< 2 Mafumu 15 >

1 Mʼchaka cha 27 cha Yeroboamu mfumu ya Israeli, Azariya mwana wa Amaziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La vingt-septième année de Jéroboam Roi d'Israël, Hazaria fils d'Amatsia Roi de Juda régnait.
2 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 16 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 52. Amayi ake anali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
Il était âgé de seize ans quand il commença à régner, et il régna cinquante-deux ans à Jérusalem; sa mère avait nom Jécolia, [et] était de Jérusalem.
3 Iyeyo anachita zabwino pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
Il fit ce qui est droit devant l'Eternel, comme avait fait Amatsia son père.
4 Komabe malo opembedzerako mafano sanawachotse ndipo anthu anapitirizabe kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
Tellement qu'il n'y eut que les hauts lieux qui ne furent point ôtés; le peuple sacrifiait encore et faisait des encensements sur les hauts lieux.
5 Ndipo Yehova analanga mfumu ndi nthenda ya khate mpaka tsiku limene inamwalira. Tsono mfumuyo inkakhala mʼnyumba yakeyake yapadera. Mwana wake Yotamu ndiye amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu ndiponso ndiye amene ankalamulira anthu mʼdzikomo.
r l'Eternel frappa le Roi, qui fut lépreux jusqu'au jour qu'il mourut, et il demeura dans une maison séquestrée; et Jotham fils du Roi avait la charge de la maison, jugeant le peuple du pays.
6 Ntchito zina za Azariya ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des faits de Hazaria, tout ce, dis-je, qu'il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
7 Azariya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide. Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Hazaria s'endormit avec ses pères, et fut enseveli avec ses pères en la Cité de David, et Jotham son fils régna en sa place.
8 Mʼchaka cha 38 cha Azariya mfumu ya Yuda, Zekariya mwana wa Yeroboamu anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira miyezi isanu ndi umodzi.
La trente-huitième année de Hazaria Roi de Juda, Zacharie fils de Jéroboam commença à régner sur Israël à Samarie, [et il régna] six mois.
9 Ndipo iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga anachitira makolo ake. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
Et il fit ce gui déplaît à l'Eternel, comme avaient fait ses pères; il ne se détourna point des péchés de Jéroboam fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
10 Salumu mwana wa Yabesi anachitira chiwembu Zekariya. Anamukantha anthu akuona, namupha, ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
Or Sallum fils de Jabés, fit une conspiration contre lui, et le frappa en la présence du peuple, et le tua, et il régna en sa place.
11 Ntchito zina za Zekariya, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Quant au reste des faits de Zacharie, voilà, ils sont écrits au Livre des Chroniques des Rois d'Israël.
12 Awa ndiwo mawu a Yehova amene anayankhula kwa Yehu kuti, “Ana ako adzalamulira Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
C'est là la parole de l'Eternel laquelle il avait prononcée à Jéhu, en disant: Tes fils seront assis sur le trône d'Israël jusqu'à la quatrième génération; et il arriva ainsi.
13 Salumu mwana wa Yabesi anakhala mfumu mʼchaka cha 39 cha ulamuliro wa Uziya mfumu ya Yuda ndipo analamulira mu Samariya mwezi umodzi.
Sallum fils de Jabés commença à régner la trente-neuvième année d'Hozias Roi de Juda, et il ne régna que l'espace d'un mois entier à Samarie.
14 Ndipo Menahemu mwana wa Gadi anachoka ku Tiriza napita ku Samariya nakantha Salumu mwana wa Yabesi ku Samariya, namupha ndipo iye analowa ufumu mʼmalo mwake.
Car Ménahem fils de Gadi, qui était de Tirtsa, monta, et entra dans Samarie, et frappa Sallum fils de Jabés à Samarie, et le tua, et il régna en sa place.
15 Ntchito zina za Salumu ndiponso za chiwembu chimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Quant au reste des faits de Sallum, et quant à la conspiration qu'il fit, voilà, ces choses sont écrites au Livre des Chroniques des Rois d'Israël.
16 Nthawi imeneyo Menahemu, kuchokera ku Tiriza, anakathira nkhondo mzinda wa Tipisa ndi anthu onse amene anali mʼmenemo ndi dera lonse lozungulira chifukwa iwo anakana kutsekula zipata zawo. Iye anatenga katundu yense mu mzinda wa Tipisa ndi kutumbula akazi onse oyembekezera.
Et Ménahem battit Tiphsah, et tous ceux qui étaient dedans, et dans sa contrée, depuis Tirtsa, parce qu'elle ne lui avait point ouvert [les portes], et les tua; et il fendit toutes les femmes grosses qui s'y trouvèrent.
17 Mʼchaka cha 39 cha Azariya mfumu ya Yuda, Menahemu mwana wa Gadi anakhala mfumu ya Israeli ndipo analamulira mu Samariya zaka khumi.
La trente-neuvième année de Hazaria Roi de Juda, Ménahem fils de Gadi, commença à régner sur Israël, [il régna] dix ans en Samarie.
18 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Nthawi yonse ya ulamuliro wake sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
Et il fit ce qui déplaît à l'Eternel; il ne se détourna point des péchés de Jéroboam fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël, durant tout son temps.
19 Tsono Puli mfumu ya ku Asiriya inadzathira nkhondo dzikolo ndipo Menahemu anapatsa Puliyo makilogalamu 34,000 a siliva kuti amuthandize ndi kulimbikitsa ufumu wake.
Alors Pul, Roi des Assyriens, vint contre le pays; et Ménahem donna mille talents d'argent à Pul, afin qu'il lui aidât à affermir son Royaume entre ses mains.
