< 2 Samueli 19 >

1 Yowabu anawuzidwa kuti, “Mfumu ikulira maliro a Abisalomu.”
On dit à Joab: « Voici que le roi pleure et se lamente sur Absalom. »
2 Ndipo kwa asilikali onse chipambano cha tsiku limenelo chinasandulika maliro, chifukwa tsiku limenelo anthu anamva kuti mfumu ili pa chisoni chachikulu chifukwa cha mwana wake.
Ce jour-là, la victoire se transforma en deuil parmi tout le peuple, car le peuple entendit dire ce jour-là: « Le roi pleure son fils. »
3 Ankhondo analowa mu mzinda mwakachetechete tsiku limenelo ngati momwe amalowera anthu mwamanyazi chifukwa athawa ku nkhondo.
Ce jour-là, le peuple se faufila dans la ville, comme se faufilent les gens qui ont honte lorsqu'ils fuient au combat.
4 Mfumu inaphimba nkhope yake ndipo inalira mofuwula, “Iwe mwana wanga Abisalomu! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”
Le roi se couvrit le visage et s'écria d'une voix forte: « Mon fils Absalom, Absalom, mon fils, mon fils! »
5 Kenaka Yowabu analowa mʼnyumba ya mfumu nafika kwa mfumuyo ndipo anati, “Lero mwachititsa manyazi asilikali anu onse, amene apulumutsa moyo wanu ndiponso moyo wa ana anu aamuna ndi aakazi, kudzanso moyo wa akazi anu ndi wa azikazi anu.
Joab entra dans la maison auprès du roi et dit: « Aujourd'hui, tu as fait honte à tous tes serviteurs qui ont sauvé ta vie, celle de tes fils et de tes filles, celle de tes femmes et celle de tes concubines,
6 Inu mumakonda amene amadana nanu ndipo mumadana ndi amene amakukondani. Inuyo mwaonetsa lero poyera kuti simusamala za atsogoleri anu a nkhondo ndi asilikali awo. Ine ndikuona kuti inu mukanakondwera ngati Abisalomu akanakhala ndi moyo lero, tonsefe titafa.
en aimant ceux qui te haïssent et en haïssant ceux qui t'aiment. Car vous avez déclaré aujourd'hui que les princes et les serviteurs ne sont rien pour vous. Car je vois aujourd'hui que si Absalom avait vécu et si nous étions tous morts aujourd'hui, cela t'aurait plu.
7 Tsopano pitani mukawalimbikitse asilikali anu. Ine ndikulumbira mwa Yehova kuti ngati inu simupita palibe munthu amene adzatsale ali ndi inu polowa dzuwa. Ichi chidzakhala choyipa kwambiri kuposa zovuta zonse zimene zinakugwerani kuyambira muli mnyamata mpaka lero.”
Maintenant, lève-toi, sors et parle pour réconforter tes serviteurs; car je jure par Yahvé que si tu ne sors pas, pas un homme ne restera avec toi cette nuit. Cela serait pire pour toi que tout le mal qui t'est arrivé depuis ta jeunesse jusqu'à maintenant. »
8 Kotero mfumu inanyamuka ndipo inakhala pa mpando wake pa chipata. Pamene asilikali anawuzidwa kuti, “Mfumu yakhala pa chipata,” onse anabwera kwa iye. Nthawi imeneyi nʼkuti Aisraeli atathawira ku nyumba zawo.
Alors le roi se leva et s'assit à la porte. On dit à tout le peuple: « Voici que le roi est assis à la porte. » Tout le peuple se présenta devant le roi. Israël s'était enfui, chacun dans sa tente.
9 Pakati pa mafuko onse a Israeli, anthu amakangana ndipo amati, “Mfumu inatipulumutsa mʼmanja mwa adani anthu. Iye ndi amene anatilanditsa mʼdzanja la Afilisti. Koma tsopano wathawa mʼdziko muno chifukwa cha Abisalomu.
