< 2 Mafumu 16 >

1 Mʼchaka cha 17 cha Peka mwana wa Remaliya, Ahazi mwana wa Yotamu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La dix-septième année de Pékach fils de Rémalia, Achaz fils de Jotham Roi de Juda, commença à régner.
2 Ahazi anakhala mfumu ali ndi zaka makumi awiri ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Iye sanachite zabwino pamaso pa Yehova Mulungu wake monga momwe Davide kholo lake ankachitira.
Achaz était âgé de vingt ans quand il commença à régner; et il régna seize ans à Jérusalem; et il ne fit point ce qui est droit devant l'Eternel son Dieu comme [avait fait] David son père.
3 Iye anayenda mʼnjira ya mafumu a Israeli mpaka kupereka mwana wake wamwamuna pa moto ngati nsembe yopsereza, potsatira zonyansa za anthu a mitundu imene Yehova anayipirikitsa mʼdzikomo Aisraeli asanafike.
Mais il suivit le train des Rois d'Israël, et même il fit passer son fils par le feu, selon les abominations des nations que l'Eternel avait chassées de devant les enfants d'Israël.
4 Iyeyo ankapereka nsembe ndi kufukiza lubani pa malo opembedzera mafano, pa mapiri ndi pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
Il sacrifiait aussi et faisait des encensements dans les hauts lieux, et sur les coteaux, et sous tout arbre verdoyant.
5 Ndipo Rezini mfumu ya Aramu ndi Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli anapita kukachita naye nkhondo ku Yerusalemu ndipo anazinga Ahazi, koma sanathe kumugonjetsa.
Alors Retsin Roi de Syrie, et Pékach fils de Rémalia Roi d'Israël, montèrent contre Jérusalem pour lui faire la guerre, et ils assiégèrent Achaz; mais ils n'en purent point venir à bout par les armes.
6 Nthawi imeneyo Rezini mfumu ya Aramu anatenganso Elati ndi kumubwezera kwa Aaramu, nathamangitsa anthu a ku Yuda mu Elatimo. Aedomu anapita kukakhala ku Elati ndipo akukhalako mpaka lero lino.
En ce temps-là Retsin Roi de Syrie, remit Elath en la puissance des Syriens, car il déposséda les Juifs d'Elath, et les Syriens entrèrent à Elath, et ils y ont demeuré jusqu'à ce jour.
7 Ahazi anatuma amithenga kwa Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya kuti, “Ine ndine mtumiki wanu ndipo ndili pansi panu. Bwerani mudzandipulumutse mʼdzanja la mfumu ya Aramu ndiponso mʼdzanja la mfumu ya Israeli amene akundithira nkhondo.”
Or Achaz avait envoyé des messagers à Tiglath-piléser Roi des Assyriens, pour lui dire: Je suis ton serviteur, et ton fils; monte et délivre-moi de la main du Roi des Syriens, et de la main du Roi d'Israël, qui s'élèvent contre moi.
8 Ndipo Ahazi anatenga siliva ndi golide amene anamupeza mʼNyumba ya Yehova ndi mosungira chuma cha nyumba ya mfumu ndi kutumiza ngati mphatso kwa mfumu ya ku Asiriya.
Et Achaz avait pris l'argent et l'or qui s'était trouvé dans la maison de l'Eternel, et dans les trésors de la maison Royale, et il l'avait envoyé en don au Roi d'Assyrie.
9 Mfumu ya ku Asiriya inamvera pokathira nkhondo mzinda wa Damasiko ndi kuwulanda. Anthu a mu mzindamo anawatumiza ku Kiri ndipo anapha Rezini.
Et le Roi d'Assyrie y acquiesça, et monta à Damas, et la prit, et en transporta le peuple à Kir, et fit mourir Retsin.
10 Kenaka mfumu Ahazi inapita ku Damasiko kukakumana ndi Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya. Iye anaona guwa lansembe ku Damasiko kuja ndipo anatumiza chitsanzo chake kwa wansembe Uriya, osasiyapo nʼkanthu komwe kuti athe kulimanga.
Alors le Roi Achaz s'en alla au devant de Tiglath-piléser Roi d'Assyrie, à Damas; et le Roi Achaz ayant vu l'autel qui était à Damas, envoya à Urie le Sacrificateur la figure et le modèle de cet autel, selon toute la façon qu'il avait.
