< 2 Samueli 20 >

1 Ndipo munthu wina wokonda kuyambitsa chisokonezo, dzina lake Seba, mwana wa Bikiri wa fuko la Benjamini, anali komweko. Iye analiza lipenga ndipo anafuwula kuti, “Ife tilibe chathu mu mfumu wa Davide, tilibe gawo mwa mwana wa Yese! Inu Aisraeli aliyense apite ku nyumba kwake!”
Il se trouvait là un méchant homme, nommé Schéba, fils de Bichri, Benjamite. Il sonna de la trompette, et dit: « Nous n'avons pas de part en David, et nous n'avons pas d'héritage dans le fils de Jessé. Chacun dans sa tente, Israël! »
2 Kotero Aisraeli onse anamuthawa Davide ndipo anatsatira Seba mwana wa Bikiri. Koma anthu a ku Yuda anakhala ndi mfumu yawo njira yonse kuchokera ku Yorodani mpaka ku Yerusalemu.
Et tous les hommes d'Israël cessèrent de suivre David et suivirent Saba, fils de Bichri; mais les hommes de Juda se rallièrent à leur roi, depuis le Jourdain jusqu'à Jérusalem.
3 Davide atabwerera ku nyumba yake yaufumu ku Yerusalemu, iye anatenga azikazi khumi aja amene anawasiya kuti aziyangʼanira nyumba yaufumu, ndipo anawayika mʼnyumba imene anayikapo mlonda. Iye ankawadyetsa koma sanagone nawonso. Anasungidwa kwa okha mpaka tsiku la kufa kwawo ndipo anakhala ngati akazi amasiye.
David arriva dans sa maison à Jérusalem; et le roi prit les dix femmes de ses concubines, qu'il avait laissées pour garder la maison, et les mit sous tutelle; il leur donna de la nourriture, mais il n'entra pas chez elles. Elles restèrent ainsi enfermées jusqu'au jour de leur mort, vivant dans le veuvage.
4 Kenaka mfumu inati kwa Amasa, “Itanitsa ankhondo a Yuda kuti abwere kwa ine pasanathe masiku atatu, ndipo iwe udzakhale nawo.”
Et le roi dit à Amasa: « Convoque-moi les hommes de Juda d'ici trois jours, et sois ici présent. »
5 Motero Amasa anakayitana Ayuda, koma anachedwa, napitirira pa nthawi imene mfumu inamuyikira.
Amasa alla donc convoquer les hommes de Juda, mais il resta plus longtemps que le temps qui lui avait été fixé.
6 Davide anati kwa Abisai, “Tsono Seba mwana wa Bikiri adzatipweteka kuposa momwe Abisalomu anatichitira. Tenga asilikali a mbuye wako ndipo umuthamangitse, mwina adzapeza mizinda yotetezedwa ndi kutithawa ife.”
David dit à Abishai: « Maintenant, Saba, fils de Bichri, nous fera plus de mal qu'Absalom. Prends les serviteurs de ton seigneur et poursuis-le, de peur qu'il ne se procure des villes fortifiées et ne se dérobe à nos yeux. »
7 Kotero anthu a Yowabu, Akereti ndi Apeleti ndiponso asilikali onse amphamvu anapita motsogozedwa ndi Abisai. Iwo anayenda kuchokera ku Yerusalemu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Les hommes de Joab partirent à sa suite, avec les Kéréthiens, les Péléthiens et tous les hommes forts, et ils sortirent de Jérusalem pour poursuivre Saba, fils de Bichri.
8 Ali pa mwala waukulu wa ku Gibiyoni, Amasa anabwera kudzakumana nawo. Yowabu anali atavala chovala chausilikali ndipo pamwamba pa malayawo, mʼchiwuno mwake anavala lamba womangirirapo lupanga lili moyikamo mwakemo. Akuyenda linasololoka kuchoka moyikamo mwake.
Lorsqu'ils arrivèrent à la grande pierre qui est à Gabaon, Amasa vint à leur rencontre. Joab était vêtu de l'habit de guerre qu'il avait revêtu, et il portait une ceinture avec une épée attachée à sa taille dans son fourreau; et comme il avançait, elle tomba.
9 Yowabu anati kwa Amasa, “Kodi uli bwanji mʼbale wanga?” Kenaka Yowabu anamugwira ndevu Amasa uja ndi dzanja lake lamanja ndi kupsompsona.
Joab dit à Amasa: « Est-ce que tu te portes bien, mon frère? » Joab prit Amasa par la barbe avec sa main droite pour l'embrasser.
10 Amasa sanayangʼanitsitse lupanga limene linali mʼdzanja la Yowabu, ndipo Yowabu anamubaya nalo mʼmimba ndipo matumbo ake anatuluka ndi kugwera pansi. Popanda kubayanso kachiwiri, Amasa anafa. Ndipo Yowabu ndi mʼbale wake Abisai anathamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Mais Amasa ne prit pas garde à l'épée qui était dans la main de Joab. Celui-ci le frappa au corps, et répandit ses entrailles à terre; il ne le frappa plus, et il mourut. Joab et son frère Abischaï poursuivirent Saba, fils de Bichri.
11 Mmodzi mwa ankhondo a Yowabu anakayimirira pafupi ndi mtembo wa Amasa ndipo anati, “Aliyense amene amakonda Yowabu ndi aliyense amene ali wa Davide, atsatire Yowabu!”
Un des jeunes gens de Joab se tenait près de lui et disait: « Que celui qui est favorable à Joab, et qui est pour David, suive Joab! »
12 Amasa anagona pakati pa msewu atasamba magazi ake, ndipo munthuyo anaona kuti asilikali onse amayima pamenepo. Atazindikira kuti aliyense amene ankafika pamene panali Amasa amayima, iye anamuchotsa mu msewu ndi kumukokera mʼmunda ndipo anamuphimba ndi nsalu.
