< Aroma 1 >
1 Ndine Paulo, mtumiki wa Khristu Yesu, woyitanidwa ndi Mulungu kukhala mtumwi. Ndinapatulidwa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Mulungu
Pavel, služabnik Jezusa Kristusa, poklican, da bi bil apostol, odbran za evangelij Boga,
2 umene analonjeza kale mʼMalemba Oyera kudzera mwa aneneri ake.
(ki ga je vnaprej obljubil po svojih prerokih v svetih pismih),
3 Uthengawu ndi wonena za Mwana wake amene mwa umunthu wake anali wochokera mwa Davide.
glede svojega Sina Jezusa Kristusa, našega Gospoda, ki je glede na meso zrasel iz Davidovega potomca;
4 Iyeyu ndi amene anatsimikizidwa kukhala Mwana wa Mulungu mwamphamvu za Mzimu Woyera pamene anauka kwa akufa. Kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu,
in z vstajenjem od mrtvih je, glede na duha svetosti, razglasil, da je Božji Sin z močjo;
5 ife tinalandira chisomo chokhala atumwi oyitana anthu a mitundu yonse kuti amukhulupirire ndi kumumvera mwachikhulupiriro kuti dzina lake lilemekezedwe.
po katerem smo zaradi njegovega imena prejeli milost in apostolstvo, za poslušnost veri med vsemi narodi;
6 Inunso muli mʼgulu la Amitundu oyitanidwawo kukhala ake a Yesu Khristu.
med katere ste po Jezusu Kristusu poklicani tudi vi.
7 Ndikulembera kwa onse okhala ku Roma amene Mulungu amakukondani nakuyitanani kuti mukhale oyera mtima. Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi kwa Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
Vsem, ki ste v Rimu, Božji ljubljenci, poklicani, da ste sveti: ›Milost vam in mir od Boga, našega Očeta in Gospoda Jezusa Kristusa.‹
8 Poyamba, ndikuthokoza Mulungu wanga kudzera mwa Yesu Khristu chifukwa cha nonsenu, pakuti pa dziko lonse lapansi anthu akukamba za chikhulupiriro chanu.
Najprej se po Jezusu Kristusu zahvaljujem svojemu Bogu za vas vse, da se o vaši veri govori po vsem celotnem svetu.
9 Mulungu amene ndimamutumikira ndi mtima wanga onse polalikira Uthenga Wabwino wa Mwana wake, ndi mboni yanga kuti ndimakupemphererani nthawi zonse.
Kajti Bog je moja priča, ki mu služim s svojim duhom v evangeliju njegovega Sina, da vas brez prenehanja vedno omenjam v svojih molitvah,
10 Mʼmapemphero anga, nthawi zonse, ndimapemphera kuti ngati nʼkotheka mwachifuniro cha Mulungu, njira inditsekukire kuti ndibwere kwanuko.
ker prosim, če bi na kakršenkoli način torej končno lahko imel uspešno potovanje, da po Božji volji pridem k vam.
11 Ine ndikulakalaka kukuonani kuti ndikugawireni mphatso zina zauzimu kuti zikulimbikitseni
Kajti hrepenim, da vas vidim, da bi vam lahko posredoval kak duhoven dar, z namenom, da boste lahko utrjeni;
12 ndiponso kuti tonsefe tilimbikitsane mʼchikhulupiriro wina ndi mnzake.
to je, da bom lahko skupaj z vami potolažen po vzajemni veri, tako vaši kakor moji.
13 Abale, ine sindifuna kuti mukhale osadziwa kuti nthawi zambiri ndakhala ndikufuna zobwera kwanuko, koma mpaka pano pali zolepheretsa, ndi cholinga choti ndidzapezeko zipatso pakati panupo monga momwe ndakhala ndikuchitira pakati pa a mitundu ina.
Torej, nočem, da bi bili nepoučeni, bratje, da sem se pogosto namenil priti k vam (toda doslej sem bil zadržan), da bi lahko imel, kakor med drugimi pogani, nekaj sadu tudi med vami.
14 Ine ndi wokakamizidwa ndi udindo wotumikira Agriki pamodzi ndi omwe si Agriki, kwa anzeru ndi kwa opusa omwe.
Dolžnik sem, tako Grkom kakor barbarom, tako modrim, kakor ne modrim.
15 Pa chifukwa chimenechi, ine ndikufunitsitsa kulalikira Uthenga Wabwino kwa inunso amene muli ku Roma.
Torej, kar se mene tiče, sem pripravljen evangelij oznaniti tudi vam, ki ste v Rimu.
16 Ine sindichita manyazi ndi Uthenga Wabwino chifukwa ndiwo mphamvu za Mulungu zopulumutsa aliyense amene akhulupirira, poyamba Myuda, kenaka Mhelene.
Kajti ne sramujem se Kristusovega evangelija, kajti ta je Božja moč za rešitev duš vsakemu, ki veruje; najprej Judu in tudi Grku.
17 Pakuti mu Uthenga Wabwino anawulula kuti chilungamo chimachokera kwa Mulungu. Kuyambira pachiyambi mpaka potsiriza ndi chilungamo chobwera mwachikhulupiriro, monga kwalembedwera kuti, “Wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.”
