< 1 Akorinto 7 >

1 Tsopano pa zinthu zomwe munandilembera nʼkwabwino kuti munthu asakwatire.
Now concerning the things whereof ye wrote: It is good for a man not to touch a woman.
2 Koma chifukwa choti chigololo chawanda, mwamuna aliyense akhale naye mkazi wakewake ndipo mkazi aliyense akhale naye mwamuna wakewake.
But, because of fornications, let each man have his own wife, and let each woman have her own husband.
3 Mwamuna akwaniritse udindo wake wa pa banja kwa mkazi wake, ndipo chimodzimodzi mkazi kwa mwamuna wake.
Let the husband render unto the wife her due: and likewise also the wife unto the husband.
4 Thupi la mkazi wokwatiwa si la iye mwini yekha koma ndi la mwamuna wakenso. Momwemonso, thupi la mwamuna si la iye mwini yekha koma ndi la mkazi wakenso.
The wife hath not power over her own body, but the husband: and likewise also the husband hath not power over his own body, but the wife.
5 Musamakanizane, pokhapokha mutagwirizana awiri kuti mwakanthawi mudzipereke kumapemphero. Kenaka mukhalirenso pamodzi kuopa kuti Satana angakuyeseni chifukwa cholephera kudziretsa.
Defraud ye not one the other, except it be by consent for a season, that ye may give yourselves unto prayer, and may be together again, that Satan tempt you not because of your incontinency.
6 Ndikunena zimenezi mokulolani chabe osati mokulamulani.
But this I say by way of permission, not of commandment.
7 Ine ndikanakonda anthu akanakhala ngati ine. Koma poti munthu aliyense ali ndi mphatso yakeyake yochokera kwa Mulungu, wina mphatso yake, wina yakenso.
Yet I would that all men were even as I myself. Howbeit each man hath his own gift from God, one after this manner, and another after that.
8 Tsono kwa osakwatira onse, ndi akazi amasiye ndikuti, ndi bwino kwa iwo kukhala osakwatira monga mmene ndilili inemu.
But I say to the unmarried and to widows, It is good for them if they abide even as I.
9 Koma ngati sangathe kudziretsa, akwatire, popeza ndi bwino kukwatira kusiyana ndi kudzizunza ndi chilakolako.
But if they have not continency, let them marry: for it is better to marry than to burn.
10 Kwa amene ali pa banja ndikupatsani lamulo ili (osati langa koma la Ambuye): Mkazi asalekane ndi mwamuna wake.
But unto the married I give charge, [yea] not I, but the Lord, That the wife depart not from her husband
11 Koma ngati atatero, asakwatiwenso, apo ayi, abwerere kwa mwamuna wakeyo. Ndipo mwamuna asaleke mkazi wake.
(but and if she depart, let her remain unmarried, or else be reconciled to her husband); and that the husband leave not his wife.
12 Kwa ena onse ndikunena izi (ineyo osati Ambuye); ngati mʼbale wina ali ndi mkazi wosakhulupirira ndipo mkaziyo walola kukhala pa banja ndi mʼbaleyo, ameneyo asamuleke.
But to the rest say I, not the Lord: If any brother hath an unbelieving wife, and she is content to dwell with him, let him not leave her.
13 Ngati mayi wina ali ndi mwamuna wosakhulupirira ndipo mwamunayo walola kukhala pa banja ndi mayiyo, ameneyo asamuleke.
And the woman which hath an unbelieving husband, and he is content to dwell with her, let her not leave her husband.
14 Pakuti mwamuna wosakhulupirirayo amayeretsedwa chifukwa cha mkazi wakeyo, ndipo mkazi wosakhulupirira amayeretsedwa chifukwa cha mwamuna wokhulupirirayo. Kupanda apo ana anu akanakhala odetsedwa, koma mmene zililimu ndi oyeretsedwa.
For the unbelieving husband is sanctified in the wife, and the unbelieving wife is sanctified in the brother: else were your children unclean; but now are they holy.