Tout le peuple se disputait dans toutes les tribus d'Israël, en disant: « Le roi nous a délivrés de la main de nos ennemis, il nous a sauvés de la main des Philistins, et maintenant il s'est enfui du pays à cause d'Absalom.
10 Ndipo Abisalomu amene ife tinamudzoza kuti atilamulire wafa pa nkhondo. Tsono nʼchifukwa chiyani simukunena kanthu za kubweretsanso mfumu?”
Absalom, que nous avons oint sur nous, est mort dans la bataille. Maintenant donc, pourquoi ne dis-tu pas un mot pour ramener le roi? »
11 Mfumu Davide inatumiza uthenga uwu kwa ansembe Zadoki ndi Abiatara, “Funsani akuluakulu a Yuda, ‘Nʼchifukwa chiyani inu mukukhala otsiriza kuyitana mfumu ku nyumba yake yaufumu, pakuti zimene zikunenedwa mu Israeli yense zamveka kwa mfumu ndi onse amene akukhala nayo.
Le roi David envoya dire aux prêtres Tsadok et Abiathar: « Parle aux anciens de Juda, et dis-leur: Pourquoi êtes-vous les derniers à ramener le roi dans sa maison, puisque la parole de tout Israël est venue au roi pour le ramener dans sa maison?
12 Inu ndinu abale anga enieni, mafupa anga ndi mnofu wanga. Nʼchifukwa chiyani inuyo mukukhala otsiriza kubweretsa mfumu?’
Vous êtes mes frères. Vous êtes mes os et ma chair. Pourquoi donc êtes-vous les derniers à ramener le roi?
13 Ndipo munene kwa Amasa, ‘Kodi iwe si mʼbale wanga weniweni? Mulungu andilange, andilange kwambiri ngati kuyambira tsopano sukhala mtsogoleri wa ankhondo anga kulowa mʼmalo mwa Yowabu.’”
Dis à Amasa: « N'es-tu pas mon os et ma chair? Que Dieu me le rende, et plus encore, si tu n'es pas continuellement le chef de l'armée devant moi, à la place de Joab.'"
14 Davide anakopa mitima ya anthu onse a Yuda ndipo anthuwo anakhala ngati munthu mmodzi. Iwo anatumiza mawu kwa mfumu, “Bwererani inu ndi anthu anu onse.”
Il fit fléchir le cœur de tous les hommes de Juda, comme un seul homme, de sorte qu'ils envoyèrent dire au roi: « Reviens, toi et tous tes serviteurs. »
15 Kotero mfumu inabwerera ndipo inakafika mpaka ku Yorodani. Tsono anthu a ku Yuda anabwera ku Giligala kuti akakumane ndi mfumu ndi kumuwolotsa Yorodani.
Le roi s'en retourna et arriva au Jourdain. Juda se rendit à Guilgal, pour aller à la rencontre du roi, afin de lui faire passer le Jourdain.
16 Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wa ku Bahurimu, anabwera mofulumira pamodzi ndi Ayuda kudzakumana ndi mfumu Davide.
Shimei, fils de Gera, Benjamite, qui était de Bahurim, se hâta de descendre avec les hommes de Juda à la rencontre du roi David.
17 Iyeyo anali ndi anthu 1,000 a fuko la Benjamini pamodzi ndi Ziba, wantchito wa banja la Sauli ndi ana ake aamuna khumi ndi asanu ndi antchito ake makumi awiri. Iwo anathamangira ku Yorodani kumene kunali mfumu.
Il y avait avec lui mille hommes de Benjamin, et Tsiba, serviteur de la maison de Saül, ses quinze fils et ses vingt serviteurs; et ils passèrent le Jourdain en présence du roi.
