< Machitidwe a Atumwi 15 >

1 Anthu ena ochokera ku Yudeya anafika ku Antiokeya ndipo amaphunzitsa abale kuti, “Ngati simuchita mdulidwe potsata mwambo wa Mose, simungapulumuke.”
Antu a ki tuunga ai asimile kupuma ku Uyahudi nu kuamanyisa i aluna, azeligitya, “angamuhite kutalwa i kidamu anga ntendo ni ang'wa Musa, shanga muhumile kugunwa.”
2 Zimenezi zinachititsa Paulo ndi Barnaba kuti atsutsane nawo kwambiri. Kotero Paulo ndi Barnaba anasankhidwa pamodzi ndi abale ena kuti apite ku Yerusalemu kukaonana ndi atumwi ndi akulu ampingo kukakambirana za nkhaniyi.
Matungo uPaulo nu Barnaba nai atulaa nu wikungumi nu witambulyi palung'wi ni enso, anyandugu ai alamue kina uPaulo, Barnaba ni auya kituunga alongole ku Yerusalemu ku itumi ni anyampala ku nsoko a ikolyo ili.
3 Mpingo unawaperekeza, ndipo pamene amadutsa ku Foinike ndi Samariya, iwo anafotokoza momwe a mitundu ina anatembenukira mtima. Nkhani imeneyi inakondweretsa kwambiri abale onse.
Kululo, kulagiiligwa kitalao ni itekeelo, ai akiie ku Foenike ni Samaria azetanantya kupiulwa insula ku anyaingu. Ai aletile ulowa ukulu ku anya ndugu ihi.
4 Atafika ku Yerusalemu, iwo analandiridwa ndi mpingo, pamodzi ndi atumwi ndiponso akulu ampingo. Paulo ndi Barnaba anawafotokozera zonse zimene Mulungu anachita kudzera mwa iwo.
Nai akapembya ku Yerusalemu, ai asingiiigwe ni itekeelo ni itumi ni anyampala, hangi ai apikilye i mpola nia makani ihi naiza Itunda witumile palung'wi ni enso.
5 Kenaka, okhulupirira ena amene kale anali a gulu la Afarisi anayimirira ndipo anati, “Anthu a mitundu ina ayenera kuchita mdulidwe ndi kusunga malamulo a Mose.”
Kuiti i antu akituunga nai ahuiie, nai akoli mi idale nila Afarisayo, ai imikile nu kuligitya, “ingi ingulu kuatwala ikidamu nu kualagiilya aliambe ilagiilyo ni lang'wa Musa.”
6 Atumwi ndi akulu ampingo anasonkhana kuti akambirane za nkhaniyi.
Iti gwa i itumi ni anyampala ai imikile palung'wi kulisiga ikolyo ili.
7 Atakambirana kwambiri Petro anayimirira, ndipo anawayankhula nati: “Abale, mukudziwa kuti masiku oyambirira Mulungu anandisankha ine pakati panu kuti anthu a mitundu ina amve kuchokera pakamwa panga mawu a Uthenga Wabwino ndi kukhulupirira.
Ze yakilaa u witambulyi ulipu, uPetro ai wimikile nu kuligitya kitalao, “Anya ndugu mulingile kina itungo iziza nilakilaa Itunda ai witumile uholania mukati anyu, kina ku mulomo nuane Anyaingu igiilye u lukani nula nkani ninza, nu kuhuiila.
8 Mulungu amene amadziwa mtima wa munthu, Iye anaonetsa kuti anawalandira powapatsa Mzimu Woyera, monga momwe anachita kwa ife.
Itunda, nuilingile i nkolo, ukuiie kitalao, ukuinkiilya uNg'wau Ng'welu, anga nai witumile kitalanyu;
9 Iye sanasiyanitse pakati pa ife ndi iwo, pakuti anayeretsa mitima yawo mwachikhulupiriro.
hangi shanga ai uzipilye utemanuli kati itu ni enso, waze yituma i nkolo niao nziza ku uhuili.
10 Tsopano, chifukwa chiyani mukuyesa Mulungu poyika goli mʼkhosi la ophunzira, limene ngakhale ife kapena makolo athu sangathe kulisenza?
Ku lulo ku niki mukumugema Itunda kina muikile kinyuli migulya a nkingo nia amanyisigwa naiza ga i atata itu ang'wi u sese shanga ai kuhumile ku gigimiilya?
11 Osatero! Ife tikukhulupirira kuti tinapulumutsidwa mwachisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu, monga iwonso anachitira.”
Kuiti ku huiie kina ku ugunwa ku ukende nua Mukulu uYesu, anga nai atulaa.”
