< 2 Mafumu 18 >

1 Mʼchaka chachitatu cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Hezekiya mwana wa Ahazi mfumu ya Yuda analowa ufumu.
In the thridde yeer of Osee, sone of Hela, kyng of Israel, regnyde Ezechie, sone of Achaz, kyng of Juda.
2 Anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Abi, mwana wa Zekariya.
He was of fyue and twenti yeer, whanne he bigan to regne, and he regnyde in Jerusalem nyne and twenti yeer; the name of his modir was Abisa, douyter of Zacharie.
3 Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova monga anachitira Davide kholo lake.
And he dide that, that was good bifor the Lord, bi alle thingis, which Dauid, his fadir, hadde do.
4 Anachotsa malo opembedzerako mafano, anaphwanya miyala yachipembedzo ndiponso anadula mafano a Asera. Iye anaphwanya njoka yamkuwa imene Mose anapanga, pakuti mpaka kufikira nthawi imeneyi Aisraeli amafukiza lubani kwa njoka imeneyi. (Imatchedwa Nehusitani).
And he distriede hiye places, and al to-brak ymagis, and kittide doun wodis, and he brak the brasun serpent, whom Moyses hadde maad; for `til to that tyme the sones of Israel brenten encense to it; and he clepide the name therof Noestam.
5 Hezekiya anadalira Yehova Mulungu wa Israeli. Kotero panalibe wina wofanana naye pakati pa mafumu onse a Yuda, asanakhale mfumu kapena atakhala kale mfumu.
And he hopide in the Lord God of Israel; therfor aftir hym noon was lijk hym of alle the kyngis of Juda, but `and nether in tho kyngis that weren bifor hym.
6 Iye anakangamira Yehova ndipo sanamusiye koma anasunga malamulo amene Yehova anapatsa Mose.
And he cleuyde to the Lord, and yede not awei fro hise steppis, and he dide the comaundementis of the Lord, whiche the Lord comaundide to Moises;
7 Ndipo Yehova anali naye ndipo kulikonse kumene anapita zinthu zinkamuyendera bwino. Iye anagalukira mfumu ya ku Asiriya ndipo sanayitumikirenso.
wherfor and the Lord was with hym, and he gouernede wiseli hym silf in alle thingis, to whiche he yede forth. Also he rebellide ayens the kyng of Assiriens, and therfor he seruede not to `that kyng of Asseriens;
8 Iye anakantha Afilisti kuyambira ku nsanja ya alonda mpaka ku mzinda wotetezedwa. Anakafika mpaka ku Gaza ndi ku malire ake.
and he smoot Philisteis `til to Gazam, and alle the termes of hem, fro the tour of keperis `til to a citee maad strong.
9 Mʼchaka chachinayi cha Mfumu Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chiwiri cha Hoseya mwana wa Ela mfumu ya Israeli, Salimenezeri, mfumu ya ku Asiriya anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Samariya ndi kuwuzinga
In the fourthe yeer of kyng Ezechie, that was the seuenthe yeer of Osee, sone of Hela, kyng of Israel, Salmanazar, kyng of Assiriens, stiede to Samarie,
10 Asiriya analanda mzindawu patatha zaka zitatu. Choncho mzinda wa Samariya unalandidwa chaka chachisanu ndi chimodzi cha Hezekiya, chimene chinali chaka chachisanu ndi chinayi cha Hoseya mfumu ya Israeli.
and fauyt ayens it, and took it. For after thre yeer, in the sixte yeer of Ezechie, that is, in the nynthe yeer of Osee, kyng of Israel, Samarie was takun;
11 Mfumu ya ku Asiriya inatenga Aisraeli kupita nawo ku ukapolo ku Asiriya ndipo anakawakhazika ku Hala, ku Habori pafupi ndi mtsinje wa Gozani ndi mʼmizinda ya Amedi.
and the kyng of Assiriens translatide Israel in to Assiriens, and settyde hem in Haila, and in Habor, ryueris of Gozam, in the citees of Medeis;
12 Izi zinachitika chifukwa sanamvere zonena za Yehova Mulungu wawo, koma anaphwanya pangano lake ndi zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anawalamula. Iwo sanamvere malamulowo kapena kuwagwiritsa ntchito.
for thei herden not the vois of her Lord God, but thei braken his couenaunt; thei herden not, nether diden alle thingis, whiche Moises, the seruaunt of the Lord, comaundide.