15 Koma ngati wosakhulupirira achoka, mulekeni achoke. Zikatero ndiye kuti mwamuna kapena mkazi wokhulupirirayo sali womangikanso. Mulungu anatiyitana kuti tikhale mu mtendere.
Yet if the unbelieving departeth, let him depart: the brother or the sister is not under bondage in such [cases]: but God hath called us in peace.
16 Kodi iwe, mkazi, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mwamuna wako? Kapena iwe, mwamuna, ungadziwe bwanji kuti mwina nʼkupulumutsa mkazi wako?
For how knowest thou, O wife, whether thou shalt save thy husband? or how knowest thou, O husband, whether thou shalt save thy wife?
17 Koma aliyense akhale moyo umene Ambuye anamupatsa, umene Mulungu anamuyitanira. Ili ndiye lamulo limene ndalikhazikitsa mʼmipingo yonse.
Only, as the Lord hath distributed to each man, as God hath called each, so let him walk. And so ordain I in all the churches.
18 Ngati pamene munthu amayitanidwa anali atachita mdulidwe, asavutike nʼkubisa za mdulidwe wakewo. Ngatinso pamene munthu amayitanidwa nʼkuti asanachite mdulidwe, asachite mdulidwe.
Was any man called being circumcised? let him not become uncircumcised. Hath any been called in uncircumcision? let him not be circumcised.
19 Mdulidwe si kanthu, kusachita mdulidwe si kanthunso. Chofunika nʼkusunga malamulo a Mulungu.
Circumcision is nothing, and uncircumcision is nothing; but the keeping of the commandments of God.
20 Aliyense akhale monga analili pamene Mulungu anamuyitana.
Let each man abide in that calling wherein he was called.
21 Kodi munali kapolo pamene Mulungu anakuyitanani? Musavutike nazo zimenezi. Koma ngati mutapeza mwayi woti mulandire ufulu, ugwiritseni ntchito mwayiwo.
Wast thou called being a bondservant? care not for it: but if thou canst become free, use [it] rather.
22 Pakuti amene anali kapolo pamene amayitanidwa ndi Ambuye, ndi mfulu wa Ambuye; chimodzimodzinso amene anali mfulu pamene anayitanidwa, ndi kapolo wa Khristu.
For he that was called in the Lord, being a bondservant, is the Lord’s freedman: likewise he that was called, being free, is Christ’s bondservant.
23 Munagulidwa ndi mtengowapatali, choncho musakhalenso akapolo a anthu.
Ye were bought with a price; become not bondservants of men.
24 Abale, aliyense angokhala pamaso pa Mulungu monga momwe analili pamene Mulungu anamuyitana.
Brethren, let each man, wherein he was called, therein abide with God.
25 Tsopano za anamwali: Ine ndilibe lamulo lochokera kwa Ambuye, koma ndipereka maganizo anga monga ngati munthu amene mwachifundo cha Ambuye ndine wodalirika.
Now concerning virgins I have no commandment of the Lord: but I give my judgment, as one that hath obtained mercy of the Lord to be faithful.
26 Chifukwa cha masautso a masiku ano, ndikuganiza kuti nʼkwabwino kuti munthu akhale monga mmene alili.
I think therefore that this is good by reason of the present distress, [namely], that it is good for a man to be as he is.
27 Kodi ndinu wokwatira? Musalekane. Kodi ndinu wosakwatira? Musafunefune mkazi.
Art thou bound unto a wife? seek not to be loosed. Art thou loosed from a wife? seek not a wife.
28 Komabe ngati mukwatira simunachimwe; ndipo ngati namwali akwatiwa sanachimwenso. Koma amene walowa mʼbanja adzakumana ndi zovuta zambiri mʼmoyo uno, ndipo sindikufuna kuti inu mukumane ndi zovutazi.
But and if thou marry, thou hast not sinned; and if a virgin marry, she hath not sinned. Yet such shall have tribulation in the flesh: and I would spare you.
