< 1 Mafumu 1 >

1 Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
Kwathi inkosi uDavida esemdala kakhulu, wayengasafudumali lanxa elele loba bemembathise kakhulu.
2 Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
Izinceku zakhe zathi kuye, “Kasidinge intombazana yokunakekela inkosi iyifudumeze. Izalala eceleni kwayo ukuze inkosi yethu ifudumale.”
3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
Ngakho balibhudula lonke elako-Israyeli bedinga intombi enhle baze bafumana u-Abhishagi, umShunami walethwa enkosini.
4 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
Intombazana leyo yayinhle kakhulu; yayinakekela inkosi yayilondoloza, kodwa inkosi kayiyenzanga umfazi.
5 Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
Kwathi u-Adonija, unina owayenguHagithi, waziveza wathi, “Yimi engizakuba yinkosi.” Waselungisa izinqola lamabhiza kanye lamadoda angamatshumi amahlanu ukumandulela.
6 (Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
(Uyise kazange amkhuze ngokumbuza ukuthi, “Ukwenzeleni konke lokhu?” Laye wayemuhle kakhulu, eselama u-Abhisalomu.)
7 Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
U-Adonija wacebisana loJowabi indodana kaZeruya lo-Abhiyathari umphristi, laba bamsekela.
8 Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
Kodwa uZadokhi umphristi, loBhenaya indodana kaJehoyada, loNathani umphrofethi, loShimeyi, loReyi kanye labalindi benkosi abamsekelanga u-Adonija.
9 Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
U-Adonija wasesenza umhlatshelo ngezimvu, ngenkomo langamathole anonileyo eLitsheni laseZohelethi eduze le-Eni Rogeli. Wanxusa abafowabo, lamadodana enkosi lawo wonke amadoda akoJuda ayengawesikhosini,
10 koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
kodwa kamnxusanga uNathani umphrofethi loba uBhenaya loba abalindi benkosi loba umfowabo uSolomoni.
11 Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
Ngakho uNathani wabuza uBhathishebha, unina kaSolomoni wathi, “Awukezwa yini ukuthi u-Adonija, indodana kaHagithi, useyinkosi, ezibeka inkosi yethu uDavida ingakakwazi lokho?
12 Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
Khathesi-ke lalela ngikweluleke, ukuze uzisindise wena lokuvikela impilo yendodana yakho uSolomoni.
13 Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
Ngena lapha okulenkosi uDavida khona ufike uthi kuyo, ‘Wena omkhulu nkosi yami, awufunganga na phambi kwami mina sichaka sakho ukuthi: “Ngoqotho sibili indodana yakho uSolomoni uzakuba yinkosi ngemva kwakho, uzahlala esihlalweni sami”? Kungani pho u-Adonija esebe yinkosi?’
14 Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
Uzakuthi usuphakathi ukhuluma layo inkosi, lami ngizangena ngifike ngigcwalisele lokho ozabe ukutshilo.”
15 Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
Ngalokho-ke uBhathishebha wayayibona inkosi eyayivele isiluphele isendlini yayo, lapho u-Abhishagi ongumShunami ayelondoloza khona inkosi.
16 Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
UBhathishebha wakhothama wazehlisa waguqa phambi kwenkosi. Inkosi yambuza yathi: “Kuyini okufunayo?”
17 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
Wathi kuyo, “nkosi yami, wena uqobo lwakho wafunga kimi inceku yakho ngoThixo uNkulunkulu wakho wathi: ‘USolomoni indodana yakho uzakuba yinkosi ngemva kwami, njalo uzahlala esihlalweni sami sobukhosi.’
18 Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
Kodwa khathesi u-Adonija usebe yinkosi, kodwa wena mbusi, nkosi yami awukwazi okwenzakalayo.
19 Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
Usenikele ngenkomo ezinengi, amaguqa anonisiweyo, kanye lezimvu, njalo usenxuse wonke amadodana enkosi, u-Abhiyathari umphristi kanye loJowabi umlawuli webutho, kodwa kamnxusanga uSolomoni inceku yakho.