18 Iwo anawoloka mtsinje kukatenga banja lonse la mfumu ndi kuchita zonse zimene mfumuyo imafuna. Pamene Simei mwana wa Gera anawoloka Yorodani, anagwa pansi chafufumimba pamaso pa mfumu,
Un bac partit pour faire passer la maison du roi, et pour faire ce qu'il jugeait bon. Shimei, fils de Gera, se prosterna devant le roi après avoir passé le Jourdain.
19 ndipo anati, “Mbuye wanga musaganizire za kulakwa kwanga. Musakumbukire zolakwa zimene mtumiki wanu anakuchitirani tsiku limene mbuye wanga mfumu mumachoka mu Yerusalemu. Mfumu musazikumbukirenso zimenezi.
Il dit au roi: « Que mon seigneur ne m'impute pas d'iniquité et ne se souvienne pas de ce que ton serviteur a fait de pervers le jour où mon seigneur le roi est sorti de Jérusalem, afin que le roi le prenne à cœur.
20 Pakuti ine mtumiki wanu ndazindikira kuti ndachimwa. Koma lero ndabwera ngati woyamba wa nyumba ya Yosefe yonse kudzakumana nanu mbuye wanga mfumu.”
Car ton serviteur sait que j'ai péché. C'est pourquoi voici, je suis venu aujourd'hui comme le premier de toute la maison de Joseph pour descendre à la rencontre de mon seigneur le roi. »
21 Ndipo Abisai mwana wa Zeruya anati, “Kodi Simei saphedwa chifukwa cha ichi? Iye anatukwana wodzozedwa wa Yehova.”
Mais Abishai, fils de Tseruiah, prit la parole et dit: « Shimei ne devrait-il pas être mis à mort pour cela, parce qu'il a maudit l'oint de Yahvé? ».
22 Davide anayankha kuti, “Kodi inu ana a Zeruya, ndikuchitireni chiyani? Lero lino iwe wakhala mdani wanga! Kodi wina aphedwe lero mu Israeli? Kodi ine sindikudziwa kuti lero ndine mfumu mu Israeli?”
David dit: « Qu'ai-je à faire avec vous, fils de Tseruja, pour que vous soyez aujourd'hui mes adversaires? Quelqu'un sera-t-il mis à mort aujourd'hui en Israël? Car ne sais-je pas que je suis aujourd'hui roi d'Israël? »
23 Ndipo mfumu inati kwa Simei, “Iwe Simei suphedwa.” Ndipo mfumuyo inalonjeza ndi lumbiro.
Le roi dit à Schimeï: « Tu ne mourras pas. » Le roi lui fit jurer.
24 Mefiboseti, mdzukulu wa Sauli, nayenso anabwera kudzakumana ndi mfumu. Kuyambira tsiku limene mfumu inachoka mpaka tsiku limene inabwerera mu mtendere, iye sanasambe mapazi kaya kumeta ndevu kapena kuchapa zovala zake.
Mephibosheth, fils de Saül, descendit à la rencontre du roi. Il n'avait ni soigné ses pieds, ni taillé sa barbe, ni lavé ses vêtements, depuis le jour où le roi était parti jusqu'au jour où il était rentré en paix.
25 Pamene anafika kuchokera ku Yerusalemu kudzakumana ndi mfumu, mfumu inamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani sunapite nane Mefiboseti?”
Lorsqu'il arriva à Jérusalem pour rencontrer le roi, celui-ci lui dit: « Pourquoi n'as-tu pas marché avec moi, Mephibosheth? »
26 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga mfumu, pakuti ine wantchito wanu ndine wolumala. Ndinati, ‘Andikonzere chishalo cha bulu wanga ndipo ndidzakwera kuti ndipite ndi mfumu.’ Koma Ziba wantchito wanga anandilakwitsa.
Il répondit: « Seigneur, ô roi, mon serviteur m'a trompé. En effet, ton serviteur a dit: « Je vais me faire seller un âne, je monterai dessus et j'irai avec le roi », car ton serviteur est boiteux.
