< Machitidwe a Atumwi 3 >

1 Tsiku lina Petro ndi Yohane ankapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera nthawi ya 3 koloko masana.
UPetro loJohane basebesenyukela bonke ethempelini ngehola lomkhuleko elesificamunwemunye.
2 Ndipo munthu wolumala chibadwire ankanyamulidwa tsiku ndi tsiku kukayikidwa pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola kuti azikapempha amene amalowa ku bwalo la Nyumbayo.
Kwasekuthwalwa indoda ethile eyayiyisiqhuli kusukela esizalweni sikanina; ababeyibeka insuku ngensuku esangweni lethempeli elithiwa eLihle, ukuthi icele isipho kulabo abangenayo ethempelini.
3 Ataona Petro ndi Yohane ali pafupi kulowa anawapempha ndalama.
Eyathi ibona uPetro loJohane sebezangena ethempelini, yacela isipho.
4 Iwo anamuyangʼanitsitsa iye. Kenaka Petro anati, “Tiyangʼane!”
UPetro waseyijolozela eloJohane, wathi: Sikhangele!
5 Munthuyo anawayangʼanitsitsa kuyembekezera kuti alandira kanthu kuchokera kwa iwo.
Yasibananzelela, ilindele ukuthi izakwemukela ulutho kubo.
6 Petro anati kwa iye, “Ine ndilibe siliva kapena golide, koma chimene ndili nacho ndikupatsa. Mʼdzina la Yesu Khristu wa ku Nazareti, yenda.”
UPetro wasesithi: Isiliva legolide kangilakho; kodwa lokho engilakho, ngikunika khona; ebizweni likaJesu Kristu umNazaretha, sukuma uhambe.
7 Ndipo anamugwira dzanja lamanja, namuthandiza kuti ayimirire ndipo nthawi yomweyo mapazi ake ndi akakolo ake analimba.
Waseyibamba ngesandla sokunene wayisukumisa; njalo kwahle kwaqiniswa inyawo lenqagala zayo.
8 Iye analumpha ndi kuyamba kuyenda. Kenaka analowa nawo pamodzi mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, akuyenda ndi kulumpha ndiponso kuyamika Mulungu.
Yasisithi lothu yema yasihamba, yangena labo ethempelini, ihamba iseqa idumisa uNkulunkulu.
9 Anthu onse atamuona akuyenda ndiponso kuyamika Mulungu,
Njalo bonke abantu bayibona ihamba, idumisa uNkulunkulu;
10 anamuzindikira kuti ndi yemwe uja ankakhala pa khomo la Nyumbayo lotchedwa Khomo Lokongola, ndipo anazizwa ndi kudabwa ndi zimene zinamuchitikira.
basebeyazi ukuthi yiyo eyayihlalela isipho esangweni eLihle lethempeli; basebegcwala ukumangala lokusanganiseka ngalokho okwenzeka kuyo.
11 Wopempha uja akuyenda pamodzi ndi Petro ndi Yohane, anthu onse anadabwa ndipo anawathamangira iwo kumalo wotchedwa Khonde la Solomoni.
Kwathi isiqhuli esasisilisiwe sibambelele kuPetro loJohane, bonke abantu bagijimela kubo ndawonye ekhulusini elithiwa elikaSolomoni, bemangala kakhulu.
12 Petro ataona zimenezi anawawuza kuti, “Inu Aisraeli, chifukwa chiyani mukudabwa ndi zimene zachitikazi? Bwanji mukuyangʼana ife ngati kuti tamuyendetsa munthuyu ndi mphamvu yathu kapena chifukwa cha kupembedza kwathu?
Kwathi uPetro ekubona lokho waphendula ebantwini wathi: Madoda maIsrayeli, limangalelani ngalokhu, kumbe lisijolozelelani, ngokungathi ngawethu amandla kumbe ukulunga simenze ukuthi lo ahambe?
13 Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, Mulungu wa makolo athu, wamulemekeza mtumiki wake Yesu. Amene inu munamukana pamaso pa Pilato ndi kumupereka Iye kuti aphedwe, ngakhale kuti Pilato anafuna kuti amumasule.
UNkulunkulu kaAbrahama lokaIsaka lokaJakobe, uNkulunkulu wabobaba bethu, uyidumisile iNdodana yakhe uJesu; elayinikelayo lina, layiphika phambi kobuso bukaPilatu, yena esequme ukuyikhulula.