20 Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
Mbusi wami, nkosi, abako-Israyeli bonke bakukhangele, badinga ukwazi ukuthi ngubani ozahlala esihlalweni sakho sobukhosi ngemva kwakho.
21 Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
Kungenzeka phela ukuthi inkosi yami ingavele iyephumula kubokhokho, mina lendodana yami uSolomoni sizaphathwa njengezigangi.”
22 Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
Kwathi elokhu esakhuluma lenkosi, kwafika uNathani umphrofethi.
23 Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
Bayibikela inkosi bathi, “UNathani umphrofethi ulapha.” Waya phambi kwenkosi wakhothama embele ubuso bakhe phansi.
24 Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
UNathani wabuza wathi, “Kambe, nkosi yami, nguwe na othe u-Adonija uzamele athathe ubukhosi bakho ungasekho wena, utshilo na ukuthi uzahlala esihlalweni sakho sobukhosi?
25 Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
Lamuhla lokhu wehlile wayakwenza umhlatshelo wenkomo ezinengi, amaguqa anonisiweyo, lezimvu. Unxuse wonke amadodana enkosi, abalawuli bamabutho enkosi kanye lo-Abhiyathari umphristi. Khona khathesi nje bayadla benatha kanye laye besitsho besithi, ‘Mpilonde nkosi Adonija!’
26 Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
Kodwa mina inceku yakho, loZadokhi umphristi, loBhenaya indodana kaJehoyada, kanye lenceku yakho uSolomoni kasinxusanga.
27 Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
Kambe kungaba yikuthi lokhu inkosi yami ikwenze ingatshelanga izinceku zayo ukuthi ngubani ozahlala esihlalweni sobukhosi benkosi yami ngemva kokuba inkosi ingasekho?”
28 Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
Ngalokho iNkosi uDavida yathi, “Mbize, angene uBhathishebha.” Ngakho weza enkosini wema phambi kwayo.
29 Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
Inkosi yasifunga yathi: “Ngeqiniso lokuthi uThixo wami ngophilayo, lowo owangikhipha ezinhluphekweni zami zonke,
30 ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
ngempela khona lamuhla lokhu ngizagcwalisa lokho engakufunga ngoThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli: uSolomoni indodana yakho uzakuba yinkosi ngemva kwami, njalo uzahlala esihlalweni sami esikhundleni sami.”
31 Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
Ngalokho uBhathishebha wakhothamisa ikhanda ekhangele phansi, kwathi eseguqe phambi kwenkosi, wathi. “Umbusi wami inkosi uDavida kaphile kuze kube nini lanini!”
32 Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
INkosi uDavida yathi, “Ngibizela uZadokhi umphristi, uNathani umphrofethi kanye loBhenaya indodana kaJehoyada.” Bathe sebephambi kwenkosi,
33 mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
yathi kubo: “Thathani izinceku zenkosi yenu lihambe lazo liyekhweza uSolomoni indodana yami phezu kwembongolo yami lehle laye liye eGihoni.
34 Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
Khonale uZadokhi umphristi loNathani umphrofethi kuzamele bamgcobe ubukhosi phezu kuka-Israyeli wonke. Livuthele icilongo limemeze lithi, ‘Kayiphile okulaphakade iNkosi uSolomoni!’
35 Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
Lizakhwela laye, abuye azohlala esihlalweni sami sobukhosi aze abuse esikhundleni sami. Sengimkhethile ukuthi abuse phezu kuka-Israyeli lakoJuda.”
36 Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
UBhenaya indodana kaJehoyada waphendula inkosi wathi, “Akube njalo! Kungathi uThixo, uNkulunkulu wombusi lenkosi yami, angakumisa kube njalo.
37 Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
Njengoba uThixo elondoloze umbusi wami oyinkosi, akube njalo lakuSolomoni ukuze enze ubukhosi bakhe bube ngaphezu kwalobo obenkosi yami iNkosi uDavida!”
