< 1 Samueli 11 >

1 Nahasi, Mwamoni anapita ndi kuzungulira mzinda wa Yabesi Giliyadi. Tsono anthu onse a ku Yabesi anapempha Nahasiyo kuti, “Muchite nafe pangano, ndipo tidzakutumikirani.”
UNahashi umʼAmoni wasuka wayivimbezela iJabheshi Giliyadi. Bonke abantu baseJabheshi bathi kuye, “Yenza isivumelwano lathi, thina sizakuba ngaphansi kwakho.”
2 Koma Nahasi Mwamoni uja anayankha kuti, “Ndidzachita nanu pangano pokhapokha nditakolowola diso lakumanja la aliyense wa inu kuti ndichititse manyazi Aisraeli onse.”
Kodwa uNahashi umʼAmoni waphendula wathi, “Ngizakwenza isivumelwano lani kuphela nxa kuyikuthi ngizakhupha ilihlo lesandla sokunene emuntwini wonke wakini ukuze u-Israyeli wonke ngimlethele ihlazo.”
3 Akuluakulu a mzinda wa Yabesi anati kwa iye, “Utipatse masiku asanu ndi awiri kuti titumize uthenga mu Israeli monse. Ngati sipapezeka wodzatipulumutsa, ndiye ife tidzadzipereka kwa iwe.”
Abadala baseJabheshi bathi kuye, “Sinike insuku eziyisikhombisa ukuze sithume izithunywa kulolonke elako-Israyeli; nxa engekho ozasihlenga sizazinikela kuwe.”
4 Amithenga aja atafika kwawo kwa Sauli ku Gibeya ndi kufotokoza nkhaniyi kwa anthu onse, iwo analira motaya mtima.
Kwathi izithunywa sezifike eGibhiya kaSawuli njalo zabika izimiso lezi ebantwini bonke bakhala kakhulu.
5 Pa nthawiyo nʼkuti Sauli akubwera kuchokera ku munda, ali pambuyo pa ngʼombe zake za ntchito ndipo anafunsa. “Nʼchiyani chawavuta anthuwa kuti azilira motere?” Ndipo anamufotokozera zomwe anthu a mu mzinda wa Yabesi ananena.
Ngalesosikhathi uSawuli wayevela emasimini, engemuva kwenkabi zakhe, wasebuza esithi, “Kuyini okonakeleyo ebantwini? Kungani bekhala?” Bamlandisela okwakutshiwo ngabantu baseJabheshi.
6 Sauli atamva mawu awo, Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwa mphamvu ndipo anakwiya kwambiri.
Kwathi uSawuli esezwe amazwi abo, uMoya kaNkulunkulu wehlela phezu kwakhe ngamandla, wathukuthela kakhulu.
7 Tsono anatenga ngʼombe ziwiri za ntchito, nazidula nthulinthuli. Ndipo anatumiza amithenga ndi nthulizo dziko lonse la Israeli ndi mawu akuti, “Umo ndi mmene adzachite ndi ngʼombe ya aliyense amene satsata Sauli ndi Samueli.” Ndipo anthu anachita mantha aakulu motero kuti onse ananyamuka ndi mtima umodzi.
Wathatha inkabi ezimbili, waziquma zaba yiziqayiqa, wathumela iziqa lezithunywa kulolonke elako-Israyeli, zimemezela zisithi, “Lokhu yikho okuzakwenziwa enkabini zikabani lobani ongalandeli uSawuli loSamuyeli.” Ukwesabeka kukaThixo kwehlela ebantwini, baphuma sebenjengomuntu munye.
8 Pamenepo Sauli anawasonkhanitsa ku Bezeki nawawerenga, ndipo Aisraeli analipo 300,000, Ayuda analipo 30,000.
Kwathi uSawuli esebaqoqile eBhezekhi, abantu bako-Israyeli babezinkulungwane ezintathu, abakoJuda bezinkulungwane ezingamatshumi amathathu.
9 Tsono Sauli anawuza amithenga ochokera ku Yabesi aja kuti, “Mukawawuze anthu a ku Yabesi Giliyadi kuti mawa nthawi ya masana adzapulumutsidwa.” Pamene amithengawo anapita ndi kukafotokoza nkhani imeneyi kwa anthu a ku Yabesi, iwo anasangalala kwambiri.
Batshela izithunywa ezazifikile bathi, “Tshelani abantu baseJabheshi Giliyadi ukuthi, ‘Kuzakuthi ilanga selitshisa kusasa, lina lizakuba selihlengiwe.’” Kwathi izithunywa sezihambe zayabika lokhu ebantwini baseJabheshi, bathokoza.
10 Choncho anthu a ku Yabesi anawuza Nahasi kuti, “Mawa tidzadzipereka kwa inu ndipo inu mudzachite nafe chilichonse chokukomerani.”
Basebesithi kuma-Amoni, “Kusasa sizazinikela kini, njalo lingenza kithi loba kuyini okukhanya kukuhle kini.”
11 Tsono mmawa mwake Sauli anagawa anthuwo mʼmagulu atatu. Mmamawa kusanache iwo analowa mʼmisasa ya Aamoni ndi kuwapha mpaka masana. Amene anapulumuka anabalalika, aliyense kwakekwake.
Ngelanga elalandelayo uSawuli wehlukanisa abantu bakhe baba ngamaviyo amathathu; kwathi ngomlindo wokucina ebusuku bafohlela ezihonqweni zama-Amoni bawabulala ilanga laze latshisa. Lawo aphephayo ahlakazeka, akwaze kwaba lamabili awo asala endawonye.
12 Kenaka anthu anafunsa Samueli kuti, “Kodi ndani aja ankanena kuti, ‘Kodi Sauli nʼkutilamulira ife?’ Bwera nawoni kuno kuti tidzawaphe.”
Abantu basebesithi kuSamuyeli, “Ngubani owabuza wathi, ‘USawuli uzasibusa na?’ Balethe kithi labobantu sibabulale.”
13 Koma Sauli anati, “Palibe amene ati aphedwe lero, pakuti lero lino Yehova wagwira ntchito yopulumutsa Israeli.”
Kodwa uSawuli wathi, “Kakho ozabulawa lamhla, ngoba ngalolusuku uThixo umhlengile u-Israyeli.”
14 Ndipo Samueli anati kwa anthuwo, “Tiyeni tipite ku Giligala kuti tikatsimikizenso kuti Sauli ndi mfumu yathu.”
USamuyeli wasesithi ebantwini, “Wozani, kasiyeni eGiligali siyeqinisa ubukhosi khona.”
15 Choncho anthu onse anapita ku Giligala ndipo kumeneko Samueli anakalonga Sauli ufumu pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anthu anapereka nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova, ndipo Sauli ndi Aisraeli onse anachita chikondwerero chachikulu.
Ngakho abantu bonke baya eGiligali bambeka uSawuli ukuba yinkosi phambi kukaThixo. Bahlaba khona imihlatshelo yeminikelo yokuthula, njalo uSawuli labantu bonke bako-Israyeli baba lomkhosi omkhulu wokuthokoza.

< 1 Samueli 11 >