< 2 Samueli 1 >

1 Atamwalira Sauli, Davide anabwerako kumene anakagonjetsa Aamaleki ndipo anakakhala ku Zikilagi masiku awiri.
Emva kokufa kukaSawuli, uDavida wabuya evela ekunqobeni ama-Amaleki wahlala eZikhilagi insuku ezimbili.
2 Pa tsiku lachitatu munthu wina wochokera ku msasa wa Sauli anafika, zovala zake zitangʼambika ndiponso anali atathira dothi pamutu pake. Atafika kwa Davide, anadzigwetsa pansi, kupereka ulemu kwa Davideyo.
Ngosuku lwesithathu kwafika umuntu evela ezihonqweni zikaSawuli, izigqoko zakhe zidabukile njalo egcwele uthuli ekhanda lakhe. Kwathi esefikile kuDavida waziwisela phansi emhlonipha.
3 Davide anamufunsa iye kuti, “Kodi iwe wachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndathawa ku misasa ya Aisraeli.”
UDavida wambuza wathi, “Uvela ngaphi?” Yena waphendula wathi, “Ngibalekile ezihonqweni zabako-Israyeli.”
4 Davide anafunsa, “Tandiwuza, chachitika ndi chiyani?” Iye anati, “Anthu athawa ku nkhondo ndipo ambiri aphedwa. Sauli ndi mwana wake Yonatani aphedwa.”
UDavida wabuza wathi, “Kutheni? Ngitshela.” Yena wathi, “Abantu babalekile empini. Inengi labo lifile. USawuli lendodana yakhe uJonathani labo bafile?”
5 Ndipo Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa nkhaniyi, “Ukudziwa bwanji kuti Sauli ndi mwana wake Yonatani afa?”
UDavida wasesithi kulelojaha elamlethela umbiko, “Wazi njani ukuthi uSawuli lendodana yakhe uJonathani bafile?”
6 Mnyamatayo anati, “Zinangochitika kuti ndinali pa phiri la Gilibowa, ndipo Sauli anali komweko ataweramira pa mkondo wake, pamodzi ndi magaleta ndi okwera ake atamuyandikira.
Ijaha lelo lathi, “Kwenzakele ukuthi mina kade ngiphezu kweNtaba iGilibhowa ngabona uSawuli eyame umkhonto wakhe, izinqola zempi labagadi bamabhiza sebebanga kuye.
7 Pamene anatembenuka ndi kundiona ine, iye anandiyitana, ndipo ndinati, ‘Kodi ndichite chiyani?’”
Uthe etshibilika wangibona, wasengibiza, mina ngathi, ‘Kuyini engingakwenza?’
8 Iye anandifunsa, “Iwe ndiwe yani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndine Mwamaleki.”
Ungibuzile wathi, ‘Ungubani wena na?’ Ngiphendule ngathi, ‘NgingumʼAmaleki.’
9 “Kenaka iye anati kwa ine, ‘Bwera pafupi ndipo undiphe! Ndikumva ululu kwambiri, koma ndikanali ndi moyo!’
Wasesithi kimi, ‘Sondela eduze ungibulale! Sengiseduze lokufa, kodwa ngisaphila.’
10 “Kotero ndinabwera pafupi ndi kumupha, chifukwa ndinadziwa kuti mmene anagweramo sakanakhalanso ndi moyo. Ndipo ndatenga chipewa chaufumu chimene chinali pamutu pake ndi khoza la pa dzanja lake ndipo ndazibweretsa kwa inu mbuye wanga.”
Ngakho ngisondele kuye ngambulala, ngoba ngazile ukuthi emva kwalokho ubengeke aphile. Njalo ngithethe umqhele obusekhanda lakhe lesongo ebelisengalweni yakhe okuyikho engikulethe lapha enkosini yami.”
11 Apo Davide ndi anthu onse amene anali nawo anangʼamba zovala zawo.
Lapho-ke uDavida labantu bonke ababelaye babamba izigqoko zabo bazidabula.
12 Iwo analira maliro ndi kusala zakudya mpaka madzulo chifukwa cha Sauli ndi mwana wake Yonatani, komanso chifukwa cha gulu la ankhondo la Yehova ndi nyumba ya Israeli, chifukwa anaphedwa ndi lupanga.
Babakhalela, babalilela, babazilela kwaze kwahlwa uSawuli lendodana yakhe uJonathani kanye lebutho likaThixo lendlu ka-Israyeli, ngoba babebulewe ngenkemba.
13 Davide anati kwa mnyamata amene anabweretsa uthengawo, “Iwe umachokera kuti?” Iye anayankha kuti, “Ine ndine mwana wa mlendo Mwamaleki.”
UDavida wasesithi ejaheni elalimlethele umbiko, “Wena ungowangaphi na?” Lona laphendula lathi, “Ngiyindodana yezizweni, umʼAmaleki.”
