< 1 Mbiri 24 >

1 Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Synů pak Aronových tato jsou zpořádaní: Synové Aronovi: Nádab, Abiu, Eleazar a Itamar.
2 Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
Ale že umřel Nádab a Abiu před otcem svým, a neměli synů, protož konali úřad kněžský Eleazar a Itamar.
3 Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
Kteréž zpořádal David, totiž Sádocha z synů Eleazarových, a Achimelecha z synů Itamarových, vedlé počtu a řádu jejich v přisluhováních jejich.
4 Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
Nalezeno pak synů Eleazarových více předních mužů, než synů Itamarových, a rozdělili je. Z synů Eleazarových bylo předních po domích otcovských šestnáct, a z synů Itamarových po čeledech otcovských osm.
5 Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
I rozděleni jsou losem jedni od druhých, ačkoli byli knížata nad věcmi svatými, a knížata Boží z synů Eleazarových a z synů Itamarových.
6 Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
I popsal je Semaiáš syn Natanaelův, písař z pokolení Léví před králem a knížaty, a Sádochem knězem a Achimelechem synem Abiatarovým i knížaty čeledí otcovských mezi kněžími a Levíty, tak že dům otcovský jeden zaznamenán Eleazarovi, tolikéž druhý zaznamenán Itamarovi.
7 Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
Padl pak los první na Jehoiariba, na Jedaiáše druhý,
8 achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
Na Charima třetí, na Seorima čtvrtý,
9 achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
Na Malkiáše pátý, na Miamin šestý,
10 achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
Na Hakkoza sedmý, na Abiáše osmý,
11 achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
Na Jesua devátý, na Sechaniáše desátý,
12 a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
Na Eliasiba jedenáctý, na Jakima dvanáctý,
13 a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
Na Chuppa třináctý, na Jesebaba čtrnáctý,
14 a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
Na Bilgu patnáctý, na Immera šestnáctý,
15 a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
Na Chezira sedmnáctý, na Happizeza osmnáctý,
16 a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
Na Petachiáše devatenáctý, na Ezechiele dvadcátý,
17 a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
Na Jachina jedenmecítmý, na Gamule dvamecítmý,
18 a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
Na Delaiáše třímecítmý, na Maaseiáše čtyřmecítmý.
19 Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
Ti jsou, jenž zřízeni byli v přisluhováních svých, aby vcházeli do domu Hospodinova podlé řádu svého, pod spravou Arona otce jejich, jakož mu byl přikázal Hospodin Bůh Izraelský.
20 Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
Z synů Léví ostatních, z synů Amramových Subael, z synů Subael Jechdeiáš.
21 Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
Z Rechabiáše, z synů Rechabiášových kníže Iziáš.
22 Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
Z Izara Selomot, z synů Selomotových Jachat.
23 Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
Synové pak Jeriášovi: Amariáš druhý, Jachaziel třetí, Jekamam čtvrtý.
24 Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
Syn Uzielův Mícha, z synů Míchy Samir.
25 Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
Bratr Míchův Iziáš, a syn Iziášův Zachariáš.
26 Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
Synové Merari: Moholi a Musi, synové Jaaziášovi: Beno.
27 Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
Synové Merari z Jaaziáše: Beno, Soham, Zakur a Ibri.
28 Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
Z Moholi Eleazar, kterýž neměl synů.
29 Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
Z Cisa synové Cisovi: Jerachmeel.
30 Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
Synové pak Musi: Moholi, Eder a Jerimot. Ti jsou synové Levítů po domích otců svých.
31 Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.
I ti také metali losy naproti bratřím svým, synům Aronovým, před Davidem králem, Sádochem a Achimelechem, i knížaty otcovských čeledí z kněží a Levítů, z čeledí otcovských, každý přednější naproti bratru svému mladšímu.

< 1 Mbiri 24 >