< Machitidwe a Atumwi 21 >
1 Titalawirana nawo, tinachoka kumeneko mʼsitima ya pamadzi, ndipo tinayenda molunjika mpaka kufika ku Kosi. Mmawa mwake tinapita ku Rode, kuchokera kumeneko tinapita ku Patara.
Nuuni Efesoona cimatappe shaakettida mela Qoose bida. Wonttetha gallas Rooda gakkidi yaappe Phaxara bida.
2 Kumeneko tinapeza sitima yapamadzi yopita ku Foinike. Choncho tinalowamo nʼkunyamuka.
Finqqe pinniya markkabie demmidi iyan gelidi baanaw denddida.
3 Tinaona chilumba cha Kupro ndipo tinadutsa kummwera kwake nʼkupita ku Siriya. Tinakayima ku Turo chifukwa sitima yathuyo imayenera kusiya katundu kumeneko.
Nuuni Qoophirosa be7anaw dandda7iya soo yidi, Qoophirosa haddirssa bagga aggidi Sooriya bida. Markkabey ba caanaa yan wothanaw koyida gisho Xiiroosa bida.
4 Tinafunafuna ophunzira kumeneko, ndipo titawapeza tinakhala nawo masiku asanu ndi awiri. Iwowa, mwa Mzimu Woyera anakakamiza Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
Yan ammaniyaa asata demmidi enttara laappun gallas uttida. Phawuloosi Yerusalaame boonna mela entti iyaw Ayyaanan odidosona.
5 Koma nthawi yathu itatha, tinachokako ndi kupitiriza ulendo wathu. Ophunzira onse pamodzi ndi akazi awo ndi ana anatiperekeza mpaka kunja kwa mzinda. Ndipo kumeneko tinagwada mʼmbali mwa nyanja ndi kupemphera.
Nuuni enttara uttiya wodey wurin keyidi bida. Entti ubbay bantta maccasataranne bantta naytara issife katamaappe kare kessidi nuna moyzidosona. Nuuni abbaa doonan gulbbatidi Xoossaa woossida.
6 Titatsanzikana, tinalowa mʼsitima ija, iwowo anabwerera ku nyumba zawo.
Hessafe guye, woli sarothidi nu markkabiyan gelida; entti bantta soo simmidosona.
7 Ife tinapitiriza ulendo wathu wochokera ku Turo mpaka tinafika ku Ptolemayi. Kumeneko tinalonjera abale ndi kukhala nawo tsiku limodzi.
Nuuni abbaa ogiya onggidi, Xiiroosappe Phexelemaysa gakkida. Yan ammaniyaa asata sarothidi, entta matan issi gallas pee7ida.
8 Tinachoka mmawa mwake, mpaka tinakafika ku Kaisareya. Tinapita kukakhala mʼnyumba ya mlaliki Filipo, amene anali mmodzi mwa atumiki a mpingo asanu ndi awiri aja.
Wonttetha gallas keyidi, Qisaariya bida. Sabaakiya Filiphphoosa soo gakkidi iya matan uttida. I Yerusalaamen kase doorettida laappunatappe issuwa.
9 Iye anali ndi ana aakazi anayi osakwatiwa amene anali ndi mphatso ya uneneri.
Filiphphoosas nabe gidida oyddu geela7o nayti de7oosona.
10 Titakhala kumeneko masiku ambiri, kunabwera mneneri wina wochokera ku Yudeya dzina lake Agabu.
Nuuni unddenna gallas yan uttidi de7ishin tinbbite odiya issi Agaboosa giya addey Yihudappe Qisaariya yis.
11 Atafika kwa ife, anatenga lamba wa Paulo, nadzimanga naye manja ake ndi mapazi ake ndipo anati, “Mzimu Woyera akuti, ‘Mwini lambayu, Ayuda adzamumanga chomwechi ku Yerusalemu, ndipo adzamupereka mʼmanja mwa anthu a mitundu ina.’”
