< 1 Akorinto 7 >
1 Tsopano pa zinthu zomwe munandilembera nʼkwabwino kuti munthu asakwatire.
Torej glede stvari, o katerih ste mi pisali: ›Dobro je za moškega ne dotikati se ženske.‹
2 Koma chifukwa choti chigololo chawanda, mwamuna aliyense akhale naye mkazi wakewake ndipo mkazi aliyense akhale naye mwamuna wakewake.
Kljub temu naj ima, v izogib prešuštvovanju, vsak mož svojo lastno ženo in vsaka ženska naj ima svojega lastnega soproga.
3 Mwamuna akwaniritse udindo wake wa pa banja kwa mkazi wake, ndipo chimodzimodzi mkazi kwa mwamuna wake.
Naj soprog ženi vrača dolžno dobrohotnost in prav tako žena soprogu.
4 Thupi la mkazi wokwatiwa si la iye mwini yekha koma ndi la mwamuna wakenso. Momwemonso, thupi la mwamuna si la iye mwini yekha koma ndi la mkazi wakenso.
Žena nima oblasti nad svojim lastnim telesom, temveč soprog. In prav tako tudi soprog nima oblasti nad svojim lastnim telesom, temveč žena.
5 Musamakanizane, pokhapokha mutagwirizana awiri kuti mwakanthawi mudzipereke kumapemphero. Kenaka mukhalirenso pamodzi kuopa kuti Satana angakuyeseni chifukwa cholephera kudziretsa.
Ne prikrajšujta se drug drugemu, razen če je to s soglasjem za nekaj časa, da se lahko predata postu in molitvi; in ponovno pridita skupaj, da vaju zaradi vajinega pomanjkanja samoobvladovanja ne skuša Satan.
6 Ndikunena zimenezi mokulolani chabe osati mokulamulani.
Toda to govorim z dovoljenjem in ne po zapovedi.
7 Ine ndikanakonda anthu akanakhala ngati ine. Koma poti munthu aliyense ali ndi mphatso yakeyake yochokera kwa Mulungu, wina mphatso yake, wina yakenso.
Kajti želim, da bi bili vsi ljudje kakor jaz. Toda vsak človek ima svoj primeren dar od Boga, eden na ta način, drugi pa na drug.
8 Tsono kwa osakwatira onse, ndi akazi amasiye ndikuti, ndi bwino kwa iwo kukhala osakwatira monga mmene ndilili inemu.
Torej neporočenim in vdovam pravim: »Zanje je dobro, če ostanejo kakor jaz.«
9 Koma ngati sangathe kudziretsa, akwatire, popeza ndi bwino kukwatira kusiyana ndi kudzizunza ndi chilakolako.
Toda če se ne morejo brzdati, naj se poročé; kajti bolje se je poročiti kakor plameneti.
10 Kwa amene ali pa banja ndikupatsani lamulo ili (osati langa koma la Ambuye): Mkazi asalekane ndi mwamuna wake.
Poročenim pa naročam, čeprav ne jaz, temveč Gospod: »Naj žena ne odide od svojega soproga.
11 Koma ngati atatero, asakwatiwenso, apo ayi, abwerere kwa mwamuna wakeyo. Ndipo mwamuna asaleke mkazi wake.
Toda če odide, naj ostane neomožena ali naj se pobota k svojemu soprogu, in soprog naj svoje žene ne odslovi.«
12 Kwa ena onse ndikunena izi (ineyo osati Ambuye); ngati mʼbale wina ali ndi mkazi wosakhulupirira ndipo mkaziyo walola kukhala pa banja ndi mʼbaleyo, ameneyo asamuleke.
Toda drugim govorim jaz, ne Gospod: »Če ima katerikoli brat ženo, ki ne veruje in je zadovoljna, da prebiva z njim, naj je ne odslovi.
13 Ngati mayi wina ali ndi mwamuna wosakhulupirira ndipo mwamunayo walola kukhala pa banja ndi mayiyo, ameneyo asamuleke.
In ženska, ki ima soproga, ki ne veruje in če je zadovoljen, da prebiva z njo, naj ga ona ne zapusti.
14 Pakuti mwamuna wosakhulupirirayo amayeretsedwa chifukwa cha mkazi wakeyo, ndipo mkazi wosakhulupirira amayeretsedwa chifukwa cha mwamuna wokhulupirirayo. Kupanda apo ana anu akanakhala odetsedwa, koma mmene zililimu ndi oyeretsedwa.
