< 2 Petro 1 >
1 Ndine Simoni Petro, mtumiki ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Kwa anthu amene analandira chikhulupiriro cha mtengowapatali chomwe ifenso tinalandira chifukwa cha chilungamo cha Mulungu ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu.
Simon Peter, servant and apostle of Jesus Christ, unto them who have obtained, equally precious, faith, with us, in the righteousness of our God, and Saviour Jesus Christ,
2 Chisomo ndi mtendere zochuluka zikhale nanu pomudziwa Mulungu ndi Yesu Ambuye athu.
Favour unto you, and peace, be multiplied, in the personal knowledge of God and of Jesus our Lord; —
3 Mulungu mwa mphamvu zake anatipatsa zonse zofunika kukhala moyo opembedza, potidziwitsa za Iyeyo amene anatiyitana ku ulemerero wake ndi ubwino wake.
As, all things, suited for life and godliness his divine power, unto us, hath given, through the personal knowledge of him that hath called us through glory and excellence, —
4 Mwa ulemerero ndi ubwino wakewo, anatipatsa malonjezo opambana kwambiri ndi a mtengowapatali. Amenewa ndi malonjezo amene amakuthandizani kulandira nawo moyo wa Mulungu, titapulumuka ku chiwonongeko chimene chili mʼdziko lapansi chifukwa cha zilakolako zoyipa.
Through which, his precious, and very great, promises, have, unto us, been given, in order that, through these, ye might become sharers in a divine nature—escaping the corruption that is in the world by coveting.
5 Choncho, chitani khama kuwonjezera moyo wabwino pa chikhulupiriro chanu, ndipo pa moyo wabwino muwonjezerepo nzeru.
And, for this very reason also—adding, on your part, all diligence, supply, in your faith, excellence, and, in your excellence, knowledge,
6 Pa nzeru muwonjezerepo kudziretsa, pa kudziretsa muwonjezerepo chipiriro, ndipo pa chipiriro muwonjezerepo khalidwe lolemekeza Mulungu.
And, in your knowledge, self-control, and, in your self-control, endurance, and, in your endurance, godliness,
7 Pa khalidwe lolemekeza Mulungu muwonjezerepo chifundo cha ubale, pa chifundo cha ubale muwonjezerepo chikondi.
And, in your godliness, brotherly affection, and, in your brotherly affection, love.
8 Ngati zonsezi zikhala mwa inu nʼkumachuluka, zidzakuthandizani kuti musakhale aulesi ndi osapindula ndi chidziwitso chanu cha Ambuye athu Yesu Khristu.
These things, unto you, belonging and abounding, neither idle nor unfruitful, constitute you, regarding the personal knowledge of our Lord Jesus Christ;
9 Koma ngati wina alibe zimenezi, ndi wakhungu sangathe kuona patali, ndipo wayiwala kuti anayeretsedwa machimo ake akale.
For, he to whom these things are not present, is, blind, seeing only what is near, having come, to forget, his purification from his old sins.
10 Nʼchifukwa chake abale anga, funitsitsani kuti mayitanidwe ndi masankhidwe anu akhale otsimikizika. Pakuti ngati muchita zinthu izi, simudzagwa konse.
Wherefore, all the more, brethren, give diligence to be making, firm, your calling and election; for, these things, doing, in nowise shall ye stumble at any time,
11 Mudzalandiridwa bwino kwambiri mu ufumu wosatha wa Ambuye ndi Mpulumutsi wathu Yesu Khristu. (aiōnios )
For, thus, shall richly be further supplied unto you—the entrance into the age-abiding kingdom of our Lord and Saviour Jesus Christ. (aiōnios )
12 Tsono ine ndidzakukumbutsani nthawi zonse za zinthu zimenezi, ngakhale kuti mumazidziwa ndipo kuti munakhazikika mʼchoonadi chimene muli nacho tsopano.
Wherefore, I shall be certain to be, always, putting you in remembrance concerning these things, —although, indeed, ye know them, and have become confirmed in the present truth;
13 Ndikuganiza kuti nʼkoyenera ndikanali mu msasa uno, kuti ndikutsitsimutseni ndi kukukumbutsani,
Right, nevertheless, I account it—as long as I am in this tent, to be stirring you up by putting you in remembrance,
14 chifukwa ndikudziwa kuti posachedwapa ndikuchoka mu msasa uno, monga Ambuye athu Yesu Khristu anandidziwitsiratu.
Knowing that, speedy, is the putting off of my tent—even as, our Lord Jesus Christ also, made clear to me:
15 Ndipo ndidzayesetsa kuti nditachoka, mudzakumbukire nthawi zonse.
Yea, I will give diligence also, that, at every time, ye may be able, after my own departure, to be keeping up the remembrance of, these very things.
16 Ife sitinatsate nkhani zongopeka titakuwuzani za mphamvu zake ndi zakubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu, koma tinaona ndi maso athu za ukulu wake.
For, not as having followed, cleverly devised stories, made we known unto you the power and presence of our Lord Jesus Christ, but as having been made, spectators, of his majesty.
17 Pakuti Iye analandira ulemu ndi ulemerero kuchokera kwa Mulungu Atate atamufikira mawu ochokera ku ulemerero wa ukulu akuti, “Uyu ndi mwana wanga amene Ine ndimukonda, amene ndimakondwera naye kwambiri.”
For, when he received from God the Father honour and glory, a voice, being borne to him such as this, by the magnificent glory—My Son, the beloved, is, this, in whom, I, delight,
18 Ifeyo tinamva mawuwa akuchokera kumwamba pamene tinali naye pamodzi pa phiri lopatulika lija.
Even this voice, we, heard, when, out of heaven, it was borne, we being, with him, in the holy mount.
19 Tsono ifenso tili ndi mawu a uneneri amene ndi odalirika kwambiri ndipo inu mudzachita bwino mukawasamalira mawuwa, monga kuwunika kumene kukuwala mu mdima, mpaka tsiku lidzayambe kucha, pamene nthanda idzayambe kuwala mʼmitima mwanu.
And we have, more firm, the prophetic word; —whereunto ye are doing, well, to take heed, —as unto a lamp shining in a dusky place, —until, day, shall dawn, and, a day-star, shall arise in your hearts: —
20 Kuposa zonse, inu muyenera kuzindikira kuti palibe mawu a uneneri amene amatanthauzidwa pa okha.
Of this, first, taking note—that, no prophecy of scripture, becometh, self-solving;
21 Pakuti mawu a uneneri sanadze mwa kufuna kwa anthu, koma anthu anayankhula zochokera kwa Mulungu, Mzimu Woyera atawayankhulitsa.
For not, by will of man, was prophecy brought in, at any time, but, as, by Holy Spirit, they were borne along, spake, men, from God.