13 Mʼchaka chakhumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, nayilanda.
In the fourtenthe yeer of kyng Ezechie, Senacherub, kyng of Assiryens, stiede to alle the strengthide citees of Juda, and took tho.
14 Choncho Hezekiya mfumu ya Yuda anatumiza uthenga kwa mfumu ya ku Asiriya ku Lakisi wonena kuti, “Ine ndalakwa. Chokani kuno ndipo ndidzakupatsani chilichonse chimene munene.” Mfumu ya ku Asiriya inalamula mfumu Hezekiya, mfumu ya Yuda, kuti azipereka makilogalamu a siliva okwana 3,000 ndi makilogalamu a golide 1,000.
Thanne Ezechie, kyng of Juda, sente messangeris to the kyng of Assiriens in to Lachis, and seide, Y haue synned; go awei fro me, and Y schal bere `al thing, which thou schalt putte to me. Therfor the kyng of Asseriens puttide on Ezechie, kyng of Juda, thre hundrid talentis of siluer, and thretti talentis of gold.
15 Mfumu Hezekiya inapereka siliva yense amene anapezeka mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba zosungiramo chuma cha mfumu.
And Ezechie yaf al the siluer, that was foundun in the hows of the Lord, and in the kyngis tresories.
16 Nthawi imeneyi Hezekiya mfumu ya Yuda anakanganula golide amene anakuta zitseko ndi mphuthu za chipata cha Nyumba ya Yehova namupereka kwa mfumu ya ku Asiriya.
In that tyme Ezechie brak the yatis of the temple of the Lord, and the platis of gold, whiche he hadde fastned, and he yaf tho to the kyng of Assiriens.
17 Mfumu ya ku Asiriya inatuma Taritani, Rabusarisi ndi Rabusake pamodzi ndi gulu lalikulu la ankhondo, kwa Mfumu Hezekiya ku Yerusalemu kuchokera ku Lakisi. Iwo anafika ku Yerusalemu nakayima pafupi ndi ngalande ya madzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu waukulu wopita ku malo a Munda wa Mmisiri Wochapa.
Forsothe the kyng of Assiriens sente Thercha and Rabsaces fro Lachis to kyng Ezechie, with strong hond to Jerusalem; and whanne thei hadden stied, thei camen to Jerusalem, and stoden bisidis the water cundijt of the hiyere cisterne, which is in the weie of the fullere, `ethir toukere.
18 Iwo anayitana mfumu, ndipo Eliyakimu mwana wa Hilikiya woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa anthuwo.
And thei clepiden the kyng; sotheli Eliachym, sone of Elchie, the souereyn of the hows, and Sobna, scryueyn, and Joahe, chaunseler, the sone of Asaph, yeden out to hem.
19 Ndipo Rabusake anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “‘Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, ‘Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?’
And Rabsaces seide to hem, Speke ye to Ezechie, The grete kyng, the kyng of Assiriens, seith these thingis, What is this trist, in which thou enforsist?
20 Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
In hap thou hast take counsel, that thou woldist make thee redi to batel. In whom tristist thou, that thou be hardi to rebelle?
21 Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.’”
Whethir thou hopist in a `staf of rehed and brokun, Egipt, on which, if a man lenith, it schal be brokun, and schal entre in to hys hond, and schal peerse it? So is Farao, kyng of Egipt, to alle men that tristen on hym.
22 Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, “Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu.” Kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, “Muzipembedza pa guwa lansembe ili mu Yerusalemu?”
