< 1 Akorinto 14 >

1 Funafunani chikondi, ndikufunitsitsa mphatso zauzimu, makamaka mphatso ya uneneri.
Recherchez avec ardeur la charité; désirez les dons spirituels, et surtout de prophétiser.
2 Pakuti aliyense amene amayankhula malilime sayankhula kwa anthu, koma kwa Mulungu. Zoonadi, palibe amene amamva zimene akunena chifukwa Mzimu ndiye amamuyankhulitsa zachinsinsi.
Car celui qui parle en une langue ne parle pas aux hommes, mais à Dieu, puisque personne ne l’entend; mais par l’Esprit il dit des choses mystérieuses.
3 Koma amene amanenera amayankhula kwa anthu kuti awapatse mphamvu, awalimbikitse ndi kuwakhazikitsa mtima pansi.
Mais celui qui prophétise parle aux hommes pour l’édification, l’exhortation et la consolation.
4 Iye amene amayankhula malilime amadzilimbikitsa yekha, koma amene amanenera amalimbikitsa mpingo.
Celui qui parle une langue s’édifie lui-même, tandis que celui qui prophétise édifie l’Eglise de Dieu.
5 Nʼkanakonda kuti aliyense mwa inu atamayankhula malilime, koma ndi bwino kuti muzinenera. Amene amanenera amaposa amene amayankhula malilime, pokhapokha atatanthauzira kuti mpingo upindule.
Je voudrais que vous pussiez tous parler les langues, mais encore plus prophétiser. Car celui qui prophétise est au-dessus de celui qui parle les langues; à moins qu’il n’interprète, afin que l’Eglise en reçoive de l’édification.
6 Tsono, abale, mudzapindula chiyani nditabwera kwa inu ndi kukuyankhulani mʼmalilime? Koma mudzapindula ngati nditakubweretserani vumbulutso lina lake, kapena chidziwitso, kapena chiphunzitso.
Aussi, mes frères, si je viens à vous parlant les langues, à quoi vous serai-je utile, si je ne joins à mes paroles ou la révélation, ou la science, ou la prophétie, ou la doctrine?
7 Ngakhale mu zinthu zopanda moyo monga chitoliro kapena gitala, zimene zimatulutsa liwu; kodi munthu akhoza kudziwa bwanji nyimbo imene ikuyimbidwa ngati mawu sakumveka mogwirizana bwino?
Les choses qui sont inanimées quoique rendant des sons, comme la flûte et la harpe, si elles ne forment des tons différents, comment saura-t-on ce qu’on joue sur la flûte ou sur la harpe?
8 Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?
Et si la trompette rend un son incertain, qui se préparera au combat?
9 Chimodzimodzinso inu. Ngati simungayankhule mawu omveka bwino mʼchiyankhulo chanu, wina angadziwe bwanji chimene mukunena? Muzingodziyankhulira nokha.
De même vous, si vous exprimez par la langue des mots qui ne sont pas clairs, comment saura-t-on ce que vous dites? Vous parlerez en l’air.
10 Mosakayika, pali ziyankhulo zosiyanasiyana pa dziko lapansi, koma palibe nʼchimodzi chomwe chimene chilibe tanthauzo.
Il y a, en effet, tant de sortes de langues dans ce monde; et il n’en est aucune qui n’ait des sons intelligibles.
11 Tsono ngati sindingatolepo tanthauzo la zimene wina akuyankhula, ndiye kuti ndine mlendo kwa oyankhulayo ndipo iyeyo ndi mlendo kwa ine.
Si donc j’ignore la valeur des mots, je serai barbare pour celui à qui je parle, et celui qui parle, barbare pour moi.
12 Chimodzimodzinso inu. Popeza mumafunitsitsa mphatso za Mzimu, yesetseni kuchita bwino pa mphatso zimene zimamanga mpingo.
Ainsi, vous-mêmes puisque vous désirez si ardemment les dons spirituels, faites que pour l’édification de l’Eglise vous en abondiez.
13 Pa chifukwa ichi munthu amene amayankhula malilime apemphere kuti azitha kutanthauzira zimene akunena.
C’est pourquoi, que celui qui parle une langue demande le don de l’interpréter.