14 Davide anamufunsanso kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunaope kukweza dzanja lako ndi kupha wodzozedwa wa Yehova?”
UDavida waselibuza esithi, “Kungani ungesabanga ukuphakamisa isandla sakho ukuba ubulale ogcotshiweyo kaThixo na?”
15 Kenaka Davide anayitana mmodzi mwa anyamata ake ndipo anati, “Pita ukamukanthe!” Kotero iye anapita kukamukantha, ndipo mnyamata uja anafa.
UDavida wabiza omunye wabantu bakhe wathi, “Sondela umgongode!” Ngakho wamgongoda wafa.
16 Pakuti Davide anali atanena kwa iye kuti, “Iwe wadzipha wekha. Pakamwa pako pakunena zokutsutsa wekha, pamene unanena kuti, ‘Ine ndapha wodzozedwa wa Yehova.’”
Ngoba uDavida wayethe kuye, “Igazi lakho kalibe phezu kwekhanda lakho. Umlomo wakho ufakaze okubi ngawe lapho wena uthe, ‘Ngimbulele ogcotshiweyo kaThixo.’”
17 Davide anayimba nyimbo iyi ya maliro, kulira Sauli ndi mwana wake Yonatani.
UDavida walila isililo lesi ngoSawuli lendodana yakhe uJonathani,
18 Ndipo analamula kuti anthu a ku Yuda aphunzitsidwe nyimbo ya maliroyi imene yalembedwa mʼbuku la Yasari:
walaya ukuthi abantu bakoJuda basifundiswe isililo sedandili lesi (silotshiwe eNcwadini kaJashari):
19 “Ulemerero wako iwe Israeli, wagona utaphedwa ku zitunda. Taonani amphamvu agwa kumeneko!
“Udumo lwakho, We Israyeli, lubulewe ezingqongweni zakho. Yeka ukufa kwamaqhawe!
20 “Musakanene zimenezi ku Gati, musazilengeze ku misewu ya ku Asikeloni, kuti ana aakazi a Afilisti angasangalale, ana aakazi a osachita mdulidwe angakondwere.
Lingabokutsho eGathi, lingakumemezeli ezindleleni zase-Ashikheloni, hlezi amadodakazi amaFilistiya athabe, hlezi amadodakazi abangasokanga athokoze.
21 “Inu mapiri a ku Gilibowa, musakhalenso ndi mame kapena mvula, kapena minda yobereka zopereka za ufa. Pakuti kumeneko chishango cha munthu wamphamvu chinadetsedwa, chishango cha Sauli sanachipakenso mafuta.
We zintaba zaseGilibhowa, kalingabi lamazolo loba izulu, kumbe amasimu athela amabele eminikelo. Ngoba khonapho ihawu leqhawe langcoliswa, ihawu likaSawuli, lingasagcotshwa ngamafutha.
22 “Pa magazi a ophedwa, pa mnofu wa amphamvu, uta wa Yonatani sunabwerere, lupanga la Sauli silinabwere chabe.
Egazini lababuleweyo, enyameni yamaqhawe umtshoko kaJonathani kawuphendukanga, umtshoko kaSawuli kawuphendukanga ungasuthanga.
23 “Sauli ndi Yonatani, pa moyo wawo anali okondedwa ndi okoma mtima, ndipo pa imfa yawo sanasiyanitsidwe. Iwo anali ndi liwiro loposa ziwombankhanga, anali ndi mphamvu zoposa mkango.
USawuli loJonathani, ekuphileni babethandeka bengababukekayo, lekufeni kabehlukaniswanga. Babelesiqubu kulengqungqulu, belamandla kulezilwane.
24 “Inu ana aakazi a Israeli, mulireni Sauli, amene anakuvekani zovala zofiira ndi zofewa, amene anakometsera zovala zanu ndi zokometsera zagolide.
Awu madodakazi ako-Israyeli, mlileleni uSawuli, owaligqokisa okubomvu lokuhle kakhulu, owacecisa izembatho zenu ngemiceciso yegolide.
25 “Taonani amphamvu agwa ku nkhondo! Yonatani wagona ataphedwa ku zitunda.
Yeka ukufa kwamaqhawe empini! UJonathani ulele efile ezingqongweni zakho.
26 Ine ndikuvutika mumtima chifukwa cha iwe mʼbale wanga Yonatani, unali wokondedwa kwambiri kwa ine. Chikondi chako pa ine chinali chopambana, chopambana kuposa chikondi cha akazi.
Ngilusizi ngawe Jonathani, mfowethu; ubuthandeka kakhulu kimi. Ukungithanda kwakho kade kumangalisa, kumangalisa okudlula okwabesifazane.
27 “Taonani amphamvu agwa! Zida zankhondo zawonongeka!”
Yeka ukufa kwamaqhawe! Izikhali zempi zitshabalele!”

< 2 Samueli 1 >