Nuukko yidi Phawuloosa saqqiya ekkidi ba kushiyanne ba tohuwa qachchidi, “Geeshsha Ayyaanay ha saqqiya godaa, Yerusalaamen Ayhudeti hayssada qachchidi, Ayhude gidonna asaas aathidi immana yaagees” yaagis.
12 Titamva zimenezi, ife pamodzi ndi anthu kumeneko tinamudandaulira Paulo kuti asapite ku Yerusalemu.
Nuuni hessa si7ida wode nunne yan de7iya asati Phawuloosi Yerusalaame boonna mela woossida.
13 Koma Paulo anayankha kuti, “Chifukwa chiyani mukulira ndi kunditayitsa mtima? Ndine wokonzeka osati kumangidwa kokha ayi, komanso kufa ku Yerusalemu chifukwa cha dzina la Ambuye Yesu.”
Shin Phawuloosi zaaridi, “Hintte hayssada yeekkishe ays ta wozanaa shugiseeti? Taani, Godaa Yesuusa sunthaa gisho qashetetha xalaala gidonnashin Yerusalaame hayqqanawukka giigettas” yaagis.
14 Titalephera kumuletsa tinamuleka ndipo tinati, “Chifuniro cha Ambuye chichitike.”
Nu zoriya I ekkenna ixxin, “Godaa sheney hano” yaagidi si7i gida.
15 Pambuyo pake, ife tinakonzeka ndi kunyamuka kumapita ku Yerusalemu.
Yan guutha wode gam77idaappe guye giigettidi Yerusalaame baanaw keyida.
16 Ena mwa ophunzira a ku Kaisareya anatiperekeza mpaka kukatifikitsa ku nyumba ya Mnasoni, kumene tinakonza kuti tizikhalako. Iye anali wa ku Kupro ndiponso mmodzi wa ophunzira oyambirira.
Qisaariyan de7iya ammaniyaa asatappe guuthati nuura bidosona. Entti nuuni shemppanasuwa Minaasona giya Qoophirosa addiya soo efidosona. Minaasoni koyro ammanida asaappe issuwa.
17 Titafika ku Yerusalemu, abale anatilandira mwachimwemwe.
Nuuni Yerusalaame gakkida wode ammaniyaa asati nuna ufayssan mokkidosona.
18 Mmawa mwake Paulo pamodzi ndi ife tonse tinapita kwa Yakobo, ndipo akulu onse a mpingo anali komweko.
Wonttetha gallas Phawuloosinne nuuni Yayqoobara gayttanaw bida. Woosa keethaa cimati ubbatikka yan de7oosona.
19 Paulo anawalonjera ndi kuwafotokozera mwatsatanetsatane zimene Mulungu anachita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mu utumiki wake.
Phawuloosi entta sarothidaappe guye Ayhude gidonna asaa giddon ba baggara Xoossay oothidabaa ubbaa enttaw odis.
20 Atamva zimenezi, iwo anayamika Mulungu. Kenaka anawuza Paulo kuti, “Mʼbale, ukuona kuti pali Ayuda ambirimbiri amene anakhulupirira, ndipo ndi okhulupirika potsatira Malamulo a Mose.
Entti hessa si7ida wode Xoossaa galatidi Phawuloosakko hessada yaagidosona: “Nu ishaw, Ayhudeta giddon aappun mukulati Xoossaa ammanidaakko ne be7aasa; entti ubbayka higgiya minthi naagoosona.
21 Iwo anawuzidwa kuti iwe umaphunzitsa Ayuda onse amene akukhala pakati pa anthu a mitundu ina kuti asiye kutsatira Mose, kuti asamachite mdulidwe kapena kutsatira miyambo.
Neeni Ayhude gidonnayssata biittan de7iya Ayhude ubbay bantta nayta qaxxaronna mela, Ayhudeta wogaa kaallonna melanne Muse higgiya ixxana mela neeni tamaarsseyssa Yerusalaamen de7iya Ayhudeti si7idosona.
22 Nanga pamenepa ife titani? Iwo adzamva ndithu kuti iwe wabwera,
Yaatin aybi lo77o? Neeni yidayssa daroti si7ana.