14 Popeza ngati ndipemphera mʼmalilime, ndi mzimu wanga umene ukupemphera, koma nzeru zanga sizikupindula kanthu.
Car si je prie en une langue, mon esprit prie, mais mon intelligence est sans fruit.
15 Tsono pamenepa nʼkutani? Ndidzapemphera ndi mzimu wanga, komanso ndidzapemphera ndi nzeru zanga. Ndidzayimba ndi mzimu wanga, komanso ndidzayimba ndi nzeru zanga.
Que ferai-je donc? je prierai d’esprit, mais je prierai aussi avec l’intelligence. Je chanterai d’esprit des cantiques, mais je les chanterai aussi avec l’intelligence.
16 Ngati mutamanda Mulungu mu mzimu, kodi munthu amene wapezeka pakati pa amene akuyankhula zomwe sakumva, adzavomereza bwanji kuti “Ameni” pa pemphero lanu loyamikalo popeza sakumva chimene mukunena?
D’ailleurs si tu ne bénis que d’esprit, comment celui qui tient la place du simple peuple répondra-t-il Amen à ta bénédiction, puisqu’il ne sait pas ce que tu dis?
17 Mukhoza kumathokoza mokwanira, koma munthu winayo sanathandizikepo.
Pour toi, tu rends bien grâces, mais l’autre n’est pas édifié.
18 Ndikuyamika Mulungu chifukwa ndimayankhula malilime kuposa nonsenu.
Je rends grâces à mon Dieu de ce que je parle les langues de vous tous.
19 Koma mu mpingo ndi kwabwino kuti ndiyankhule mawu asanu okha omveka bwino kuti ndilangize bwino ena kusiyana ndikuyankhula mawu ambirimbiri mʼmalilime.
Mais dans l’Eglise, j’aime mieux dire cinq mots que je comprends, pour en instruire les autres, que dix mille en une langue.
20 Abale, lekani kuganiza ngati ana. Mukhale ana pa nkhani ya zoyipa koma mʼmaganizo anu mukhale okhwima.
Mes frères, ne devenez pas enfants par l’intelligence; mais soyez petits enfants en malice, et hommes faits en intelligence.
21 Zinalembedwa mʼMalamulo kuti, “Ndidzayankhula kwa anthu awa, kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo ndiponso ndi milomo yachilendo. Koma ngakhale nthawi imeneyo sadzandimvera Ine, akutero Ambuye.”
Il est écrit dans la loi: Je parlerai à ce peuple en d’autres langues et avec d’autres lèvres; et ainsi ils ne me prêteront même pas l’oreille, dit le Seigneur.
22 Kotero, malilime ndi chizindikiro, osati cha kwa okhulupirira koma kwa osakhulupirira. Koma kunenera ndi chizindikiro kwa okhulupirira osati kwa osakhulupirira.
C’est pourquoi les langues sont un signe, non pour les fidèles, mais pour les infidèles; au contraire, les prophéties sont, non pour les infidèles, mais pour les fidèles.
23 Kotero kuti ngati mpingo wonse utasonkhana pamodzi ndipo aliyense namayankhula malilime, ndipo wina amene sangazindikire kapena ena osakhulupirira nabwerapo, kodi sadzanena kuti mwachita misala?
Si donc une Eglise étant réunie en un seul lieu, tous parlent diverses langues, et qu’il entre des ignorants ou des infidèles, ne diront-ils pas que vous êtes fous?
24 Koma ngati wosakhulupirira kapena wina amene sakuzindikira abwera pamene aliyense akunenera, adzatsutsika mu mtima ndi zonse zimene akumva ndipo adzaweruzidwa ndi onse
Mais si tous prophétisent, et que quelque ignorant, ou quelque infidèle entre, il est convaincu par tous et jugé par tous;
25 ndipo zinsinsi za mu mtima mwake zidzawululika. Kotero kuti adzadzigwetsa pansi ndi kupembedza Mulungu akufuwula kuti, “Mulungu ali pakati panudi!”