12 Gulu lonse linakhala chete pamene amamvetsera Barnaba ndi Paulo akuwawuza za zizindikiro zodabwitsa zimene Mulungu anazichita pakati pa anthu a mitundu ina kudzera mwa iwo.
uMilundo wihi ai ukilagilye nai atulaa akumutegeelya uBarnaba nu Paulo nai atulaa akupumya i mpola nia ilingasiilyo nu ukuilwa naiza Itunda ai witumile palung'wi ni enso kati a antu a anyaingu.
13 Iwo atatha kuyankhula, Yakobo anayankhula nati: “Abale, tandimverani.
Nai akaleka kuligitya, uYakobo ai usukiiye wazeligitya, “Anyandugu ntegeelyi.
14 Simoni watifotokozera mmene Mulungu poyamba paja anaonetsa kukhudzidwa kwake pomwe anatenga anthu a mitundu ina kukhala ake.
uSimioni waganula iti hanza Itunda ku ukende ai ua aiye i anyaingu iti kina wiligilye kupuma kitalao antu kunsoko a lina nilakwe.
15 Mawu a aneneri akuvomereza zimenezi, monga kwalembedwa kuti,
iMakani a anyakidagu igombilye ni ili anga nilikilisigwe.
16 “‘Zitatha izi Ine ndidzabwerera ndipo ndidzamanganso nyumba ya Davide imene inagwa. Ndidzakonzanso malo amene anagumuka, ndi kuyimanganso,
Ze yakilaa i makani aya nikasuka kukizenga hangi ikitala nikang'wa Daudi, naikagwizaa pihi; nikanyansula nu ku sukiilya ubipigwa nuakwe,
17 kuti anthu otsalawo afunefune Ambuye, ndi anthu onse a mitundu ina amene atchedwa ndi dzina langa, akutero Ambuye, amene amachita zinthu zimenezi
iti kina antu nai asagiie amudume uMukulu, palung'wi ni antu a ingu nai itangilwe kulina nilane.'
18 zinaululidwa kuyambira kalekale.’ (aiōn g165)
Iti uu nuiligityaa u Mukulu nai witumile i makani aya nakumukile puma ikali nia kali. (aiōn g165)
19 “Chifukwa chake, ine ndikuweruza kuti tisamavute anthu a mitundu ina amene atembenuka mtima kutsata Mulungu.
Iti gwa, u usiji nuane ingi, kina kuleke kuinkiilya ulwago i antu i anya ingu niakumupilukila Itunda.
20 Koma tiwalembere iwo, kuwawuza kuti asadye chakudya choperekedwa kwa mafano, apewenso dama, asadyenso nyama zochita kupotola kapena kudya magazi.
Kuiti kukilise kitalao kina ihuje nu ubipigwa nua adudu, nsula nia usambo, hangi ni igogilwe, ni sakami.
21 Pakuti malamulo a Mose akhala akulalikidwa mu mzinda uliwonse, kuyambira kalekale ndipo amawerengedwa mʼMasunagoge tsiku la Sabata.”
Kupuma u utugwaa nua anyampala akoli antu mu kila isali ni itanantya nu kumusoma u Musa mu matekeelo kila luhiku nula kusupya.”
22 Pamenepo atumwi ndi akulu ampingo, pamodzi ndi mpingo onse, anagwirizana zosankha anthu ena pakati pawo kuti awatume ku Antiokeya pamodzi ndi Paulo ndi Bamaba. Iwo anasankha Yudasi, wotchedwa Barsaba ndi Sila, anthu awiri amene anali atsogoleri pakati pa abale,
Ku lulo yikigeeleka kutula ia loeeye i itumi ni anyampala, palung'wi ni itekeelo lihi kumuholania uYuda nai witangwaa Barnaba, nu Silas nai atulaa atongeeli i tekeelo, nu kualagiilya ku Antiokia palung'wi nu Paulo nu Barnaba.
23 kuti akapereke kalata yonena kuti, Kuchokera kwa atumwi ndi akulu ampingo, abale anu, Kwa anthu a mitundu ina okhulupirira a ku Antiokeya, Siriya ndi Kilikiya: Tikupereka moni.
Ai akilisilye iti, “Itumi, anyampala ni anya ndugu, ku anya ndugu a anyaingu niakoli ku Antiokia, Shamu ni Kilikia, Milamu.
24 Ife tamva kuti anthu ena ochokera pakati pathu, amene sitinawatume anakusokonezani maganizo ndi kukuvutitsani ndi zimene amakuwuzani.
Ai kijaa kina antu a kituunga naza shanga ai kuinkiiye ilagiilyo nilanso, ai apumaa kitalanyu hangi akumajaa ku umanyisigwa nuiletaa u lwago mu umi nuanyu.
