< 1 Samueli 26 >
1 Anthu a ku Zifi anapita kwa Sauli ku Gibeya nati, “Davide akubisala ku phiri la Hakila, limene limayangʼanana ndi Yesimoni.”
Zifiterne kom til Saul i Gibea og sagde: "Mon ikke David holder sig skjult i Gibeat-Hakila over for Jesjimon!"
2 Choncho Sauli ananyamuka pamodzi ndi ankhondo ake 3,000 napita ku chipululu cha Zifi kukafunafuna Davide ku chipululuko.
Da brød Saul op og drog ned til Zifs Ørken med 3000 udsøgte Mænd af Israel for at søge efter David i Zifs Ørken;
3 Sauli anamanga msasa wake mʼmbali mwa njira yopita ku phiri la Hakila moyangʼanana ndi Yesimoni. Koma Davide anali mʼchipululumo. Davide ataona kuti Sauli amamulondola mpaka kumeneko,
og han slog Lejr i Gibeat-Hakila østen for Jesjimon ved Vejen, medens David opholdt sig i Ørkenen. Da David erfarede, at Saul var draget ind i Ørkenen for at forfølge ham,
4 iye anatumiza anthu okazonda ndipo anapeza kuti Sauli wafikadi ndithu.
udsendte han Spejdere og fik at vide, at Saul var kommet til Nakon.
5 Tsono Davide ananyamuka napita kumalo kumene Sauli anamanga misasa. Iye anaona pamene Sauli ndi Abineri mwana wa Neri mkulu wa ankhondo anagona. Sauli anagona mʼkati mwa tenti ndipo asilikali anagona momuzungulira.
Da stod David op og begav sig til det Sted, hvor Saul havde lejret sig, og David fik Øje på det Sted, hvor Saul og hans Hærfører Abner, Ners Søn, lå; det var i Vognborgen, Saul lå, og hans Folk var lejret rundt om ham.
6 Ndipo Davide anafunsa Ahimeleki Mhiti ndi Abisai mwana wa Zeruya, mʼbale wa Yowabu kuti, “Ndani adzapita nane ku msasa kwa Sauli?” Abisai anayankha kuti, “Ine ndidzapita nanu.”
Og David tog til Orde og sagde til Hetiten Ahimelek og til Joabs Broder Abisjaj, Zerujas Søn: "Hvem vil følge mig ned til Saul i Lejren?" Abisjaj svarede: "Det vil jeg!"
7 Choncho Davide ndi Abisai anapita ku misasa ya ankhondowo usiku. Atafika anangopeza Sauli ali gone mu msasa wake mkondo wake atawuzika pansi pafupi ndi mutu wake, Abineri ndi ankhondo onse anali atagona momuzungulira.
Så kom David og Abisjaj om Natten til Hæren, og se, Saul lå og sov i Vognborgen med sit Spyd stukket i Jorden ved sit Hovedgærde, medens Abner og Krigerne lå rundt om ham.
8 Abisai anawuza Davide kuti, “Lero Mulungu wapereka mdani wanu mʼmanja mwanu. Tsopano ndiloleni ndimukhomere pansi ndi mkondo wangawu kamodzinʼkamodzi. Sindimulasa kawiri.”
Da sagde Abisjaj til David: "Gud har i Dag givet din Fjende i din Hånd! Lad mig nagle ham til Jorden med hans Spyd, så jeg ikke skal behøve at gøre det om!"
9 Koma Davide anamuyankha Abisai kuti, “Usamuphe! Ndani adzapha wodzozedwa wa Yehova ndi kupezeka wosalakwa?
Men David svarede Abisjaj: "Gør ham ikke noget ondt! Thi hvem lægger ustraffet Hånd på HERRENs Salvede?"
10 Davide anati, Pali Yehova wamoyo, Yehova mwini ndiye adzamukanthe, mwina tsiku lake lomwalira lidzafika, kapena adzapita ku nkhondo nakaphedwa komweko.
Og David sagde endvidere: "Nej, så sandt HERREN lever, HERREN selv vil ramme ham; hans Time kommer, eller han vil blive revet bort, når han drager i Krigen.
11 Koma Yehova andiletse kuti ndisapweteke wodzozedwa wa Yehova. Tsopano tingotenga mkondo umene uli ku mutu kwakewo ndi botolo la madzilo ndipo tizipita.”
HERREN lade det være langt fra mig at lægge Hånd på HERRENs Salvede! Men tag nu Spydet ved hans Hovedgærde og Vandkrukken, og lad os så gå vor Vej!"
12 Motero Davide anatenga mkondo ndi botolo lamadzi zimene zinali ku mutu kwa Sauli ndipo anachoka. Palibe amene anaona zimenezi kapena kudziwa, ndipo palibenso amene anadzuka. Onse anali mʼtulo, chifukwa Yehova anawagonetsa tulo tofa nato.
Så tog David Spydet og Vandkrukken fra Sauls Hovedgærde, og de gik deres Vej, uden at nogen så eller mærkede det eller vågnede; thi de sov alle, eftersom en tung Søvn fra HERREN var faldet over dem.
13 Pambuyo pake Davide anadutsa nakakwerera mbali ina ya phiri, ndi kuyimirira pamwamba pa phiri patali. Pakati pawo panali mpata waukulu.
Derpå gik David over på den anden Side og stillede sig langt borte på Toppen af Bjerget, så at der var langt imellem dem.