Kajti v njem se razodeva Božja pravičnost, iz vere v vero, kakor je pisano: ›Pravični bo živel iz vere.‹
18 Mkwiyo wa Mulungu ukuonekera kuchokera kumwamba. Ukutsutsana ndi kusapembedza konse ndi kuyipa kwa anthu amene amapondereza choonadi mwa chikhalidwe chawo choyipa.
Kajti Božji bes je razodet iz nebes zoper vso brezbožnost in nepravičnost ljudi, ki resnico zadržujejo v nepravičnosti;
19 Za Mulungu zimene zingathe kudziwika, ndi zomveka bwino kwa iwo pakuti Mulungu anazionetsera kwa iwo.
zato ker je to, kar je lahko spoznano od Boga, očitno v njih; kajti Bog jim je to pokazal.
20 Pakuti kuyambira pamene dziko lapansi linalengedwa, zinthu zosaoneka za Mulungu, mphamvu zake zosatha ndi chikhalidwe cha umulungu, zakhala zikuoneka bwinobwino. Akhala akuzindikira poona zimene Mulungu analenga, kotero kuti anthu sangathe kuwiringula. (aïdios )
Kajti od stvarjenja sveta so nevidne stvari o njem jasno vidne, ker so razumljene po stvareh, ki so narejene; celó njegova večna moč in Božanstvo, tako da so brez opravičila. (aïdios )
21 Ngakhale iwo anadziwa Mulungu, sanamulemekeze ngati Mulungu kapena kumuthokoza, koma maganizo awo anasanduka wopanda pake ndipo mʼmitima yawo yopusa munadzaza mdima.
Zato ker ko so spoznali Boga, ga niso slavili kakor Boga niti niso bili hvaležni, temveč so v svojih zamislih postali prazni in njihovo nespametno srce je otemnelo.
22 Ngakhale ankadzitama kuti ndi anzeru, anasanduka opusa.
Ker so o sebi izpovedovali, da so modri, so postali bedaki
23 Iwo anasinthanitsa ulemerero wa Mulungu wosafa ndi mafano opangidwa ndi manja wooneka ngati munthu amene amafa, kapena ngati mbalame, ndi nyama kapena zokwawa.
in slavo netrohljivega Boga spremenili v podobo, podobno trohljivemu človeku in pticam in štirinožnim živalim in plazečim stvarem.
24 Nʼchifukwa chake Mulungu anawasiya kuti azingochita zilakolako zochititsa manyazi zauchimo zomwe mitima yawo inkafuna. Zotsatira zake anachita za chiwerewere wina ndi mnzake kunyazitsa matupi awo.
Zato jih je tudi Bog, zaradi poželenj njihovih lastnih src, prepustil nečistosti, da med seboj onečaščajo svoja lastna telesa.
25 Iwo anasinthanitsa choonadi cha Mulungu ndi bodza ndipo anapembedza ndi kutumikira zinthu zolengedwa mʼmalo mwa Mlengi amene ali woyenera kutamandidwa mpaka muyaya. Ameni. (aiōn )
Ki so Božjo resnico zamenjali v laž in so bolj oboževali in služili stvarstvu kakor Stvarniku, ki je blagoslovljen na veke. Amen. (aiōn )
26 Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.
Zaradi tega razloga jih je Bog prepustil ogabnim strastem; kajti celó njihove ženske so spremenile naravno uporabo v to, kar je protinaravno.
27 Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo.
In prav tako so tudi moški, ki so opustili naravno uporabo ženske, v svojem poželenju goreli eden k drugemu; moški so z moškimi počenjali to, kar je nespodobno in na sebi prejemali to povračilo svoje zablode, ki je bilo primerno.
28 Ndipo popeza anaona kuti nʼchopanda nzeru kumvera Mulungu, Iye anawasiya kuti atsatire maganizo achitayiko kuti achite zosayenera kuchitazo.
In celó kot v svojem spoznanju niso želeli obdržati Boga, jih je Bog izročil pokvarjenemu umu, da počenjajo te stvari, ki niso primerne.
29 Iwo ndi odzazidwa ndi mtundu uliwonse wa makhalidwe oyipa, zonyansa, umbombo ndi dumbo. Iwo ndi odzazidwa ndi kaduka, kupha, mikangano, chinyengo ndi udani. Iwowo ndi amiseche,
Izpolnjeni so z vso nepravičnostjo, prešuštvom, zlobnostjo, pohlepnostjo, zlonamernostjo; polni zavisti, umora, razpravljanja, prevar, pogubnosti; opravljivci,
30 osinjirira, odana ndi Mulungu, achipongwe, odzitama ndi odzitukumula. Iwo amapeza njira zochitira zoyipa. Samvera makolo awo,
obrekovalci, sovražniki Boga, kruti, ponosni, bahači, izmišljevalci hudobnih stvari, neposlušni staršem,
31 alibe nzeru, chikhulupiriro, sakhudzidwa mu mtima ndipo ndi ankhanza.
brez razumevanja, lomilci zavez, brez naravne naklonjenosti, nespravljivi, neusmiljeni.
32 Ngakhale kuti amadziwa chiweruzo cholungama cha Mulungu chakuti amene amachita zinthu zotere amayenera imfa, iwo sangopitiriza chabe zimenezi, koma amavomerezanso amene amazichita zimenezi.
Ki poznajo Božje sodbe, da so tisti, ki zagrešijo takšne stvari, vredni smrti, ne samo, da to počenjajo, temveč imajo zadovoljstvo v tistih, ki jih počno.