25 Tsono ife tagwirizana kuti, tisankhe anthu ena ndi kuwatumiza kwa inu pamodzi ndi abale athu okondedwa Paulo ndi Barnaba,
Ku lulo yigeeleka ikende kitaitu kihi kuholania antu nu kualagiilya kitalanyu palung'wi ni alowa itu Barnaba nu Paulo,
26 anthu amene anapereka moyo wawo chifukwa cha dzina la Ambuye athu Yesu Khristu.
antu nai agilye u likalo nulao ku nsoko a lina nila Mukulu uYesu Kristo
27 Nʼchifukwa chake, tikutumiza Yudasi ndi Sila kuti adzachitire umboni ndi mawu a pakamwa pawo za zimene ife talemba.
Ku lulo kamulagiilya uYuda nu Sila, akumutambuila makani yao yaayo.
28 Pakuti zinakomera Mzimu Woyera ndiponso ife kuti tisakusenzetseni katundu wina, kupatula zoyenera zokhazi:
Ku nsoko ai yigeeleka ikende ku Ng'wau Ng'welu nu kitaitu, Kuleka kuika migulya anyu muligo ukulu kukila imakani aya naiza a kusinja;
29 Mupewe kudya chakudya choperekedwa nsembe kwa mafano, musadye magazi, kapena nyama yopha mopotola ndiponso musachite dama. Mudzachita bwino mukapewa zimenezi. Tsalani bwino.
Kina mupiluke kupuma mu intu ni ipumigwa ku adudu, sakami intu nia kugogwa, nu usambo. Anga miki ika kuli ni izi, ikutula ikende kitalanyu. Mu lamu.”
30 Anthu aja anatumidwa ndipo anafika ku Antiokeya, kumene anasonkhanitsa mpingo pamodzi napereka kalatayo.
Iti gwa nai asapatiligwa, ai asimiie ku Atiokia; ze yakilaa kilingiila u milundo palung'wi, ai ainkiiye ibada.
31 Anthuwo anawerenga kalatayo ndipo abalewo anakondwa chifukwa cha mawu ake achirimbikitso.
Nai akatula asomaa, ai iloile kunsoko a kukinyilwa inkolo.
32 Yudasi ndi Sila amene analinso aneneri, ananena zambiri zowalimbikitsa ndi kuwapatsa mphamvu abalewo.
uYuda nu Sila, ni anyakidagu, ai a akinyie inkolo i aluna ku nkani idu nu kuakinyila ingulu.
33 Atakhala kumeneko kwa kanthawi, abale aja anatsanzikana nawo mwamtendere kuti abwerere kwa amene anawatuma.
Ze yakilaa kikie itungo nila kituunga kuko, ai asapatiigwe ku ulyuuku kupuma ku anya ndugu ku awo nai a alagiiye.
34 Koma Sila anasankha kuti akhale komweko.
(Kuiti ai yigeelekile ikende uSila kusaga kuko)
35 Koma Paulo ndi Barnaba anatsalira ku Antiokeya kumene iwo pamodzi ndi ena ambiri anaphunzitsa ndi kulalikira Mawu a Ambuye.
Kuiti uPaulo ni auya ai ikie ku Antiokia palung'wi ni auya idu, naize akumanyisa nu kutanantya lukani nula Mukulu.
36 Patapita masiku ena Paulo anati kwa Barnaba, “Tiyeni tibwerere kuti tikaone abale ku mizinda yonse imene tinalalika Mawu a Ambuye ndipo tikaone mmene akuchitira.”
Ze yakilaa mahiku kituunga uPaulo ai uligitilye kung'wa Barnaba, “Ni kusuke itungili nu kuagendeela i aluna mu kila kisali naikatanantya u lukani nula Mukulu, nukuihenga ni ili.
37 Barnaba anafuna kutenga Yohane, wotchedwanso Marko, kuti apite nawo.
uBarnaba ai utakile ga nu kumuhola palungwi nienso uYohana nai witangwaa Marko.
38 Koma Paulo anaganiza kuti sichinali cha nzeru kumutenga Yohane chifukwa iye anawathawa ku Pamfiliya ndipo sanapitirire nawo pa ntchito.
Kuiti uPaulo ai usigile shanga iza kumuhola uMarko, nai ualekile uko ku Pamfilia hangi shanga ai ulongolekile ni enso mu mulimo.
39 Iwo anatsutsana kwambiri kotero kuti anapatukana. Barnaba anatenga Marko ndipo anakwera sitima ya pamadzi kupita ku Kupro.
Uugwa pang'wanso ikapumila wikungumi ukulu ku lulo ai atemanukile. nu Barnaba akamuhola uMarko nu kulongola muhinzo ku meli kupikiila ku Kipro.
40 Paulo anasankha Sila. Abale atawapempherera kwa Ambuye kuti alandire chisomo, ananyamuka.
Kuiti uPaulo ai umuhole uSila nu kuhega, ze yakilaa kinkiiligwa ni anya ndugu mu ukende nua Mukulu.
41 Iye anadutsa ku Siriya ndi ku Kilikiya kupita akulimbikitsa mipingo.
Hangi ai ulongoe kukiila ku Shamu nu ku Kilikia, waze makomisa i matekeelo.

< Machitidwe a Atumwi 15 >