< 2 Mafumu 10 >

1 Tsono Ahabu anali ndi ana aamuna 70 a ku Samariya. Ndipo Yehu analemba makalata nawatumiza ku Samariya kwa atsogoleri a mu mzinda wa Yezireeli, kwa akuluakulu ndiponso kwa amene ankalera ana a Ahabu, nati,
Forsothe seuenti sones in Samarie weren to Achab. Therfor Hieu wroot lettris, and sente in to Samarie to the beste men of the citee, and to the gretter men in birthe, and to alle the nurschis of Achab, and seide,
2 “Inu mukangolandira kalatayi, popeza ana a mbuye wanu ali ndi inu ndiponso muli ndi magaleta ndi akavalo, mzinda wotetezedwa ndi zida zankhondo,
Anoon as ye han take these lettris, ye that han the sones of youre lord, and the charis, and horsis, and stronge citees, and armeris,
3 sankhani mwana wa mbuye wanu amene ndi wooneka bwino ndiponso woyenera, mulowetseni ufumu wa abambo ake. Kenaka muchite nkhondo kuteteza nyumba ya mbuye wanu.”
chese the beste, and hym that plesith to you of the sones of youre lord, and sette ye him on the trone of his fadir, and fiyte ye for the hows of youre lord.
4 Koma anthuwo anachita mantha kwambiri ndipo anati, “Taonani, mafumu awiri sanathe kulimbana naye, nanga ife tingathe bwanji?”
And thei dredden greetli, and seiden, Lo! twei kyngis myyten not stonde bifor hym, and how schulen we mowe ayenstonde hym?
5 Choncho woyangʼanira nyumba ya mfumu, bwanamkubwa wa mzinda, akuluakulu ena ndiponso olera anawo anatumiza uthenga uwu kwa Yehu: “Ife ndife atumiki anu ndipo tidzachita chilichonse chomwe mutiwuze. Sitidzasankha munthu wina aliyense kukhala mfumu ndipo chitani chimene mukuganiza kuti nʼchabwino kwa inu.”
Therfor the souereyns of the hows, and the prefect of the citee, and the grettere men in birthe, and the nurchis senten to Hieu, and seiden, We ben thi seruauntis; what euer thingis thou comaundist, we schulen do, and we schulen not make a kyng to vs; do thou what euer thing plesith thee.
6 Ndipo Yehu anawalembera kalata yachiwiri yonena kuti, “Ngati inu muli mbali yanga ndi kuti mudzandimvera, mudule mitu ya ana a mbuye wanu ndipo mubwere nayo kwa ine ku Yezireeli mawa nthawi ngati yomwe ino.” Tsono ana a mfumu onse 70 anali pamodzi ndi akuluakulu a mu mzindamo, amene ankawalera.
Forsothe he wroot ayen to hem lettris the secunde tyme, and seide, If ye ben myne, and obeien to me, take ye the heedis of the sones of youre lord, and come ye to me in this same our to morewe in to Jezrael. Sotheli the sones of the kyng, seuenti men, weren nurschid at the beste men of the citee.
7 Kalatayo itafika, anthuwo anatenga ana a mfumu 70 aja ndi kuwapha onse. Anayika mitu yawo mʼmadengu ndi kuyitumiza ku Yezireeli kwa Yehu.
And whanne the lettris hadden come to hem, thei token the sones of the kyng, and killiden seuenti men, and puttiden the heedis of hem in coffyns; and senten to hym in to Jezrael.
8 Mthenga uja atafika, anamuwuza Yehu kuti, “Abweretsa mitu ya ana a mfumu.” Ndipo Yehu analamula kuti, “Unjikani mituyo mʼmilu iwiri pa chipata cha mzinda ndipo ikhale pamenepo mpaka mmawa.”
Forsothe a messanger cam to hym, and schewide to hym, and seide, Thei han brouyt the heedis of the sones of the king. Which answeride, Putte ye tho heedis to tweyne hepis, bisidis the entring of the yate, til the morewtid.
9 Mmawa mwake Yehu anatuluka. Iye anayimirira pamaso pa anthu onse ndipo anati, “Inu ndinu osalakwa. Ndine amene ndinachita chiwembu mbuye wanu ndi kumupha, koma kodi wapha anthu onsewa ndani?
And whanne it was cleer dai, he yede out, and stood, and seide to al the puple, Ye ben iust men; if Y conspiride ayens my lord, and killide hym, who killide alle these?
10 Koma dziwani tsono, kuti mawu amene Yehova anayankhula kunena za banja la Ahabu sadzapita padera. Yehova wachita chimene analonjeza kudzera mwa mtumiki wake Eliya.”
Therfor se ye now, that noon of the wordis of the Lord felde doun in to the erthe, whiche the Lord spak on the hows of Achab; and the Lord hath do that, that he spak in the hond of his seruaunt, Elie.
11 Choncho Yehu anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Yezireeli, pamodzinso ndi akuluakulu ake onse, abwenzi ake ndiponso ansembe ake, sanasiyeko ndi mmodzi yemwe wamoyo.
