< 1 Samueli 10 >

1 Ndipo Samueli anatenga botolo la mafuta nathira mafutawo pa mutu wa Sauli ndipo anapsompsona nati, “Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake, Aisraeli. Iwe udzalamulira anthu a Yehova ndiponso udzawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo owazungulira. Chizindikiro chakuti Yehova wakudzoza kuti ukhale mtsogoleri wa anthu ake ndi ichi:
USamuyeli wasethatha umfuma wamafutha wawathela ekhanda likaSawuli wasemanga, esithi, “Uthixo kakugcobanga ukuba ngumbusi welifa lakhe na?
2 Ukachoka pano lero lino, udzakumana ndi amuna awiri kufupi ndi manda a Rakele ku Zeliza mʼmalire mwa dziko la Benjamini ndipo adzakuwuza kuti, ‘Abulu amene munkafunafuna aja apezeka. Ndipo tsopano abambo ako asiya kuganiza za abulu ndipo akudera nkhawa za iwe.’ Iwo akufunsa kuti, ‘Kodi ndidzachita chiyani mmene mwana wanga sakuoneka?’”
Ekusukeni kwakho kimi lamhla, uzahlangana lamadoda amabili eduze kwengcwaba likaRasheli, eliseZeliza esemngceleni wakoBhenjamini. Azakuthi kuwe, ‘Obabhemi obuyebadinga sebetholakele. Khathesi uyihlo kasacabangi ngabo kodwa usekhathazeka ngawe. Uyabuza esithi, “Ngizakwenzanjani ngendodana yami na?”’
3 “Ndipo udzapyola pamenepo ndi kufika ku mtengo wa thundu wa ku Tabori. Kumeneko udzakumana ndi anthu atatu akupita kukapereka nsembe ku Nyumba ya Mulungu ku Beteli. Mmodzi adzakhala atanyamula ana ambuzi atatu, wina atanyamula malofu atatu a buledi, ndi winayo atanyamula thumba la vinyo.
Uzahamba-ke usuka lapho uze ufike esihlahleni esikhulu saseThabhori. Amadoda amathathu aya kuNkulunkulu eBhetheli azahlangana lawe khonapho. Enye izathwala amazinyane embuzi amathathu, enye izinkwa ezintathu lenye umgodla wewayini.
4 Adzakupatsa moni ndi kukupatsa malofu awiri a buledi. Iwe udzalandire bulediyo.
Azakubingelela akuphe izinkwa ezimbili, ozazamukela kuwo.
5 “Pambuyo pake, udzafike ku Gibeyati-Elohimu, kumene kuli gulu la ankhondo la Afilisti. Pamene ukuyandikira mzindawo, udzakumana ndi gulu la aneneri akutsika kuchokera ku phiri, akuyimba zeze, ngʼoma, zitoliro ndi pangwe, ndiponso akulosera.
Emva kwalokho, uzakuya eGibhiya kaNkulunkulu lapho okulesilindo sebutho lamaFilistiya khona. Lapho usubanga emzini, uzahlangana lodwendwe lwabaphrofethi besehla bevela endaweni ephakemeyo, phambi kwabo kutshaywa imiqangala lamagedla lemifece kanye lemihubhe, njalo bazakuba bephrofetha.
6 Kenaka Mzimu wa Yehova udzabwera pa iwe ndi mphamvu, ndipo udzayamba kulosera nawo pamodzi. Ndipo udzasinthika kukhala munthu wina.
UMoya kaThixo uzakwehlela phezu kwakho ngamandla, lawe uzaphrofetha labo, njalo uzaguqulwa ube ngomunye umuntu.
7 Zizindikiro izi zikakachitika, dzachite chilichonse manja ako angathe kuchita, pakuti Mulungu ali nawe.
Izibonakaliso lezi zingagcwaliseka, yenza loba yini okubona kufanele ukuba ukwenze, ngoba uNkulunkulu ulawe.
8 “Tsono tsogola kupita ku Giligala. Ine ndidzabwera ndithu kudzapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Koma ukandidikire masiku asanu ndi awiri mpaka ine nditabwera kuti ndidzakuwuze zomwe udzachite.”
