< 1 Yohane 5 >
1 Aliyense amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Khristu, iyeyo ndi mwana wa Mulungu, ndipo aliyense amene amakonda Atate amakondanso Mwana wake.
Whosoever believeth that, Jesus, is the Christ, of God, hath been born: and, whosoever loveth him that begat, loveth him that hath been begotten of him.
2 Chodziwira kuti timakonda ana a Mulungu nʼchakuti timakonda Mulungu ndi kusunga malamulo ake.
Hereby, perceive we, that we love the children of God, as soon as, God, we love, and, his commandments, we are doing.
3 Pakuti kukonda Mulungu ndiye kusunga malamulo ake. Ndipo malamulo ake siwolemetsa,
For, this is the love of God—that, his commandments, we be keeping, and, his commandments, are not burdensome;
4 chifukwa aliyense amene ndi mwana wa Mulungu amagonjetsa dziko lapansi. Chikhulupiriro chathu ndicho timagonjetsera dziko lapansi.
Because, whatsoever hath been born of God, overcometh the world; and, this, is the victory that hath overcome the world—our faith.
5 Ndani amagonjetsa dziko lapansi? Yekhayo amene amakhulupirira kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu.
[And] who is he that overcometh the world, save he that believeth that, Jesus, is the Son of God?
6 Uyu ndiye anabwera mwa madzi ndi magazi, ndiye Yesu Khristu. Sanabwere mwa madzi okha, koma mwa madzi ndi magazi. Ndipo ndi Mzimu Woyera amene akuchitira umboni, chifukwa Mzimu Woyera ndi choonadi.
This, is he that came through means of water and blood, Jesus Christ: not, by the water, only, but, by the water and by the blood, —and, the Spirit, it is, that is bearing witness, because, the Spirit, is the truth.
7 Pakuti pali atatu amene amachitira umboni.
Because, three, are they who are bearing witness—
8 Mzimu Woyera, madzi ndi magazi; ndipo atatu amavomerezana.
The Spirit, and the Water, and the Blood; and, the three, are, [witnesses], unto one thing.
9 Timalandira umboni wa anthu, koma umboni wa Mulungu ndi wopambana. Umboniwo ndi umene anachitira Mwana wake.
If, the witness of men, we receive, the witness of God, is, greater. Because, this, is the witness of God—in that he hath borne witness concerning his Son, —
10 Aliyense amene amakhulupirira Mwana wa Mulungu ali nawo umboniwu mu mtima mwake, koma aliyense amene sanakhulupirire Mulungu amayesa kuti Mulunguyo ndi wonama, chifukwa sanakhulupirire umboni umene Mulungu anachitira wa Mwana wake.
He that believeth on the Son of God, hath the witness, within himself: He that doth not believe God, false, hath made him, —because he hath not believed on the witness which, God, hath witnessed, concerning his Son—
11 Ndipo umboniwo ndi uwu: Mulungu anatipatsa moyo wosatha, ndipo moyowu uli mwa Mwana wake. (aiōnios )
And, this, is the witness: —that, life age-abiding, hath God given unto us, and, this life, is, in his Son: (aiōnios )
12 Iye amene ali ndi Mwana ali ndi moyo, amene alibe Mwana wa Mulungu alibe moyo.
He that hath the Son, hath, the life, —he that hath not the Son of God, hath not, the life.
13 Ine ndikulemba zimenezi kwa inu, amene mwakhulupirira dzina la Mwana wa Mulungu kuti mudziwe kuti muli ndi moyo wosatha. (aiōnios )
These things, have I written unto you—in order that ye may know that ye have, Life Age-abiding—unto you who believe on the name of the Son of God. (aiōnios )
14 Ife timalimba mtima tikamafika pamaso pa Mulungu, popeza kuti ngati tipempha kanthu kalikonse monga mwa chifuniro chake, amatimvera.
And, this, is the boldness which we have towards him: that, if, anything, we ask, according to his will, He doth hearken unto us.
15 Ndipo ngati tikudziwa kuti amatimvera, chilichonse chimene timapempha, tikudziwanso kuti tili nacho chimene tamupempha Iye.
And, if we know that he doth hearken unto us, whatsoever we ask, we know that we have the things asked, which we have asked of him,
16 Ngati wina aona mʼbale wake akuchita tchimo losadzetsa imfa, apemphere ndipo Mulungu adzamupatsa moyo mʼbale wakeyo. Ndikunena za ochita tchimo losadzetsa imfa. Pali tchimo lodzetsa imfa. Ine sindikunena kuti apemphere ayi.
If one should see his brother committing a sin, not unto death, he shall ask, and He will grant unto him life, —for them who are sinning, not unto death. There, is, a sin, unto death: not concerning that, am I saying, that he should make request.
17 Chilichonse chosalungama ndi tchimo ndipo pali tchimo losadzetsa imfa.
All unrighteousness, is, sin, and there, is, a sin, not unto death.
18 Tikudziwa kuti aliyense amene ndi mwana wa Mulungu sachimwirachimwirabe. Yesu, Mwana wa Mulungu, amamusunga ndipo woyipa uja sangamukhudze.
We know that, whosoever hath been born of God, is not committing sin, —Nay, he that hath been born of God, He keepeth him, and, the wicked one, doth not touch him.
19 Tikudziwa kuti ndife ana a Mulungu ndi kuti dziko lonse lapansi lili pansi pa ulamuliro wa woyipayo.
We know that, of God, are we; and, the whole world, in the wicked one, is lying.
20 Tikudziwa kuti Mwana wa Mulungu anafika ndipo anatipatsa nzeru, kuti timudziwe Iye amene ali woona. Ndipo ife tili mwa Iye amene ndi woona, Mwana wake, Yesu Khristu. Iye ndi Mulungu woona ndi moyo wosatha. (aiōnios )
We know, moreover, that, the Son of God, hath come, and hath given us insight, so that we are getting to understand, him that is Real, —and we are in him that is Real, in his Son Jesus Christ. This, is the Real God, and life age-abiding. (aiōnios )
21 Ana okondedwa, dzisungeni bwino, osapembedza mafano.
Dear children! Guard yourselves from idols.