< 1 Samueli 28 >
1 Mʼmasiku amenewo Afilisti anasonkhanitsa ankhondo awo kuti akamenyane ndi Aisraeli. Akisi anawuza Davide kuti, “Udziwe kuti iwe pamodzi ndi anthu ako mudzapita nane ku nkhondo.”
På den Tid samlede Filisterne deres Hær til Kamp for at angribe Israel. Da sagde Akisj til David: "Det må du vide, at du og dine Mænd skal følge med mig i Hæren!"
2 Davide anayankha kuti, “Tsono inu mudzaona zimene mtumiki wanune ndingachite.” Akisi anayankha kuti, “Chabwino ine ndidzakuyika iwe kukhala mlonda wanga moyo wako wonse.”
David svarede Akisj: "Godt, så skal du også få at se, hvad din Træl kan udrette!" Da sagde Akisj til David: "Godt, så sætter jeg dig til hele Tiden at vogte mit Liv!"
3 Nthawi imeneyi nʼkuti Samueli atamwalira, ndipo Aisraeli onse anamulira namuyika mʼmanda ku mzinda wake wa Rama. Sauli anali atachotsa mʼdzikomo anthu owombeza mawula ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa.
Samuel var død, og hele Israel havde holdt Klage over ham, og han var blevet jordet i Rama, hans By. Og Saul havde udryddet Dødemanerne og Besværgerne af Landet.
4 Tsono Afilisti anasonkhana nabwera kudzamanga misasa yawo ku Sunemu. Nayenso Sauli anasonkhanitsa Aisraeli onse ndi kumanga misasa yawo ku Gilibowa.
Imidlertid samlede Filisterne sig og kom og slog Lejr i Sjunem, og Saul samlede hele Israel, og de slog Lejr på Gilboa.
5 Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.
Da Saul så Filisternes Hær, grebes han af Frygt og blev såre forfærdet.
6 Choncho Sauli anafunsa nzeru kwa Yehova koma Yehova sanamuyankhe ngakhale kudzera mʼmaloto, kapena mwa Urimu ngakhalenso kudzera mwa aneneri.
Da rådspurgte Saul HERREN; men HERREN svarede ham ikke, hverken ved Drømme eller ved Urim eller ved Profeterne.
7 Kenaka Sauli anawuza nduna zake kuti, “Mundipezere mkazi amene amawombeza mawula kuti ndipite ndikafunse kwa iye.” Nduna zakezo zinamuyankha kuti, “Alipo mkazi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa ku Endori.”
Saul sagde derfor til sine Folk: "Opsøg mig en Kvinde, som kan mane; så vil jeg gå til hende, og rådspørge hende!" Hans Folk svarede ham: "I En-Dor er der en Kvinde, som kan mane!"
8 Kotero Sauli anadzizimbayitsa navala zovala zachilendo. Tsono iye pamodzi ndi anthu awiri anapita nakafika kwa mkazi uja usiku, ndipo anamupempha kuti, “Chonde ndifunsireni nzeru kwa mizimu ya anthu akufa. Koma makamaka munditulutsire mzimu wa amene ndimutchule.”
Da gjorde Saul sig ukendelig og tog andre Klæder på og gav sig på Vej, fulgt af to Mænd. Da de om Natten kom til Kvinden, sagde han: "Spå mig ved en Genfærdsånd og man mig den, jeg siger dig, frem!"
9 Koma mkaziyo anayankha kuti, “Ndithu inu mukudziwa chimene Sauli anachita. Paja iye anachotsa mʼdziko muno anthu onse owombeza ndi woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa. Chifukwa chiyani mukutchera moyo wanga msampha kuti ndiphedwe?”
Kvinden svarede ham: "Du ved jo, hvad Saul har gjort, hvorledes han har udryddet Dødemanerne og Besværgerne af Landet. Hvorfor vil du da lægge Snare for mit Liv og volde min Død?"
10 Koma Sauli analonjeza mkaziyo molumbira nati, “Pali Yehova wamoyo, iweyo sudzalangidwa chifukwa cha zimenezi.”
Da tilsvor Saul hende ved HERREN: "Så sandt HERREN lever, skal intet lægges dig til Last i denne Sag!"
11 Kenaka mkaziyo anafunsa, “Ndikuyitanireni yani?” Iye anati, “Undiyitanire Samueli.”
Så sagde Kvinden: "Hvem skal jeg da mane dig frem?" Han svarede: "Man mig Samuel frem!"
12 Pamene mkaziyo anaona Samueli anakuwa kwambiri, nawuza Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani inu mwandipusitsa? Inu ndinu Sauli!”
Kvinden så da Samuel og udstødte et højt Skrig; og Kvinden sagde til Saul: "Hvorfor har du ført mig bag Lyset? Du er jo Saul!"
13 Mfumuyo inamuwuza kuti, “Usaope. Kodi ukuona chiyani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Ndikuona mzimu ukutuluka pansi.”
Da sagde Kongen til hende: "Frygt ikke! Men hvad ser du?" Kvinden svarede Saul: "Jeg ser en Ånd stige op af Jorden!"