23 tsono iwe chita zimene ife tikuwuze. Tili nawo amuna anayi pano amene anachita lumbiro kwa Mulungu.
“Hessa gisho, nuuni new odeyssa si7a; gasoy de7iya oyddu asati nu matan de7oosona.
24 Muwatenge anthu amenewa, ndipo muchite nawo mwambo wowayeretsa ndipo muwalipirire zoti apereke kuti amete tsitsi lawo. Kotero aliyense adzadziwa kuti palibe choonadi pa zimene anamva za inu, koma kuti inu mwini mumakhala moyo womvera Malamulo.
Entta ekkada enttara geeya; qassi entti bantta huu7iya meedettana mela enttaw miishe imma. Entti kase nebaa si7idayssi tuma gidonnayssanne neeni ne huu7enkka higge naagiya asi gideyssa ubbay erana.
25 Koma kunena za anthu a mitundu ina amene asandulika okhulupirira, ife tinawalembera zimene tinavomerezana zakuti asadye chakudya choperekedwa ku mafano, asadye magazi, asadye nyama yopotola ndiponso asachite zadama.”
“Shin ammanida Ayhude gidonna asata gidikko, entti eeqas yarshshettidabaa moonna mela, suuthu uyonna mela, bawuta moonna melanne laymatonna mela, nuuni oda qachchidi, enttaw dabddaabbe xaafida” yaagidosona.
26 Mmawa mwake Paulo anatenga amuna aja ndipo anachita mwambo wodziyeretsa. Kenaka anapita ku Nyumba ya Mulungu nakadziwitsa ansembe za tsiku limene adzatsiriza nthawi ya kudziyeretsa ndi kuperekera nsembe aliyense wa iwo.
Hessafe guye, Phawuloosi wonttetha gallas asata ekkidi, enttara geeyis. I bantta geeya gallasay awude polettiyakko erisanawunne bantta yarshshuwa awude yarshshaneekko erisanaw Xoossa Keethi gelis.
27 Ali pafupi kutsiriza masiku asanu ndi awiriwo, Ayuda ena ochokera ku Asiya anaona Paulo mʼNyumba ya Mulungu. Iwo anawutsa gulu lonse la anthu ndipo anamugwira Paulo,
Laappun gallasay wurana hanishin, Iisiyappe yida Ayhudeti Xoossa Keethan Phawuloosa be7idi, asa ubbaa denthethidi Phawuloosa oykkidosona.
28 akufuwula kuti, “Inu Aisraeli, tithandizeni! Ndi uyu munthu uja amaphunzitsa anthu onse ponseponse kuti azinyoza mtundu wathu ndiponso Malamulo athu ndi malo ano. Kuwonjezera pamenepo, walowetsa Agriki mʼbwalo la Nyumba ino ndipo wadetsa malo opatulika.”
“Isra7eele asaw, nuna maaddite; ha uray, nu deriya, nu higgiyanne ha Xoossa Keetha ixxana mela asa ubbaa tamaarssees. Hessika gidonna ixxin Ayhude gidonnayssata Xoossa Keethi gelssidi, ha geeshsha bessaa tunisis” yaagidi waassidosona.
29 Iwo ananena izi chifukwa anali ataona Trofimo wa ku Efeso ali ndi Paulo mu mzindamo ndipo iwo ankaganiza kuti Paulo anamulowetsa mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu.
Entti hessa giday kase Efesoona Xirofimoosa Phawuloosara kataman be7ida gisho ha77i Phawuloosi Xoossa keethi iya ekki gelidabaa enttaw daanis.
30 Mzinda wonse unasokonezeka, ndipo anthu anabwera akuthamanga kuchokera kumbali zonse. Anamugwira Paulo, namukokera kunja kwa Nyumbayo, ndipo nthawi yomweyo anatseka zipata.
Katama ubbay buqettis; asay ubbay shiiqidi Phawuloosa oykkidi Xoossa Keethafe kare goochchidosona. Xoossa Keethaa penggeti ellesidi gorddettidosona.