Les secrets de son cœur sont dévoilés, de sorte que, tombant sur sa face, il adorera Dieu, déclarant que Dieu est vraiment en vous.
26 Kodi tsono abale, tinene chiyani? Pamene musonkhana pamodzi, aliyense amakhala ali ndi nyimbo yoti ayimbe, kapena mawu oti alangize, vumbulutso, malilime, kapena kumasulira kwake. Zonsezi cholinga chake chikhale kulimbikitsa mpingo.
Que faut-il donc, mes frères? Que quand vous vous assemblez, l’un ayant le chant, un autre l’enseignement, un autre la révélation, un autre les langues, un autre l’interprétation, tout se fasse pour l’édification.
27 Ngati wina ayankhula malilime, awiri kapena akachulukapo atatu ndiye ayankhule mmodzimmodzi, ndipo wina ayenera kutanthauzira zimene ayankhulazo.
S’il y en a qui parlent les langues, que deux seulement parlent, ou au plus trois, et tour à tour; et qu’un seul interprète.
28 Ngati palibe wotanthauzira, woyankhulayo akhale chete mu mpingo ndipo adziyankhulire iye mwini ndi Mulungu.
S’il n’y a point d’interprète, que chacun se taise, et qu’il parle à lui-même et à Dieu.
29 Aneneri awiri kapena atatu anenere, ndipo enawo asanthule mosamalitsa zimene anenerazo.
Quant aux prophètes, que deux ou trois parlent, et que les autres jugent.
30 Ndipo ngati vumbulutso labwera kwa munthu amene wakhala pansi, amene akuyankhulayo akhale chete.
Que s’il se fait une révélation à un autre de ceux qui sont assis, que le premier se taise.
31 Pakuti nonse mukhoza kunenera mmodzimmodzi motsatana kuti aliyense alangizidwe ndi kulimbikitsidwa.
Car vous pouvez tous prophétiser l’un après l’autre, afin que tous apprennent et soient exhortés;
32 Mizimu ya aneneri imamvera ulamuliro wa aneneri.
Et les esprits des prophètes sont soumis aux prophètes.
33 Pakuti Mulungu si Mulungu wachisokonezo koma wamtendere. Monga mwa mipingo yonse ya oyera mtima.
Car Dieu n’est pas un Dieu de dissension, mais de paix; comme je l’enseigne dans toutes les Eglises des saints.
34 Amayi akhale chete mʼmisonkhano ya mpingo. Iwo asaloledwe kuyankhula, koma azikhala omvera monga mmene lamulo linenera.
Que les femmes se taisent dans les Eglises, car il ne leur est pas permis de parler, mais elles doivent être soumises, comme la loi elle-même le dit.
35 Ngati ali ndi mafunso, akafunse amuna awo ku nyumba. Nʼchochititsa manyazi kuti mkazi ayankhule mu msonkhano wa mpingo.
Si elles veulent s’instruire de quelque chose, qu’elles interrogent leurs maris dans leur maison. Car il est honteux à une femme de parler dans l’Eglise.
36 Kodi kapena mawu a Mulungu anachokera kwa inu? Kapena anafika kwa inu nokha?
Est-ce de vous qu’est sortie la parole de Dieu? Est-ce à vous seuls qu’elle est parvenue?
37 Ngati wina aliyense akuganiza kuti ndi mneneri kapena kuti ali ndi mphatso za Mzimu, ayenera kudziwa kuti zimene ndikukulemberanizi ndi lamulo la Ambuye.
Si quelqu’un croit être prophète, ou spirituel, qu’il reconnaisse que les choses que je vous écris sont des commandements du Seigneur.
38 Ngati munthu savomereza zimenezi, iyeyonso sadzavomerezedwa.
Si quelqu’un l’ignore, il sera ignoré.
39 Nʼchifukwa chake, abale anga, funitsitsani kunenera, ndipo musaletse anthu kuyankhula malilime.
C’est pourquoi, mes frères, employez tout votre zèle à prophétiser, et n’empêchez point de parler les langues.
40 Koma chilichonse chichitike moyenera ndi mwadongosolo.
Mais que tout se fasse décemment et avec ordre.

< 1 Akorinto 14 >