14 Koma inu munamukana Woyera ndi Wolungamayo ndipo munapempha kuti akumasulireni munthu wakupha anthu.
Kodwa lina lamphika oNgcwele loLungileyo, lacela ukuthi liphiwe indoda engumbulali,
15 Inu munapha mwini moyo, koma Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Ife ndife mboni za zimenezi.
labulala uMqali wempilo; amvusayo uNkulunkulu kwabafileyo, esingabafakazi bakho thina.
16 Mwachikhulupiriro mʼdzina la Yesu, munthu uyu amene mukumuona ndi kumudziwa analimbikitsidwa. Mʼdzina la Yesu ndi chikhulupiriro chimene chili mwa iye chamuchiritsa kwathunthu, monga nonse mukuona.
Njalo ngokholo ebizweni lakhe, lo elimbonayo lelimaziyo ibizo lakhe limqinisile; lokholo olungaye lumnike lokhukusila okupheleleyo phambi kwenu lonke.
17 “Tsopano abale ine ndikudziwa kuti inu munachita zimenezi mosadziwa, monga momwenso anachitira atsogoleri anu.
Njalo khathesi, bazalwane, ngiyazi ukuthi lakwenza ngokungazi, njengababusi benu futhi.
18 Koma umu ndi mmene Mulungu anakwaniritsira zimene zinanenedwa kale ndi aneneri onse, kuti Khristu adzamva zowawa.
Kodwa uNkulunkulu wagcwalisa ngokunjalo lokhu akukhuluma phambili ngomlomo wabaprofethi bakhe bonke, ukuthi uKristu uzahlupheka.
19 Chifukwa chake, lapani, bwererani kwa Mulungu, kuti machimo anu afafanizidwe, kuti nthawi ya kutsitsimuka ibwere kuchokera kwa Ambuye,
Ngakho phendukani libuye futhi, ukuze kwesulwe izono zenu, ukuze kufike izikhathi zokukhudumala ezivela ebusweni beNkosi,
20 ndi kuti Iye atumize Yesu Khristu amene anasankhidwa chifukwa cha inu.
njalo ithume lo owamenyezelwa kini phambili, uJesu Kristu;
21 Iye ayenera kukhalabe kumwamba mpaka nthawi ya kukonzanso zinthu zonse monga Mulungu analonjeza kale kudzera mwa aneneri ake oyera mtima. (aiōn g165)
okumele ukuthi izulu limemukele kuze kufike izikhathi zokubuyisela konke, uNkulunkulu akutshoyo ngomlomo wabo bonke abaprofethi bakhe abangcwele endulo. (aiōn g165)
22 Pakuti Mose anati, ‘Ambuye Mulungu wanu adzakuukitsirani mneneri monga ine kuchokera pakati pa anthu anu; mumvere zonse zimene iye akuwuzeni.
Ngoba uMozisi wathi kubobaba: INkosi uNkulunkulu wenu izalivusela umprofethi kubazalwane benu onjengami; yena lizamlalela kukho konke azakukhuluma kini.
23 Aliyense amene sadzamvera mawu a mneneriyo, adzayenera kuchotsedwa pakati pa abale ake.’
Njalo kuzakuthi, wonke umphefumulo, loba ngubani ongayikumlalela lowomprofethi, uzachithwa ebantwini.
24 “Ndipo aneneri onse ambiri amene anayankhula kuyambira Samueli, ananeneratu za masiku ano.
Njalo labaprofethi bonke, kusukela kuSamuweli labalandelayo, bonke abakhulumayo, bamemezela phambili lezinsuku.
25 Inu ndinu ana a aneneri ndiponso ana apangano limene Mulungu anachita ndi makolo anu. Iye anati kwa Abrahamu, ‘Anthu onse a pa dziko lapansi adzadalitsika kudzera mwa zidzukulu zako.’
Lina lingabantwana babaprofethi, labesivumelwano uNkulunkulu asenza labobaba bethu, esithi kuAbrahama: Langenzalo yakho zizabusiswa zonke izizukulwana zomhlaba.
26 Pamene Mulungu anaukitsa mtumiki wake, anamutuma Iye poyamba kwa inu kuti akudalitseni pobweza aliyense wa inu ku zoyipa zake.”
UNkulunkulu, eseyivusile iNdodana yakhe uJesu, wayithuma kini kuqala ukulibusisa, ngokuliphendula ngulowo lalowo ebubini bakhe.

< Machitidwe a Atumwi 3 >