Therfor Hieu smoot alle that weren residue of the hows of Achab in Jezrael, and alle the beste men of hym, and knowun men, and preestis, til no relikis of hym leften.
12 Kenaka Yehu ananyamuka kupita ku Samariya. Atafika pa malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa,
And he roos, and cam in to Samarie; and whanne he hadde come to the chaumbir of schepherdis in the weie,
13 Yehu anakumana ndi abale ena a Ahaziya mfumu ya Yuda nawafunsa kuti, “Kodi ndinu yani?” Iwo anayankha kuti, “Ndife abale ake a Ahaziya, ndipo tabwera kulonjera banja la mfumu ndi ana a mfumukazi.”
he foond the britheren of Ocozie, kyng of Juda; and he seide to hem, Who ben ye? And thei answeriden, We ben the britheren of Ocozie, and we comen doun to grete the sones of the kyng and the sones of the queen.
14 Yehu analamula kuti, “Atengeni amoyo!” Choncho anawatenga amoyo ndipo anakawaphera ku chitsime cha ku malo otchedwa Beti-Ekedi wa abusa; anthu onse 42. Iye sanasiyepo ndi mmodzi yemwe wamoyo.
Which Hieu seide, Take ye hem quyke. And whanne thei hadden take hem quyke, thei strangliden hem in the cisterne, bisidis the chaumbre, two and fourti men; and he lefte not ony of hem.
15 Yehu atachoka kumeneko anakumana ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu, amene amabwera kudzakumana naye. Yehu anamulonjera nati kwa iye, “Kodi mtima wako uli bwino monga momwe mtima wanga ugwirizana nawo mtima wako?” Yehonadabu anayankha kuti, “Inde ndikugwirizana nawe.” Yehu anati, “Ngati ndi choncho, gwire dzanja.” Ndipo iye anaterodi, ndipo Yehu anamugwira dzanja namulowetsa mʼgaleta lake.
And whanne he hadde go fro thennus, he foond Jonadab, the sone of Rechab, in to meetyng of hym; and he blesside hym. And Hieu seide to hym, Whether thin herte is riytful with myn herte, as myn herte is with thin herte? And Jonadab seide, It is. Hieu seide, If `it is, yyue thin hond. Which yaf his hond to hym; and he reiside hym to hym silf in to the chare.
16 Yehu anati, “Tiye kuno uwone mmene ndikudziperekera kwa Yehova.” Ndipo anayenda naye mʼgaleta mwake.
And he seide to hym, Come thou with me, and se my feruent loue for the Lord.
17 Yehu atafika ku Samariya, anapha onse amene anatsala a mʼbanja la Ahabu ku Samariya; anawawonongeratu potsata mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa Eliya.
And he ledde hym, put in hys chare, in to Samarie. And he killide alle men that weren residue of Achab in Samarie `til to oon, bi the word of the Lord, which he spak bi Elie.
18 Ndipo Yehu anasonkhanitsa anthu onse pamodzi nawawuza kuti, “Ahabu ankatumikira Baala pangʼono chabe; Yehu adzamutumikira kwambiri.
Therfor Hieu gaderide to gidere alle the puple, and seide to hem, Achab worschipide Baal a litil, but Y schal worschipe hym more.
19 Tsopano itanani aneneri a Baala onse, atumiki ake onse ndi ansembe ake onse. Pasapezeke ndi mmodzi yemwe wotsala chifukwa ine ndidzapereka nsembe yayikulu kwa Baala. Aliyense amene alephere kubwera adzaphedwa.” Koma Yehu anachita zimenezi mwachinyengo ndi cholinga choti awononge atumiki onse a Baala.
Now therfor clepe ye to me alle the prophetis of Baal, and alle hise seruauntis, and alle hise preestis; `noon be that come not, for grete sacrifice is of me to Baal; who euer schal faile, he schal not lyue. Forsothe Hieu dide this bi tresoun, that he schulde distrie alle the worschipers of Baal.
20 Yehu anati, “Itanitsani msonkhano wodzalemekeza Baala.” Ndipo analengeza za msonkhanowo.
And he seide, Halewe ye a solempne day to Baal.
21 Pamenepo Yehu anatumiza mawu ku dziko lonse la Israeli ndipo atumiki onse a Baala anabwera; palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala. Iwo anadzaza nyumba ya Baala. Nyumbayo inadzaziratu kuchokera ku khoma lina mpaka ku khoma lina.
And he clepide, and sente in to alle the termes of Israel; and alle the seruauntis of Baal camen, `noon was residue, and sotheli `not oon was that cam not. And thei entriden in to the temple of Baal; and the hows of Baal was fillid, fro oon ende `til to `the tothir.
22 Ndipo Yehu anawuza munthu wosunga mikanjo kuti, “Bweretsa mikanjo yokwanira atumiki onse a Baala.” Ndipo iye anabweretsa mikanjoyo.
And he seide to hem that weren souereyns ouer the clothis, Bringe ye forth clothis to alle the seruauntis of Baal; and thei brouyten forth clothis to hem.