27 Ndipo wayankhula zosinjirira za ine mtumiki wanu kwa inu mbuye wanga mfumu. Mbuye wanga mfumu ali ngati mngelo wa Mulungu ndipo chitani chimene chikukomerani.
Il a calomnié ton serviteur devant le roi mon seigneur, mais le roi mon seigneur est comme un ange de Dieu. Fais donc ce qui est bon à tes yeux.
28 Zidzukulu zonse za agogo anga sizinayenera chilichonse koma imfa kuchokera kwa inu mbuye wanga mfumu, koma inu munapereka malo kwa mtumiki wanu pakati pa amene amadya pa tebulo lanu. Tsono ine ndili ndi chiyaninso kuti ndipitirize kudandaula kwa mfumu?”
Car toute la maison de mon père n'était qu'un mort devant le roi mon seigneur, et tu as mis ton serviteur au nombre de ceux qui ont mangé à ta table. Quel droit ai-je donc encore d'en appeler au roi? »
29 Mfumu inayankha kuti, “Uneneranji zambiri? Ine ndikulamula kuti iwe ndi Ziba mugawane minda.”
Le roi lui dit: « Pourquoi parles-tu encore de tes affaires? Je dis que toi et Ziba, vous vous partagerez le pays. »
30 Mefiboseti anati kwa mfumu, “Muloleni atenge zonse, pakuti tsopano mbuye wanga mwafika kwanu mu mtendere.”
Mephibosheth dit au roi: « Oui, qu'il prenne tout, car mon seigneur le roi est venu en paix dans sa maison. »
31 Barizilai Mgiliyadi anabweranso kuchokera ku Rogelimu kudzawoloka Yorodani ndi mfumu ndi kumuperekeza kuchokera kumeneko.
Barzillai, le Galaadite, descendit de Rogelim; et il passa le Jourdain avec le roi pour le conduire au delà du Jourdain.
32 Tsono Barizilai anali wokalamba kwambiri, wa zaka makumi asanu ndi atatu. Iye ndi amene anapereka zinthu kwa mfumu pamene anali ku Mahanaimu pakuti anali wolemera kwambiri.
Or Barzillai était un homme très âgé, de quatre-vingts ans même. Il avait assuré la subsistance du roi pendant son séjour à Mahanaïm, car il était un très grand homme.
33 Mfumu inati kwa Barizilai, “Woloka nane ndipo ukakhale ndi ine mu Yerusalemu ndipo ineyo ndidzakusamalira.”
Le roi dit à Barzillai: « Passe avec moi, et je te soutiendrai avec moi à Jérusalem. »
34 Barizilai anayankha mfumu kuti, “Kodi zakhala zaka zingati zoti ndikhale ndi moyo, kuti ndipite ku Yerusalemu ndi mfumu?
Barzillaï dit au roi: Combien y a-t-il de jours des années de ma vie, pour que je monte avec le roi à Jérusalem?
35 Ine tsopano ndili ndi zaka 80. Kodi ndingathe kusiyanitsa pakati pa chabwino ndi choyipa? Kodi mtumiki wanu angathe kuzindikira kukoma kwa zimene akudya ndi kumwa? Kodi ndingathe kumva kuyimba kwa amuna ndi akazi? Nʼchifukwa chiyani wantchito wanu akakhale ngati katundu kwa mbuye wanga mfumu?
J'ai aujourd'hui quatre-vingts ans. Saurai-je discerner le bien du mal? Ton serviteur peut-il goûter ce que je mange ou ce que je bois? Est-ce que je peux encore entendre la voix des chanteurs et des chanteuses? Pourquoi donc ton serviteur serait-il un fardeau pour mon seigneur le roi?
36 Koma ine mtumiki wanu ndingoyenda pangʼono kuti ndiwoloke Yorodani pamodzi ndi mfumu. Amfumu mungandipatsirenji mphotho yotere?