29 Abale, chimene ndikutanthauza nʼchakuti nthawi yatha. Kuyambira tsopano anthu okwatira akhale ngati sanakwatire.
But this I say, brethren, the time is shortened, that henceforth both those that have wives may be as though they had none;
30 Amene akulira akhale monga ngati sakulira. Amene akukondwa akhale ngati sakukondwa. Amene akugula zinthu akhale ngati alibe zinthuzo.
and those that weep, as though they wept not; and those that rejoice, as though they rejoiced not; and those that buy, as though they possessed not;
31 Amene akugwiritsa ntchito zinthu za dziko lapansi lino, akhale ngati sizikuwakhudza. Pakuti dziko lapansi lino mmene lilirimu, likupita.
and those that use the world, as not abusing it: for the fashion of this world passeth away.
32 Ine ndikufuna kuti mumasuke ku nkhawa zanu. Munthu wosakwatira amangolabadira za Ambuye, mmene angakondweretsere Ambuyewo.
But I would have you to be free from cares. He that is unmarried is careful for the things of the Lord, how he may please the Lord:
33 Koma wa pa banja amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mkazi wake,
but he that is married is careful for the things of the world, how he may please his wife.
34 ndipo chifukwa ichi amatanganidwa kwambiri. Mkazi wosakwatiwa kapena namwali, amalabadira za Ambuye. Cholinga chake ndi kudzipereka kwa Ambuye mʼthupi ndi mu uzimu momwe. Koma mkazi wokwatiwa amalabadira za dziko lapansi lino, mmene angakondweretsere mwamuna wake.
And there is a difference also between the wife and the virgin. She that is unmarried is careful for the things of the Lord, that she may be holy both in body and in spirit: but she that is married is careful for the things of the world, how she may please her husband.
35 Ndikunena izi kufuna kuthandiza inu nomwe osati kukupanikizani. Ine ndikufuna mukhale moyenera mosadzigawa pa kudzipereka kwanu kwa Ambuye.
And this I say for your own profit; not that I may cast a snare upon you, but for that which is seemly, and that ye may attend upon the Lord without distraction.
36 Ngati wina akuganiza kuti akumulakwira namwali yemwe anapalana naye ubwenzi, ndipo ngati chilakolako chake chikunka chikulirakulirabe, ndipo akuona kuti nʼkofunika kumukwatira, ayenera kuchita monga wafunira, kutero si kuchimwa ayi.
But if any man thinketh that he behaveth himself unseemly toward his virgin [daughter], if she be past the flower of her age, and if need so requireth, let him do what he will; he sinneth not; let them marry.
37 Koma ngati wina motsimikiza mtima wake, popanda womukakamiza, koma akuchita mwa chifuniro chake, ndipo watsimikiza mtima kuti samukwatira namwaliyo, munthuyu akuchitanso chokhoza.
But he that standeth stedfast in his heart, having no necessity, but hath power as touching his own will, and hath determined this in his own heart, to keep his own virgin [daughter], shall do well.
38 Choncho amene akukwatira namwali amene ali naye pa ubwenzi, akuchita bwino, koma amene sangakwatire namwaliyo akuchita bwino koposa.
So then both he that giveth his own virgin [daughter] in marriage doeth well; and he that giveth her not in marriage shall do better.
39 Mkazi amamangika ndi lamulo la ukwati nthawi zonse pamene mwamuna wake ali ndi moyo. Koma mwamuna wake akamwalira, ali ndi ufulu kukwatiwa ndi wina aliyense amene akumufuna, koma mwamunayo akhale wa mwa Ambuye.
A wife is bound for so long time as her husband liveth; but if the husband be dead, she is free to be married to whom she will; only in the Lord.
40 Mʼmaganizo anga, mkaziyo adzakhala wokondwa koposa ngati atangokhala wosakwatiwa. Ndipo ndikuganiza kuti inenso ndili naye Mzimu wa Mulungu.
But she is happier if she abide as she is, after my judgment: and I think that I also have the Spirit of God.

< 1 Akorinto 7 >