Kajti neverni soprog je posvečen po ženi in neverna žena je posvečena po soprogu; sicer bi bili vaši otroci nečisti, toda sedaj so sveti.
15 Koma ngati wosakhulupirira achoka, mulekeni achoke. Zikatero ndiye kuti mwamuna kapena mkazi wokhulupirirayo sali womangikanso. Mulungu anatiyitana kuti tikhale mu mtendere.
Toda če neverni odide, naj odide. Brat ali sestra v teh primerih nista pod suženjstvom; toda Bog nas je poklical k miru.
16 Kodi iwe, mkazi, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mwamuna wako? Kapena iwe, mwamuna, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mkazi wako?
Kajti kaj veš ti, oh žena, če boš rešila svojega soproga? Ali kako veš ti, oh mož, če boš rešil svojo ženo?«
17 Koma aliyense akhale moyo umene Ambuye anamupatsa, umene Mulungu anamuyitanira. Ili ndiye lamulo limene ndalikhazikitsa mʼmipingo yonse.
Toda kakor je Bog vsakemu človeku razdelil, kakor je Gospod vsakogar poklical, tako naj hodi. In tako določam v vseh cerkvah.
18 Ngati pamene munthu amayitanidwa anali atachita mdulidwe, asavutike nʼkubisa za mdulidwe wakewo. Ngatinso pamene munthu amayitanidwa nʼkuti asanachite mdulidwe, asachite mdulidwe.
Ali je poklican katerikoli mož, ki je obrezan? Naj ne postane neobrezan. Ali je kateri poklican neobrezan? Naj ne bo obrezan.
19 Mdulidwe si kanthu, kusachita mdulidwe si kanthunso. Chofunika nʼkusunga malamulo a Mulungu.
Obreza ni nič in neobreza ni nič, temveč izpolnjevanje Božjih zapovedi.
20 Aliyense akhale monga analili pamene Mulungu anamuyitana.
Naj vsak ostane v isti poklicanosti, v katero je bil poklican.
21 Kodi munali kapolo pamene Mulungu anakuyitanani? Musavutike nazo zimenezi. Koma ngati mutapeza mwayi woti mulandire ufulu, ugwiritseni ntchito mwayiwo.
Ali si bil poklican kot služabnik? Ne skrbi za to. Toda če lahko postaneš svoboden, to vsekakor izkoristi.
22 Pakuti amene anali kapolo pamene amayitanidwa ndi Ambuye, ndi mfulu wa Ambuye; chimodzimodzinso amene anali mfulu pamene anayitanidwa, ndi kapolo wa Khristu.
Kajti kdor je poklican v Gospodu kot služabnik, je Gospodov osvobojenec; prav tako tudi kdor je poklican kot svoboden, je Kristusov služabnik.
23 Munagulidwa ndi mtengowapatali, choncho musakhalenso akapolo a anthu.
Odkupljeni ste za ceno; ne bodite služabniki ljudem.
24 Abale, aliyense angokhala pamaso pa Mulungu monga momwe analili pamene Mulungu anamuyitana.
Bratje, naj vsak ostane z Bogom v tem, v čemer je bil poklican.
25 Tsopano za anamwali: Ine ndilibe lamulo lochokera kwa Ambuye, koma ndipereka maganizo anga monga ngati munthu amene mwachifundo cha Ambuye ndine wodalirika.
Torej glede devic nimam zapovedi od Gospoda; čeprav dam svoje mnenje kakor nekdo, ki je dosegel usmiljenje od Gospoda, da je zvest.
26 Chifukwa cha masautso a masiku ano, ndikuganiza kuti nʼkwabwino kuti munthu akhale monga mmene alili.
Domnevam torej, da je to dobro zaradi sedanje stiske; pravim, da je to dobro za človeka, da je tako.
27 Kodi ndinu wokwatira? Musalekane. Kodi ndinu wosakwatira? Musafunefune mkazi.
Ali si vezan k ženi? Ne skušaj biti razvezan. Ali si razvezan od žene? Ne išči žene.
28 Komabe ngati mukwatira simunachimwe; ndipo ngati namwali akwatiwa sanachimwenso. Koma amene walowa mʼbanja adzakumana ndi zovuta zambiri mʼmoyo uno, ndipo sindikufuna kuti inu mukumane ndi zovutazi.
Toda če pa se poročiš, nisi grešil; in če se devica poroči, ni grešila. Vendar bodo taki imeli stisko v mesu; toda prizanašam vam.