Ton serviteur n'aura qu'à passer le Jourdain avec le roi. Pourquoi le roi me rendrait-il une telle récompense?
37 Muloleni, mtumiki wanu abwerere, kuti ndikafere kwathu pafupi ndi manda a abambo ndi amayi anga. Koma nayu mtumiki wanu Kimuhamu. Muloleni iye awoloke nanu mbuye wanga mfumu. Mumuchitire chilichonse chimene chikukomereni!”
Je te prie de laisser ton serviteur revenir sur ses pas, afin que je meure dans ma ville, près du tombeau de mon père et de ma mère. Mais voici ton serviteur Chimham; qu'il passe avec mon seigneur le roi, et fais-lui ce qui te semblera bon. »
38 Mfumu inati, “Kimuhamu adzawoloka ndi ine, ndipo ndidzamuchitira iye chilichonse chimene chidzakondweretsa iwe. Ndipo chilichonse chimene udzandipempha ine ndidzakuchitira.”
Le roi répondit: « Chimham passera avec moi, et je lui ferai ce qui te semblera bon. Tout ce que tu me demanderas, je le ferai pour toi. »
39 Kotero anthu onse anawoloka Yorodani ndipo kenaka mfumu inawoloka. Mfumu inapsompsona Barizilai ndi kumupatsa madalitso ndipo Barizilaiyo anabwerera kwawo.
Tout le peuple passa le Jourdain, et le roi aussi. Le roi embrassa Barzillai et le bénit, puis il retourna à sa place.
40 Pamene mfumu inawolokera ku Giligala, Kimuhamu anawoloka naye. Ankhondo onse a Yuda ndi theka la ankhondo a Israeli onse anaperekeza mfumu.
Le roi passa à Guilgal, et Chimham passa avec lui. Tout le peuple de Juda fit passer le roi, ainsi que la moitié du peuple d'Israël.
41 Kenaka Aisraeli onse amabwera kwa mfumu nʼkumati kwa iye, “Nʼchifukwa chiyani abale athu, anthu a ku Ayuda, anakubani mfumu, nawoloka nanu Yorodani inu ndi banja lanu, pamodzi ndi anthu ake onse?”
Voici, tous les hommes d'Israël vinrent auprès du roi et lui dirent: « Pourquoi nos frères, les hommes de Juda, t'ont-ils enlevé et ont-ils fait passer le Jourdain au roi et à sa famille, et à tous les hommes de David avec lui? »
42 Ayuda onse anayankha Aisraeli kuti, “Ife timachita zimenezi chifukwa mfumu ndi mʼbale wathu. Nʼchifukwa chiyani inu mwapsa mtima ndi zimenezi? Kodi ife tinadya chakudya chilichonse cha mfumu? Kodi chilipo chimene ife tatenga kukhala chathu?”
Tous les hommes de Juda répondirent aux hommes d'Israël: « Parce que le roi est un proche parent pour nous. Pourquoi donc êtes-vous en colère à ce sujet? Avons-nous mangé aux frais du roi? Ou bien nous a-t-il fait un quelconque cadeau? »
43 Aisraeli anayankha Ayuda kuti, “Ife ndi magawo khumi mwa mfumu imeneyi, ndipo kuwonjezera apo, ife tili ndi zinthu zambiri mwa Davide kuposa inu. Tsono nʼchifukwa chiyani mukutichita chipongwe? Kodi ife si amene tinayamba kunena za kubweretsa mfumu yathu?” Koma anthu a Yuda anayankha mwaukali kwambiri kupambana anthu a ku Israeli.
Les hommes d'Israël répondirent aux hommes de Juda, et dirent: « Nous avons dix parts dans le roi, et nous avons aussi plus de droits que vous sur David. Pourquoi donc nous avez-vous méprisés, pour ne pas être les premiers à nous conseiller de ramener notre roi? » Les paroles des hommes de Juda étaient plus ardentes que celles des hommes d'Israël.

< 2 Samueli 19 >