23 Kenaka Yehu ndi Yehonadabu mwana wa Rekabu analowa mʼnyumba ya Baala. Yehu anawawuza atumiki a Baala kuti, “Yangʼanitsitsani ndipo muone kuti muno musapezeke atumiki a Yehova, koma mukhale atumiki okhawo a Baala.”
And Hieu entride, and Jonadab, the sone of Rechab, in to the temple of Baal. And Hieu seide to the worschiperis of Baal, Enquere ye, and se, lest perauenture ony of the seruauntis of the Lord be with you; but that the seruauntis be aloone of Baal.
24 Choncho Yehu analowa kukapereka nsembe zina ndi nsembe zopsereza. Nthawi iyi nʼkuti Yehu atayika anthu 80 kunja kwa nyumbayo ndi chenjezo lakuti, “Ngati wina aliyense wa inu adzathawitsa wina aliyense wa anthu amene ndayika kuti muziwayangʼanira, munthu woteroyo adzaphedwa.”
Therfor thei entriden, to make slayn sacrifices, and brent sacrifices. Sotheli Hieu hadde maad redi to hym with outforth foure scoore men, and hadde seid to hem, Who euer schal fle of alle these, whiche Y schal brynge in to youre hondis, the lijf of hym schal be for the lijf of hym that ascapith.
25 Yehu atangotsiriza kupereka nsembe yopsereza, analamula alonda ndi akulu a ankhondo kuti, “Lowani ndipo mukawaphe ndipo musalole kuti wina athawe.” Choncho iwo anawapha ndi lupanga. Alonda ndi akulu a ankhondo anaponya mitembo ya anthuwo panja ndipo anakalowa mʼkati mwenimweni mwa nyumba ya Baala.
Forsothe it was don, whanne the brent sacrifice was fillid, Hieu comaundide to hise knyytis and duykis, Entre ye, and sle hem, that noon ascape. And the knyytis and duykis smytiden `hem bi the scharpnesse of swerd, and castiden forth. And `thei yeden into the citee of the temple of Baal,
26 Iwo anakatulutsa mwala wopatulika umene unali mʼnyumba ya Baala ndipo anawutentha.
and thei brouyten forth the ymage fro the temple of Baal,
27 Anawononga mwala wopatulika wa Baala ndi kugwetsa nyumba ya Baala, ndipo anthu anayisandutsa chimbudzi mpaka lero lino.
and brenten it, and al to braken it. Also thei destrieden the hows of Baal, and maden priuyes for it `til in to this dai.
28 Motero Yehu anawononga Baala mu Israeli.
Therfor Hieu dide awei Baal fro Israel;
29 Koma Yehuyo sanaleke machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati amene anachimwitsa nawo Israeli kupembedza mafano a golide a ana angʼombe ku Beteli ndi ku Dani.
netheles he yede not awei fro the synnes of Jeroboam, sone of Nabath, that made Israel to do synne, nether he forsook the goldun caluys, that weren in Bethel and in Dan.
30 Yehova anati kwa Yehu, “Chifukwa wachita bwino pokwaniritsa kuchita zabwino pamaso panga ndipo wachitira banja la Ahabu zonse zimene zinali mʼmaganizo anga, zidzukulu zako zidzakhala pa mpando waufumu wa Israeli mpaka mʼbado wachinayi.”
Forsothe the Lord seide to Hieu, For thou didist bisili that that was riytful, and pleside in myn yyen, and hast do ayens the hows of Achab alle thingis that weren in myn herte, thi sones `til to the fourthe generacioun schulen sitte on the trone of Israel.
31 Komatu Yehu sanasamalire kusunga lamulo la Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wake wonse. Iyeyo sanaleke machimo a Yeroboamu amene anachimwitsa nawo Israeli.
Forsothe Hieu kepte not, that he yede in the lawe of the Lord God of Israel in al his herte; for he yede not awei fro the synnes of Jeroboam, that made Israel to do synne.
32 Masiku amenewo Yehova anayamba kuchepetsa dziko la Israeli. Hazaeli anagonjetsa Aisraeli,
In tho daies the Lord bigan to be anoyed on Israel; and Asahel smoot hem in alle the coostis of Israel,
33 kuyambira kummawa kwa Yorodani, dziko lonse la Giliyadi (chigawo cha Gadi, Rubeni ndi Manase), kuchokera ku Aroeri pafupi ndi chigwa cha Arinoni kudutsa Giliyadi mpaka ku Basani.
fro Jordan ayens the eest coost, al the lond of Galaad, and of Gad, and of Ruben, and of Manasses, fro Aroer which is on the stronde of Arnon, and Galaad, and Baasan.
34 Ntchito zina za Yehu ndi zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?
Forsothe the residue of wordis of Hieu, and alle thingis whiche he dide, and his strengthe, whether these ben not writun in the book of wordis of daies of the kyngis of Israel?
35 Yehu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake ku Samariya. Ndipo Yehowahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
And Hieu slepte with hise fadris; and thei birieden hym in Samarie; and Joachaz, his sone, regnyde for hym.
36 Yehu analamulira Aisraeli ku Samariya zaka 28.
Forsothe the daies, in whiche Hieu regnede on Israel in Samarie, ben eiyte and twenti yeer.

< 2 Mafumu 10 >