< 1 Akorinto 10 >

1 Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja.
Car je ne veux pas que vous ignoriez, mes frères, que nos pères ont tous été sous la nuée, et qu’ils ont tous passé la mer;
2 Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja.
Qu’ils ont tous été baptisés sous Moïse, dans la nuée et dans la mer;
3 Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu
Qu’ils ont tous mangé la même nourriture spirituelle,
4 ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu.
Et qu’ils ont tous bu le même breuvage spirituel (car ils buvaient de l’eau de la pierre spirituelle qui les suivait; or cette pierre était le Christ);
5 Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.
Cependant la plupart d’entre eux ne furent pas agréables à Dieu; car ils succombèrent dans le désert.
6 Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo.
Or toutes ces choses ont été des figures de ce qui nous regarde, afin que nous ne convoitions pas les choses mauvaises, comme eux les convoitèrent;
7 Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.”
Et que vous ne deveniez point idolâtres, comme quelques-uns d’eux, selon qu’il est écrit: Le peuple s’est assis pour manger et pour boire, et s’est levé pour se divertir.
8 Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000.
Ne commettons pas la fornication comme quelques-uns d’entre eux la commirent, et il en tomba vingt-trois mille en un seul jour.
9 Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka.
Ne tentons point le Christ comme quelques-uns d’eux le tentèrent, et ils périrent par les serpents.
10 Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.
Et ne murmurez point comme quelques-uns d’eux murmurèrent, et ils périrent par l’exterminateur.
11 Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. (aiōn g165)
Or toutes ces choses leur arrivaient en figure, et elles ont été écrites pour nous être un avertissement à nous pour qui est venue la fin des temps. (aiōn g165)
12 Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe!
Que celui donc qui se croit être ferme prenne garde de tomber.
13 Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.
Qu’il ne vous survienne que des tentations qui tiennent à l’humanité. Or Dieu est fidèle, et il ne souffrira pas que vous soyez tentés par-dessus vos forces; mais il vous fera tirer profit de la tentation même, afin que vous puissiez persévérer.
14 Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano.
C’est pourquoi, mes bien-aimés, fuyez le culte des idoles.
15 Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi.
C’est comme à des hommes sages que je parle; jugez vous-mêmes de ce que je dis.
16 Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu?
Le calice de bénédiction que nous bénissons n’est-il pas la communication du sang du Christ? et le pain que nous rompons n’est-il pas la participation au corps du Seigneur?
17 Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.
Car, quoique en grand nombre, nous sommes un seul pain, un seul corps, nous tous qui participons à un seul pain.
18 Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo?
Voyez Israël selon la chair; ceux qui mangent des victimes ne participent-ils pas à l’autel?
19 Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse?
Quoi donc? Veux-je dire que ce qui est immolé aux idoles soit quelque chose? ou que l’idole soit quelque chose?
20 Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo.
Mais ce qu’immolent les gentils, ils l’immolent aux démons et non à Dieu. Or je désire que vous n’ayez aucune société avec les démons: vous ne pouvez boire le calice du Seigneur et le calice des démons.
21 Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda.
Vous ne pouvez avoir part à la table du Seigneur et à la table des démons.
22 Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?
Voulons-nous provoquer le Seigneur? Sommes-nous plus forts que lui? Tout m’est permis, mais tout ne m’est pas avantageux.
23 Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza.
Tout m’est permis, mais tout n’édifie pas.
24 Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.
Que personne ne cherche son propre avantage, mais celui des autres.
25 Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
Mangez tout ce qui se vend à la boucherie, ne faisant aucune question par conscience.
26 Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”
Car au Seigneur est la terre et toute sa plénitude.
27 Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu.
Si un infidèle vous invite, et que vous vouliez aller, mangez de tout ce qu’on vous servira, ne faisant aucune question par conscience.
28 Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima.
Mais si quelqu’un dit: Ceci a été immolé aux idoles, n’en mangez point, à cause de celui qui vous a avertis, et par conscience.
29 Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina?
Or je dis la conscience, non la tienne, mais celle d’autrui. Car pourquoi ma liberté serait-elle condamnée par la conscience d’un autre?
30 Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?
Si je mange avec actions de grâces, pourquoi me laisserai-je maudire pour une chose dont je rends grâces?
31 Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu.
Soit donc que vous mangiez, soit que vous buviez, ou que vous fassiez quelque autre chose, faites tout pour la gloire de Dieu.
32 Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu.
Ne soyez une occasion de scandale ni pour les Juifs, ni pour les gentils, ni pour l’Eglise de Dieu;
33 Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.
Comme moi-même je complais à tous en toutes choses, ne cherchant pas ce qui m’est avantageux, mais ce qui l’est au grand nombre, afin qu’ils soient sauvés.

< 1 Akorinto 10 >