< 2 Samueli 2 >

1 Patapita nthawi, Davide anafunsa Yehova kuti, “Kodi ndipite ku umodzi mwa mizinda ya Yuda?” Yehova anayankha kuti, “Pita.” Davide anafunsanso kuti, “Kodi ndipite kuti?” Yehova anayankha kuti, “Ku Hebroni.”
А после тога Давид упита Господа говорећи: Хоћу ли отићи у који град Јудин? А Господ му рече: Отиди. А Давид рече: У који да отидем? Рече: Хеврон.
2 Choncho Davide anapita kumeneko ndi akazi ake awiri, Ahinoamu wa ku Yezireeli ndi Abigayeli mkazi wamasiye uja wa Nabala wa ku Karimeli.
И Давид отиде онамо са две жене своје, Ахиноамом из Језраела и Авигејом која пре беше жена Навала из Кармила.
3 Davide anatenganso anthu amene anali nawo aliyense ndi banja lake, ndipo anakakhala ku midzi ya ku Hebroni.
И људе који беху с њим одведе Давид, све с породицама њиховим, и настанише се по градовима хевронским.
4 Kenaka amuna a ku Yuda anabwera ku Hebroni ndipo kumeneko anadzoza Davide kukhala mfumu ya fuko la Yuda. Davide atawuzidwa kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi ndi amene anayika mʼmanda Sauli,
И дођоше људи од Јуде, и помазаше онде Давида за цара над домом Јудиним. И јавише Давиду говорећи: Људи из Јависа Галадовог погребоше Саула.
5 iye anatuma amithenga kwa anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti akayankhule nawo kuti, “Yehova akudalitseni poonetsa kukoma mtima kwanu kwa Sauli mbuye wanu pomuyika mʼmanda.
И Давид посла посланике к људима у Јавису Галадовом, и рече им: Да сте благословени Господу што учинисте милост господару свом, Саулу и погребосте га.
6 Tsopano Yehova akuonetseni kukoma mtima ndi kukhulupirika kwake ndipo inenso ndidzakukomerani mtima chifukwa munachita zimenezi.
Зато да учини Господ вама милост и веру; а ја ћу вам учинити добро, што сте то учинили.
7 Tsopano khalani amphamvu ndi olimba mtima, pakuti Sauli mbuye wanu wafa, ndipo fuko la Yuda landidzoza kukhala mfumu yawo.”
И нека вам се укрепе руке и будите храбри; јер Саул, господар ваш, погибе, а дом Јудин помаза мене за цара над собом.
8 Pa nthawi imeneyi Abineri mwana wa Neri, wolamulira ankhondo a Sauli, anatenga Isi-Boseti mwana wa Sauli ndi kubwera naye ku Mahanaimu.
Али Авенир, син Ниров, војвода Саулов узе Исвостеја сина Сауловог, и одведе га у Маханајим.
9 Iye anamuyika kuti akhale mfumu yoyangʼanira Giliyadi, Asuri ndi Yezireeli, pamodzi ndi Efereimu, Benjamini ndi Israeli yense.
И зацари га над Галадом и над Асуром и Језраелом и Јефремом и Венијамином и над свим Израиљем.
10 Isi-Boseti mwana wa Sauli anali wa zaka makumi anayi pamene anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira zaka ziwiri. Koma fuko la Yuda linatsatira Davide.
Четрдесет година беше Исвостеју сину Сауловом кад поче царовати над Израиљем; и царова две године. Само дом Јудин држаше се Давида.
11 Davide anakhala mfumu ku Hebroni akulamulira fuko la Yuda, kwa zaka zisanu ndi chimodzi ndi miyezi isanu ndi umodzi.
А Давид царова у Хеврону над домом Јудиним седам година и шест месеци.
12 Abineri mwana wa Neri, pamodzi ndi ankhondo a Isi-Boseti mwana wa Sauli, anachoka ku Mahanaimu ndi kupita ku Gibiyoni.
Потом изиђе Авенир, син Ниров, и слуге Исвостеја сина Сауловог из Маханајима у Гаваон.
13 Yowabu mwana wa Zeruya pamodzi ndi ankhondo a Davide anapita ndi kukakumana nawo ku dziwe la ku Gibiyoni. Gulu lina linakhala mbali ina ya dziwelo pamene gulu lina linakhala mbali inayo.
Такође и Јоав син Серујин и слуге Давидове изиђоше и сретоше се с њима код језера гаваонског, и стадоше један с једне стране а други с друге стране.
14 Kenaka Abineri anati kwa Yowabu, “Tiye tibweretse ena mwa anyamata athu kuti amenyane patsogolo pathupa.” Yowabu anayankha, “Chabwino, amenyane.”
Тада рече Авенир Јоаву: Нека устану момци и нека се проиграју пред нама. И рече Јоав: Нека устану.
15 Kotero anayimirira ndipo anawawerenga: anyamata khumi ndi awiri a fuko la Benjamini ndi Isi-Boseti mwana wa Sauli ndiponso anyamata khumi ndi awiri a Davide.
И устадоше, и изиђоше на број: дванаест од Венијамина са стране Исвостеја сина Сауловог, и дванаест између слуга Давидових.
16 Tsono aliyense anagwira mutu wa mnzake namubaya mnzakeyo mʼnthiti ndi mpeni ndipo onse anagwera pansi limodzi. Kotero malo amenewo ku Gibiyoni amatchedwa Helikati Hazurimu.
И ухватише један другог за главу, и тисну један другом мач свој у бок, и попадаше заједно. Отуда се прозва оно место Халкат-Асурим код Гаваона.
17 Tsiku limeneli nkhondo yake inali yoopsa kwambiri, ndipo Abineri ndi ankhondo a Israeli anagonjetsedwa ndi ankhondo a Davide.
И би жесток бој оног дана; и слуге Давидове разбише Авенира и Израиљце.
18 Ana atatu aamuna a Zeruya, Yowabu, Abisai ndi Asaheli anali komweko. Koma Asaheli anali waliwiro ngati insa.
А онде беху три сина Серујина: Јоав и Ависај и Асаило. А Асаило беше лак на ногу као срна у пољу;
19 Iye anathamangitsa Abineri ndipo sanakhotere kumanja kapena kumanzere pamene amamutsatira.
И потера Асаило Авенира, и не сврну ни надесно ни налево иза Авенира.
20 Abineri anayangʼana mʼmbuyo ndipo anafunsa, “Kodi ndiwe Asaheli?” Iye anayankha kuti, “Ndine.”
И Авенир обазре се натраг и рече: Јеси ли ти, Асаило? А он рече: Ја сам.
21 Ndipo Abineri anati kwa iye, “Khotera kumanja kapena kumanzere: tsatira mmodzi mwa anyamatawa ndipo umulande zida zake.” Koma Asaheli sanasiye kumuthamangitsa.
А Авенир му рече: Сврни надесно или налево, и узми једног од тих момака, и скини одору с њега. Али не хте Асаило сврнути иза њега.
22 Abineri anamuchenjezanso Asaheli, “Siya kuthamangitsa ine! Kodi ndikukanthe chifukwa chiyani? Kodi ndikaonana naye bwanji mʼbale wako Yowabu?”
И Авенир опет рече Асаилу: Одступи од мене; зашто да те саставим са земљом? И како бих смео погледати у Јоава брата твог?
23 Koma iye anakana kuleka kumuthamangitsa. Choncho Abineri anabaya Asaheli mʼmimba ndi msonga ya mkondo wake ndipo mkondowo unatulukira mbali ina. Iye anagwa ndi kufera pamalo pomwepo. Ndipo munthu aliyense amayima akafika pamalo pamene anagwera ndi kufa.
Али он не хте одступити; и Авенир га удари копљем под пето ребро, и изађе му копље на леђа, те он паде онде и умре на месту. И ко год дође на оно место где паде и погибе Асаило, устављаше се.
24 Koma Yowabu ndi Abisai anathamangitsa Abineri, ndipo dzuwa likulowa, anafika ku phiri la Ama, pafupi ndi Giya pa njira yopita ku chipululu cha ku Gibiyoni.
Али Јоав и Ависај потераше Авенира, и сунце зађе кад дођоше до брда Аме, која је према Гији на путу у пустињу гаваонску.
25 Pamenepo anthu a fuko la Benjamini anasonkhana kudzathandiza Abineri. Iwo anapanga gulu ndipo anayima pamwamba pa phiri.
И скупише се синови Венијаминови за Авениром, те се начини чета, и стадоше на врх једног брда.
26 Abineri anayitana Yowabu, “Kodi tipitirize kumenyana mpaka kalekale? Kodi sukuzindikira kuti mathero ake kudzakhala kuwawidwa mitima? Kodi udzawaletsa liti ankhondo ako kuthamangitsa abale awo?”
И Авенир викну Јоава и рече: Хоће ли мач прождирати довека? Не знаш ли да јади бивају напослетку? Зашто већ не кажеш народу да се прођу браће своје?
27 Yowabu anayankha kuti, “Pali Yehova wamoyo, ukanapanda kuyankhula, ankhondo anga akanapitiriza kuthamangitsa abale awo mpaka mmawa.”
А Јоав рече: Тако жив био Бог, да ниси казао, народ би још јутрос отишао, ниједан не би терао брата свог.
28 Chomwecho Yowabu analiza lipenga, ndipo ankhondo onse anayima. Iwo analeka kuthamangitsa Aisraeli kapena kumenyana nawo.
Тада затруби Јоав у трубу, и устави се сав народ и престаше терати Израиља, и не бише се више.
29 Usiku wonsewo Abineri ndi ankhondo ake anayenda kudutsa Araba. Iwo anawoloka Yorodani, napitirira mpaka kudutsa dera lonse la Bitironi ndipo anafika ku Mahanaimu.
И тако Авенир и људи његови идоше преко поља целу ону ноћ, и пређоше преко Јордана, и прошавши сав Витрон дођоше у Маханајим.
30 Choncho Yowabu anabwerera kuchokera kothamangitsa Abineri ndipo anasonkhanitsa ankhondo ake onse. Kupatula Asaheli, panali ankhondo khumi ndi anayi a Davide amene anasowa.
А Јоав се врати од Авенира, и кад скупи сав народ, не беше од слуга Давидових деветнаест људи и Асаила.
31 Koma ankhondo a Davide anapha ankhondo a fuko la Benjamini 360 amene anali ndi Abineri.
Али слуге Давидове побише синова Венијаминових, људи Авенирових, три стотине и шездесет људи, који изгибоше.
32 Iwo anatenga Asaheli ndi kukamuyika mʼmanda a abambo ake ku Betelehemu. Ndipo Yowabu ndi ankhondo ake anayenda usiku wonse ndi kufika ku Hebroni kukucha.
А Асаила узеше и погребоше у гробу оца његовог који беше у Витлејему. И Јоав и људи његови идоше сву ноћ, и освануше у Хеврону.

< 2 Samueli 2 >