okhala mu Yerusalemu akudziwa kuti achita chodabwitsachi, ndipo ife sitingathe kukana.
besithi: Sizabenzani lababantu? Ngoba ukuthi isibonakaliso esidumisekayo senziwa yibo, kusobala kubo bonke abahlezi eJerusalema, njalo singekuphike;
17 Koma kuti mbiriyi isapitirire kuwanda pakati pa anthu, ife tiwachenjeze anthu amenewa kuti asayankhulenso kwa wina aliyense mʼdzina la Yesu.”
kodwa ukuze kungabe kusanda phakathi kwabantu, asibaqonqosele ukuthi bangabe besakhuluma lamuntu ngalelibizo.
18 Pamenepo anawayitananso ndipo anawalamula kuti asayankhule kapena kuphunzitsa konse mʼdzina la Yesu.
Basebebabiza, babalaya ukuthi bangakhulumi lakanye njalo bangafundisi ngebizo likaJesu.
19 Koma Petro ndi Yohane anayankha kuti, “Weruzani nokha ngati nʼkwabwino pamaso pa Mulungu kumvera inu koposa Mulungu.
Kodwa uPetro loJohane babaphendula bathi: Yehlukanisani ukuthi kulungile phambi kukaNkulunkulu ukulalela lina kuloNkulunkulu.
20 Ife sitingaleke kuyankhula za zimene tinaziona ndi kuzimva.”
Ngoba thina kasilakuyekela ukukhuluma izinto esizibonileyo lesizizwileyo.
21 Atawonjeza kuwaopseza anawamasula. Sanathe kugwirizana njira yowalangira, chifukwa anthu onse amayamika Mulungu chifukwa cha zimene zinachitika.
Kwathi sebebaqonqosele futhi, babayekela bahamba; bengatholi lutho lokuthi bangabajezisa njani, ngenxa yabantu, ngoba bonke badumisa uNkulunkulu ngalokho okwenzakeleyo.
22 Ndipo munthu amene anachiritsidwayo anali ndi zaka makumi anayi.
Ngoba umuntu wayeleminyaka edlula amatshumi amane esenziwa kuye lesisibonakaliso seselapho.
23 Atamasulidwa Petro ndi Yohane anapita kwa anzawo ndipo anawafotokozera zonse zimene akulu a ansembe ndi akulu anawawuza.
Kwathi sebeyekelwe basuka baya kwabakibo, bababikela konke abapristi abakhulu labadala abakutshiloyo kubo.
24 Anthu atamva zimenezi anafuwula ndi mtima umodzi napemphera kwa Mulungu. Iwo anati, “Ambuye wolamulira zonse, Inu munalenga kumwamba ndi dziko lapansi ndi nyanja ndiponso zonse zili mʼmenemo.
Kwathi bona sebezwile baphakamisela ilizwi nganhliziyonye kuNkulunkulu, bathi: Nkosi, wena unguNkulunkulu owenza izulu lomhlaba lolwandle lakho konke okukukho;
25 Inu munayankhula mwa Mzimu Woyera kudzera pakamwa pa Davide kholo lathu, mtumiki wanu kuti, “‘Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu, ndipo akonzekera kuchita zopandapake?
owathi ngomlomo wenceku yakho uDavida: Kungani abezizwe bexokozela, labantu banakane okuyize?
26 Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo; ndipo olamulira asonkhana pamodzi kulimbana ndi Ambuye ndi wodzozedwa wakeyo.’
Amakhosi omhlaba ema, lababusi bahlangana ndawonye ukumelana leNkosi, lokumelana loGcotshiweyo wayo;
27 Zoonadi, Herode ndi Pontiyo Pilato anasonkhana pamodzi ndi amitundu ndiponso Aisraeli, mu mzinda muno, kupanga zolimbana ndi mtumiki wanu woyera Yesu, amene Inu munamudzoza.
ngoba isibili bahlangana ndawonye bemelane leNdodana yakho engcwele uJesu, owayigcobayo, bonke uHerodi loPontiyusi Pilatu, kanye labezizwe labantu bakoIsrayeli,
28 Iwo anachita zimene munakonzeratu mwachifuniro chanu ndi mphamvu yanu kuti zichitike.
ukwenza konke isandla sakho lecebo lakho elakumisa phambili ukuthi kwenzeke.
29 Tsopano, Ambuye taonani kuti atiopseza, tithandizeni ife atumiki anu, kuti tiyankhule mawu anu molimba mtima.
Njalo ngalesisikhathi, Nkosi, khangela ukusonga kwabo, unike izinceku zakho ukuthi zikhulume ilizwi lakho ngesibindi sonke,
30 Tambasulani dzanja lanu kuchiritsa anthu ndipo kuti, zizindikiro zodabwitsa zichitike mʼdzina la mtumiki wanu woyera Yesu.”
ngokuthi welule isandla sakho ukusilisa, lokuthi kwenziwe izibonakaliso lezimangaliso ngebizo leNdodana yakho engcwele uJesu.
31 Iwo atatha kupemphera, malo amene anasonkhanapo anagwedezeka. Ndipo iwo onse anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo anayankhula Mawu a Mulungu molimba mtima.
Kwathi sebekhulekile kwazanyazanyiswa indawo ababebuthene kuyo, basebegcwaliswa bonke ngoMoya oNgcwele, basebekhuluma ilizwi likaNkulunkulu ngesibindi.
32 Okhulupirira onse anali a mtima umodzi, ndi maganizo amodzi. Palibe munthu amene amati zomwe anali nazo zinali zake zokha, koma amagawana chilichonse chimene anali nacho.
Lexuku labakholwayo lalinhliziyonye lomoya munye; njalo kungekho oyedwa owathi ezintweni alazo ngezakhe, kodwa bahlanganyela izinto zonke.
33 Atumwi anapitirira kuchitira umboni mwa mphamvu zakuuka kwa Ambuye Yesu, ndipo pa iwo panali chisomo chochuluka.
Langamandla amakhulu abaphostoli baveza ubufakazi bokuvuka kweNkosi uJesu, lomusa omkhulu waba phezu kwabo bonke.
34 Panalibe anthu osowa kanthu pakati pawo. Pakuti amene anali ndi malo, kapena nyumba amagulitsa ndi kubweretsa ndalamazo
Ngoba kwakungekho futhi oswelayo phakathi kwabo; ngoba bonke ababengabanikazi bemihlaba kumbe izindlu, bathengisa baletha intengo zalokho okuthengisiweyo,
35 ndi kuzipereka kwa atumwi, ndipo zimagawidwa kwa aliyense amene anali ndi chosowa.
bayibeka enyaweni zabaphostoli; njalo kwabelwa ngulowo lalowo njengokuswela kwakhe.
36 Yosefe, wa fuko la Levi, wochokera ku Kupro amene atumwi anamutcha Barnaba, kutanthauza kuti mwana wachilimbikitso,
Kwathi uJose owabizwa ngabaphostoli ngokuthi nguBarnabasi, okuyikuthi ngokuphendulelwa, indodana yenduduzo, umLevi, umKuprosi ngokuzalwa,
37 anagulitsa munda wake ndipo anadzapereka ndalamazo kwa atumwi.
elesiqinti, wasithengisa, waletha imali, wayibeka enyaweni zabaphostoli.

< Machitidwe a Atumwi 4 >