38 Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
Ngakho uZadokhi umphristi, loNathani umphrofethi, loBhenaya indodana kaJehoyada lamaKherethi lamaPhelethi behla bafika bakhweza uSolomoni embongolweni yeNkosi uDavida bamqhuba bamusa eGihoni.
39 Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
UZadokhi umphristi wathatha uphondo lwamafutha ethenteni elingcwele wagcoba uSolomoni. Ngakho bahle bavuthela icilongo, abantu bonke bahlaba umkhosi behaya besithi, “Mpilonde Nkosi Solomoni!”
40 Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
Bonke bamlandela, bavuthela imihubhe bejabula kakhulu, kwaze kwanyikinyeka umhlaba.
41 Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
U-Adonija kanye lezethekeli ezazilaye zawuzwa lumkhosi njengoba bona basebeqedisa ukudla. UJowabi wathi esizwa icilongo wabuza wathi, “Utshoni umsindo wonke lo edolobheni?”
42 Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
Kwathi elokhu esakhuluma kwafika uJonathani indodana ka-Abhiyathari umphristi. U-Adonija wathi, “Ngena phakathi. Indoda eqakathekileyo njengawe kufanele ukuthi isiphathele izindaba ezimnandi.”
43 Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
UJonathani waphendula wathi, “Akulalutho. Inkosi uDavida uMbusi wethu usegcobe uSolomoni ubukhosi.
44 Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
Inkosi isimthumele kanye loZadokhi umphristi, loNathani umphrofethi, loBhenaya indodana kaJehoyada, lamaKherethi lamaPhelethi, njalo sebehle bamkhweza embongolweni yenkosi.
45 ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
Njalo uZadokhi umphristi loNathani umphrofethi sebehle bamgcobela ubukhosi eGihoni. Besuka lapho bahle bahaya bembuka, kanti ledolobho lonke lihlokoma ngenjabulo. Yiwo lo umkhosi eliwuzwayo.
46 Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
Kunjalo-nje uSolomoni usehle wahlala esihlalweni sobukhosi.
47 Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
Phezu kwalokho izikhulu zesikhosini sezifikile ukuthi zizokwenzela iNkosi uDavida amhlophe zisithi, ‘Sengathi uNkulunkulu wakho angenza ibizo likaSolomoni lidume kulelakho kuthi lesihlalo sakhe sobukhosi sibe lodumo ukwedlula esakho!’ Ngalokho inkosi yakhothama yakhonza isembhedeni wayo
48 inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
yathi, ‘Udumo alube kuye uThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli, yena ovumele ukuthi ngizibonele ngawami amehlo lowo ozathatha isihlalo sami sobukhosi lamuhla.’”
49 Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
Ngenxa yalokhu, izethekeli zika-Adonija zathi lothu zaphakama ngokwethuka zachitheka.
50 Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
Kodwa u-Adonija, ngokwesaba uSolomoni, wahamba wayabamba impondo ze-alithare.
51 Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
USolomoni wasetshelwa ukuthi, “U-Adonija uyayesaba iNkosi uSolomoni ngakho usegagadlele impondo ze-alithare. Uthi yena, ‘INkosi uSolomoni kayifunge kimi lamuhla ithi kayiyikubulala isichaka sayo ngenkemba.’”
52 Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
USolomoni waphendula wathi, “Nxa angatshengisela ukuthi uyindoda uqobo lwayo akulanwele lolulodwa lwekhanda lakhe oluzawela emhlabathini; kodwa nxa ebanjwe yikona, uzakufa.”
53 Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
Ngakho iNkosi uSolomoni yathumela amadoda, ayamethula e-alithareni abuya laye. Ngalokho u-Adonija weza wafika wazehlisa wakhothama enkosini uSolomoni, yena uSolomoni wathi. “Hamba, yana emzini wakho.”

< 1 Mafumu 1 >