< Machitidwe a Atumwi 22 >

1 Iye anati, “Inu abale anga ndi makolo anga, tamvani mawu akudziteteza kwanga.”
« Frères et pères, écoutez la défense que je vous fais maintenant. »
2 Atamva iye akuyankhula Chihebri, anakhala chete. Kenaka Paulo anati,
Lorsqu'ils entendirent qu'il leur parlait en langue hébraïque, ils furent encore plus silencieux. Il dit:
3 “Ine ndine Myuda, wobadwira ku Tarisisi wa ku Kilikiya, koma ndinaleredwa mu mzinda muno, ndinaphunzitsidwa mwatsatanetsatane kusunga malamulo a makolo athu ndi Gamalieli ndipo ndinali wodzipereka pa za Mulungu monga mmene inu mulili lero.
« Je suis vraiment Juif, né à Tarse en Cilicie, mais élevé dans cette ville aux pieds de Gamaliel, instruit selon la stricte tradition de la loi de nos pères, zélé pour Dieu, comme vous l'êtes tous aujourd'hui.
4 Ine ndinkazunza anthu otsatira Njirayi mpaka kuwapha. Ndinkagwira amuna ndi amayi ndi kuwayika mʼndende.
J'ai persécuté cette voie jusqu'à la mort, liant et livrant en prison hommes et femmes,
5 Mkulu wa ansembe ndiponso akuluakulu a Ayuda angathe kundichitira umboni. Iwowa anandipatsa makalata opita nawo kwa abale awo ku Damasiko. Ndipo ndinapita kumeneko kuti ndikawagwire anthu amenewa ndi kubwera nawo ku Yerusalemu kuti adzalangidwe.
comme en témoignent le souverain sacrificateur et tout le conseil des anciens, de qui j'ai aussi reçu des lettres pour les frères, et je me suis rendu à Damas pour amener à Jérusalem ceux qui s'y trouvaient, liés pour être punis.
6 “Nthawi ya masana, nditayandikira ku Damasiko, mwadzidzidzi kuwala kwakukulu kochokera kumwamba kunandizungulira.
« Comme je faisais route et que j'approchais de Damas, vers midi, une grande lumière jaillit soudain du ciel autour de moi.
7 Ndinagwa pansi ndipo ndinamva mawu akuti, ‘Saulo! Saulo! Ukundizunziranji?’”
Je tombai à terre et j'entendis une voix qui me disait: « Saul, Saul, pourquoi me persécutes-tu? »
8 Ine ndinafunsa kuti, “Ndinu ndani Ambuye?” Iye anayankha kuti, “Ndine Yesu wa ku Nazareti, amene iwe ukumuzunza.”
Je répondis: « Qui es-tu, Seigneur? » Il me dit: « Je suis Jésus de Nazareth, que tu persécutes.
9 Anzanga a paulendo anaona kuwalako, koma sanamve mawuwo, a Iye amene amayankhula nane.
Ceux qui étaient avec moi virent la lumière et eurent peur, mais ils ne comprirent pas la voix de celui qui me parlait.
10 Ine ndinafunsa kuti, “Kodi ndichite chiyani Ambuye?” Ambuye anati, “Imirira ndipo pita ku Damasiko. Kumeneko adzakuwuza zonse zimene ukuyenera kuchita.”
Je disais: Que dois-je faire, Seigneur? Le Seigneur me répondit: 'Lève-toi, et va à Damas. Là, tu seras informé de tout ce qui t'est prescrit.
11 Anzanga anandigwira dzanja kupita nane ku Damasiko, popeza kuwala kunja kunandichititsa khungu.
Comme je ne pouvais pas voir à cause de la gloire de cette lumière, étant conduit par la main de ceux qui étaient avec moi, j'entrai dans Damas.
12 “Munthu wina dzina lake Hananiya anabwera kudzandiona. Iyeyu anali munthu woopa Mulungu ndi wosunga Malamulo. Ayuda onse okhala kumeneko amamupatsa ulemu waukulu.
Un certain Ananias, homme pieux selon la loi, bien connu de tous les Juifs qui habitaient Damas,
13 Iye anayimirira pafupi nane nati, ‘Mʼbale Saulo, penyanso!’ Ndipo nthawi yomweyo ndinapenya ndikumuona iyeyo.
vint vers moi, et, se tenant près de moi, il me dit: « Frère Saul, recouvre la vue. A l'heure même, je levai les yeux vers lui.
14 “Ndipo iye anati, ‘Mulungu wa makolo athu wakusankha iwe kuti udziwe chifuniro chake ndi kuona Wolungamayo ndi kumva mawu ochokera pakamwa pake.
Il dit: « Le Dieu de nos pères t'a destiné à connaître sa volonté, à voir le Juste et à entendre la voix de sa bouche.
15 Iwe udzakhala mboni yake kwa anthu onse pa zimene waziona ndi kuzimva.
Car tu seras pour lui le témoin devant tous les hommes de ce que tu as vu et entendu.
16 Ndipo tsopano ukudikira chiyani? Dzuka ndi kutama dzina la Ambuye mopemba, ubatizidwe ndi kuchotsa machimo ako.’
Maintenant, pourquoi attendez-vous? Lève-toi, sois baptisé, et lave-toi de tes péchés, en invoquant le nom du Seigneur'.
