< Псалми 78 >
1 Асафово поучение. Слушайте, люде мои, поучението ми: Приклонете ушите си към думите на устата ми.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 Ще отворя устата си в притча, Ще произнеса гатанки от древността.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Това, което чухме и научихме, И нашите бащи ни разказаха,
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 Няма да го скрием от чадата им в идното поколение, Но ще повествуваме хвалите на Господа, Неговата сила и чудесните дала, които извърши,
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Защото Той постави свидетелство в Якова, И положи закон в Израиля, За които заповяда в Израиля, За които заповяда на бащите ни Да ги възвестяват чадата си,
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 За да ги знае идното поколение, Децата, които щяха да се родят, - Които да настанат и да ги разказват на своите чада.
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 За да възложат надеждата си на Бога, И да не забравят делата на Бога, Но да пазят Неговите заповеди,
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 И да не станат като бащите си, Упорито и непокорно поколение, Поколение, което не утвърди сърцето си. И чийто дух не биде непоколебим за Бога.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Ефремците, макар въоръжени и запъващи лъкове, Върнаха се назад в деня на боя.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Не опазиха завета на Бога, И в закона Му не склониха да ходят,
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 А забравиха Неговите деяния И чудесните дела, които им показа.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Пред бащите им извърши чудеса В Египетската земя, в полето Танис
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Раздвои морето и ги преведе, И направи водите да стоят като грамада.
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Води ги денем с облак, И цялата нощ с огнена виделина.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Разцепи канари в пустинята, И ги напои изобилно като от бездни.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 И изведе потоци из канарата, И направи да потекат води като реки.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Но те продължиха да Му съгрешават още И да огорчават Всевишния в безводната страна.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Със сърцето си изпитаха Бога, Като искаха ястия за лакомството си,
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 И говориха против Бога, казвайки: Може ли Бог да приготви трапеза в пустинята?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Ето, Той удари канарата, та потекоха води и потоци преляха; А може ли и хляб да даде, или да достави месо за людете Си?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 Затова Господ чу и се разгневи, И огън пламна против Якова, А още и гняв обсипа Израиля;
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Защото не повярваха в Бога, Нито Му уповаваха, че ще ги избави.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 При все това Той заповяда на облаците горе, И отвори небесните врати,
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 Та им наваля манна да ядат И даде им небесно жито.
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Всеки ядеше ангелски хляб; Прати им храна до насита.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Подигна източен вятър на небето, И със силата Си докара южния вятър.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Наваля върху тях и месо изобилно като прах, И птици крилати много като морския пясък;
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 И направи ги да падат всред стана им, Около жилищата им.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 И тъй, ядоха и се преситиха, Като им даде това, което желаеха.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 А докато още не бяха се отказали от лакомството си, И ястието им бе в устата им,
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Гневът Божий ги обсипа та изби по-тлъстите от тях, И повали отборните на Израиля.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 При всичко това те следваха да съгрешават, И не вярваха поради чудесните Му дела.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 Затова Той изнуряваше дните им със суета, И годините им с ужас.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Когато ги умъртвяваше, тогава питаха за Него, Та изново търсеха Бога ревностно;
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 И спомниха, че Бог им беше канара, И всевишният Бог техен изкупител.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Но с устата си Го ласкаеха, И с езика си Го лъжеха;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Защото сърцето им не беше право пред Него, Нито бяха верни на завета Му.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Но Той, като многомилостив, прощаваше беззаконието им и не ги погубваше; Да! много пъти въздържаше гнева Си, И не подигаше всичкото Си негодувание;
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 И си спомняше, че бяха плът, Вятър, който прехожда и не се връща.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Колко пъти Го огорчаваха в пустинята И Го разгневяваха в безводната страна,
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Като изново изпитваха Бога, И предизвикваха Светия Израилев!
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Не си спомнюваха силата на ръката Му В деня, когато ги избави от противника,
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 Как показа в Египет знаменията Си, И чудесата на полето Танис,
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 И превърна вадите им в кръв, И потоците им, та не можаха да пият;
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Как прати върху тях рояци мухи, които ги изпоядоха, И жаби, които ги изпогубиха,
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 И предаде произведенията им на гъсеници, И трудовете им на скакалци
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Как порази с град лозята им, И със светкавици черниците им,
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 И предаде на град добитъка им, И стадата им на мълнии;
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Как изля върху тях пламенния Си гняв, Негодувание, ярост и неволя, - Нашествие на ангелите на злощастието,
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Изравни пътя за гнева Си, Но пощади от смърт душата им, Но предаде на мор живота им;
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Как порази всеки първороден заведе ги като стадо в Египет, Първака на силите им в шатрите на Хама,
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 А людете Си изведе като овци и заведе ги като стадо в пустинята,
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 И води ги безопасно, така щото не се бояха, А неприятелите им - морето ги покри;
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Как ги въведе в светия Си предел. В тая поляна, която десницата Му придоби,
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 И изгони пред тях народите, Та им ги раздели за наследство с въже, И в шатрите им настани Израилевите племена.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Но въпреки това те изпитваха Всевишния Бог и се бунтуваха против Него, И не пазеха наредбите Му,
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Но връщаха се назад, и обхождаха се неверно както бащите им; Измятаха се като неверен лък.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Защото Го разгневиха с високите си места, И с ваяните си идоли Го подбуждаха към ревност.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Чу Бог и възнегодува, И много се погнуси от Израиля,
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Тъй че напусна скинията в Сило, Шатъра, който бе поставил между човеците,
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 И предаде на пленение Силата Си, Славата Си в неприятелска ръка.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Тоже и людете Си предаде на меч, Като се разгневи на наследстовото Си.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Огън пояде момците им, И девиците им не се възпяваха с венчални песни.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Свещениците им паднаха от нож; И вдовиците им не плакаха.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Тогава се събуди Господ като от сън, Като силен мъж, който ободрен от вино, вика;
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 И, като порази враговете Си, отблъсна ги назад, Та ги предаде на вечно посрамяване.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 При това Той се отказа от Иосифовия шатър, И Ефремовото племе не избра;
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Но избра Юдовото племе, Хълма Сион, който възлюби.
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Съгради светилището Си като небесните възвишения, Като земята, която е утвърдил за винаги.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Избра и слугата Си Давида, И го взе от кошарите на овците;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 Отподир дойните овци го доведе За да пасе людете Му Якова и наследството Му Израиля.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Така той ги пасеше според незлобието на сърцето си, И ги водеше с изкуството на ръцете си.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.