< Ezara 1 >

1 Mʼchaka choyamba cha ufumu wa Koresi mfumu ya Perisiya, pofuna kukwaniritsa zimene anayankhula kudzera mwa Yeremiya, Yehova anayika maganizo mu mtima mwa Koresi mfumu ya Perisiya kuti alengeze mʼdziko lake lonse ndi mawu apakamwa ngakhalenso ochita kulemba.
Or, la première année de Cyrus, roi de Perse, pour que s'accomplisse la parole de Yahvé par la bouche de Jérémie, Yahvé excita l'esprit de Cyrus, roi de Perse, de sorte qu'il fit une proclamation dans tout son royaume et l'écrivit, disant,
2 Iye anati, “Koresi mfumu ya Perisiya ikunena kuti, “‘Yehova, Mulungu wakumwamba wandipatsa maufumu onse a dziko lapansi, ndipo wandipatsa udindo woti ndimumangire Nyumba ku Yerusalemu mʼdziko la Yuda.
Cyrus, roi de Perse, dit: « Yahvé, le Dieu du ciel, m'a donné tous les royaumes de la terre, et il m'a ordonné de lui bâtir une maison à Jérusalem, en Juda.
3 Aliyense wa inu amene ali wa Yehova, Mulungu wakeyo akhale naye. Tsono aliyense wa inu apite ku Yerusalemu, mʼdziko la Yuda kuti akamange Nyumba ya Yehova, Mulungu wa Israeli. Iyeyu ndi Mulungu amene ali mu Yerusalemu.
Que celui d'entre vous qui est de son peuple, que son Dieu soit avec lui, monte à Jérusalem, en Juda, et bâtisse la maison de l'Éternel, le Dieu d'Israël (c'est lui le Dieu), qui est à Jérusalem.
4 Ndipo kumalo kulikonse kumene otsalawo akukhala, athandizidwe ndi eni dzikolo powapatsa siliva, golide, katundu ndi ziweto ndi zopereka za ufulu zoti akapereke ku Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.’”
Celui qui restera, dans le lieu où il habite, que les gens de son lieu l'aident avec de l'argent, de l'or, des biens et des animaux, en plus de l'offrande volontaire pour la maison de Dieu qui est à Jérusalem.'"
5 Choncho atsogoleri a mabanja afuko la Yuda ndi la Benjamini komanso ansembe ndi Alevi, aliyense amene Mulungu anawutsa mtima wake, anayamba kukonzeka kupita kukamanga Nyumba ya Yehova imene ili ku Yerusalemu.
Et les chefs de famille de Juda et de Benjamin, les prêtres et les lévites, tous ceux que Dieu avait incités à monter, se levèrent pour bâtir la maison de l'Éternel à Jérusalem.
6 Onse oyandikana nawo anawathandiza powapatsa ziwiya za siliva ndi zagolide, kuphatikizaponso katundu ndi ziweto, ndiponso mphatso zamtengo wapatali, kuwonjezera pa zopereka zaufulu zija.
Tous ceux qui les entouraient renforcèrent leurs mains avec des objets d'argent, d'or, des biens, des animaux et des objets précieux, en plus de tout ce qui était offert volontairement.
7 Nayenso mfumu Koresi anatulutsa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara anazitenga kuzichotsa ku Yerusalemu ndi kuziyika mʼnyumba ya milungu yake.
Le roi Cyrus fit aussi sortir les ustensiles de la maison de l'Éternel, que Nabuchodonosor avait emportés de Jérusalem et mis dans la maison de ses dieux.
8 Koresi, mfumu ya ku Perisiya inatulutsa ziwiyazi ndi kuzipereka kwa Miteridati, msungichuma amene anaziwerenga pamaso pa Sesibazara nduna yayikulu ya dziko la Yuda.
Ces ustensiles, Cyrus, roi de Perse, les fit sortir par Mithredath, le trésorier, et en fit le compte à Schischbatsar, prince de Juda.
9 Chiwerengerochi chinali motere: Mabeseni agolide 30 mabeseni asiliva 1,000 a zopereka 29
Voici leur nombre: trente plateaux d'or, mille plateaux d'argent, vingt-neuf couteaux,
10 timiphika tagolide 230 timiphika tasiliva 410 ziwiya zina 1,000.
trente coupes d'or, quatre cent dix coupes d'argent d'une autre espèce, et mille autres ustensiles.
11 Ziwiya zonse zagolide ndi siliva pamodzi zinalipo 5,400. Zonsezi ndi zimene Sezi-Bazara anabwera nazo pamene otengedwa ukapolo aja ankabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku Babuloni.
Tous les vases d'or et d'argent étaient au nombre de cinq mille quatre cents. Sheshbazzar fit monter tout cela lorsque les captifs furent ramenés de Babylone à Jérusalem.

< Ezara 1 >