31 Pamene anthuwo ankafuna kupha Paulo, nkhaniyi inamveka kwa mkulu wa magulu a asilikali a Aroma kuti mzinda wonse wa Yerusalemu wasokonezeka.
Asay Phawuloosa wodhana hanishin, “Yerusalaame katamay kumethi buqettis” giya oday Roome shaalaqaakko gakkis.
32 Nthawi yomweyo iye anatenga asilikali ndi atsogoleri a magulu a asilikali ndi kuthamangira kumene kunali anthuwo. Anthuwo ataona mkuluyo ndi asilikali ake analeka kumenya Paulo.
Shaalaqay wotaaddaretanne mato halaqata ekkidi woxxishe yis. Asay shaalaqaanne wotaaddareta be7ida wode Phawuloosa wadhdheyssa aggaagidosona.
33 Mkulu wa asilikaliyo anabwera nagwira Paulo, ndipo analamula kuti amangidwe ndi maunyolo awiri. Kenaka iye anafunsa kuti ndi ndani ndipo wachita chiyani.
He wode shaalaqay shiiqidi, Phawuloosa oykkidi, nam77u santhalaatan qashettana mela kiittis. Yaatidi, I ooneekkonne ay oothidaakko asaa oychchis.
34 Ena mʼgulumo anafuwula chinthu china ndi enanso chinanso. Tsono popeza mkulu wa asilikaliyo sanathe kudziwa choonadi chenicheni chifukwa cha phokoso, analamula kuti Paulo atengedwe kupita ku malo a asilikali.
Asaappe baggay issibaa gidi waassiya wode, harati harabaa gidi waasses. Waasoy darida gisho, shaalaqay tumaa shaakkanw dandda7ettonna ixxin, wotaaddareti Phawuloosa bantta de7iyaso efana mela kiittis.
35 Paulo atafika pa makwerero olowera ku malo a asilikaliwo, ananyamulidwa ndi asilikali chifukwa cha ukali wa anthuwo.
Phawuloosi yedhdhi keyaa dethaa gakkiya wode asaa sugethaa gisho wotaaddareti iya tookkidosona.
36 Gulu la anthu limene linamutsatira linapitiriza kufuwula kuti, “Ameneyo aphedwe basi!”
Daro asay, “I hayqqo!” yaagidi waassishe kaalloosona.
37 Asilikali ali pafupi kulowa naye ku malo awo, iye anapempha mkulu wa asilikaliyo kuti, “Kodi mungandilole ndiyankhulepo?” Mkulu wa asilikaliyo anafunsa kuti, “Kodi umayankhula Chigriki?
Wotaaddareti Phawuloosa bantta de7iyasuwa gelssana hanishin, Phawuloosi shaalaqaakko, “Taani new issibaa odo?” yaagis. I Phawuloosakko, “Neeni Girike doona eray?
38 Kodi sindiwe Mwigupto uja amene masiku apitawo unayambitsa kuwukira ndi kutsogolera anthu 4,000 owukira aja nʼkupita nawo ku chipululu?”
Neeni hayssafe sinthe buqethi medhdhidi shemppo wodhida oyddu mukulu asata ekkidi bazzo gelida Gibxe uraa gidikkii?” yaagis.
39 Paulo anayankha kuti, “Ine ndine Myuda, wa ku Tarisisi ku Kilikiya. Sindine nzika ya mzinda wamba. Chonde loleni ndiyankhule nawo anthuwa.”
Shin Phawuloosi, “Taani, Kilqiyan de7iya erettida Terseese kataman yelettida Ayhude asi. Hayyana tana odisarkkii?” yaagis.
40 Ataloledwa ndi mkulu wa asilikaliyo, Paulo anayimirira pa makwereropo nakweza dzanja lake kwa gulu la anthuwo. Onse atakhala chete, iye anayankhula nawo mʼChihebri.
Shaalaqay iyaakko, “Oda” yaagin Phawuloosi dethaa bolla eqqidi, asay si7i gaana mela ba kushiyan mallis. Asay si7i gin Ibraysxe doonan hayssada yaagis: