< 1 Mafumu 1 >

1 Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti.
А цар Давид остаре и би временит, и колико га покриваху хаљинама не могаше се загрејати.
2 Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”
Тада му рекоше слуге његове: Нека потраже цару господару нашем младу девојку, па она нека стоји пред царем и двори га, и на крилу нека му спава, да се загрева цар, господар наш.
3 Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu.
И потражише лепу девојку по свим крајевима израиљским, и нађоше Ависагу Сунамку, те је доведоше цару.
4 Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.
А та девојка беше врло лепа, и двораше цара и служаше му: али је цар не позна.
5 Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake.
А Адонија, син Агитин подиже се говорећи: Ја ћу бити цар. И набави себи кола и коњике, и педесет људи који трчаху пред њим.
6 (Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).
И отац га никада не накара, нити му рече: Зашто радиш тако? А он беше врло леп, и мати га роди иза Авесалома.
7 Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza.
И договараше се с Јоавом сином Серујиним и с Авијатаром свештеником, који помагаху Адонији.
8 Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.
Али Садок свештеник и Венаја син Јодајев и Натан пророк и Семај и Реј и јунаци Давидови не присташе за Адонијом.
9 Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda,
Тада накла Адонија оваца и волова и угојене стоке код камена Зоелета, који је код извора Рогила, и позва сву браћу своју, синове цареве, и све људе од Јуде, слуге цареве;
10 koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.
Али не позва Натана пророка, ни Венаје, ни осталих јунака, ни Соломуна брата свог.
11 Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa?
Тада рече Натан Витсавеји, матери Соломуновој говорећи: Јеси ли чула да се зацарио Адонија син Агитин? А господар наш Давид не зна.
12 Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni.
Него сада хајде, ја ћу те саветовати како ћеш избавити душу своју и душу сина свог Соломуна.
13 Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’
Хајде, отиди к цару Давиду и реци му: Ниси ли се ти, господару мој царе, заклео слушкињи својој говорећи: Соломун, син твој, биће цар после мене и он ће седети на престолу мом? Зашто се дакле зацари Адонија?
14 Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”
И гле, док ти још будеш онде говорећи с царем, ја ћу доћи за тобом, и допунићу твоје речи.
15 Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira.
И тако уђе Витсавеја к цару у клет. А цар беше врло стар; и Ависага Сунамка двораше га.
16 Batiseba anagwada nalambira mfumu. Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”
И савивши се Витсавеја поклони се цару; а цар јој рече: Шта ћеш?
17 Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’
А она му рече: Господару мој, ти си се заклео Господом Богом својим слушкињи својој: Соломун, син твој, биће цар после мене, и он ће седети на престолу мом.
18 Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi.
А сад ево Адонија се зацари, а ти, господару мој царе, и не знаш.
19 Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni.
Наклао је волова и угојене стоке и оваца много, и позвао све синове цареве, и Авијатара свештеника и Јоава војводу; а Соломуна слуге твог није позвао.
20 Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu.
Сада, царе господару мој, очи су свега Израиља упрте у тебе, да им кажеш ко ће сести на престо твој, господару мој царе, после тебе.
21 Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”
Иначе, кад господар мој цар почине код отаца својих, бићемо ја и син мој Соломун криви.
22 Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa.
И гле, док она још говораше цару, дође пророк Натан.
23 Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
И јавише цару говорећи: Ево Натана пророка. И он ступивши пред цара поклони се цару лицем до земље.
24 Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu?
И рече Натан: Царе, господару мој, јеси ли ти казао: Адонија ће бити цар после мене, и он ће седети на престолу мом?
25 Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’
Јер отиде данас и накла волова и угојене стоке и оваца много, и позва све синове цареве и војводе и Авијатара свештеника; и ено једу и пију с њим и говоре: Да живи цар Адонија.
26 Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane.
Мене пак, слуге твог, не позва, ни Садока свештеника, ни Венаје сина Јодајевог, ни Соломуна слуге твог.
27 Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”
Је ли то цар господар мој наредио? Не казавши слузи свом ко ће сести на престо господара мог цара после њега.
28 Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.
А цар Давид одговори и рече: Зовите ми Витсавеју. И она дође пред цара, и стаде пред царем.
29 Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse,
Тада се закле цар говорећи: Тако да је жив Господ, који је избавио душу моју од сваке невоље,
30 ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”
Како сам ти се заклео Господом Богом Израиљевим рекавши: Соломун син твој биће цар после мене, и он ће седети на престолу мом место мене, тако ћу учинити данас.
31 Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”
Тада Витсавеја сави се лицем до земље и поклони се цару, па рече: Да живи господар мој цар Давид довека!
32 Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu,
Потом рече цар Давид: Зовите ми Садока свештеника и Натана пророка и Венају, сина Јодајевог. И они дођоше пред цара.
33 mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’
А цар им рече: Узмите са собом слуге господара свог, и посадите Соломуна, сина мог, на моју мазгу и и одведите га до Гиона;
34 Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’
И нека га онде Садок свештеник и Натан пророк помажу за цара над Израиљем, и затрубите у трубу и реците: Да живи цар Соломун!
35 Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”
Потом се вратите за њим, и он нека дође и седне на престо мој и царује место мене; јер сам њега одредио да буде вођ Израиљу и Јуди.
36 Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero.
А Венаја, син Јодајев, одговори цару и рече: Амин! Нека тако каже Господ Бог господара мог цара.
37 Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”
Како је Господ био с господарем мојим царем тако нека буде и са Соломуном, и нека подигне престо његов још више него престо господара мог, цара Давида.
38 Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni.
И тако отиде Садок свештеник и Натан пророк и Венаја син Јодајев и Херетеји и Фелетеји, и посадише Соломуна на мазгу цара Давида и одведоше га до Гиона.
39 Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!”
И Садок свештеник узе рог с уљем из шатора, и помаза Соломуна. Потом затрубише у трубу и сав народ рече: Да живи цар Соломун!
40 Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.
И сав народ пође за њим, и народ свираше у свирале и весељаше се веома да се земља разлегаше од вике њихове.
41 Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”
И зачу Адонија и све званице које беху с њим, пошто једоше; зачу и Јоав глас трубни, па рече: Каква је то вика и врева у граду?
42 Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”
И докле он још говораше, гле, дође Јонатан син Авијатара свештеника; и Адонија му рече: Ходи, јер си јунак и носиш добре гласе.
43 Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu.
А Јонатан одговори и рече Адонији: Та, господар наш, цар Давид, постави Соломуна царем.
44 Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu,
Јер цар посла с њим Садока свештеника и Натана пророка и Венају, сина Јодајевог, и Херетеје и Фелетеје, и посадише га на цареву мазгу.
45 ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo.
И помазаше га Садок свештеник и Натан пророк код Гиона за цара, и отидоше оданде веселећи се тако да је град узаврео; то је вика коју чусте.
46 Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu.
И Соломун је већ сео на царски престо.
47 Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake,
И дошле су слуге цареве, и благословише господара нашег, цара Давида говорећи: Да Бог прослави име Соломуново још већма него твоје, и престо његов да подигне још више него твој. И поклони се цар на постељи својој.
48 inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’”
Још овако рече цар: Да је благословен Господ Бог Израиљев, који даде данас ко ће седети на престолу мом, да виде моје очи.
49 Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana.
Тада се препадоше, и усташе све званице Адонијине, и отидоше свак својим путем.
50 Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe.
А Адонија бојећи се Соломуна уста и отиде, и ухвати се за рогове олтару.
51 Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’”
И јавише Соломуну говорећи: Ено, Адонија се уплашио од цара Соломуна, и ено га, ухватио се за рогове олтару, и вели: Нека му се закуне цар Соломун да неће убити слугу свог мачем.
52 Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.”
А Соломун рече: Ако буде поштен човек, ни длака с главе његове неће пасти на земљу; али ако се нађе зло на њему, погинуће.
53 Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”
И тако посла цар Соломун, те га доведоше од олтара; и кад дође, поклони се цару Соломуну; а Соломун му рече: Иди кући својој.

< 1 Mafumu 1 >