29 Abale, chimene ndikutanthauza nʼchakuti nthawi yatha. Kuyambira tsopano anthu okwatira akhale ngati sanakwatire.
Toda pravim to, bratje, čas je kratek. Preostaja to, da so tisti, ki imajo žene, kakor da jih ne bi imeli;
30 Amene akulira akhale monga ngati sakulira. Amene akukondwa akhale ngati sakukondwa. Amene akugula zinthu akhale ngati alibe zinthuzo.
in tisti, ki jokajo, kakor ne bi jokali; in tisti, ki se veselijo, kakor da se ne bi veselili; in tisti, ki kupujejo, kakor ne bi imeli v lasti;
31 Amene akugwiritsa ntchito zinthu za dziko lapansi lino, akhale ngati sizikuwakhudza. Pakuti dziko lapansi lino mmene lilirimu, likupita.
in tisti, ki uporabljajo ta svet, kakor ga ne bi zlorabljali; kajti videz tega sveta mineva.
32 Ine ndikufuna kuti mumasuke ku nkhawa zanu. Munthu wosakwatira amangolabadira za Ambuye, mmene angakondweretsere Ambuyewo.
Toda hočem, da ste brez skrbi. Kdor je neporočen, skrbi za stvari, ki pripadajo Gospodu, kako bi lahko ugajal Gospodu;
33 Koma wa pa banja amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mkazi wake,
toda kdor je poročen, skrbi za stvari, ki so od sveta, kako bi lahko ugajal svoji ženi.
34 ndipo chifukwa ichi amatanganidwa kwambiri. Mkazi wosakwatiwa kapena namwali, amalabadira za Ambuye. Cholinga chake ndi kudzipereka kwa Ambuye mʼthupi ndi mu uzimu momwe. Koma mkazi wokwatiwa amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mwamuna wake.
Razlika je tudi med ženo in devico. Neporočena ženska skrbi za Gospodove stvari, da bi bila lahko sveta, tako v telesu kakor v duhu; toda tista, ki je poročena, skrbi za svetne stvari, kako bi lahko ugodila svojemu soprogu.
35 Ndikunena izi kufuna kuthandiza inu nomwe osati kukupanikizani. Ine ndikufuna mukhale moyenera mosadzigawa pa kudzipereka kwanu kwa Ambuye.
In to govorim v vašo lastno korist; ne da bi na vas lahko vrgel zanko, temveč k temu kar je ljubko in da bi lahko nemoteno služili Gospodu.
36 Ngati wina akuganiza kuti akumulakwira namwali yemwe anapalana naye ubwenzi, ndipo ngati chilakolako chake chikunka chikulirakulirabe, ndipo akuona kuti nʼkofunika kumukwatira, ayenera kuchita monga wafunira, kutero si kuchimwa ayi.
Toda če kateri človek misli, da se do svoje device vede nespodobno, če je minil cvet njenih let in potreba tako zahteva, naj stôri, kar hoče, ne greši; naj se poročita.
37 Koma ngati wina motsimikiza mtima wake, popanda womukakamiza, koma akuchita mwa chifuniro chake, ndipo watsimikiza mtima kuti samukwatira namwaliyo, munthuyu akuchitanso chokhoza.
Vendar kdor v svojem srcu neomajno stoji in nima nujne potrebe, temveč ima oblast nad svojo lastno voljo in je v svojem srcu tako določil, da bo ohranil svojo devico, stori pravilno.
38 Choncho amene akukwatira namwali amene ali naye pa ubwenzi, akuchita bwino, koma amene sangakwatire namwaliyo akuchita bwino koposa.
Tako torej kdor jo daje v zakon, stori pravilno; toda kdor je ne daje v zakon, stori bolje.
39 Mkazi amamangika ndi lamulo la ukwati nthawi zonse pamene mwamuna wake ali ndi moyo. Koma mwamuna wake akamwalira, ali ndi ufulu kukwatiwa ndi wina aliyense amene akumufuna, koma mwamunayo akhale wa mwa Ambuye.
Žena je vezana s postavo, dokler njen soprog živi; toda če njen soprog umre, je prosta, da se poroči s komer hoče; le v Gospodu.
40 Mʼmaganizo anga, mkaziyo adzakhala wokondwa koposa ngati atangokhala wosakwatiwa. Ndipo ndikuganiza kuti inenso ndili naye Mzimu wa Mulungu.
Toda po moji sodbi je srečnejša, če ostane tako; in mislim, da imam tudi jaz Božjega Duha.