< 1 Samueli 28 >

1 Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
Kwasekusithi ngalezonsuku amaFilisti abuthanisela impi amabutho awo ukuze alwe loIsrayeli. UAkishi wasesithi kuDavida: Yazi lokwazi ukuthi uzaphuma impi lami, wena labantu bakho.
2 Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
UDavida wasesithi kuAkishi: Sibili, wena uzakwazi ukuthi inceku yakho ingenzani. UAkishi wasesithi kuDavida: Ngakho, ngizakubeka ube ngumlindi wekhanda lami zonke izinsuku.
3 Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
USamuweli wayesefile, loIsrayeli wonke wayemlilele, bamngcwabela eRama, ngitsho emzini wakibo. USawuli wayebasusile-ke elizweni abalamadlozi labalumbayo.
4 Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
AmaFilisti asebuthana afika amisa inkamba eShunemi. USawuli wasebuthanisa uIsrayeli wonke, bamisa inkamba eGilibowa.
5 Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
Lapho uSawuli ebona inkamba yamaFilisti, wesaba, lenhliziyo yakhe yathuthumela kakhulu.
6 Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
Lapho uSawuli ebuza eNkosini, iNkosi kayimphendulanga langamaphupho langeUrimi langabaprofethi.
7 Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
USawuli wasesithi ezincekwini zakhe: Ngidingelani owesifazana oledlozi ukuze ngiye kuye, ngibuze kuye. Inceku zakhe zasezisithi kuye: Khangela, kulowesifazana oledlozi eEndori.
8 Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
USawuli wasezifihla isimo, wagqoka ezinye izigqoko, wahamba, yena lamadoda amabili laye; basebefika kowesifazana ebusuku. Wathi: Akungivumisele ngedlozi, ungenyusele engizamutsho kuwe.
9 Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
Kodwa owesifazana wathi kuye: Khangela, wena uyazi ukuthi uSawuli wenzeni, ukuthi ubaqumile elizweni abalamadlozi labalumbayo. Pho, uwuthiyelani umphefumulo wami ukungibulala?
10 Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
Kodwa uSawuli wafunga kuye ngeNkosi, esithi: Kuphila kukaJehova, isijeziso kasiyikuza kuwe ngaloludaba.
11 Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
Owesifazana wasesithi: Ngikwenyusele bani? Wasesithi: Ngenyusela uSamuweli.
12 Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
Lapho owesifazana ebona uSamuweli, wakhala ngelizwi elikhulu; owesifazana wasekhuluma kuSawuli esithi: Ungikhohliseleni? Ngoba unguSawuli.
13 Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
Inkosi yasisithi kuye: Ungesabi; kodwa ubonani? Owesifazana wasesithi kuSawuli: Ngibona onkulunkulu besenyuka emhlabathini.
14 Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
Wasesithi kuye: Sinjani isimo sakhe? Wasesithi: Kwenyuka ixhegu elembethe isembatho. Lapho uSawuli esesazi ukuthi nguSamuweli, wakhothama ngobuso emhlabathini, wakhonza.
15 Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
USamuweli wasesithi kuSawuli: Ungikhathazeleni ngokungenyusa? USawuli wasephendula wathi: Ngibandezelekile kakhulu, ngoba amaFilisti alwa lami, loNkulunkulu usukile kimi, kasangiphenduli, langesandla sabaprofethi langamaphupho. Ngakho ngikubizile ukuthi ungazise ukuthi ngenzeni.
16 Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
USamuweli wasesithi: Pho, ubuzelani kimi, lokhu iNkosi isisukile kuwe, yaba yisitha sakho?
17 Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
INkosi isizenzele njengokukhuluma kwayo ngesandla sami; iNkosi isidabule umbuso usuka esandleni sakho, yawunika umakhelwane wakho, uDavida.
18 Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
Njengoba ungalilalelanga ilizwi leNkosi, futhi ungenzanga ukuvutha kolaka lwayo kumaAmaleki, ngakho iNkosi yenzile linto kuwe lamuhla.
19 Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
Futhi iNkosi izanikela uIsrayeli laye kanye lawe esandleni samaFilisti; kusasa-ke wena lamadodana akho lizakuba lami. Lenkamba yakoIsrayeli iNkosi izayinikela esandleni samaFilisti.
20 Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
USawuli wasehle edilikela emhlabathini, ngokuphelela kobude bakhe, wesaba kakhulu ngenxa yamazwi kaSamuweli, njalo kwakungelamandla kuye, ngoba wayengadlanga kudla usuku lonke lobusuku bonke.
21 Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
Owesifazana wasesiza kuSawuli, wabona ukuthi wethukile kakhulu, wathi kuye: Khangela, incekukazi yakho ililalele ilizwi lakho, ngifakile umphefumulo wami esandleni sami, ngalalela amazwi owakhulume kimi.
22 Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
Ngakho-ke lawe akulalele ilizwi lencekukazi yakho, ngifake phambi kwakho ucezwana lwesinkwa ukuze udle, ukuze amandla abe kuwe nxa uhamba indlela yakho.
23 Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
Kodwa wala wathi: Kangiyikudla. Kodwa inceku zakhe kanye lowesifazana bamcindezela; waselalela ilizwi labo. Wasesukuma emhlabathini, wahlala embhedeni.
24 Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
Njalo owesifazana wayelethole elinonileyo endlini; waphangisa walihlaba; wathatha impuphu, wayixova, wabhaka isinkwa esingelamvubelo ngayo;
25 Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.
wasisondeza phambi kukaSawuli laphambi kwenceku zakhe; badla. Basukuma bahamba ngalobobusuku.

< 1 Samueli 28 >