< 2 Akorinto 10 >

1 Mwa kufatsa ndi kuleza mtima kwa Khristu, ndikukupemphani, ine Paulo amene anthu ena amati ndimachita manyazi tikaonana maso ndi maso ndi inu, koma wosaopa pamene ndili kutali nanu!
But as for me Paul, I entreat you by the gentleness and self-forgetfulness of Christ--I who when among you have not an imposing personal presence, but when absent am fearlessly outspoken in dealing with you.
2 Ndikukupemphani kuti ndikadzafika kumeneko ndisadzachite kuyankhula mwamphamvu monga mmene ndimayembekezera kudzachita kwa anthu ena amene amaganiza kuti machitidwe athu ndi ofanana ndi anthu a dziko lapansi.
I beseech you not to compel me when present to make a bold display of the confidence with which I reckon I shall show my 'courage' against some who reckon that we are guided by worldly principles.
3 Ngakhale ife timakhala mʼdziko lapansi, sitimenya nkhondo monga mmene dziko lapansi limachitira.
For, though we are still living in the world, it is no worldly warfare that we are waging.
4 Pakuti zida zathu zankhondo si zida za dziko lapansi. Koma ndi mphamvu zochokera kwa Mulungu zotha kugwetsa malinga.
The weapons with which we fight are not human weapons, but are mighty for God in overthrowing strong fortresses.
5 Timagonjetsa maganizo onse onyenga ndiponso kudzikuza kulikonse kolimbana ndi anthu kuti asadziwe Mulungu. Ndipo timagonjetsa ganizo lililonse kuti limvere Khristu.
For we overthrow arrogant 'reckonings,' and every stronghold that towers high in defiance of the knowledge of God, and we carry off every thought as if into slavery--into subjection to Christ;
6 Ndipo ife tidzakhala okonzeka kulanga aliyense wosamvera ngati inuyo mutakhala omvera kwenikweni.
while we hold ourselves in readiness to punish every act of disobedience, as soon as ever you as a Church have fully shown your obedience.
7 Inu mukuweruza potengera zimene maso anu akuona. Ngati wina akutsimikiza kuti ndi wake wa Khristu, iye aganizenso kuti ifenso ndife a Khristu monga iye.
Is it outward appearances you look to? If any man is confident as regards himself that he specially belongs to Christ, let him consider again and reflect that just as he belongs to Christ, so also do we.
8 Tsono ngakhale nditadzitama momasuka za ulamuliro umene Ambuye anatipatsa woti tikukuzeni osati kukuwonongani, ndithu sindidzachita manyazi.
If, however, I were to boast more loudly of our Apostolic authority, which the Lord has given us that we may build you up, not pull you down, I should have no reason to feel ashamed.
9 Ine sindikufuna kuoneka ngati ndikukuopsezani ndi makalata anga.
Let it not seem as if I wanted to frighten you by my letters.
10 Pakuti ena amati, “Makalata ake ndi awukali ndi amphamvu koma maonekedwe a thupi lake ndi wosagwira mtima ndipo mayankhulidwe ake ndi achabechabe.”
For they say "His letters are authoritative and forcible, but his personal presence is unimpressive, and as for eloquence, he has none."
11 Anthu oterewa ayenera kuzindikira kuti zomwe timalemba mʼmakalata tili kutali ndi zomwe tidzakhale tili komweko.
Let such people take this into their reckoning, that whatever we are in word by our letters when absent, the same are we also in act when present.
12 Sitikudziyika kapena kudzifananiza tokha ndi anthu ena amene amadziyenereza okha. Pamene akudzifanizira okha podziyerekeza ndi anzawo a mʼgulu lawo lomwe, ndi opanda nzeru.
For we have not the 'courage' to rank ourselves among, or compare ourselves with, certain persons distinguished by their self-commendation. Yet they are not wise, measuring themselves, as they do, by one another and comparing themselves with one another.
13 Komabe, ifeyo sitidzitama modutsa malire ake enieni, koma kudzitama kwathu kudzalekeza mʼmalire amene Mulungu anatiyikira, malire ake ndi mpaka kwa inu.
We, however, will not exceed due limits in our boasting, but will keep within the limits of the sphere which God has assigned to us as a limit, which reaches even to you.
14 Pakuti sitikudzitama modutsa malire ngati kuti sitinafike kwa inu, popeza tinali oyamba kufika kwa inu ndi Uthenga Wabwino wa Khristu.
For there is no undue stretch of authority on our part, as though it did not extend to you. We pressed on even to Corinth, and were the first to proclaim to you the Good News of the Christ.
15 Choncho sitinyadiranso ntchito imene ena anayigwira. Chiyembekezo chathu nʼchakuti, pamene chikhulupiriro chanu chikukulirakulira, dera lathu la ntchito pakati panu lidzakulanso kwambiri,
We do not exceed our due limits, and take credit for other men's labours; but we entertain the hope that, as your faith grows, we shall gain promotion among you--still keeping within our own sphere--promotion to a larger field of labour,
16 kuti tikalalikire Uthenga Wabwino mu zigawo zina kupitirira kwanuko. Pakuti sitikufuna kudzitama pa ntchito yogwira ena kale mʼdera la munthu wina.
and shall tell the Good News in the districts beyond you, not boasting in another man's sphere about work already done by him.
17 Koma, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
But "whoever boasts, let his boast be in the Lord."
18 Pakuti munthu amene amavomerezedwa, si amene amadziyenereza yekha, koma munthu amene Ambuye amuyenereza.
For it is not the man that commends himself who is really approved, but he whom the Lord commends.

< 2 Akorinto 10 >