< 2 Mbiri 32 >
1 Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
Après ces choses et cette fidélité, Sennachérib, roi d'Assyrie, arriva, entra en Juda, campa contre les villes fortifiées et eut l'intention de les gagner pour lui.
2 Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
Lorsqu'Ézéchias vit que Sennachérib était venu et qu'il projetait de combattre Jérusalem,
3 iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
il consulta ses princes et ses hommes forts pour arrêter les eaux des sources qui étaient à l'extérieur de la ville, et ils l'aidèrent.
4 Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
Alors beaucoup de gens se rassemblèrent et ils arrêtèrent toutes les sources et le ruisseau qui coulait au milieu du pays, en disant: « Pourquoi les rois d'Assyrie viendraient-ils et trouveraient-ils de l'eau en abondance? »
5 Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
Il prit courage, rebâtit toute la muraille abattue, l'éleva jusqu'aux tours, avec l'autre muraille en dehors, et renforça Millo dans la ville de David; il fabriqua des armes et des boucliers en abondance.
6 Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
Il plaça des chefs de guerre à la tête du peuple, les rassembla auprès de lui sur la grande place à la porte de la ville, et leur adressa des paroles d'encouragement en disant:
7 “Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
« Soyez forts et courageux. Ne craignez pas et ne soyez pas effrayés à cause du roi d'Assyrie et de toute la multitude qui est avec lui, car il y a plus grand que lui avec nous.
8 Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
Il a avec lui un bras de chair, mais Yahvé notre Dieu est avec nous pour nous secourir et mener nos combats. » Le peuple se reposa sur les paroles d'Ézéchias, roi de Juda.
9 Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
Après cela, Sennacherib, roi d'Assyrie, envoya ses serviteurs à Jérusalem (il était en train d'attaquer Lachish, et toutes ses forces étaient avec lui), à Ézéchias, roi de Juda, et à tous les Judéens qui étaient à Jérusalem, en disant:
10 “Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
Sennacherib, roi d'Assyrie, dit: « En qui vous confiez-vous, puisque vous restez assiégés à Jérusalem?
11 Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
Ézéchias ne vous persuade-t-il pas de vous livrer à la mort par la famine et par la soif, en disant: « Yahvé notre Dieu nous délivrera de la main du roi d'Assyrie? »
12 Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
Le même Ézéchias n'a-t-il pas enlevé ses hauts lieux et ses autels, et n'a-t-il pas donné cet ordre à Juda et à Jérusalem: « Vous vous prosternerez devant un seul autel, et vous y brûlerez des parfums? »
13 “Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
Ne savez-vous pas ce que moi et mes pères avons fait à tous les peuples du pays? Les dieux des nations de ces pays étaient-ils en mesure de délivrer leur pays de ma main?
14 Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
Qui, parmi tous les dieux de ces nations que mes pères ont dévastées, pouvait délivrer son peuple de ma main, pour que ton Dieu puisse te délivrer de ma main?
15 Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
Maintenant, ne vous laissez pas tromper par Ezéchias et ne vous persuadez pas de cette manière. Ne le croyez pas, car aucun dieu d'aucune nation ni d'aucun royaume n'a pu délivrer son peuple de ma main et de la main de mes pères. A combien moins forte raison votre Dieu vous délivrera-t-il de ma main? »
16 Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
Ses serviteurs parlèrent encore contre l'Éternel Dieu et contre son serviteur Ézéchias.
17 Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
Il écrivit aussi des lettres insultant Yahvé, le Dieu d'Israël, et parlant contre lui, disant: « Comme les dieux des nations du pays, qui n'ont pas délivré leur peuple de ma main, ainsi le Dieu d'Ézéchias ne délivrera pas son peuple de ma main. »
18 Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
Ils appelèrent d'une voix forte, dans la langue des Juifs, les habitants de Jérusalem qui étaient sur la muraille, pour les effrayer et les troubler, afin de prendre la ville.
19 Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
Ils parlaient du Dieu de Jérusalem comme des dieux des peuples de la terre, qui sont l'œuvre de mains d'hommes.
20 Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
Le roi Ézéchias et le prophète Ésaïe, fils d'Amoz, prièrent à cause de cela et crièrent au ciel.
21 Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
Yahvé envoya un ange qui extermina tous les vaillants hommes, les chefs et les capitaines dans le camp du roi d'Assyrie. Celui-ci s'en retourna, honteux de son visage, dans son pays. Comme il était entré dans la maison de son dieu, ceux qui étaient sortis de son propre corps l'y tuèrent par l'épée.
22 Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
Ainsi Yahvé sauva Ézéchias et les habitants de Jérusalem de la main de Sennacherib, roi d'Assyrie, et de la main de tous les autres, et il les guida de tous côtés.
23 Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
Beaucoup apportèrent des présents à Yahvé à Jérusalem et des objets précieux à Ézéchias, roi de Juda, de sorte qu'il fut désormais exalté aux yeux de toutes les nations.
24 Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
En ces jours-là, Ézéchias était en phase terminale, et il pria Yahvé; celui-ci lui parla et lui donna un signe.
25 Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
Mais Ézéchias ne rendit pas le bienfait qui lui avait été fait, parce que son cœur s'élevait. C'est pourquoi il y eut de la colère sur lui, sur Juda et sur Jérusalem.
26 Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
Cependant, Ézéchias s'humilia à cause de l'orgueil de son cœur, lui et les habitants de Jérusalem, de sorte que la colère de Yahvé ne s'abattit pas sur eux du temps d'Ézéchias.
27 Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
Ézéchias eut des richesses et des honneurs immenses. Il se pourvut de trésors pour l'argent, pour l'or, pour les pierres précieuses, pour les aromates, pour les boucliers, et pour toutes sortes de vases précieux;
28 Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
il se pourvut aussi de magasins pour la production du blé, du vin nouveau et de l'huile, et d'étables pour toutes sortes de bêtes, et de troupeaux en plis.
29 Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
Il se procura aussi des villes, et des biens en abondance pour le bétail et les troupeaux, car Dieu lui avait donné des biens en abondance.
30 Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
Ce même Ézéchias arrêta aussi la source supérieure des eaux du Gihon, et les fit descendre directement à l'ouest de la ville de David. Ézéchias prospéra dans toutes ses œuvres.
31 Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
Cependant, à propos des ambassadeurs des princes de Babylone, qui l'envoyèrent s'enquérir du prodige qui se faisait dans le pays, Dieu le laissa pour l'éprouver, afin qu'il sache tout ce qui était dans son cœur.
32 Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
Le reste des actes d'Ézéchias et ses bonnes actions, voici, ils sont écrits dans la vision du prophète Ésaïe, fils d'Amoz, dans le livre des rois de Juda et d'Israël.
33 Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
Ézéchias se coucha avec ses pères, et on l'enterra dans la montée des tombeaux des fils de David. Tout Juda et les habitants de Jérusalem l'honorèrent à sa mort. Manassé, son fils, régna à sa place.