< 1 Samueli 31 >

1 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa.
AmaFilisti alwa-ke loIsrayeli; lamadoda akoIsrayeli abaleka phambi kwamaFilisti, awa efile entabeni yeGilibowa.
2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa.
AmaFilisti asenamathela kuSawuli lamadodana akhe; amaFilisti abulala uJonathani, loAbinadaba, loMaliki-Shuwa, amadodana kaSawuli.
3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.
Lempi yaba nzima kuSawuli, abatshoki bamfica, amadoda edandili; wasesiba lobuhlungu kakhulu ngabatshoki.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.” Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo.
USawuli wasesithi kumthwali wezikhali zakhe: Hwatsha inkemba yakho, ungigwaze ngayo, hlezi laba abangasokanga bafike bangigwaze, badlale kubi ngami. Kodwa umthwali wezikhali zakhe kavumanga, ngoba wesaba kakhulu. Ngakho uSawuli wathatha inkemba, waziwisela phezu kwayo.
5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi.
Lapho umthwali wezikhali zakhe ebona ukuthi uSawuli usefile, laye waziwisela phezu kwenkemba yakhe, wafa kanye laye.
6 Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.
Wafa-ke uSawuli lamadodana akhe amathathu lomthwali wezikhali zakhe labo bonke abantu bakhe ngalolosuku ndawonye.
7 Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
Lapho amadoda akoIsrayeli ayengaphetsheya kwesigodi layengaphetsheya kweJordani ebona ukuthi amadoda akoIsrayeli abalekile, lokuthi uSawuli lamadodana akhe sebefile, atshiya imizi, abaleka; amaFilisti asefika, ahlala kiyo.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa.
Kwasekusithi kusisa lapho amaFilisti efika ukuhlubula ababuleweyo, afica uSawuli lamadodana akhe amathathu bewile entabeni yeGilibowa.
9 Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo.
Asequma ikhanda lakhe, ahlubula izikhali zakhe, athumela elizweni lamaFilisti inhlangothi zonke ukumemezela imibiko endlini yezithombe zabo lebantwini.
10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.
Abeka izikhali zakhe endlini kaAshitarothi. Abophela isidumbu sakhe emdulini weBeti-Shani.
11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli,
Kwathi abahlali beJabeshi-Gileyadi sebezwile ngalokho amaFilisti akwenze kuSawuli,
12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto.
asukuma wonke amaqhawe, ahamba ubusuku bonke, athatha isidumbu sikaSawuli lezidumbu zamadodana akhe emdulini weBeti-Shani, eza eJabeshi, azitshisa khona.
13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
Asethatha amathambo abo, awangcwaba ngaphansi kwesihlahla setamarisiki eJabeshi, azila ukudla insuku eziyisikhombisa.

< 1 Samueli 31 >