11 Choncho wansembe Uriya anamanga guwa lansembe molingana ndi chitsanzo chimene anamutumizira Mfumu Ahazi kuchokera ku Damasiko ndipo anatsiriza kumanga guwalo Ahazi asabwere kuchokera ku Damasiko kuja.
Et Urie le Sacrificateur bâtit un autel, suivant tout ce que le Roi Achaz avait mandé de Damas; Urie le Sacrificateur le fit tout semblable, en attendant que le Roi Achaz fût revenu de Damas.
12 Mfumu itabwera kuchokera ku Damasiko kuja ndi kuona guwalo, inasendera pafupi ndi kupereka nsembe paguwapo.
Et quand le Roi Achaz fut revenu de Damas, et eut vu l'autel, il s'en approcha, et offrit sur cet autel;
13 Mfumu inapereka nsembe yopsereza ndi nsembe ya chakudya. Inapereka nsembe yachakumwa ndi kuwaza magazi a nsembe yake yachiyanjano paguwapo.
Et fit fumer son holocauste et son sacrifice, et versa ses aspersions, et répandit le sang de ses sacrifices de prospérité sur cet autel-là.
14 Guwa lamkuwa limene linali pamaso pa Yehova analichotsa kutsogolo kwa nyumbayo, kulichotsa pakati pa guwa latsopano ndi Nyumba ya Yehova ndi kukaliyika cha kumpoto kwa guwa latsopanolo.
Et quant à l'autel d'airain qui était devant l'Eternel, il le fit reculer de devant la maison, d'entre l'autel et la maison de l'Eternel, et le mit à côté de cet [autre] autel, vers le Septentrion.
15 Pamenepo Mfumu Ahazi inalamula wansembe Uriya kuti, “Pa guwa lalikulu latsopano uziperekapo nsembe yopsereza ya mmawa ndi nsembe ya chakudya ya madzulo, nsembe yopsereza ya mfumu ndi nsembe yake ya chakudya ndiponso nsembe za anthu onse a mʼdziko, za chakudya ndi chakumwa. Pa guwali uziwazapo magazi a nsembe zonse zopsereza ndi nsembe zina zonse. Koma ine ndizigwiritsa ntchito guwa lansembe lamkuwa pofuna kufunsira nzeru.”
Et le Roi Achaz commanda à Urie le Sacrificateur, et lui dit: Fais fumer l'holocauste du matin, et l'oblation du soir, et l'holocauste du Roi avec son gâteau, et l'holocauste de tout le peuple du pays avec leurs gâteaux et leurs aspersions sur le grand autel, et répands tout le sang des holocaustes et tout le sang des sacrifices sur cet autel; mais l'autel d'airain sera pour moi, afin de m'y enquérir [du Seigneur].
16 Ndipo wansembe Uriya anachita monga analamulira Mfumu Ahazi.
Et Urie le Sacrificateur fit comme le Roi Achaz lui avait commandé.
17 Mfumu Ahazi anachotsa maferemu a maphaka nachotsapo mabeseni. Iye anatsitsa mbiya yayikulu imene inali pamwamba pa ngʼombe zamkuwa ndipo anayika pansi pa chiwundo cha miyala.
Le Roi Achaz retrancha aussi les embattements des soubassements, et en ôta les cuviers qui étaient dessus, et fit ôter la mer de dessus les bœufs d'airain, qui étaient dessous, et la mit sur un pavé de pierre.
18 Iye anachotsa kadenga ka pa Sabata kamene kanamangidwa mʼkati mwa Nyumba ya Yehova ndiponso anatseka chipata cholowera mfumu cha kunja kwa nyumba ya Yehova pofuna kukondweretsa mfumu ya ku Asiriya.
Il ôta aussi de la maison de l'Eternel le couvert du Sabbat qu'on avait bâti au Temple, et l'entrée du Roi qui était en dehors, à cause du Roi des Assyriens.
19 Ntchito zina za Ahazi ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des faits d'Achaz, lesquels il a faits, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
20 Ahazi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Hezekiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Puis Achaz s'endormit avec ses pères, et fut enseveli avec eux en la Cité de David; et Ezéchias son fils régna en sa place.

< 2 Mafumu 16 >