14 Davide anayitana gulu lankhondo ndi Abineri mwana wa Neri nawafunsa kuti, “Kodi sundiyankha ine Abineri?” Abineri anayankha kuti, “Ndiwe yani amene ukuyitana mfumu?”
Så råbte han til Krigerne og Abner, Ners Søn: "Svarer du ikke, Abner?" Abner svarede: "Hvem er det, som kalder på Kongen?"
15 Davide anamufunsa Abineri kuti, “Kodi sindiwe mwamuna? Ndipo wofanana nawe ndani mu Israeli? Nʼchifukwa chiyani sunateteze mbuye wako mfumu? Munthu wina anabwera kumeneko.
David sagde til Abner: "Er du ikke en Mand? Og hvem er din Lige i Israel? Hvorfor vogtede du da ikke din Herre Kongen? Thi en af Krigerne kom for at gøre din Herre Kongen Men.
16 Chimene wachita iwe si chabwino. Pali Yehova wamoyo iwe ndi asilikali ako muyenera kufa chifukwa simunateteze mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Tayangʼanayangʼana. Uli kuti mkondo wa mfumu ndi botolo lamadzi zimene zinali kumutu kwa mfumu?”
Der har du ikke båret dig vel ad! Så sandt HERREN lever: I er dødsens, I, som ikke vogtede eders Herre, HERRENs Salvede! Se nu efter: Hvor er Kongens Spyd og Vandkrukken, som stod ved hans Hovedgærde?"
17 Sauli anazindikira mawu a Davide ndipo anafunsa kuti, “Kodi amenewa ndi mawu ako Davide mwana wanga?” Davide anayankha, “Inde ndi anga, mbuye wanga mfumu.
Da kendte Saul Davids Røst, og han sagde: "Er det din Røst, min Søn David?" David svarede: "Ja, Herre Konge!"
18 Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukundilonda ine mtumiki wanu? Kodi ine ndachita chiyani ndipo ndapezeka ndi cholakwa chotani?
Og han føjede til: "Hvorfor forfølger min Herre dog sin Træl? Hvad har jeg gjort, og hvad ondt har jeg øvet?
19 Tsopano mbuye wanga mfumu tamverani mawu a mtumiki wanu. Ngati ndi Yehova wautsa mtima wanu kuti mundiwukire, ndiye alandire chipepeso. Koma ngati ndi anthu amene achita zimene, ndiye Yehova awatemberere popeza andipirikitsa lero kundichotsa mʼdziko la Yehova, namati, ‘Pita kapembedze milungu ina.’
Måtte min Herre Kongen nu høre sin Træls Ord! Hvis det er HERREN, der har ægget dig imod mig, så lad ham få Duften af en Offergave. Men er det Mennesker, da være de forbandet for HERRENs Åsyn, fordi de nu har drevet mig bort, så at jeg er udelokket fra HERRENs Arvelod, og fordi de har sagt til mig: Gå bort og dyrk fremmede Guder!
20 Tsopano musalole kuti magazi anga akhetsedwe kutali ndi Yehova pakuti mfumu ya Israeli yatuluka kudzafunafuna ine nsabwe, monga mmene munthu asakira nkhwali ku mapiri.”
Nu beder jeg: Lad ikke mit Blod væde Jorden fjernt fra HERRENs Åsyn! Israels Konge er jo draget ud for at stå mig efter Livet, som når Ørnen jager en Agerhøne på Bjergene!"
21 Ndipo Sauli anati, “Ine ndachimwa. Bwerera mwana wanga Davide. Sindidzakuchitanso choyipa popeza lero wauwona moyo wanga ngati wamtengowapatali. Taona, ndachita zauchitsiru ndipo ndachimwa kwambiri.”
Da sagde Saul: "Jeg har syndet; kom tilbage, min Søn David! Thi jeg vil ikke mer gøre dig noget ondt, eftersom mit Liv i Dag var dyrebart i dine Øjne. Se, jeg har handlet som en Dåre og gjort mig skyldig i en såre stor Vildfarelse!
22 Davide anayankha kuti, “Nawu mkondo wanu, mfumu. Tumani mmodzi wa anyamata anu abwere adzatenge.
David svarede: "Se, her er Kongens Spyd; lad en af Folkene komme herover og hente det.
23 Yehova amadalitsa munthu aliyense wolungama ndi wokhulupirika. Yehova anakuperekani lero mʼmanja mwanga, koma ine sindinakhudze wodzozedwa wa Yehova.
Men HERREN vil gengælde enhver hans Retfærdighed og Troskab; HERREN gav dig i Dag i min Hånd, men jeg vilde ikke lægge Hånd på HERRENs Salvede!
24 Monga momwe ine lero ndachitira kuwuyesa moyo wanu ngati wamtengowapatali, momwemonso Yehova awuyese moyo wanga wamtengowapatali ndipo andipulumutse mʼmavuto anga onse.”
Men som dit Liv i Dag var agtet højt i mine Øjne, måtte således mit Liv være agtet højt i HERRENs Øjne, så at han frier mig fra al Nød!"
25 Ndipo Sauli anawuza Davide kuti, “Yehova akudalitse iwe Davide mwana wanga. Udzachita zinthu zazikulu ndipo udzapambana.” Choncho Davide anayenda njira yake ndipo Sauli anabwerera kwawo.
Da sagde Saul til David: "Velsignet være du, min Søn David! For dig lykkes alt, hvad du tager dig for!" Derpå gik David sin Vej, og Saul vendte tilbage til sit Hjem.