Amasa gisait, baignant dans son sang, au milieu de la route. Quand l'homme vit que tout le peuple s'arrêtait, il emporta Amasa hors du chemin dans les champs et jeta sur lui un vêtement, quand il vit que tous ceux qui passaient près de lui s'arrêtaient.
13 Amasa atachotsedwa pa msewu anthu onse anapita ndi Yowabu kuthamangitsa Seba mwana wa Bikiri.
Lorsqu'il fut retiré de la route, tout le peuple se mit à la suite de Joab pour poursuivre Saba, fils de Bichri.
14 Seba anadutsa mafuko onse a Israeli mpaka ku Abeli ndi Beti-Maaka ndiponso chigawo chonse cha Abeli, amene anasonkhana pamodzi ndi kumutsata iye.
Il traversa toutes les tribus d'Israël, jusqu'à Abel, jusqu'à Beth Maaca, et tous les Berites. Ils se rassemblèrent, et marchèrent aussi après lui.
15 Ankhondo onse pamodzi ndi Yowabu anafika ndi kumuzungulira Seba mu Abeli-Beti-Maaka. Iwo anapanga mzere wa nkhondo mpaka ku mzinda, ndipo unayangʼanana ndi malo otetezera a kunja. Pamene amalimbana ndi khoma kuti aligwetse,
Ils vinrent l'assiéger à Abel, à Beth Maaca, et ils élevèrent contre la ville un monticule qui se dressait contre le rempart; tout le peuple qui était avec Joab frappait la muraille pour la renverser.
16 mayi wina wanzeru anafuwula kuchokera mu mzindawo, “Tamverani! Tamverani! Muwuzeni Yowabu abwere pano kuti ndiyankhule naye.”
Alors une femme sage cria de la ville: « Écoute, écoute! Dis à Joab: Approche-toi d'ici, que je te parle. »
17 Yowabu anayandikira kumene kunali mayiyo, ndipo iye anafunsa kuti, “Kodi ndinu Yowabu?” Iye anayankha kuti, “Ndine.” Mayiyo anati, “Tamverani zimene mtumiki wanu akuti anene.” Yowabu anayankha kuti, “Ndikumvetsera.”
Il s'approcha d'elle; et la femme dit: « Es-tu Joab? » Il a répondu: « Je le suis. » Puis elle lui dit: « Écoute les paroles de ton serviteur. » Il a répondu: « J'écoute. »
18 Iye anapitiriza kunena kuti, “Kalekale ankanena kuti, ‘Kapeze yankho lako ku Abeli,’ ndipo nkhani imathera pamenepo.
Elle prit alors la parole et dit: « Autrefois, on disait: « On demandera conseil à Abel », et c'est ainsi qu'on a réglé une affaire.
19 Ife ndife anthu a mtendere ndi okhulupirika mu Israeli. Inu mukufuna kuwononga mzinda umene ndi mayi mu Israeli. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kufafaniza cholowa cha Yehova?”
Je suis de ceux qui sont pacifiques et fidèles en Israël. Vous cherchez à détruire une ville et une mère en Israël. Pourquoi voulez-vous engloutir l'héritage de Yahvé? »
20 Yowabu anayankha kuti, “Ayi ndisatero. Ine sindikufuna kuwufafaniza kapena kuwuwononga.
Joab répondit: Loin de moi, loin de moi l'idée d'engloutir ou de détruire.
21 Nkhani simeneyo ayi. Koma munthu wina wa ku dziko lamapiri la Efereimu, dzina lake Seba mwana wa Bikiri, wawukira mfumu Davide. Muperekeni munthuyo ndipo ine ndidzachoka pa mzinda uno.” Mayiyo anati kwa Yowabu, “Mutu wake tikuponyerani pa khoma pano.”
Il n'en est pas ainsi. Mais un homme de la montagne d'Ephraïm, nommé Schéba, fils de Bichri, a levé la main contre le roi, contre David. Délivre-le, et je quitterai la ville. » La femme dit à Joab: « Voici, on te jettera sa tête par-dessus la muraille. »
22 Ndipo mayiyo anapita kwa anthu onse ndi malangizo ake anzeru, ndipo anadula mutu wa Seba mwana wa Bikiri ndipo anawuponya kwa Yowabu. Kotero iye analiza lipenga ndipo anthu ake anachoka pa mzindawo, aliyense nʼkubwerera kwawo. Ndipo Yowabu anabwerera kwa mfumu ku Yerusalemu.
Alors la femme alla vers tout le peuple dans sa sagesse. Ils coupèrent la tête de Saba, fils de Bichri, et la jetèrent à Joab. Celui-ci sonna de la trompette, et ils se dispersèrent hors de la ville, chacun dans sa tente. Puis Joab retourna à Jérusalem auprès du roi.
23 Yowabu ndiye amalamulira gulu lonse la ankhondo. Benaya mwana wa Yehoyada amalamulira Akereti ndi Apeleti.
Joab était à la tête de toute l'armée d'Israël; Benaja, fils de Jehojada, était à la tête des Kéréthiens et des Péléthiens;
24 Adoramu amayangʼanira anthu ogwira ntchito ya thangata, Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika,
Adoram était à la tête des hommes soumis au travail forcé; Josaphat, fils d'Ahilud, était archiviste;
25 Seva anali mlembi wa mfumu. Zadoki ndi Abiatara anali ansembe
Sheva était scribe; Tsadok et Abiathar étaient sacrificateurs;
26 ndipo Ira wa ku Yairi anali wansembe wa Davide.
Ira, le Jaïrite, était chef des services de David.

< 2 Samueli 20 >