Hamba ungandulele eGiligali. Ngizakuza kuwe impela ngizenikela umhlatshelo weminikelo yokutshiswa leminikelo yobuzalwane. Kodwa kuzamele ulinde insuku eziyisikhombisa ngize ngifike kuwe ngikutshele okumele ukwenze.”
9 Sauli akutembenuka kusiyana ndi Samueli, Mulungu anasintha mtima wa Sauli, ndipo zinthu zonsezi zinakwaniritsidwa tsiku lomwelo.
Kwathi uSawuli ephenduka esesuka kuSamuyeli, uNkulunkulu waguqula inhliziyo kaSawuli, njalo zonke izibonakaliso lezi zagcwaliseka mhlalokho.
10 Atafika ku Gibeya, anakumana ndi gulu la aneneri. Mzimu wa Mulungu unabwera pa iye mwamphamvu, nayamba kulosa nawo.
Bathi befika eGibhiya, udwendwe lwabaphrofethi lwabahlangabeza; uMoya kaNkulunkulu wehlela phezu kwakhe ngamandla, laye wahlanganyela ekuphrofitheni kwabo.
11 Pamene onse amene ankamudziwa kale anamuona akulosera pamodzi ndi aneneri, anafunsana wina ndi mnzake. “Kodi nʼchiyani chachitika ndi mwana wa Kisi? Kodi Sauli alinso mʼgulu la aneneri?”
Kwathi labo ababevele bemazi bembona esephrofitha labaphrofethi, babuzana besithi, “Kuyini kanti lokhu osekwenzakale endodaneni kaKhishi? USawuli laye ungomunye wabaphrofethi na?”
12 Munthu wina wa kumeneko anayankha kuti, “Nanga enawa abambo awo ndani?” Kotero kunayambika mwambi wakuti, “Kodi Saulinso ali mʼgulu la aneneri?”
Umuntu owayehlala lapho waphendula wathi, “Uyise wabo ngubani na?” Ngakho kwaba yisitsho ukuthi: “USawuli laye ungomunye wabaphrofethi na?”
13 Sauli atasiya kuloserako, anapita ku kachisi ku phiri.
Kwathi uSawuli eseyekele ukuphrofetha, wasesiya endaweni ephakemeyo.
14 Tsono amalume ake a Sauli anamufunsa ndi mnyamata wake kuti, “Munapita kuti?” Iye anayakha, “Timakafunafuna abulu koma titaona kuti sakupezeka, tinapita kwa Samueli.”
Ngalesosikhathi uyise omncane kaSawuli wambuza kanye lenceku yakhe wathi, “Kanti kade lingaphi?” USawuli waphendula wathi, “Kade sidinga obabhemi. Kodwa kuthe sibona ukuthi kabatholakali, sasesisiya kuSamuyeli.”
15 Amalume ake a Sauli anati, “Chonde, ndifotokozereniko zimene Samueli wakuwuzani.”
Uyise omncane kaSawuli wasesithi, “Ngitshela ukuthi uSamuyeli utheni kuwe.”
16 Sauli anati, “Iye anatitsimikizira kuti abulu anapezeka.” Koma sanawawuze amalume akewo za nkhani ija ya ufumu imene Samueli anamuwuza.
USawuli waphendula wathi, “Uqinise kithi ukuthi obabhemi sebebonakele.” Kodwa kamtshelanga uyise omncane okwakutshiwo nguSamuyeli ngobukhosi.
17 Samueli anayitana Aisraeli onse kuti asonkhane pamaso pa Yehova ku Mizipa.
USamuyeli wabizela abantu bako-Israyeli kuThixo eMizipha
18 Ndipo anawuza Aisraeli onse kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi kukupulumutsani mʼdzanja la Igupto ndi mʼdzanja la mafumu onse amene ankakuzunzani.’
wathi kubo, “Nanku okutshiwo yiThixo, uNkulunkulu ka-Israyeli: ‘Ngakhupha u-Israyeli eGibhithe, njalo ngalikhulula esandleni seGibhithe lakuyo yonke imibuso eyayilincindezela.’
