< Притчи 1 >

1 Притчи на Давидовия син Соломон, Израилев цар,
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Записани за да познае някой мъдрост и поука, За да разбере благоразумни думи,
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 За да приеме поука за мъдро постъпване, В правда, съдба и справедливост,
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 За да се даде остроумие на простите, знание и разсъждение на младежа,
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 За да слуша мъдрият и да стане по-мъдър И за да достигне разумният здрави начала,
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 За да се разбират притча и иносказание, Изреченията на мъдрите и гатанките им.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 Страх от Господа е начало на мъдростта; Но безумният презира мъдростта и поуката.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Сине мой, слушай поуката на баща си, И не отхвърляй наставлението на Майка си,
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Защото те ще бъдат благодатен венец за главата ти, И огърлица около шията ти.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Сине мой, ако грешните те прилъгват, Да се не съгласиш.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 Ако рекат: Ела с нас, Нека поставим засада за кръвопролитие. Нека причакаме без причина невинния,
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Както ада нека ги погълнем живи, Даже съвършените, като ония, които слизат в рова, (Sheol h7585)
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol h7585)
13 Ще намерим всякакъв скъпоценен имот, Ще напълним къщите си с користи,
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Ще хвърлим жребието си като един от нас, Една кесия ще имаме всички;
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Сине мой, не ходи на пътя с тях, Въздържай ногата си от пътеката им,
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Защото техните нозе тичат към злото, И бързат да проливат кръв.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Защото напразно се простира мрежа Пред очите на каква да било птица.
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 И тия поставят засада против своята си кръв, Причакват собствения си живот.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Такива са пътищата на всеки сребролюбец: Сребролюбието отнема живота на завладените от него.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 Превъзходната мъдрост възгласява по улиците, Издига гласа си по площадите,
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Вика по главните места на пазарите, При входовете на портите, възвестява из града думите си:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Глупави, до кога ще обичате глупостта? Присмивачите до кога ще се наслаждавате на присмивките си, И безумните ще мразят знанието?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Обърнете се при изобличението ми. Ето, аз ще излея духа си на вас, Ще ви направя да разберете словата ми.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Понеже аз виках, а вие отказахте да слушате, Понеже простирах ръката си, а никой не внимаваше,
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Но отхвърлихте съвета ми, И не приехте изобличението ми,
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 То аз ще се смея на вашето бедствие, Ще се присмея, когато ви нападне страхът,
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Когато ви нападне страхът, като опустошителна буря, И бедствието ви се устреми като вихрушка, Когато скръб и мъки ви нападнат,
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Тогава те ще призоват, но аз няма да отговоря, Ревностно ще ме търсят, но няма да ме намерят.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Понеже намразиха знанието, И не разбраха страха от Господа,
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Не приеха съвета ми, И презряха всичкото ми изобличение,
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Затова, ще ядат от плодовете на своя си път, И ще се наситят от своите си измислици.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Защото глупавите ще бъдат умъртвени от своето си отстъпване, И безумните ще бъдат погубени от своето си безгрижие,
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Но всеки, който ме слуша, ще живее в безопасност, И ще бъде спокоен без да се бои от зло.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”

< Притчи 1 >