14 Sauli anafunsa, “Kodi mzimuwo ukuoneka motani?” Mkaziyo anayankha kuti, “Amene akutuluka ndi munthu wokalamba ndipo wavala mkanjo.” Apo Sauli anadziwa kuti anali Samueli ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.
Han sagde atter til hende: "Hvorledes ser han ud?" Hun svarede: "En gammel Mand stiger op, hyllet i en Kappe!" Da skønnede Saul, at det var Samuel, og han kastede sig med Ansigtet til Jorden og bøjede sig.
15 Samueli anafunsa Sauli kuti, “Nʼchifukwa chiyani wandivutitsa pondiyitana kuti ndibwere kuno?” Sauli anayankha kuti, “Ine ndavutika kwambiri mʼmaloto. Afilisti akumenyana nane, ndipo Mulungu wandifulatira. Iye sakundiyankhulanso, ngakhale kudzera mwa aneneri kapena maloto. Choncho ndakuyitanani kuti mundiwuze zoti ndichite.”
Men Samuel sagde til Saul: "Hvorfor har du forstyrret min Ro og kaldt mig frem?" Saul svarede: "Jeg er i stor Vånde; Filisterne angriber mig, og Gud har forladt mig og svarer mig ikke mere, hverken ved Profeterne eller ved Drømme. Derfor lod jeg dig kalde, for at du skal sige mig, hvad jeg skal gribe til."
16 Samueli anati, “Nʼchifukwa chiyani ukundifunsa ine, pakuti tsopano Yehova wakufulatira ndipo wasanduka mdani wako?
Da sagde Samuel: "Hvorfor spørger du mig, når HERREN har forladt dig og er blevet din Fjende?
17 Yehova wakuchita zimene ananeneratu kudzera mwa ine. Yehova wachotsa ufumu mʼmanja mwako ndipo waupereka kwa mnansi wako, kwa Davide.
HERREN har handlet imod dig, som han kundgjorde ved mig, og HERREN har revet Kongedømmet ud af din Hånd og givet din Medbejler David det.
18 Yehova wachita zimenezi lero chifukwa sunamvere mawu ake ndipo sunawawonongeretu Aamaleki.
Eftersom du ikke adlød HERREN og ikke lod hans glødende Vrede ramme Amalek, så har HERREN nu voldet dig dette;
19 Yehova adzapereka ndithu iweyo pamodzi ndi Aisraeli kwa Afilisti. Ndipo mmawa iweyo ndi ana ako mudzakhala ndi ine kuno. Ndithu Yehova adzapereka gulu lankhondo la Aisraeli kwa Afilisti.”
HERREN vil også give Israel i Filisternes Hånd sammen med dig! I Morgen skal både du og dine Sønner falde; også Israels Hær vil HERREN give i Filisternes Hånd!"
20 Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.
Da faldt Saul bestyrtet til Jorden, så lang han var, rædselsslagen over Samuels Ord; han var også ganske afkræftet, da han Døgnet igennem intet havde spist.
21 Mkazi uja tsono anasendera kufupi ndi Sauli, ndipo ataona kuti Sauli akuchita mantha, anamuwuza kuti, “Taonani, mdzakazi wanune ndakumverani. Ndayika moyo wanga pa chiswe ndipo ndamvera zimene munandiwuza.
Kvinden kom nu hen til Saul, og da hun så, at han var ude af sig selv af Skræk, sagde hun til ham: "Se, din Trælkvinde adlød dig; jeg satte mit Liv på Spil og adlød de Ord, du talte til mig.
22 Tsono inunso mumvere mawu a mdzakazi wanune. Mundilole kuti ndikupatseni ka buledi pangʼono kuti mukhale ndi mphamvu zoyendera pa ulendo wanu.”
Så adlyd du nu også din Trælkvinde; lad mig sætte et Stykke Brød frem for dig; spis det, for at du kan være ved Kræfter, når du går bort!"
23 Iye anakana ndipo anati, “Ayi, ine sindidya.” Koma nduna zake pamodzi ndi mkaziyo anamuwumiriza, ndipo anawamvera. Choncho anadzuka pansi nakhala pa bedi.
Men han værgede sig og sagde: "Jeg kan ikke spise!" Men da både hans Mænd og Kvinden nødte ham, gav han efter for dem, rejste sig fra Jorden og satte sig på Lejet.
24 Mkaziyo anali ndi mwana wangʼombe wonenepa ndipo anamupha mwachangu. Anatenga ufa nawukanyanga ndipo anaphika buledi wopanda yisiti.
Kvinden havde en Fedekalv i Huset, den skyndte hun sig at slagte; derpå tog hun Mel, æltede det og bagte usyret Brød deraf.
25 Tsono anapereka bulediyo kwa Sauli ndi nduna zake ndipo anadya. Pambuyo pake ananyamuka kupita kwawo usiku womwewo.
Så satte hun det frem for Saul og hans Mænd; og da de havde spist, stod de op og gik bort samme Nat.