< Псалми 17 >

1 Давидова молитва. Послушай, Господи, правото; внимавай на вика ми; Дай ухо на молитвата ми, която принасям с искрени устни.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 Нека излезе присъдата ми от присъствието Ти; Очите Ти нека гледат справедливо.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Изпитал си сърцето ми; посетил си ме нощно време; Опитал си ме; и не си намерил в мене никакво зло намерение. Мислите ми не надвишават устата ми.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Колкото за човешките дела, чрез думите на Твоята уста Аз опазих себе си от пътищата на насилниците.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Стъпките ми са се пазили здраво в Твоите пътища; Нозете ми не са се подхлъзнали.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Аз Те призовах, Боже, защото ще ми отговориш; Приклони към мене ухото Си и послушай думите ми.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Яви чудните Си милосърдия, Ти, Който с десницата Си избавяш уповаващите на Тебе. От ония, които въстават против тях.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Пази ме като зеница на око; Скрий ме под сянката на крилата Си
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 От нечестивите, които ме съсипват, От неприятелите на душата ми, които ме окръжават.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Обградени са от своята тлъстина; Устата им говорят горделиво.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Те обиколиха вече стъпките ми; Насочиха очите си, за да ни тръшнат на земята;
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Всеки един от тях прилича на лъв, който желае да разкъса. И на лъвче, което седи в скришни места.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Стани, Господи, предвари го, повали го; С меча Си избави душата ми от нечестивия,
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 От човеци, Господи, с ръката Си, От светските човеци, чиито дял е в тоя живот, И чиито корем пълниш със съкровищата Си; Които са наситени с чада, И останалия си имот оставят на внуците си.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 А аз ще видя лицето Ти в правда; Когато се събудя ще се наситя от изгледа Ти.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

< Псалми 17 >