< 2 Akorinto 9 >

1 Nʼkosafunika kuti ndikulembereni za utumiki othandiza anthu a Mulungu.
As to the services which are being rendered to God's people, it is really unnecessary for me to write to you.
2 Popeza ndikudziwa mtima wanu wofuna kuthandiza, ndipo ndakhala ndikuwawuza monyadira a ku Makedoniya za chimenechi. Ndimawawuza kuti inu a ku Akaya munakonzeka kale chaka chatha kuti mupereke. Ndipo changu chanu chapatsa chidwi ambiri mwa iwo kuti nawonso achitepo kanthu.
For I know your earnest willingness, on account of which I habitually boast of you to the Macedonians, pointing out to them that for a whole year you in Greece have been ready; and the greater number of them have been spurred on by your ardour.
3 Koma ndikutumiza abalewo kuti kukunyadirani kwathu pa zimenezi kutsimikizike kuti si kwachabe ndi kuti mukhale okonzeka monga ndinanenera.
Still I send the brethren in order that in this matter our boast about you may not turn out to have been an idle one; so that, as I have said, you may be ready;
4 Pakuti nditabwera kumeneko ndi abale ena a ku Makedoniya, ndikukupezani kuti simunakonzeke, tingadzachite manyazi chifukwa chokudalirani. Koma amene angadzachite manyazi kwambiri ndi inuyo.
for fear that, if any Macedonians come with me and find you unprepared, we--not to say you yourselves--should be put to the blush in respect to this confidence.
5 Choncho ndinaganiza kuti nʼkofunika kupempha abale kuti adzakuchezereni ineyo ndisanafike, ndikuti adzatsirize kukonzekera mphatso zomwe munalonjeza kupereka mowolowamanja. Motero mphatsoyo idzakhala yokonzeratu, ndipo idzakhala mphatso yoperekedwa mowolowamanja, osati mokakamizidwa.
I have thought it absolutely necessary therefore to request these brethren to visit you before I myself come, and to make sure beforehand that the gift of love which you have already promised may be ready as a gift of love, and may not seem to have been something which I have extorted from you.
6 Takumbukirani mawu awa: Amene adzala pangʼono, adzakololanso pangʼono, ndipo amene adzala zochuluka, adzakololanso zochuluka.
But do not forget that he who sows with a niggardly hand will also reap a niggardly crop, and that he who sows bountifully will also reap bountifully.
7 Munthu aliyense apereke chimene watsimikiza mu mtima mwake kuti apereka, osati monyinyirika kapena mokakamizidwa, pakuti Mulungu amakonda wopereka mokondwera.
Let each contribute what he has decided upon in his own mind, and not do it reluctantly or under compulsion. "It is a cheerful giver that God loves."
8 Ndipo Mulungu akhoza kukudalitsani kwambiri, kuti inuyo nthawi zonse mukhale ndi zinthu zokukwanirani, ndiponso ndi zina zochuluka kuti muthandize pa ntchito zonse zabwino.
And God is able to bestow every blessing on you in abundance, so that richly enjoying all sufficiency at all times, you may have ample means for all good works.
9 Paja analemba kuti, “Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya.” (aiōn g165)
As it is written, "He has scattered abroad, he has given to the poor, his almsgiving remains for ever." (aiōn g165)
10 Tsono Mulungu amene amapereka mbewu kwa wofesa, ndiponso chakudya kuti adye, adzaperekanso mbewu mʼnkhokwe zanu ndi kuzichulukitsa. Iye adzachulukitsanso zipatso za chilungamo chanu.
And God who continually supplies seed for the sower and bread for eating, will supply you with seed and multiply it, and will cause your almsgiving to yield a plentiful harvest.
11 Adzakulemeretsani pa zonse kuti mukhale owolowamanja pa nthawi zonse. Ndipo kuwolowamanja kwanu kudzera mwa ife, kudzakhala kuthokoza kwa Mulungu.
May you be abundantly enriched so as to show all liberality, such as through our instrumentality brings thanksgiving to God.
12 Ntchito imene mukugwirayi siyongothandiza kokha anthu a Mulungu kupeza zosowa, komanso ikuthandiza kuti anthu ambiri ayamike Mulungu.
For the service rendered in this sacred gift not only helps to relieve the wants of God's people, but it is also rich in its results and awakens a chorus of thanksgiving to God.
13 Chifukwa cha ntchito imene mwawatsimikizira nokha, anthu ena onse adzayamika Mulungu chifukwa cha kumvera kwanu kumene kumaonekera pamene mukuvomereza Uthenga Wabwino wa Khristu, ndiponso chifukwa chowagawira mowolowamanja iwowo pamodzi ndi wina aliyense.
For, by the practical proof of it which you exhibit in this service, you cause God to be extolled for your fidelity to your professed adherence to the Good News of the Christ, and for the liberality of your contributions for them and for all who are in need,
14 Ndipo iwowo adzakupemphererani mwachikondi chifukwa cha chisomo choposa chimene Ambuye wakupatsani.
while they themselves also in supplications on your behalf pour out their longing love towards you because of God's surpassing grace which is resting upon you.
15 Tiyamike Mulungu chifukwa cha mphatso zake zosaneneka!
Thanks be to God for His unspeakably precious gift!

< 2 Akorinto 9 >