That if thou seist to me, We han trist in `oure Lord God; whether this is not he, whos hiye thingis and auteris Ezechie took awei, and comaundide to Juda and to Jerusalem, Ye schulen worschipe bifor this auter in Jerusalem?
23 “‘Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
Now therfor passe ye to my lord, the kyng of Assiriens, and Y schal yyue to you twei thousynde of horsis, and se ye, whether ye moun haue rideris of `tho horsis?
24 Ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo?
And hou moun ye withstonde bifor o prince of the leste seruauntis of my lord? Whether thou hast trist in Egipt, for charis and knyytis?
25 Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga malo ano popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.’”
Whether Y stiede with outen `Goddis wille to this place, that Y schulde distrie it? `The Lord seide to me, `Stie thou to this lond, and distrie thou it.
26 Pamenepo Eliyakimu mwana wa Hilikiya, Sebina ndi Yowa anawuza Rabusakeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
Forsothe Eliachym, sone of Elchie, and Sobna, and Joahe, seiden to Rabsaces, We preien, that thou speke bi the langage of Sirie to vs, thi seruauntis; for we vndirstondun this langage; and that thou speke not to vs bi the langage of Juwis, while the puple herith, which is on the wal.
27 Koma Rabusake anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
And Rabsaces answeride, `and seide, Whethir my lord sente me to thi lord and to thee, that Y schulde speke these wordis, and not rather to the men `that sitten on the wal, that thei ete her toordis, and drynke her pisse with you?
28 Tsono Rabusake anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
Therfor Rabsaces stood, and criede with greet vois bi langage of Jewis, and seide, Here ye the wordis of the greet kyng, the kyng of Assiriens.
29 Zimene mfumu ikunena ndi izi: ‘Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni mʼdzanja langa.
The kyng seith these thingis, Ezechie disceyue not you, for he may not delyuere you fro myn hond;
30 Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
nether yyue he trist to you on the Lord, and seie, The Lord delyuerynge schal delyuere vs, and this citee shal not be bitakun in the hond of the kyng of Assiriens;
31 “Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
nyle ye here Ezechie. For the kyng of Assiriens seith these thingis, Do ye with me that, that is profitable to you, and go ye out to me; and eche man schal ete of his vyner, and of his fige tree, and ye schulen drynke watris of youre cisternes,
32 mpaka nditabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanuli, dziko la tirigu ndi vinyo watsopano, dziko la chakudya ndi minda ya mipesa, dziko la mitengo ya olivi ndi uchi. Sankhani moyo osati imfa! “Musamvere zonena Hezekiya, pakuti iye akukusocheretsani ponena kuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’
til Y come, and translate you in to a lond which is lijk youre lond, in to a fruytful lond, and plenteuouse of wyn, a lond of breed, and of vineris, a lond of olyue trees, and of oile, and of hony; and ye schulen lyue, and ye schulen not die. Nyle ye here Ezechie, that disseyueth you, and seith, The Lord schal delyuere yow.
33 Kodi mulungu wa anthu a mtundu wina uliwonse wapulumutsapo dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
Whether the goddis of hethene men delyueriden her lond fro the hond of the kyng of Assiriens?
34 Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu, Hena ndi Ivani? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
Where is god of Emath, and of Arphat? Where is god of Sapharuaym, of Ana, and of Aua? Whether thei delyueriden Samarie fro myn hond?
35 Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja langa? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
For who ben thei in alle goddis of londis, that delyueriden her cuntrey fro myn hond, that the Lord may delyuere Jerusalem fro myn hoond?
36 Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
Therfor the puple was stille, and answeride not ony thing to hym; for thei hadden take comaundement of the kyng, that thei schulden not answere to hym.
37 Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo ndi Yowa mwana wa Asafu, mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza Hezekiya zonse zimene anayankhula Rabusake uja.
And Eliachym, sone of Elchie, the souereyn of the hows, and Sobna, scryuen, and Joahe, chaunceler, the sone of Asaph, camen with to-rent clothis to Ezechie; and telden to hym the wordis of Rabsaces.

< 2 Mafumu 18 >