20 Menahemu anapeza ndalamazo kudzera mu msonkho umene ankakhometsa Aisraeli. Munthu aliyense wachuma ankapereka masekeli a siliva makumi asanu kwa mfumu ya ku Asiriya. Choncho mfumu ya ku Asiriya inabwerera ndipo sinakhalenso mʼdzikomo.
Et Ménahem tira cet argent d'Israël, de tous ceux qui étaient puissants en biens, pour le donner au Roi des Assyriens, de chacun cinquante sicles d'argent; ainsi le Roi des Assyriens s'en retourna, et ne s'arrêta point au pays.
21 Ntchito zina za Menahemu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits de Ménahem, tout ce, dis-je, qu'il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois d'Israël?
22 Menahemu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Pekahiya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Ménahem s'endormit avec ses pères, et Pékachia son fils régna en sa place.
23 Mʼchaka cha makumi asanu a Azariya mfumu ya Yuda, Pekahiya mwana wa Menahemu anakhala mfumu ya Israeli mu Samariya ndipo analamulira zaka ziwiri.
La cinquantième année d'Hazaria Roi de Juda, Pékachia fils de Ménahem commença à régner sur Israël à Samarie, [et il régna] deux ans.
24 Pekahiya anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Iye sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, omwe anachimwitsa nawo Israeli.
Et il fit ce qui déplaît à l'Eternel, et ne se détourna point des péchés de Jéroboam fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
25 Ndipo Peka mwana wa Remaliya, mtsogoleri wake wa ankhondo, anamuchita chiwembu. Iye pamodzi ndi anthu makumi asanu a ku Giliyadi anapha Pekahiya pamodzi ndi Arigobu ndi Ariyeli mʼchipinda choteteza nyumba ya mfumu mu Samariya. Kotero Peka anapha Pekahiya ndipo analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Pékach fils de Rémalia son capitaine fit une conspiration contre lui, et le frappa à Samarie, au palais de la maison Royale, avec Argob et Arié, ayant avec soi cinquante hommes des enfants des Galaadites; ainsi il le tua, et il régna en sa place.
26 Ntchito zina za Pekahiya ndi zonse zimene anachita zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
Le reste des actions de Pékachia, tout ce, dis-je, qu'il a fait, voilà, il est écrit au Livre des Chroniques des Rois d'Israël.
27 Mʼchaka cha 52 cha Azariya mfumu ya Yuda, Peka mwana wa Remaliya anakhala mfumu ya Israeli ku Samariya ndipo analamulira zaka makumi awiri.
La cinquante et deuxième année d'Hazaria Roi de Juda, Pékach fils de Rémalia commença à régner sur Israël à Samarie, [et il régna] vingt ans.
28 Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
Et il fit ce qui déplaît à l'Eternel, il ne se détourna point des péchés de Jéroboam fils de Nébat, par lesquels il avait fait pécher Israël.
29 Nthawi ya Peka mfumu ya Israeli, Tigilati-Pileseri mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kudzalanda Iyoni, Abeli-Beti-Maaka, Yanowa, Kedesi ndi Hazori. Mfumu ya ku Asiriya inatenga Giliyadi ndi Galileya, kuphatikizanso madera onse a Nafutali ndipo anatumiza Aisraeli ku Asiriya.
Aux jours de Pékach Roi d'Israël, Tiglath-piléser Roi des. Assyriens, vint, et prit Hijon, et Abel-bethmahaca, et Janoah, et Kédés, et Hatsor, et Galaad, et la Galilée, même tout le pays de Nephthali, et en transporta le peuple en Assyrie.
30 Kenaka Hoseya mwana wa Ela anachitira chiwembu Peka mwana wa Remaliya. Anamukantha ndi kumupha ndipo anakhala mfumu mʼmalo mwake mʼchaka makumi awiri cha Yotamu mwana wa Uziya.
Or Hosée, fils d'Ela, fit une conspiration contre Pékach fils de Rémalia, et le frappa, et le tua, et il régna en sa place la vingtième année de Jotham fils de Hozias.
31 Ntchito zina za Peka ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
Le reste des faits de Pékach, tout ce, dis-je, qu'il a fait, voilà, il est écrit au Livre des Chroniques des Rois d'Israël.
32 Mʼchaka chachiwiri cha Peka mwana wa Remaliya mfumu ya Israeli, Yotamu mwana wa Uziya mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
La seconde année de Pékach fils de Rémalia Roi d'Israël, Jotham fils de Hozias, Roi de Juda commença à régner.
33 Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 16. Amayi ake anali Yerusa mwana wa Zadoki.
Il était âgé de vingt et cinq ans quand il commença à régner; et il régna seize ans à Jérusalem; sa mère avait nom Jérusa, [et] était fille de Tsadok.
34 Iye anachita zabwino pamaso pa Yehova monga anachitira Uziya abambo ake.
Il fit ce qui est droit devant l'Eternel; il fit comme Hozias son père avait fait.
35 Komabe malo opembedzera mafano sanawachotse ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
De sorte qu'il n'y eut que les hauts lieux qui ne furent point ôtés, le peuple sacrifiait encore et faisait des encensements dans les hauts lieux; ce fut lui qui bâtit la plus haute porte de la maison de l'Eternel.
36 Ntchito zina za Yotamu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
Le reste des faits de Jotham, tout ce, dis-je, qu'il a fait, n'est-il pas écrit au Livre des Chroniques des Rois de Juda?
37 (Nthawi imeneyo, Yehova anayamba kumatuma Rezini mfumu ya Aaramu ndi Peka mwana wa Remaliya kudzamenyana ndi Yuda).
En ces jours-là l'Eternel commença d'envoyer contre Juda Retsin Roi de Syrie et Pékach fils de Rémalia.
38 Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Et Jotham s'endormit avec ses pères, et fut enseveli en la Cité de David son père, et Achaz son fils régna en sa place.

< 2 Mafumu 15 >