17 “Nditabwerera ku Yerusalemu, ndikupemphera mʼNyumba ya Mulungu, ndinachita ngati ndakomoka.
« Lorsque je fus de retour à Jérusalem et que je priais dans le temple, je tombai en transe
18 Ndinaona Ambuye akundiwuza kuti, ‘Fulumira! Tuluka mu Yerusalemu msangamsanga, chifukwa anthuwa sadzavomereza umboni wako wonena za Ine.’”
et je le vis qui me disait: « Dépêche-toi de sortir de Jérusalem, car ils ne veulent pas recevoir de toi le témoignage qui me concerne.
19 Ine ndinayankha Ambuye kuti, “Anthu awa akudziwa kuti ine ndinkapita ku sunagoge iliyonse ndipo ndinkawaponya mʼndende ndi kuwakwapula amene ankakhulupirira inu.
Je lui répondis: « Seigneur, ils savent eux-mêmes que j'ai emprisonné et battu dans toutes les synagogues ceux qui croyaient en toi.
20 Ndipo pamene ankapha Stefano, ine ndinali pomwepo kuvomereza ndi kusunga zovala za amene amamupha.”
Et quand le sang d'Étienne, ton témoin, a été versé, j'étais là, moi aussi, à consentir à sa mort et à garder les manteaux de ceux qui l'ont tué.
21 Pamenepo Ambuye anandiwuza kuti, “Nyamuka; Ine ndidzakutuma kutali kwa anthu a mitundu ina.”
« Il me dit: 'Va-t'en, car je t'enverrai loin d'ici vers les païens'. »
22 Gulu la anthu linamvetsera mawu a Paulo mpaka pamene ananena izi, kenaka anakweza mawu awo nafuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi! Ngosayenera kukhala moyo!”
Ils l'ont écouté jusqu'à ce qu'il dise cela, puis ils ont élevé la voix et ont dit: « Débarrassez la terre de cet homme, car il n'est pas digne de vivre. »
23 Akufuwula ndi kuponya zovala zawo ndi kuwaza fumbi kumwamba,
Comme ils poussaient des cris, jetaient leurs manteaux et lançaient de la poussière en l'air,
24 mkulu wa asilikali analamulira kuti amutenge Paulo kupita naye ku malo a asilikali. Iye analamula kuti Paulo akwapulidwe kwambiri ndi kumufunsa kuti apeze chimene anthu ankafuwulira chotere.
le tribun ordonna de le faire entrer dans la caserne, et de le faire examiner par la flagellation, afin de savoir pour quel crime ils criaient ainsi contre lui.
25 Atamumanga kuti amukwapule, Paulo anati kwa msilikali wolamulira asilikali 100 amene anayima pamenepo, “Kodi malamulo amalola kukwapula nzika ya Chiroma imene sinapezedwe yolakwa?”
Lorsqu'ils l'eurent attaché avec des lanières, Paul demanda au centurion qui se tenait là: « Vous est-il permis de flageller un homme qui est romain et qui n'a pas été déclaré coupable? »
26 Wolamulira asilikali 100 uja atamva zimenezi, anapita kwa mkulu wa asilikali ndi kumufotokozera. Iye anafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani ndi munthuyu amene ndi nzika ya Chiroma?”
Le centurion, ayant entendu cela, alla trouver le commandant et lui dit: « Fais attention à ce que tu vas faire, car cet homme est un Romain! »
27 Mkulu wa asilikali uja anapita kwa Paulo ndipo anamufunsa kuti, “Tandiwuze, kodi ndiwe nzika ya Chiroma?” Paulo anayankha kuti, “Inde.”
Le commandant vint et lui demanda: « Dis-moi, es-tu un Romain? » Il a dit: « Oui. »
28 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anati, “Ine ndinapereka ndalama zambiri kuti ndikhale nzika.” Paulo anayankha kuti, “Koma ine ndinabadwa nzika.”
Le commandant répondit: « J'ai acheté ma citoyenneté à un grand prix. » Paul a dit: « Mais je suis né romain. »
29 Iwo amene anati amufunse analeka nthawi yomweyo. Mkulu wa asilikali uja anachita mantha atazindikira kuti wamanga Paulo amene ndi nzika ya Chiroma.
Aussitôt, ceux qui allaient l'interroger s'éloignèrent de lui, et le tribun eut aussi peur lorsqu'il s'aperçut que c'était un Romain, car il l'avait fait lier.
30 Mmawa mwake, mkulu wa asilikali pofuna kupeza chifukwa chenicheni chimene Ayuda amamunenera Paulo, anamumasula ndipo analamula kuti akulu a ansembe ndi onse akuluakulu a Bwalo Lalikulu asonkhane. Ndipo iye anabweretsa Paulo namuyimiritsa patsogolo pawo.
Mais le lendemain, désireux de connaître la vérité sur les raisons pour lesquelles il était accusé par les Juifs, il le libéra des liens et ordonna aux chefs des prêtres et à tout le conseil de se réunir, de faire descendre Paul et de le faire comparaître devant eux.

< Machitidwe a Atumwi 22 >