< Aroma 1 >
1 Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
Yesuus Kiristtoosa aylle gidida, hawaare gidana mela xeegettidayssafenne Xoossaa Wonggelaa sabbakana mela doorettida Phawuloosi kiittida kiitaa.
2 umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
Xoossay daro wodeppe sinthe ba nabeta baggara immana yaagida Wonggelay Xoossaa Geeshsha Maxaafatan xaafettis.
3 Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
He Wonggelay ashon Dawite sheeshaappe yelettida, Xoossaa Na7aa, nu Godaa Yesuus Kiristtoosabaa.
4 Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
Qassi I ba geeshsha Ayyaanan hayqoppe denddidi, Xoossaa Na7aa gideyssa gita wolqqan bessis.
5 ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
Iya baggara Ayhude gidonna asay ubbay, ammanidi kiitettana mela Kiristtoosa sunthaa gisho, Xoossay aadho keehatethinne hawaaretetha maata nuus immis.
6 Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
Yesuus Kiristtoosas gidana mela xeegettida asatappe baggati hinttena.
7 Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Roomen de7iya, Xoossay siiqeyssatasinne iya geeshsha dere gidana mela dooridayssatas. Xoossaa nu Aawappenne Godaa Yesuus Kiristtoosappe aadho keehatethaynne sarotethay hinttew gido.
8 Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
Ubbaafe koyrottada, hintte ammanoy biitta ubban si7ettida gisho, Yesuus Kiristtoosa baggara hintte gisho ta Xoossaa galatays.
9 Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
Taani iya Na7aa wonggelabaa kumetha wozanan odiya Xoossay, taani ta woossan ubba wode hinttena qoppeyssas I markka.
10 Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
Wurssethan, Xoossaa shene gidikko, taani hintteko baanaw ogey taw injjetana mela ubba wode woossays.
11 Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
Taani hinttew Ayyaana imuwa shaakkanawunne hinttena be7anaw laamotays.
12 ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
Hessika, taani hintte ammanuwan, qassi hintte ta ammanuwan minettana melassa.
13 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
Ta ishato, taani Ayhude gidonna asaappe ayfe demmidayssada, hinttefekka ayfe demmanaw hintteko baanaw qoppas, shin digettas.
14 Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
Tamaarida asaasinne tamaariboonna asaas qassi cinccatasinne eeyatas taw acoy de7ees.
15 Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
Hessa gisho, Roomen de7iya hinttewuka Wonggelaa odanaw amottays.
16 Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
Iya ammaniyaa ubbaa, koyrottidi Ayhudeta, kaallidi Ayhude gidonnayssata ashshanaw Wonggelay Xoossaa wolqqaa gidiya gisho, ta Wonggelan yeellatikke.
17 Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Xilloy ammanon de7on daana geetettidi Geeshsha Maxaafan xaafettis. Wonggelaan Xoossaa xillotethay qonccis; koyroppe wurssethi gakkanaw, asay xilley ammanonna.
18 Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
Tumay erettonna mela bantta iita ooson kammiya asaa bollanne nagara ubbaa bolla, Xoossaa hanqoy saloppe wodhdhees.
19 Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
Xoossay enttaw qonccanaw bessiyabaa qonccisida gisho, entti Xoossabaa eroosona.
20 Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
Alamey medhettosappe doomidi, asaas beettonna Xoossaa kanddoy, hessika iya merinaa wolqqaynne Xoossatethay iya medhetethan qonccidi de7iya gisho, asay bantta iitatethaas gaasoyiyabay baawa. (aïdios )
21 Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
Entti Xoossaa erishe, iya bonchchibookonanne galatibookkona. Entta qofay maaddonnabaa gidis; entta akeekonna wozanay dhumis.
22 Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
Entti banttana cinccata goosona, shin eeyata.
23 Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
Entti hayqqonna Xoossaa goynnanayssa aggidi, hayqqiya asa medhon, kafota medhon, do7ata medhoninne ulora gooshettiyabata daanisidi oothida misileta goynnidosona.
24 Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
Hessa gisho, entti issoy issuwara borssobaa oothidi, bantta asatethaa kawushshana mela Xoossay entta wozanay amottiya tuna oosos entta yeggi aggis.
25 Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Hessi haniday entti Xoossaa tumaa worddon laammida gishonne medhdhida Xoossaa aggidi, medhetethi goynnida gishossa. Xoossay merinaw galatettidayssa. Amin7i. (aiōn )
26 Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
Hessa gisho, Xoossay enttana entta borsso amuwaas yeggi aggis. Entta maccasay bantaw bessiya addera gaytethi aggidi, bessonnabaa hanidi maccasi maccasara gayttidosona.
27 Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
Hessadakka, addeti bantaw bessiya maccasara gaytethi aggidi, addey addera gayttidosona. Addeti issoy issuwara amon xuugettidi, borssobaa oothidosona. Bantta oothida balaas bessiya pirddaa ekkidosona.
28 Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
Entti Xoossaa erishe, hari attoshin iyabaa qoppanaw koyonna ixxida gisho, bessonnabaa oothana mela Xoossay enttana pathonna qofas aathi immis.
29 Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
Enttan geellatethi, iitatethi, yiiqey, geney, qanaatey, shemppo wodhoy, palami, cimoynne iita amoy kumis. Entti zigireyssata,
30 osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
asa sunthi iisseyssata, Xoossaa ixxeyssata, cayeyssata, otoreyssata, ceeqetteyssata, iitabaa oothanaw koyeyssatanne bantta aayesinne aawas kiitettonayssata,
31 alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
akeekonnayssata, caaqo mentheyssata, siiqoy baynnayssata, qadhey baynnayssata.
32 Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
Hayssata mela ootheyssatas hayqoy bessees giya Xoossaa higgiya erishe, hayssata oothoosona. Entti banttaw ooso xalaala gidonnashin, oothiya haratakka nashshoosona.