19 Koma lero mwamukana Mulungu wanu amene amakupulumutsani mʼmavuto anu onse ndi mʼzowawa zanu. Ndipo mukuti, ‘Ayi, koma mutipatse mfumu yotilamulira.’ Tsopanotu sonkhanani pamaso pa Yehova mwa mafuko ndi mabanja anu.”
Kodwa khathesi selimalile uNkulunkulu wenu, olihlengayo ezingozini zenu zonke lasezinsizini. Njalo selithe, ‘Hatshi, sibekele inkosi ezasibusa.’ Ngakho-ke khathesi zibonakaliseni phambi kukaThixo ngezizwana zenu langezinsendo zenu.”
20 Samueli atasonkhanitsa mafuko onse a Israeli, fuko la Benjamini linasankhidwa.
Kwathi uSamuyeli esezilethe eduze zonke izizwana zako-Israyeli, isizwana sikaBhenjamini sakhethwa.
21 Anasonkhanitsa fuko la Benjamini banja ndi banja. Pomaliza anasonkhanitsa banja la Matiri mmodzimmodzi ndipo Sauli mwana wa Kisi anasankhidwa. Koma atamufunafuna, sanamupeze.
Emva kwalokho waletha isizwana sikaBhenjamini phambili, usendo ngosendo, kwakhethwa usendo lukaMathiri. Ekucineni kwakhethwa uSawuli, indodana kaKhishi. Kodwa kwathi sebemdinga akaze abonakala.
22 Tsono anthu anafunsanso kwa Yehova kuti, “Kodi munthuyu wabwera kale kuno?” Ndipo Yehova anayankha kuti, “Inde wabisala pakati pa katundu.”
Ngakho babuza njalo kuThixo bathi, “Umuntu lo uke wafika lapha na?” UThixo wathi, “Ye, usezifihle phakathi kwezimpahla.”
23 Iwo anathamanga ndi kukamutenga kumeneko. Atayimirira pakati pa anthu anapezeka kuti anali wamtali kuposa anthu ena mwakuti ankamulekeza mʼmapewa.
Bagijima bayamkhipha, njalo kwathi esemi phakathi kwabantu, wayemude kulabo bonke.
24 Samueli anafunsa anthu onse kuti, “Kodi mukumuona munthu amene Yehova wasankha? Palibe wofanana naye pakati pa anthu onse.” Kenaka anthu onse anafuwula kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wautali!”
USamuyeli wasesithi ebantwini bonke, “Liyambona yini umuntu osekhethwe nguThixo? Kakho lamunye onjengaye phakathi kwabantu bonke bako-Israyeli.” Abantu baklabalala besithi, “Impilo ende enkosini!”
25 Samueli anafotokozera anthu ntchito ndi udindo wa mfumu. Pambuyo pake analemba mʼbuku zonse zokhudza ntchito ndi udindo wa mfumu, ndipo bukulo analiyika pamaso pa Yehova. Kenaka Samueli analola aliyense kuti abwerere kupita kwawo.
USamuyeli wachaza ebantwini imithetho yobukhosi. Wayiloba emqulwini wayibeka phambi kukaThixo. Emva kwalokho wabachitha abantu, ngulowo lalowo waya emzini wakhe.
26 Sauli anapitanso ku mudzi kwawo ku Gibeya, pamodzi ndi anthu amphamvu amene Mulungu anawafewetsa mitima.
USawuli laye waya kibo eGibhiya ephelekezelwa ngabantu abangamaqhawe uNkulunkulu ayethinte inhliziyo zabo.
27 Koma anthu ena achabechabe anati, “Kodi munthu uyu angathe bwanji kutipulumutsa?” Iwo anayamba kumunyoza Sauliyo, ndipo sankamupatsa ngakhale mphatso. Koma iye sanalabadireko.
Kodwa ezinye izidlwangudlwangu zathi, “Umuntu lo angasikhulula kanjani na?” Zameyisa kazaze zamlethela zipho. Kodwa uSawuli wazithulela.

< 1 Samueli 10 >